Malawi Muslim Magazine

Malawi Muslim Magazine Spiritual knowledge

Tangoganizani inuyo ndi ineyo pamodzi ndi okondedwa athu, titakhala ku Jannah yapamwamba pamodzi ndi Mtumiki wathu okond...
24/08/2026

Tangoganizani inuyo ndi ineyo pamodzi ndi okondedwa athu, titakhala ku Jannah yapamwamba pamodzi ndi Mtumiki wathu okondedwa Muhammad [S A W] tikumvera nkhani zake zopatsa chidwi akufotokoza ndi mawu ake okoma.

Ya Allah! zatipatseni tsiku limenelo. Ameen 🤲

20/08/2026

Maulidi Nabbi ndi zachilendo mu Chisilamu, mulibe kukondwelera kubadwa kwa Mtumiki (SAW) mu Chisilamu.

Pa nkhani ya maulid nabbi [kukondwelera tsiku la kubadwa kwa mtumiki Muhammad (S A W)

1.FUNSO :

Kodi ndikangati komwe mtumiki (S A W) anakondwelera za tsiku lomwe anabadwa?

YANKHO:

Palibe
[Musaiwaleso kuti Mtumiki anakhala zaka 63 pa moyo wake].

2.FUNSO:

Abu Bakr, Omar, Othman ndi Ali anali anthu omwe akamukonda ndi kusatira ma SUNNAH a Mtumiki anthu amenewa ndi liti lomwe anakondwelera birthday ya Mtumiki?

YANKHO:

Sanakondwelerepo ngakhale tsiku limodzi.

3.FUNSO:

Fatima mwana wa mtumiki(S.A.W) Pali tsiku lomwe Fatima anakondwelera birthday ya bambo ake

YANKHO:

sanapangepo ngakhale tsiku limodzi

4.FUNSO:

Bukhu lathu la Al Quran linavumbulusidwa zaka 23 mu Al Qur'an muli verse yomwe imafotoza za MAULIDI?

YANKHO:

Mulibemo

5. FUNSO:

Ndi form iti yomwe ma Sahaba amagwiritsa ntchito pophunzitsa anthu za MAULIDI mu Taab'eem?.

YANKHO:

palibe

6.FUNSO:

Nankha ndi dziko liti kapena town iti yomwe ma Sahaba anayamba kukondwelera birthday ya Mtumiki?

YANKHO:

Kulibe.

Ndikudziwa kuti ena mu dana nane,ndipepese, ngati muli ndi zina tipatseni maumboni kapena mayankho omwe mukudziwa pa Nkhaniyi tiphunzira nawo insha'Allah

Timupempheni Allah kuti ationgolere ku njira yake yoongoka. Ameen 🤲❤️

Kodi Msilamu amaloledwa kuvala zovala za Gule Wamkulu kapena kutenga nawo mbali pa mwambowu?Msilamu ayenera kusamala kwa...
19/08/2026

Kodi Msilamu amaloledwa kuvala zovala za Gule Wamkulu kapena kutenga nawo mbali pa mwambowu?

Msilamu ayenera kusamala kwambiri pa nkhani ya miyambo ndi zikhalidwe. Sikuti chikhalidwe chilichonse ndi choletsedwa, koma ngati mwambo uli ndi zinthu zotsutsana ndi chikhulupiriro cha Chisilamu, kapena munthu akutenga nawo mbali pa zinthu za chipembedzo chosakhala Chisilamu, Msilamu ayenera kuupewa.
Choncho, ngati kuvala zovala za Gule Wamkulu ndi cholinga chochita nawo mwambowo kapena kusonyeza kuvomereza miyambo yake yauzimu, Msilamu sayenera kutero.

Komanso, zovala zomwe zimasiya thupi lambiri poyera sizikugwirizana ndi malamulo a Chisilamu okhudza kudzilemekeza ndi kuphimba thupi.

Tisanyoze anthu kapena chikhalidwe chawo. Titha kulemekeza anthu ena pamene tikusunga chikhulupiriro chathu. Msilamu ayenera kutsatira zomwe Allah ndi Mtumiki Muhammad (SAW)adatiphunzitsa.

Allah atipatse nzeru, atilimbikitse pa Deen yathu, ndipo atithandize kusunga Tawhid. Ameen.

Malawi Muslim Magazine
Chidziwitso • Chikhulupiriro • Chikumbutso

15/08/2026

Subhanallah!

eti timadandaula komasa kukhala ndi ma stress tikaganiza za mawa kumachita kuti sitikudziwa zomwe zikhale mmawalo

Imfa ndi yomwe imachotsa ndikuononga zitsangalaro  zonse za moyo.Moyo wa padziko lapansi ndi waufupi. Titha kukhala ndi ...
11/08/2026

Imfa ndi yomwe imachotsa ndikuononga zitsangalaro zonse za moyo.

Moyo wa padziko lapansi ndi waufupi. Titha kukhala ndi chuma, nyumba, magalimoto ndi zinthu zambiri, koma tsiku lina zonsezi tidzazisiya.

Chofunika kwambiri ndi zimene tidzapite nazo kwa Allah.

Tiyeni tikonzekere tsiku limene tidzayime pamaso pa Allah.

Tiyeni tizipemphera
Tiyeni tilape machimo athu.
Tiyeni tikhululukire ena.
Tiyeni tigwire ntchito zabwino.
Tiyeni tibwerere kwa Allah tisanakumane ndi imfa.

