06/02/2024
PHUNZIRO LA SABATA SUKULU KOTALE M'CHIGAWO CHA AKURU.
PHUNZIRO: 6
Mutu: NDIDZAUKA
Lasabata Masana
Phunziro Lathu Mlungu Uno Tiwerenga Kuchokera mu:
Masalimo 18:3-18, Masalimo 4l:13, Deuteronomo 15:7-11, Masalimo 82,
Masalimo 96:6-10, Masalimo 99:1-4, Aroma 8:34. 8:34.
Vesi Loloweza: "Chifiukwa cha kupasuka kwa ozunzika, chifukwa cha kuusa moyo kwa aumphawi, Ndiuka tsopano, ati Yehova; Ndidzamlonga mosungika muja alakalakamo " (Masalimo 12:5).
Mbadwo wathuwu si wokhawo momwe choipa, chosalungama ndi kuponderezana zakhala zikuchitika mochuluka kwambiri. Nawonso olemba Masalimo anakhala mu nyengo zangati zomnwezi. Ndipo
chidzudzulo chimene Mulungu akuchita pofuna kudzudzura ziwawa ndi kuponderezana zomwe zikuchitika m'dziko lapansi lathuli komanso chidzudzulo cha olemba masalimowo eni.
Inde, Yehova ndi woleza mtima ndipo Iye amagwira mkwiyo Wake mu
chilekerero Chake chachikulu, osafuna wina awonongeke,koma kuti onse afike ku kulapa ( 2 Petro 3:9-15). Komabe,ngakhale nthawi yoikika ya kulowelerapo kwa chiweruziro cha Mulungu ikubwera ndithu (Masalimo 96:13,Masalimo 98:9). Ife tikungoyenera kukhulupira Yehova ndi malonkezo Ake,kufikira nthawi yomwe tsikulo lidzafika.
Mlengi yekha, amene mpando Wake wachifumu wakhazikitsidwa pa chilungamo (Masalimo 89:14, Masalimo 97:2), ndipo chiweruziro Chake ndi chachikulu ndi yemwe angapereke mtendere ndi chipambano ku dziko lino lapansi. Magawo awiri a chiweruziro cha Mulungu akuphatikizira chiombolo cha oponderezedwa komanso kuonongedwa kwa oipa (Masalimo 7:6-17).
Izitu ndi zimene ife talonjezedwa,ndipo ndithudi tsiku lina zimenezi zidzachitika, koma iyi idzakhala nthawi yoikika ya Mulungu,osati yathu ayi,ndipo imeneyi ndi mfundo imene olemba Masalimoyu akutsindika kwambiri.
TSIKU LOYAMBA
WANKHONDO WAMPHAMVU
Werengani Masalimo 18:3-18, Masalimo 76:3-9, 12; ndi Masalimo
144:5-7. Kodi Yehova wafotokozedwa motani mmavesi amenewa? nanga zifanizo zimenezi zikuti chiyani za mmene Mulungu alili wokonzeka kuombola anthu Ake?
Nyimbozi zikuyamika Yehova chifukwa cha mphamvu Zake zodabwitsa zomwe ndi zoposa mphamvu za chopa zimene zikuopseza anthu Ake. Masalimo anaonetsera Mulungu mu ulemelero Wake monga Wankhondo chilkupezeka mmalo ambiri m'buku la Masalimo ndipo chagwiritsidwa ntchito kutsindika za kufunikira ndi kutsimikizika kwa yankho la Malungu loyankha anthu Ake amene
akulira chifukwa cha mavuto awo.
"Ndipo anagunda m'mwamba Yehova. Ndipo Wam'mwambamwamba anamvetsa liwu lake; Matalala ndi makala amoto. Ndipo anatuma mivi yake nawabalalitsa;Inde mphezi yaunyinji nawamwaza. Ndipo zikuoneka zoyendamo madzi,Nafukuka madziko a dziko lapansi,mwa kidzudzula kwanu, Yehova mwa Mpumo wa mpweya wa mphuno mwanu" (Masalimo 18:13-15).
Kutsimikizika ndi kukula Kwa ntchito ya Mulungu kukuyenera kuchosa
chikaiko china chilichonse chokaikira za chitsamaliro ndi chifundo chake chachikulu pa odzunzidwa kapena chokaikira za mphamvu yake yogonjetsa choipa. Ifetu tikungoyenera kudikira iye kuti achite motero.
