Zomba District Church of Christ Youth Ministry

Zomba District Church of Christ Youth Ministry You're the light of the world. A city set on a hill cannot be hidden. Matthew 5:14

Today, 25th October, 2025, Ntonda Zone Church of Christ Youth Ministry is hosting a Bible study an event which is taking...
25/10/2025

Today, 25th October, 2025, Ntonda Zone Church of Christ Youth Ministry is hosting a Bible study an event which is taking place at Jali Hunger Center Hall in Zomba District.. Over 200 Youths from over 20 Church of Christ congregations are in attendance.
Zomba District Youth Ministry - Church of Christ works with 5 Zones (Sections). These are;
1. Ntonda
2. Thondwe
3. Zomba Central
4. Chingale
5. Sakata.

15/06/2025
Lipoti la momwe utumiki wa chinyamata m'boma la Zomba wayendera mu Chaka Cha 2024. Utumiki wa chinyamata m'boma la Zomba...
03/01/2025

Lipoti la momwe utumiki wa chinyamata m'boma la Zomba wayendera mu Chaka Cha 2024.

Utumiki wa chinyamata m'boma la Zomba unakhazikitsa zochitika zikuluzikulu zitatu. Zochitikazi ndi monga izi;
1. Kuthandiza ophunzira mu Sukulu zapulaimale.
2. Maphunziro amasiku atatu.
3. Ulendo waku Cape Maclear.

Chochitika choyamba mu chaka Cha 2024, chinali kuthandiza ophunzira apa Sukulu ya namisunju yomwe ili kwa Jali m'boma la Zomba. Ophunzira opitilira 1000 analandira thandizo monga;
-Makope
- Zolembera
- mipando ( Mabetchi)
- Zodzisamalira atsikana Nthaw ya msambo (sanitary pads).
Utumiki wachinyamata ukuthokoza kwambiri kwa onse omwe anatenga gawo kupeleka thandizo lachuma kapena katundu amene amafunika ku ntchitoyi. Ena mwa anthuwa anali oti samasonkhana mu mpingo wa Khristu koma anadzichepetsa kupeleka thandizo lopita ku ntchito imeneyi.

Chochitika chachiwiri unali msonkhano umene unachitika mu mwezi wa August kuchingale. Msonkhano umenewu unali wamasiku atatu ndipo mutu wake unali " UMODZI UMENE AMBUYE YESU KHRISTU ADAUPEMPHERERA.
Achinyamata oposa 250 kuchokera mmagome oposa 30 ndiwo anabwera ku msonkhanowu.
Chochitika chomaliza unali msonkhano umene unachitika kuyambira pa 29 November ndipo unatha pa 1 December 2024. Msonkhano umenewu unali wamasiku atatu ndipo unachitikira pa Sukulu yapulaimale ya Cape Maclear ku mangochi.
Maphunziro anali apamwamba kwambiri pamene aphunzitsi athu achitsulo kuchokera ku ntaja, komanso a G Phiri kuchokera ku mangochi anaphunzitsa zozama kwambiri pa mutu onena kuti KUYENDA MOYENERA MAITANIDWE ATHU.
Achinyamata pafupipafup 300 ochokera ku Zomba komanso boma lamangochi anali nawo pa msonkhano umenewu. Mwa zina, msonkhanowu unakulitsa ubale pakati pa mipingo yaku mangochi ndi Zomba.
Zochitika zina zinali monga kukwera maboti, kusambira pa nyanja ndi zina. Izi zinapeleka chimwemwe chachikulu kwa achinyamata chifukwa ena kanali koyamba kubwera ku nyanja.
Mmalo mwa achinyamata onse ku Zomba, timafuna tithokoze kwambiri atsogoleri ampingo omwe amadzipeleka kuutumiki wachinyamata popeleka thandizo la ndalama, malangizo komanso ena amapezeka pa msonkhano.
Tithokoze kwambiri makolo amene amapeleka ndalama komanso chilolezo kwa achinyamata. Achinyamata eni ayeneranso kuthokozedwa chifukwa kupanga ganizo lopita ku msonkhano sichinthu chapafupi maka mmoyo uno pamene achinyamata akuyenda munyengo zovuta.
Chaka Cha 2024 Chinali chovuta kwambiri ku dziko la Malawi kumbali ya chuma. Izi zinadza chifukwa anthu sadakolole bwino kamba kamavuto odza chifukwa Cha namondwe. Chuma chikavuta mudziko, mpingo nawo umavutika kukwanitsa ma program amene akhazikitsidwa.
Ngakhale panali zovuta zonsezi, Mulungu wakhala okhulupilika ku utumiki wa chinyamata m'boma la Zomba pamene takwanitsa zochitika ZONSE.
Pamene 2024 wapita, tikuyang'ana chitsogolo kuti 2025 atibweretsera zotani.
Zina mwa zochitika chaka chino, achinyamata ndi atsogoleri ampingo adzakumana ku Chikamveka Church of Christ pa 15 komwe akudzasankha atsogoleri atsopano omwe ayendetse utumiki kwa zaka zomwe zikudzazi. Pa msonkhano umenewu mpamene padzaikidweso ndondomeko ya zochitika za 2025.
Tipemphera kuti Chaka chino Mulungu atipatse chuma choyendetsera zochitika zake. Tipemphera kuti Mulungu apeleke atsogoleri amasomphenya omwe adzapitiliza kuchita pamene komiti yakale yakhala ikuchita ndikubweranso zina zatsopano.

