Ngangala CCAP YOUTH GROUP

Ngangala CCAP YOUTH GROUP A CHINYAMATA OKHALA NAYE YESU NDI CHIYEMBEKEZO CHA MOYO UNO

30/01/2026

YAKOBO 2:26
Pakuti monga thupi lopanda mzimu liri lakufa, koteronso chikhulupiriro chopanda ntchito chiri chakufa.

Mukhale ndi Tsiku lopambana

LERO KUNALI CHIMWEMWE PAMENE AMUNA 12 APATULIDWA KUKHALA ABAMBO PA MPINGO WATHU.
04/01/2026

LERO KUNALI CHIMWEMWE PAMENE AMUNA 12 APATULIDWA KUKHALA ABAMBO PA MPINGO WATHU.

Linali la Mulungu labwino pamene a Rev C Ntonya amatsogolera mgonero wa Ambuye, ndi Ntchito zina.
14/12/2025

Linali la Mulungu labwino pamene a Rev C Ntonya amatsogolera mgonero wa Ambuye, ndi Ntchito zina.

12/12/2025

YESU M'BUSA WABWINO

Yesu akuzionetsera yekha kuti iye ndi M'BUSA wabwno, amene atsamalira, ateteza, apulumutsa nkhosa zake kuzolutsa (mimbulu). Yohane 10:11-12

11Ine ndine Mbusa Wabwino; mbusa wabwino ataya moyo wace cifukwa ca nkhosa.12Wolipidwa amene sakhala mbusa, amene nkhosa siziri zace za yekha, aona mmbulu ulinkudza, nasiya nkhosazo, nathawa; ndipo mmbulu uzikwatula, nuzibalalitsa;

Pamene Yesu akunena Za nkhosa, mawu amenewa ndi fanizo, Nkhosazo ndiye anthu okhulupilira iye, Yesu khristu Ali ndi udindo pa moyo uli wonse ndipo iye salora kuti asiye moyo wa munthu mumavuto, Koma amausaka ndikuupulumutsa.

Ndimati ndinene kuti abale, anzanu akhonza kukusiyani Koma Yesu amene ndi M'BUSA wabwino sangakuthaweni, amayima nafe mu nyengo zonse . Taperekani moyo wanu Kwa Yesu khristu kuti azikusamalirani popeza iye ndi mbusa wabwino amene sataya nkhosa zake.

Ambuye akudalitseni Nonse, Amen.

10/12/2025

MPHAMVU YA MWAZI WA YESU KHRISTU (1 PETRO 1:17-19)

podziwa kuti simunaomboledwa ndi zobvunda, golidi ndi siliva, kusiyana nao makhalidwe anu acabe ocokera kwa makolo anu: koma ndi mwazi wa mtengo wace wapatali monga wa mwana wa nkhosa wopanda cirema, ndi wopanda banga, ndiwo mwazi wa Kristu:

Mwazi umene Yesu khristu anakhetsa pa mtanda paja, pa ife tonse unagwira Ntchito yotiombola Ku utchimo, mwazi umenewu kufikira lero uli ndi mphamvu Kwa okhulupilira khristu.

Chimene ndikufuna kufotokoza Pano nchakuti, aliyense akuyenera kutsata maomboledwe mwa yesu khristu kudzera Ku mwazi wake. Anthufe pobadwa tinalowa mu dziko lodzala ndi uchimo komatu ndi mwazi wa Yesu khristu timaomboledwa ndikutilekanitsa kuzoipa Za pansi Pano.

Ndimati ndikambe nanu kuti simungathe kusiya kuchita zoipa popanda mphamvu imene Yesu anaonetsa pa mtanda paja, mphamvu yakuomboledwa ndi mwazi. Likhale pemphero lanu Kupempha Ambuye kuti aombole moyo wanu Ku utchimo kuti tikapeze chipulumutso moyo winawo umene uli kudza.

27/10/2025

YAKOBO 5: 13
13Kodi wina wa inu akumva zowawa? Apemphere, Kodi wina akusekelera? Ayimbire.

Kwa aliyense amene akumva zowawa apemphere Kwa Mulungu, pamene Tili m'masautso si nthawi yodandaula Koma ikhale nthawi yopemphera kufuna chipulumutso Kwa Mulungu.

Pamene tikukondwa ndi nyengo Zabwino zimene Mulungu watipatsa tikuyenera kumuyimbira Mulungu, Kumuyamika chifukwa cha Za bwino zake. Mu zinthu zonse Ambuye akhalemo.

Mukhale ndi Tsiku lopambana abale nonse.

17/10/2025

MIYAMBO 18:10
Dzina la Yehova ndilo linga lolimba;
Wolungama athamangiramo napulumuka.

Mulungu akudalitseni

15/10/2025

MTENDERE WA MULUNGU

Abale tiyeni tisankhale amantha ndi nkhawa chifukwa cha zovuta zosiyasiyana Za moyo uno, malo mwake tilimbikibe kupemphera poonetsa chikhulupiliro chathu mwa yesu khristu, ndipo Yesu apereka mayankho a moyo pa moyo wathu.

Mawu a Mulungu pa AFILIPI 4:6-7 akuti :

Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi chiyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu.

7Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana chidziwitso chonse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Kristu Yesu..

Mulungu akudalitseni!!

14/10/2025
03/12/2024

LONJEZO LA EMMANUELI

Yesaya 7:14 Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli. Ndilo losandulika, Mulungu nafe. (Mateyu 1:23)

Yesaya mneneri analosela kuti namwali adzakhala ndi pakati nadzabala mwana wamwamuna amene adzakhala Mulungu pakati pathu.

Ndipo munthawi yoyikika Mariya namwaliyo anawuzidwa ndi mngelo, "Taona, udzakhala ndi pakati, nudzabala mwana wamwamuna, nudzamutcha dzina lake Yesu. Mzimu Woyera adzafika pa iwe, ndi mphamvu ya Wamkulukulu idzakuphimba iwe, chifukwa chakenso Choyeracho chikadzabadwa, chidzatchedwa Mwana wa Mulungu. (Luka 1:31,35)

Mngelo anapitiliza kuti, "Iye adzakhala wamkulu, nadzatchedwa Mwana wa Wamkulukulu: ndipo Ambuye Mulungu adzampatsa Iye mpando wachifumu wa Davide atate wake: ndipo Iye adzachita ufumu pa banja la Yakobo kunthawi zonse; ndipo ufumu wake sudzatha. (Luka 1:32-33)

Zonsezi zinali kupherezela mau aYesaya, "Chifukwa mwana watibadwira, mwana wamwamuna wapatsidwa kwa ife, ndipo ulamuliro udzakhala pa phewa lake. Ndipo adzamutcha dzina lake lakuti Phungu Wodabwitsa, Mulungu Wamphamvu, Atate Amuyaya, ndi Mfumu ya Mtendere.

Ulamuliro ndi mtendere wake zidzakhala zopanda malire. Iye adzalamulira ufumu wake ali pampando waufumu wa Davide, ndipo adzawukhazikitsa ndi kuwuchirikiza mwa chiweruzo cholungama ndi pochita zachilungamo kuyambira nthawi imeneyo mpaka muyaya. Ndi mtima wake wonse, Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza kuchita zimenezi. (Yesaya 9:6-7)

Address

Lujeri

Telephone

+265991748867

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Ngangala CCAP YOUTH GROUP posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share