Ndipo pamapeto pake , ngakhale pamene anthu a Mulungu monga Davide anali kumenya nkhondo,chiombolo sichinachitidwe ndi mphamvu ya munthu. Mu nkhondo zake zomenyana ndi adani a anthu a Mulungu,mfumu Davide analemekeza Mulungu kuti iye yekha ndi amene anachita zipambano zonse.
Ndithudi chikadatha kukhala chinthu chofewa kwa Davide kudzitamandira pa zomwe zinachitika pa zipambano ndi zigonjetso zakezo, chikhalirecho iye sanaganize motero ayi. Davide ankadziwa bwino lomwe gwero la mphamvu zake.
Ngakhale Davide akunena kuti Yehova akuphunzitsa manja Ake nkhondo (Masalimo 18:34) mu nkhondo zake zonsezo, palibe pena paliponse m'masalimo pamene iye akudzitamandira chifukwa Cha luntha lake lodziwa kumenya nkhondo. M'malo mwake Davide akutama Yehova monga amene akumumenyera iye nkhondo ndi kukuombola (Masalimo 18:47-48).
M'Masalimo, mfumu Davide amene watchulidwa monga wankhondo wamkulu, akugwira ntchito yake monga katswiri odziwa kuimba nyimbo mwanthetemya komanso amene akulemekeza Yehova monga mombolo ndi wakusunga wa anthu Ake yekhayo (Masalimo 114:10-15). Kulemekeza Mulungu ndi kupemphera ndi zomwe zili gwero la mphamvu za Davide,zinthu zimene zinali zamphamvu kuposa chida china chilichonse cha nkhondo. Mulungu yekha ndi amene ayenera kukhulupilidwa ndi kulambiridwa ndi anthu onse.
*Posatengera kuti muli ndi mphatso,maluso ndi zipambano zanji mmoyo mwanu,Kodi ndi chifukwa chiyani kuli koyenera kuti nthawi zonse inu muzikumbukira gawo la zonsezi? Nanga pamene inu mwaiwala gwero la mphamvu zanu,pakakhala choopsa chanji?*
TSIKU LACHIWIRI
CHILUNGAMO KWA OPONDEREZEDWA
Werengani Masalimo 9:18, Masalimo 12:5, Masalimo 40:17,Masalimo 41:1-3, Masalimo 113:7, Masalimo 146:6-10. Kodi ndi uthenga wanji
umene uli m'mavesi amenewa, womwe ukubwera ngakhalenso kwa ife lino??
Mulungu akuonetsera chitsamaliro chapadera komanso nkhawa yake pa momwe adindo ambiri akulepherelera kuchita chilungamo pa magulu osiyanasiyana a anthu osowa chitetezo,monga osauka,aumphawi,oponderezedwa, opanda bambo,akazi amasiye ,amuna amasiye ndi alendo. Masalimo akufotokoza bwino mfundo imeneyi,monganso chilamulo ndi aneneri (Eksodo 22:21-27,Yesaya 3:13-15).
Masalimo ambiri amagwiritsa ntchito mawu oti "osauka ndi aumphawi" ndipo amapewa kuwatchula oponderezedwa pogwiritsa ntchito mawu ozolowereka ku fuko ndi chipembedzo cha Chiyuda. Izi zachitika pofuna kusindika kuti chitsamaliro Cha Mulungu ndi chopita Kwa anthu onse apadziko lapansi.
Mawu oti "osauka ndi aumphawi" sakungonena za umphawi wakusowa
chuma wokha, koma akuoneranso za umphawi wakusowa chitetezo ndi thandizo. Mawuwa akunena za chifundo Cha Mulungu,ndipo kupereka ganizo lakuti munthu wosaukayo ali yekha yekha komanso alibe thandizo lina lililonse ndipo thandizo lake lokhalo ndi Mulungu yekha basi.
Chithunzithunzi cha "osauka ndi aumphawi" chikukambanso za kukhulupirika, kuona mtima, ndikukonda Mulungu povomereza kuti ife timadalira pa Iye yekha basi ndi kukana khalidwe lina lililonse losonyeza kudzidalira ndi kuzitamandira tokha.
Ndithudi,panopa kusamalira osauka (Masalime 41:1-3) kuli chisonyezo cha kukhulupiriku kwa anthu pamaso pa Mulungu. Zoipa zimene anthu osowa chitetezo anali kuchitiridwa zinali zoipa Kwambiri maka mu chikhalidwe Cha Baibulo nthawi ya (Deuteronomy 15:7-11). Masalimo akulimbikitsa anthu okhulupilira kukweza mawu awo podzudzula mchitidwe uliwonse wankhanza ndi wopondereza osauka.
