28/01/2026
MUTU 12
KUTHA KWA BANJA
Tiyeni tione mwa zina zomwe zimachitika ngati banja latha. Nthawi zambiri banja limakathera kukhoti, mwamuna kapena mkazi akakasuma.
Yesaya 41:10
Usaope, pakuti Ine ndili pamodzi ndi iwe; usaopsedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakuchirikiza ndi dzanja langa lamanja la chilungamo.
Ngati wachotsedwa ku banja opanda chifukwa chokwanira Yehova amakhala nawe nthawi zonse.
Mukasankha kuti banja lithe, mungalandidwe mwana, nyumba kapena kulipira ndalama. Mungayesetse kudandaulira woweruza koma mwina iye sangasinthe chigamulo. Mapeto ake woweruzayo, yemwe mwina simukudziwana naye nβkomwe, angakuuzeni masiku amene muyenera kukaona mwana wanu pa mwezi, ndiponso ndalama zimene muyenera kumamupatsa. Zimene woweruzayu angakulamuleni kuchita zingakhale zosiyana kwambiri ndi zimene inuyo mukanachita panokha.
1 Akorinto 1:10
Koma ndikudandaulirani inu, abale, mwa dzina la Ambuye wathu Yesu Khristu, kuti munene chimodzimodzi inu nonse, ndi kuti pasakhale malekano pakati pa inu; koma mumangike mu mtima womwewo ndi m'chiweruziro chomwecho.
Nthawi zambiri kuthetsa banja kumangoyambitsa mavuto ena. Chilichonse chimasintha, kungoyambira kokhala komanso ndalama, ndipo nthawi zambiri kusintha kwake kumakhala kopweteka. Komanso kutha kwa banja kumawakhudza kwambiri ana.
Mateyu 19:9
Ndipo Ine ndinena kwa inu, Amene aliyense akachotsa mkazi wake, kosakhala chifukwa cha chigololo, nadzakwatira wina, achita chigololo: ndipo iye amene akwatira wochotsedwayo, achita chigololo.
Ena amathetsa banja ati chifukwa mkazi sakubereka kapena mwamunsa koma tizindikire mawu ochokera ku Genesis 25:21, Ndipo Isaki anampembedzera mkazi wake kwa Yehova popeza anali wouma: ndipo Yehova analola kupembedza kwake, ndipo Rebeka mkazi wake anatenga pakati.