19/12/2024

2024 Youth Retreat - Cape Maclear - Mangochi

Help help help
04/12/2024

Help help help

In the same way, after supper he took the cup, saying, "This cup is the new covenant in my blood; do this, whenever you ...
16/09/2024

In the same way, after supper he took the cup, saying, "This cup is the new covenant in my blood; do this, whenever you drink it, in remembrance of me.
For whenever you eat this bread and drink this cup, you proclaim the Lord's death until he comes.
1 Corinthians 11:25-26.( The NIV Study Bible).

Church of Christ - Zomba District Youth Ministry.Utumiki wa chinyamata mu mpingo wa Khristu m'boma la Zomba, unakonza ms...
04/08/2024

Church of Christ - Zomba District Youth Ministry.

Utumiki wa chinyamata mu mpingo wa Khristu m'boma la Zomba, unakonza msonkhano kuyambira lachisanu pa 2 Mpaka laMulungu pa 4 August 2024. Msonkhanowu unali pa Ntungulutsi primary school motsogozedwa ndi Mpingo wa Misenjere Church of Christ.

Mutu wa msonkhano unali UMODZI Omwe YESU KHRISTU adaupempherera (Yohane 17:20-23).
Mutu umenewu unakonzedwa Poona kuti Mpingo wa Khristu kuno ku Malawi wataya umodzi umene Yesu Khristu akufuna ndipo aphunzitsi omwe anali kuphunzitsa anaunikira kufunika kosunga umodzi ngati Mpingo, komanso kuyang'ana zifuwa zomwe zikusokoneza umodzi mu Mpingo wa Khristu.

Tithokoze kwambiri Mulungu chifukwa Cha msonkhanowu.
Msonkhano onse tinali ndi osonkhana 262 omwe anachokera m'mipingo 40. Mipingo imeney ndiochokera mu boma la Zomba.

Bester Muliya ndi m'bale mwa Ambuye ameneso amakangalika kutumikira mu utumiki wa chinyamata m'boma lino la Zomba. Tiyen...
21/07/2024

Bester Muliya ndi m'bale mwa Ambuye ameneso amakangalika kutumikira mu utumiki wa chinyamata m'boma lino la Zomba. Tiyeni tidzamupange support pa 31 August pamene akukwatira Martha.

ZOMBA District Church of Christ Youth ministry meeting with Sakata Youth Ministry Zone.Venue: Makumba 2 Church of Christ...
10/06/2024

ZOMBA District Church of Christ Youth ministry meeting with Sakata Youth Ministry Zone.
Venue: Makumba 2 Church of Christ
09/06/2024.

Address

Zomba

Telephone

+265882412614

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Zomba District Church of Christ Youth Ministry posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Place Of Worship

Send a message to Zomba District Church of Christ Youth Ministry:

Share