Masalimo akutsindikanso za kupanda pake koika chikhulupiriro chathu pa zinthu zokutha,kuzitenga ngati izo ndi gwero podalirika la nzeru ndi chitetezo chathu. Anthu a Mulungu akuyenera kukana yesero loika chikhulupiliro chonse Cha chipulumutso chawo mwa atsogoleri awo komanso mu nzeru za anthu,maka pamene zinthu zimenezi zili zosemphana ndi njira za Mulungu.
Mu chisomo chake Ambuye wathu Yesu Khristu anamvetsetsa mavuto amene osauka amakumana nawo,pokhala osauka Iye mwini ,kuti m'kusauka Kwake ambiri akhale olemera (2 Akorinto 8:9). Kulemera Kwa Khristu kukuphatikizira kumasulidwa kwathu ku kuponderezedwa kulikonse kobwera kamba ka uchimo,ndipo Iye akutilonjeza moyo wosatha mu ufumu wa Mulungu (Chivumbulutso 21:4).
Yesu Khristu akukwaniritsa malonjezo amene akupezeka m'masalimo okamba za Woweruza wa Mulungu,amene adzaweruze aliyense wochita nkhanza anthu osauka komanso aliyense wonyalanyaza udindo wosamalira aumphawi (Mateyu 25:31-46).
*Kodi ndi kangati ife timaganizira za "osauka ndi aumphawi" amene ali pakati pathu,nanga ndi kangatinso ife timawasamalira anthu oterewa??*
TSIKU LACHITATU
KODI MUDZAWERUZA MOPANDA CHILUNGAMO KUFIKIRA LITI?
Yehova wapatsa atsogoien a lsrayeli mphamvu zosunga ndi kulimbikitsa chilungamo mu ISrayeli (Masalimo 72:1-7, 12-14). Mafumua Israyeli ankayenera kugwiritsa ntchito mphamvu zawo motsatira chifuniro cha Mulungu. Cholinga chachikulu cha atsogoleriwo chinayenera kukhala kuonetsetsa ku mdzikomo muli mtendere ndi chilungamo komanso kuti osauka akusamaliridwa,ndipo pokhapo ndi pamene dzikolo ndi anthu ake onse akadapedza chipambano .
Ufumuwo ukukhala Wamphamvu chifukwa Cha kukhulupilika Kwa atsogoleri ndi anthu Ake pamaso pa Mulungu,osati chifukwa za mphamvu zawo za umunthu.
*Werengani Masalimo 82. Kodi chinkachitika ndi chiyani atsogoleriwo akakhotetsa chilungamo ndi kupondereza anthu amene iwo anapatsidwa kuti awateteze???*
Mu Masalimo 82. Mulungu akulengeza zilango zake pa oweruza a ISrayeli omwe anali opanda chilungamo, "Milungu" (Masalimo 87:1,6) yomwe yatchulidwayi,modziwikiratu singakhale milungu yachikunja kapena angelo, chifukwatu magulu awiriwa sanapatsidwe udindo opereka chilango Kwa anthu a Mulungu,chotero iwo sakanalangidwa chifukwa cholephera kukwaniritsa udindo umenewu.
Malamulo amene alembedwa mu Masalimo 82:2-4 akubwereza Malamulo omwe ali m'mabuku asanu oyambilira a Baibulo olembedwa ndi Mose momwe atsogoleri a ISrayeli atchulidwa monga 'milungu' (Deuteronomo 1:16-18,16:18-20, Yohane 10:33-35), Mulungu akufunsa "ana a anthu" ngati akuweruza mwa chilungamo ndipo chilungamo chao chilengezedwa chifukwa iwo apezeka opanda chilungamo. Atsogoleri apunthwa mu mdima koma sakudziwa (Masalimo 82:5), chifukwa iwo asiya chilamulo cha Mulungu chomwe chili kuunika (Masalimo 119:105).
Malembo akulimbikitsa motsindika ganizo lakuti Yehova ali Mulungu yekhayo. Mulungu amalamulira dziko lapansi kupyolera mwa atsogoleri a anthu amene asankhidwa ndi Iye kukhaka akazembe Ake (Aroma 13:1), Chikhalirecho,kodi ndi kangati mu mbiri za dziko ngakhalenso panopa akazembe amenewa,akhala akugwiritsa ntchito udindo wawo molakwika.
