11/08/2025
from apostle Saiti
*ABALE CHONDE TAWERENGANI CHENJEDZO ILI MOSAMALITSA KWAMBIRI KUTI MUDZIWE ZOMWE ZIKUFUNA KUCHITIKA POSACHEDWAPA*
*AMBUYE ATICHITILE CHIFUNDO*
Ino ndi 2025 ndipo tsopano kuchokera panopa kupita kutsogoloku mpingo ukupita kwao basi ! Nthawi palibepo ndipo ngati sitigwiritsa ntchito mpata omwe tili nao panopo kulibekonso mpata wina ! Ma Simucard akukalembetsedwa kena kutifikitsa pachimake penipeni pa dongosolo la lemba la chirombo !
Koma mtima wanga ukutsautsika kwambiri poona kuti ino ndi 2025 koma anthu adakalimbanabe za sabata ,za ubatizo ,za mabvalidwe ndi zina zoterozo ,kuiwala Mau a pa Ahebri 6:1-2
Okondedwa! Ndikasuzumira ambiri amene tinayamba ano abwerera mmbuyo ,ena ayamba kumeta mmbali ,ena abwerera ku mabanja achiwiri komanso ena abwerera ngakhale kunjira za aneneri onyenga ineyo ndikusowa kunena kuti chani abale !
2018,2019,2020,2021 ndikamakuchenjedzani ndimaona misonzi ikulengeza mmaso mwa anthu ambiri ndipo pena tikamakaliza kulalikira ndimaona anthu akulira pena uthenga umatha tonse tikulira limodzi ,koma pano kulalikira pamtima umachita kumamva kuti anthu awa atopa nao uthenga wa Mulungu !
Abale takuchenjedzani za mkwaturo, takuchenjedzani za gehena , takuchenjedzani za mabvalidwe , takuchenjedzani za kubwezeretsa ,takuuzani za maloto oipa ndikuthandizana mapemphero ,chatsala ndi chani ? Timatenga nthawi yaitali pa media pano kumalalikira mau a Mulungu mmalo motambalala mmipingo mwathu koma ndikuuzani kuti ifika nthawi simudzationanso pano,kuonana kwachiwiri pakakhala pa kulira kwa lipenga!
Anzathu amene mukukhala maiko a kunja ,eee mukukhala kumeneko koma dziwani kuti nthawi yanu yakutherani yokhala kumeneko ndipo ndipemphero langa kuti mukamakhala kumeneko muziikiratu maziko kumaiko akwanu komanso musaiwale kubwerera mwachangu!
Ikubwera Lock down koma sitikudziwa kuti ndiliti koma ulendo uno masewera kulibe ! Anzathu amene mukusunga ndalama zankhaninkhani ku bank ,dziwani kuti posachedwapa simukwanitsa kutenga ndalamazo pokhapokha mutakhala ndi lemba la chirombo! Chotero yetsetsani kuchotsa ndalamazo mwanthawi yake ndipo muonetsetse kuti simunatsale ndi ngongole kumeneko !
Inu amene Mulungu anakudalitsani ndi ndalama zambiri musachedwenso chonde yambani kuthandiza osowa ndipo chuma chanu mukachipeza kumwamba . Ngati muli ndi mangawa ndi munthu mukhululukireni ,musakhale ndi nthawi yosungira mkwiyo. Inu anzanga amene mumadalira chipatala chonde pemphani chisomo cha Mulungu chikukwanireni chifukwa satilolanso kupezeka mu zipatala za boma popanda kulandira lemba la chirombo!
Ndikukumverani chisoni inuyo ogwira ntchito mboma chifukwa ambirinu mudzakakamizika kukatenga lemba la chirombo chifukwa chotetezera ntchito zanu monga zinalili nthawi ya katemera ija,koma ndikuchondererani kuti chonde musapange zimenezo chonde lolani kudzabvutika koma bola tidzakwatulidwe limodzi . Anthu amene mumakhala mtawuni pa nyumba zobwereka ,inde rent ndikupempheni kuti chonde ngati nkotheka kapezeni malo kumudzi ndikumakalima mbewu zina ndi zina nthawiyo ikafika chifukwa ulendo uno microchip sizaphweketsa
Alaliki amene mwangoyamba kumene ,ngati simunamangidwepo dziwani kuti tikagonako ku chichiri ,maula ngakhale kundende zonse zotsautsa ,anzanufe tinabvomereza osati kumangidwa kokha komanso kufa chifukwa cha khristu.Ngati tinalimbana ndi zirombo zija nthawi ya Covid 19 panonso sitikuopa kapena kufooka koma kuimabe nji pamaso pa Mulungu!Ndipo ngati inu mukuopa kufa ndiye beteli musakhalenso mtsogoleri !
Konzekani ! Konzekani ! Konzekani ! Chifukwa anthu onse azadana nafe chifukwa cha dzina la Yesu koma yekhayo amene adzalimbikire kufikira kumapeto ameneyo adzapulumuka ! Chonde abale ndi alongo ndikukuchondererani panopa musaziyese zochezanso ayi koma nthawi tilibe !
Amene mumagwiritsa ntchito masamba a mchezo a TikTok ,YouTube ,Facebook ngakhale WhatsApp samalani kwambiri,makamaka TikTok ndi Facebook pali akamuna amphamvu amene akuyamwa mizimu ya anthu pamenepo ! Pali ziwanda zadama zomwe zikuwalowa anthu ndikumawayambitsa mizimu ya chiwerewere komanso kuwabwezera mudziko tsono ngati uzimu wanu sunakhwime ndibwino osakhalanso pamasamba a mchedzo amenewa koma kungokhala chabe ndi foni !
Inu amene muli pabanja chonde yetsetsani kumapempherera mabanja anu tsiku lililonse chifukwatu ziwanda zamphamvu zalowa mmabanjamu kufuna kumasokoneza ndikumayambanitsa anthu ,Tsoka lake polira lipenga azakupezani mwanyanyalitsana ,ndiye kuti dziwani kuti simudzakwatulidwa . Tiyeni tipepesane ndikukhululukirana nthawi isanathe chifukwa masiku a mdima ayandikira kwambiri ndipo satana sakuchedza ,sakugona ngakhale kupanga masewera akudziwa kuti nthawi yamuthera kwambiri.
Waika ziwanda zamphamvu zoyambanitsa mabanja ,zophwasula mipingo ,kuyambanitsa azitumiki ndi kuyambitsa nkhondo mmaiko pazifukwa zandale . Satana waika kuti anthu akhale pa umphawi wazaoneni cholinga anthu azichedwa kusakasaka chakudya chalero komatu kwinaku ntchito ya Ambuye ikuonongeka . Ndipo musalole kuti ntchito zanu,