10/12/2022
Assalaam alykum warahmatullah wabarakaatuh!!!!!!
Kuyamikidwa konse ndikwa Allahu Taala mafuno Abwino apite kwa mtumiki saw a kubanja kwake komanso ndi masahabah ake.
LERO TIYENI TIPHUNZIRE ZA TWAHARAH.
🖋️🖋️🖋️🖋️🖋️🖋️🖋️🖋️🖋️🖋️🖋️
Twaharah ndi liwu la Chiarabu lomwe tanthauzo lake ndi kuyera kapena kuti Ubwino wa kusakhala ndi umve ulionse.
Ndipo Twaharah imayang'anidwa mmagawo anayi⤵️
1 Twaharah yapathupi
2 Twaharah yamuzovala
3 Twaharah yammadzi
4 Twaharah ya pamalo oswalira
Choncho mitundu imafunika kuilabadila pa nthawi yomwe tikupanga za Twahara
Mtumiki saw Adalankhula kuti,
ألطهور شطر الإيمان
Ndithu ukhondi ndigawo lachikhulupiliro chachislamu.
🌴🌴🌴🌴🌴🌴🌴🌴🌴🌴🌴
Komanso Mtumiki saw adalankhulanso kuti, ⤵️
ألطهور مفتاح الصلاة
Ukhondo(kuziyeretsa) ndimakiyi aswalah
Choncho msilamu kuti akhale wa chire watayali pa ibadah akuyenera kukhala waukhondo nthawi zonse.
Nde mmene tafotokozera poyamba muja
Twaharah tikuyenera kuyang'ana mmagawo anayi amenewa.
Ungathe kukhala nditwahara yapathupi koma zovala zilibe Twaharah zikatero swalah sizingatheke.
Utha Kukhala nditwahara m'thupi ndimuzovala koma Malo oswalira ndikukhala opanda Twaharah,
Kapena tingathe kukhala oti tasamba bwinobwino komanso tachapa bwinobwino koma ndikukhala opanda Twaharah chifukwa cha madzi omwe tagwilitsa ntchito anali opanda Twaharah.................................
Ikupitilira
Pangani like kapena comment post yi kuti tidziwe kuti tikamapanga post awerengi alipo ndipo ife tudzalimbikitsika pomalembapo zambiri pa page pano
#