Malawi Muslim Magazine

Malawi Muslim Magazine Spiritual knowledge
(1)

Ya Allah,titetezeni ku umphawi, mutisunge kutali ndi ngongole,mavuto, ndi chilichonse chimene chimabweretsa manyazi.Dzaz...
23/05/2026

Ya Allah,titetezeni ku umphawi, mutisunge kutali ndi ngongole,
mavuto, ndi chilichonse chimene chimabweretsa manyazi.

Dzazani mitima yathu ndi chiyamiko
ndipo manja athu ndi riziki ya halal.

Tipatseni kukhutira ndi zimene Mwatipatsa,
ndipo tipatseni zofunika kuchokera ku njira
zimene sititha kuganizira. Ameen

Kodi mundandanda wa atumiki a Allah omwe ali musiwa ndi Mtumiki uti wa Allah yemwe adali mwana wa mtumiki Yaqub (AS)(A)....
20/05/2026

Kodi mundandanda wa atumiki a Allah omwe ali musiwa ndi Mtumiki uti wa Allah yemwe adali mwana wa mtumiki Yaqub (AS)

(A). M***a (AS)
(B). Yaqub (AS)
(C). Yusuf (AS)
(D). Issa Yesu (AS)

20/05/2026

Tsiku lina limodzi, tsiku lizayamba popanda inu ndi ine koma eti dziko lizapitilira monga mwa nthawi zonse popanda chosinthika

17/05/2026

Mtumiki (SAW) adati:
“Palibe ntchito zabwino zoposa zomwe zimachitika m’masiku khumi oyambirira a mwezi wa Dhul Hijjah.”
(Ṣaḥīḥ al-Bukhārī)

Ntchito Zolimbikitsidwa Kuchita:
* Kupemphera kwambiri
* Kuwerenga Qur’an
* Kupereka sadaqah
* Kusala kudya
* Kuchita dhikr ndi takbir
* Kupempha chikhululuko kwa Allah

Tigwiritse ntchito masiku opatulika awa kuti tiyandikire kwa Allah

Asilamu ku Britain Akuchuluka Ndi AchinyamataLipoti latsopano lomwe wailesi ya Al Jazeera latulusa lasonyeza kuti pafupi...
16/05/2026

Asilamu ku Britain Akuchuluka Ndi Achinyamata

Lipoti latsopano lomwe wailesi ya Al Jazeera latulusa lasonyeza kuti pafupifupi 50% ya Asilamu onse ku Britain ali ndi zaka zosakwana 25. Izi zikusonyeza kuti gulu la Asilamu likukula kwambiri komanso lili ndi tsogolo lalikulu mdzikolo.

Achinyamata ambiri achisilamu akupita patsogolo pa maphunziro.
Azimayi achisilamu ambiri tsopano akugwira ntchito komanso kuthandiza mabanja awo.

Ngakhale pali mavuto ena a moyo, Asilamu ambiri akupitiriza kulimbikira ndi kukhala gawo lofunika m’dziko la Britain ndi Wales komaso maiko ena ku Ulaya
Ichi ndi chisonyezo chakuti Chisilamu ikupitiriza kukula padziko lonse lapansi mwa chilolezo cha Allah.

Akatswiri akuti kusintha kumeneku kungakhale ndi mphamvu pa ndale ndi tsogolo la maiko a England ndi Wales m’zaka zikubwerazi.

“Ndipo Allah ndi amene amapereka ulemerero kwa amene wamufuna.”

Welengani zambiri apa:https://www.facebook.com/100064930892385/posts/1441977764643240/?app=fbl
Malawi Muslim Magazine

"Ya Allah, dalitsani abale achisilanu onse pa tsamba lathu lino. Awapatseni moyo wabwino, rizq ya halal, mtendere wa mum...
15/05/2026

"Ya Allah, dalitsani abale achisilanu onse pa tsamba lathu lino.

Awapatseni moyo wabwino, rizq ya halal, mtendere wa mumtima, thanzi labwino ndi mapeto abwino. Akwaniritsereni zokhumba zawo zabwino, akhululukireni machimo awo, ndipo tsiku lina tikakumanenso ku Jannah. Ameen.”

Allah atithandize tonse tikakumanenso ku Jannah. Ameen.
15/05/2026

Allah atithandize tonse tikakumanenso ku Jannah. Ameen.

Ndine Msilamu, ndili Msilamu, ndizakhala Msilamu, In sha'Allah ndizamwalira ndili Msilamu.•Analuza mgwirizano wa ndalama...
14/05/2026

Ndine Msilamu, ndili Msilamu, ndizakhala Msilamu, In sha'Allah ndizamwalira ndili Msilamu.

•Analuza mgwirizano wa ndalama zoposa 220 million pounds, omwe anapanga ndi Company ya Adidas, chifukwa chodzudzula dziko la china pa nkhanza zomwe limapangira Asilamu a UYGHUR.

•Team ya Germany inamuchotsa mu ndandanda wa osewera a team ya dzikolo kamba ka chithuzi chomwe anajabulitsa ndi mtsogoleri wa dziko la TURKEY.

•Team ya Arsenal inamuchotsa mu ndandanda wa osewera a teamyo kamba koti anaidzudzula kuti siikuchitapo kanthu pomuthandiza kudzudzula dziko la la China kuti lisiye kuchitila nkhanza ndi kudzudza Asilamu.

•Analuza zambiri koma anapambana pokhala msilamu Masha Allah ❤️

Dzina lake ndi .

Allah amudalitse Mesut Ozil Ameen 🤲

Kodi Malume ake a Marriam (AS) yemwe ndi mayi ake a Mtumiki Issa (AS) Adali ndani?.(A). Dawud (AS)(B).Zakariyah (AS)(C)....
13/05/2026

Kodi Malume ake a Marriam (AS) yemwe ndi mayi ake a Mtumiki Issa (AS) Adali ndani?.

(A). Dawud (AS)
(B).Zakariyah (AS)
(C). Yusuf (AS)
(D). Muhammad (S A W)
(E). Idris (AS)

Kodi ndi Mtumiki uti wa Allah, yemwe Allah adamupatsa luso loti amatha kulankhurana ndi nyama?
12/05/2026

Kodi ndi Mtumiki uti wa Allah, yemwe Allah adamupatsa luso loti amatha kulankhurana ndi nyama?

11/05/2026

Tiyeni tikumbusaneni ma Sunnah Tisanagone tulo kutheka wina sadziwa apindule nawo.

Address

OK
Limbe
MUHAMMAD

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Malawi Muslim Magazine posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share