Masalimo 82 monyogodola akuika poyera mpatuko wa atsogoleri ena amene amadzikweza pamwamba pa anthu awo,podziyetsa iwo eni 'milungu'. Ngakhale Mulungu amapereka ulamuliro ndi mwayi Kwa atsogoleri a ISrayeli,wotchedwa "ana a Mwambamwamba" komano womuimikira Iye monga akazembe Ake, Iye anadzudzulabe atsogoleri oipawa .
Mulungu akukumbutsa atsogoleriwo kuti ali chimodzi modzi anthu ena onse,ndipo akuyenera kumvera Malamulo otsogolera anthu ku khalidwe,mmene zilili ndi anthu ena onse, chifukwa palibe munthu amene ali opambana woposa malamulo a Mulungu (Masalimo 82:6-8).
Mulungu adzaweruza dziko lonse lapansi; nawonso anthu a Mulungu adzayankha milandu yawo kwa Mulungu. Magulu onse awiri, atsogoleriwo ndi anthu awo,onse akuyenera kutsanza chitsanzo cha Woweruza wa Umulungu ndi kuika chiyembekezo chawo chonde mwa Iye.
Kodi inu muli ndi ulamuliro wanji pa ena? Nanga mukugwiritsa ntchito ulamuliro wanuwo molungama ndi m***a mtima motani?
Inutu mukuyenera kumvera zimene zanenedwazi.
TSIKU LACHINAYI
TSANULANI MKWIYO WANU
Werengani Masalimo 58:6-8;Masalimo 69:22-28;Masalimo 83:9-17;Masalimo 137:7-9, Masalimo 94:12. Kodi Masalimo amenewa akutipatsa malingaliro anji?Nanga m'Masalimo amenewa ndi ndani amene watchulidwa kuti ndi mkhalapakati wa chiweruziro ??
Masalimo ena akupempha Mulungu kubwezera chilango pa anthu ndi mafuko amene akufuna kuononga, kapena amene aononga kale,Alembi a Masalimo kapena ngakhale anthu awo.
Masalimo akhoza kuoneka ndi kumveka ngati ndi ovuta kuwamvetsetsa kamba ka mawu ake achindunji amene akuoneka ngati ali osemphana ndi mfundo ya Baibulo yotilangiza kukonda adani athu (Mateyu 5:44).
Komabe, mkwiyo wa mlembi wa Masalimoyu wodana ndi nkhanza kapena kuponderezana uli mkwiyo wothandiza ndi wabwino. Zikutanthauza kuti olemba Masaimowa anali osamala kwambiri pa mfundo zokhudza chabwino ndi choipa kuposa mmene ena ambiri ankakhalira. Iwo anali okhuzika
chifukwa zoipa zomwe zinali kuchitidwa m'dziko lapansi osati zochitidwa kwa iwo kokha koma ngakhalenso zimene zimachitidwa Kwa anthu ena.
Komabe, palibe pamene wolemba Masalimoyu mwini wanena kuti abwezera choipacho yekha. Koma mmalo mwake iye akusiya nkhani yobwezerayo m'manja
mwa Mulungu mwini Wake. Masalimowa akukumbutsa anthu za matemberero a
pangano la Mulungu (Denteronomo 27:916), ndipo olemba Masalimowa akupempha Mulungu kuti lye achitepo kanthu posatira lonjezo Lake.
Masalimo ali malangizo olembedwa mu ulosi onena za chiweruziro Cha
Mulungu chimene chilinkudza; iwo sanangokhala mapemphero a wolemba Masalimo kokha. Salimo 137 likuonetsera kulengezedwa kwa chiweruziro cha
Mulungu pa Baibulo, monganso mmene zaonetseredwa kupyolera mwa aneneri.
Chionongêko chimene anthu a Baibulo anachita pa mafuko ena chidzabwerera pa iwo eni. Masalimo akupereka malangizo a umulungu oti ochita choipa sadzakhala osalangidwa mpaka kale.
Kubwezera kwa Mulungu kumachitika mwa chilungamo ndi mwa chisomo. Ana a Mulungu akupemphedwa kupempherera iwo amene akuwachitira nkhanza ndi
khumbo lalikulu loti anthu oterowo atembenuke (Masalimo 83:18,Yeremiya 29:7).