Allah atithandize kukonzekera imfa tisanakumane nayo. Ameen

QUIZ YA CHISLAMU Ndi Mneneri uti amene bambo ake anali Mneneri, ndipo agogo ake nawonso anali Mneneri? A️⃣ Mneneri Yusuf...
10/08/2026

QUIZ YA CHISLAMU

Ndi Mneneri uti amene bambo ake anali Mneneri, ndipo agogo ake nawonso anali Mneneri?

A️⃣ Mneneri Yusuf (AS)
B️⃣ Mneneri Ya’qub (AS)
C️⃣ Mneneri Musa (AS)
D️⃣ Mneneri Nuh (AS)

👇 Lembani yankho lanu mu ma comment!
Tiyeni tiwone amene akudziwa.

Allah apange Jannah  kukhala malo athu omaliza, atikhululukire machimo athu, alandire zabwino zomwe timachita, ndipo aka...
09/08/2026

Allah apange Jannah kukhala malo athu omaliza, atikhululukire machimo athu, alandire zabwino zomwe timachita, ndipo akatisonkhanitse pamodzi ndi okondedwa athu ku malo apamwamba kwambiri ku Jannah.

Jannah ndiye cholinga chathu. Allah atipatse tonse Jannatul Firdaus. Ameen!

ANYAMATA ACHISILAMU, BANJA NDI UDINDOAnyamata achisilamu, musamaone banja ngati nkhani ya chikondi chokha. Banja ndi udi...
07/08/2026

ANYAMATA ACHISILAMU, BANJA NDI UDINDO

Anyamata achisilamu, musamaone banja ngati nkhani ya chikondi chokha. Banja ndi udindo waukulu pamaso pa Allah.

Mukakwatira, mwakhala ndi udindo wosamalira mkazi wanu, kumulemekeza, kumuteteza, kumupatsa zofunikira za moyo komanso kukhala naye mwachifundo.

Musamangofuna kukwatira chifukwa cha kukongola, chikondi kapena zomwe mumaona pa social media. Dziwani kuti banja lenileni limakhala ndi masiku osangalatsa komanso masiku ovuta. Zimafunika Sabr (kuleza mtima), kukhulupirika, kulankhulana bwino komanso kuopa Allah.

Musanalowe m’banja dzifunseni mafunso awa:
👉 Kodi ndine wokonzeka kunyamula udindo wa banja?

👉 Kodi ndingathe kusamalira mkazi ndi ana anga?

👉 Kodi ndingathe kukhala wokhulupirika komanso wachilungamo?

👉 Kodi ndili wokonzeka kupirira mavuto osathawa banja?

Allah atipatse anyamata achisilamu omwe ndi amuna odziwa udindo, oopa Allah komanso omanga mabanja olimba.
Ameen Ya Rabb!

Azimayi Achisilamu, dziwani kuti banja silili monga momwe limaonekera pa social media.Musamayerekezere banja lanu ndi zi...
06/08/2026

Azimayi Achisilamu, dziwani kuti banja silili monga momwe limaonekera pa social media.

Musamayerekezere banja lanu ndi zithunzi kapena mavidiyo amene mumawaona pa Facebook, TikTok, Instagram kapena malo ena. Anthu ambiri amaonetsa nthawi zosangalatsa zokha, osati mayesero ndi mavuto amene amakumana nawo.

Banja labwino limamangidwa ndi taqwa (kuopa Allah), kuleza mtima, kulekererana, kukhululukirana ndi kulankhulana bwino, osati ndi zithunzi zokongola kapena moyo wowoneka ngati wangwiro pa social media.
Pempherani kuti Allah adalitse banja lanu, ndipo musalole zomwe mumawona pa social media zikubweretsereni kusakhutira ndi zomwe Allah wakupatsani.

Allah ndiye Wodziwa bwino zomwe zili zabwino kwa ife.

Kodi mwamuna wa Chisilamu amafunika chilolezo cha mkazi wake woyamba kuti akwatire mkazi wachiwiri?Yankho: Ayi. Malinga ...
04/08/2026

Kodi mwamuna wa Chisilamu amafunika chilolezo cha mkazi wake woyamba kuti akwatire mkazi wachiwiri?

Yankho: Ayi. Malinga ndi Shariah, mwamuna safunika chilolezo cha mkazi wake woyamba kuti akwatire mkazi wachiwiri.

Komabe, Allah walamula mwamuna aliyense amene akwatira akazi oposa mmodzi kuti azichita chilungamo pakati pawo. Ngati akuopa kuti sangathe kuchita chilungamo, Allah wamulangiza kukwatira mkazi mmodzi.

Allah akuti:
"Ngati muopa kuti simudzatha kuchita chilungamo, ndiye (kwatirani) mkazi mmodzi."(Surah An-Nisa 4:3)

Choncho, ngakhale chilolezo cha mkazi woyamba sichili chofunikira mu Shariah, mwamuna ayenera kuopa Allah, kusamalira akazi ake onse mwachilungamo, ndi kukwaniritsa maufulu awo monga momwe Chisilamu chimalamulira.

Ngakhale chilolezo cha mkazi woyamba sichikhala chofunikira mwachindunji mu Shariah, ndi makhalidwe abwino (husn al-mu'āsharah) kumudziwitsa, kumufotokozera, ndi kuyesetsa kusunga mtendere ndi ubale wabwino m'banja.

Allah ndi Wodziwa kwambiri.

Address

OK
Limbe
LILONGWE

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Malawi Muslim Magazine posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share