30/10/2020
Moni abale ndi Alongo kuli konse komwe muli.
NTHAWI YA UTHENGA
YESAYA 61:1
Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine , pakuti Yehova wandizodza ine ndilalikire mawu abwino kwa ofatsa.Iye wandituma ndikamange osweka mtima , ndikalalikire kwa a msinga mamasulidwe , ndi kwa omangidwa kutsegulidwa kwa mndende. aleluyaaa!
KODI VUTO LANU NDICHANI ?
Mmene tawerengera mawuwa tikumva za cholinga chimene Yesu khristu anabwerera pa dziko lino lapansi .Cholinga choyambirira akufuna alalikire " UTHENGA WABWINO" Akuti akapolo akhale omasulidwa .Kodi inu okondedwa satana wakumangani magoli otani?
Ngati mukukumana ndi mavuto osiyana siyana , ndipo mwayesera apa ndi apo koma zinthu sizikutheka.Yesu khristu mamuna wamtanda akulankhula nanu lero kuti cholinga chake potifera pa mtanda paja inu ndiine kuti titonthore pa vuto lomwe tili nawo, chofunika mupereke moyo wanu kwa Mulungu .Ndipo mndende zimene mwamangidwa nazo , kaya banja likuvuta , kaya mukufuna machiritso .Ambuye Yesu akuti mukangozipereka inuyo mogonja ndi mozichepesa achosa zonsezo .
Apapa nkhani ndiyoti yesu khristu anabwerera inu ndiine mcholinga choti tisavutike ndi zovuta za dziko lino lapansi .Vuto lanu lirilonse limene likuoneka losatheka taliperekeni kwa mbuye wathu yesu khristu , ndikukutsimikizirani lero kuti mudzamulemekeza ndipo muzakhala mboni .Asing'anga asakunamizeni dziwani kuti kwa yesu kokha nkomwe kuli mayankho . YEREMIYA 33:3 Tawerengeni chapter chimenechi pali mawu achirimbikitso Mulungu kudalitseni nonse ndipo ndipo ndikukufunirani Week end yopambana Amen👏