Komabe, pamene alembi a Masalimo akufuna kuti Masalimowa agwirizane
Ndi ndondomeko ya chikondi cha pa adani, ife tikuyenera kusamala kuti tisachepese zochitika zoipa ndi zowawa zimene zafotokozedwa m'Masalimo amenewa.
Mulungu akuvomereza za kutsautsidwa Kwa ana Ake ndipo lye akuwatsimikizira kuti 'imfa' ya okondedwa Ake nja mtengo wake pamaso pa Yehova" (Masalimo 116:15).
Chiweruzo cha Mulungu chimkakamiza anthu Ake kukweza mawu awo podzudzula choipa ndi kufuna kuti ufumu Wake udze m'chidzalo chake chonse. Masalimo akulankhula kwa anthu amene akuvutika ,kuwadziwitsa kuti Mulungu akudziwa za kuvutika kwawo ndi kuti tsiku lina chilungamo chidzafika ndithu.
*Kodi ndi ndani amene nthawi zina sakhala ndi maganizo kapena malingaliro ofuna kubwezera Kwa anthu amene anamuchitira choipa kapena amene anachitira okondedwa ake chinthu choipa Kwambiri? Kodi Masalimo amenewa angakuthandizeni bwanji kuchosa malingaliro otero??*
TSIKU LACHISANU
CHIWERUZO CHA YEHOVA NDI KACHISI
Werengani Masalimo 96:6-10; Masalimo 99:1-4; ndi Masalimo 132:7-9,13-18. Kodi chiweruzo cha Mulungu chikuchitikira kuti, nanga yankholi lili ndi zotsatira zanji pa ife? Kodi kachisi amatithandiza bwanji kumvetsetsa momwe Mulungu adzachitire ndi choipa?
Chiweruziro cha Yehova chili cholumikizana Kwambiri ndi kachisi. Kachisi ndi kumalo komwe wolemba Masalimo anayamba kumvetsetsa bwino za vuto la choipa (Masalimo 73:17 20). Kachisi anakazikitsidwa monga malo a chiweruziro cha Mulungu monga mmene zaonetseredwa ndi chiweruziro cha
Urimu (Numeri 27:21) komanso chapachifuwa cha chiweruziro cha mkulu wa ansembe (Eksodo 28:5, 28-30). Chotsatira chake, Masalimo ambiri akutionetsera Mulungu Ali pa mpando Wake wa chifumu m'kachisi, ali wokonzeka Kuweruza dziko lapansi chifukwa cha tchimo ndi choipa chake.
Nayonso nzeru ya chipulunutso inaonetseredwa kuchokera ku kachisi. Poyamba, anthu achikunja ankalimvetsa tchimo monga banga looneka ndi maso lomwe linkayenera kuchotsedwa pogwiritsa ntchito njira za matsenga Mosiyana
ndi zimenezi, Baibulo limati tchimo ndiko kuchita khalidwe lolakwika la lamulo la Mulungu.
Chiyero cha Mulungu chimatanthauza kuti lye ndi Mulungu wokonda chilungamo ndi kuongoka mtima. Momwemonso anthu Ake akuyenera kutsata
chilungamo Chake ndi kukhala a mtima woongoka, konanso ampembedze lye
m'chiyero Chake. Anthuwo angathe kupembedza Mulungu mchiyero pokha pokha ngati iwo atasunga chilamulo Chake, chomwe chili chitsanzo cha chiyero Chakecho.
Choteroo monga zaonetseredwa ndi mpando wa chifundo wa Mulungu komanso "nsembe za chilungamo," kachisi ndi kumalo kumene machimo
amakhululukidwa ndi komwenso chilungamo chimabwezeretsedwa (Deuteronomo 33:19, Masalimo 4:5:).
Chikhalirecho, "Mulungu wakuwakhululukira" akubwera chilango pa ntchito zoipa za anthu osalapa (Masalimo 99:8). Zotsatira zoonekeratu zoonetsera kachisi monga malo a chiweruziro cha Mulungu zikuoneka mu kutchulidwe Kwa nthawi ndi nthawi kwa chiyero cha Mulungu komanso m'malamulo otilangiza kukhala moyo wa chilungamo, wogwiriza ndi mfundo za Mulungu zomwe zili m'pangano Lake.
Chotsatira Cha chiweruziro Cha Yehova chochokera m'ziyoni chili moyo wabwino wa olungama ndi kugonjetsedwa Kwa ochimwa (Masalimo 132:13-18). Kachisi akulimbikitsa chiyembekezo chotsangalatsa cha kubwera Kwa Yehova monga Woweruza Maka pa Tsiku la Chitetezero.
Momwemonso Masalimo akutitsimikizira kuti Woweruza wa Umulungu wotchedwa Yesu Khristu afika posachedwa m'kachisi wa kumwamba (Masalimo 96:13,98:9, chivumbulutso 11:15-19).
*Werengani Aroma 8:34. Kodi vesi limeneli likutisonyeza bwanji zoti zimene Khristu akuchita m'Kachisi wa kumwamba ndi nkhani yokomeraa anthu Ake*
TSIKU LACHISANU NDI CHIMODZI
KUPITIRIZA PHUNZIRO:
Werengani Ellen G. White, "The Beatitudes," masanmba 6-13, 29-35. M'bukhu la Thoughts From the Mount of blessing.
Masalimo ali mfundo zodzula anthu amene salabadira pamene ena akuchitidwa chosalungama; mfundo zimene zimaletsa anthu kuyanjana ndi choipa. Masalimo salimbikitsa ndi khumbo lofuna kubwezera choipa koma ndi olombikitsidwa ndi changu chofuna kulemekeza dzina la Mulungu.
Pa chifukwachi,ndi
koyenera kuti olungama akondwere pamene akuona kubwezera
kwa Mulungu pa choipa, chifukwa kudzera mu njira imeneyi ndi momwe dzina la
Mulungu ndi chilungamo Chake zibwezeretsedwe m'dziko lapansi (Masalimo 58:10,11).
Masalimo akukakamiza anthu kuti akweze mawu awo, adzudzule choipa ndipo iwo afune kuti ufumu wa Mulungu udeze m'chidzalo chake. M'masalimo,ife tapatsidwa chitsimikizo cha chitonthozo ndi chiombolo cha umulungu. Yehova adzauka!
Mmene adzanyazitsa inu, nadzazunza inu,. .chifukwa cha Ine. Sekerani,
sungalalani. Ndipo Yesu analozera omvera Ake kwa aneneri amene analankhula
m'dzina a Yehova, monga chitsanzo cha kumva zowawa ndi kuleza mtima (Yakobo 5:10).
Abele, MKhristu woyamba mwa ana a Adamu, anaphedwa
chifukwa cha chikhulupiriro chake. Enoke anayenda ndi Mulungu, ndipo dziko lapansi silinamuzindikira. Nowa ananyozedwa monga wochita zinthu moonjeza
ndi mokomeza. Koma ena anayesedwa ndi matonzo ndi zokwapulira,ndiponso nsinga,ndi kuwatsekera m'ndende.
Ena anakwapulidwa, osalola kuomboledwa,kuti akalandire kuuka koposa; Ahebri 11:35,36. -Ellen G White 'Thoughts from the Mount of Blessing,tsamba 33.
MAFUNO OKAMBIRANA: :
1️⃣. Chifukwa chowawidwa mtima kamba ka kupezeka kwa choipa m'dziko lapansi munthu akhoza kukaikira ngati Mulungu akulamuliradi,kodi tingakuze bwanji chikhulupiriro chathu kuti chikhale chosagwezeka chomwe chingaime nji ngakhale m'mayesero? Ndiye kunena kuti, kodi ife chiyang'aniro
chathu pa Chiyani kuti tisunge chikhulupiriro chathu mu chikondi, ubwino ndi mphamvu za Mulungu? Nanga mtanda ukuyenera kutiuza chiyani zokhudza Mulungu ndi khalidwe Ake?
2️⃣. Kodi ndi chifukwa chiyani kuli kofunikira kuti tisadalire njira za anthu (atsogoleri, magulu, ndi mabungwe) monga ndi mayankho opambana a chilungamo m'dziko lino lapansi,koma ife tidalire kwathunthu pa Mawu a Mulungu ndi chiweruzo Chake??
3️⃣. Kodi zotsatira zenizeni za choonadi choti kachisi ndi malo a chiweruziro
cha umulungu ndi chiyani?
4️⃣. Kodi ife
tingamvetsetse bwanji mawu achindunji omwe
anenedwa m'Masalimo ena? Nanga mawu amenewa akutanthauza bwanji kumvetsetsa nyengo zimene alembi a Masalimowa anali kudutsamo??
MATHERO A PHUNZIRO LATHU.
Follow Pastor L Khomera on Facebook