Chipasula Seventh Day Adventist Church

Chipasula Seventh Day Adventist Church Chipasula Seventh Day Adventist Church is a place where every person is loved, encouraged, challenged, and strengthened as we grow in our faith.

23/01/2026

Happy preparation day

21/01/2026

Psalm 118:13 I was pushed back and about to fall, but the Lord helped me.

19/01/2026

Pachisankho – Nkhondo ya Mitima

🏔️ Pachisankho: Nkhondo ya Mitima

Kuyambira kumwamba mpaka pano pa dziko lapansi, pali nkhondo yayikulu imene ikupitirirabe. Ndi nkhondo pakati pa chabwino ndi choipa, pakati pa Mulungu ndi Satana. Koma chofunika kwambiri n’chakuti:
👉 Nkhondo imeneyi imachitika tsiku lililonse mu mtima mwathu.

Mulungu sanatilenge ngati makina. Iye anatipatsa mphatso yaikulu kwambiri — mphamvu yosankha. Chisankho ndi chimene chimasonyeza amene timamvera, amene timakonda, ndi amene timatsatira.

Tsiku lililonse timayimilira pa pachisankho:
Kodi tidzasankha kutsatira Mawu a Mulungu, kapena kutsatira malingaliro a dziko?
Kodi tidzasankha chivumbulutso cha Mulungu chamoyo, kapena kumangotsatira mwambo opanda mphamvu ya mzimu?

Baibulo limati:

“Onani, ndakhazikitsa pamaso panu lero moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero; chifukwa chake sankhani moyo, kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo.”
— Deuteronomo 30:19

Mfumu ya nkhondoyi ndi Yesu Khristu. Iye anagonjetsa kale pa mtanda. Iye anagonjetsa uchimo, imfa, ndi Satana. Koma lero, kupambana kwake kumayenera kuwonekera mu zisankho zathu.

Tikamasankha chilungamo, tikuyimira Yesu.
Tikamasankha kukhulupirika, tikuyimira Yesu.
Tikamasankha kumtsatira ngakhale zitakhala zovuta, tikuyimira Mfumu ya nkhondo.

Lero, Mulungu akukuyitana kuti:
✔ Sankhani moyo
✔ Sankhani chowonadi
✔ Sankhani Yesu

🙏 Pemphero

Atate wathu wakumwamba,
tikubwera pamaso panu podziwa kuti pali nkhondo yaikulu ya mitima.
Tithandizeni kuti tisamagwe mu chisankho choipa.
Tipatseni mphamvu ya Mzimu Woyera kuti tisankhe chilungamo,
kutsatira Mawu anu,
ndi kukhalabe okhulupirika mpaka mapeto.

Tikupempha zonsezi m’dzina la Mfumu yathu,
Yesu Khristu, amene anagonjetsa kale.
Amen.









Khalani ndi tsiku lodalitsidwa. Mulungu akutsogolereni pa chisankho chilichonse chimene muchite.

---

🌟 Happy Sabbath, everyone! 🌟May this beautiful Sabbath bring you rest, peace, and joy as we pause from our busy week and...
17/01/2026

🌟 Happy Sabbath, everyone! 🌟

May this beautiful Sabbath bring you rest, peace, and joy as we pause from our busy week and reflect on the blessings around us. May today be filled with calm moments, meaningful connections, and gratitude in your heart.

Whether you’re spending it with family, in prayer, in worship, or simply resting — enjoy every peaceful moment of this sacred day.

Don’t forget to follow me on TikTok for more uplifting content and fun updates.
Check it out here: https://vt.tiktok.com/ZSa1xtccn/

Happy Sabbath and be blessed.

Check out CHIPASULA S.D.A. YOUTH CHOIR’s video.

GOOD MORNING AND BE BLESSED. ☀️Morning Devotion: We Are Living in Borrowed TimeThe Bible tells us in Psalm 90 verse 12:“...
16/01/2026

GOOD MORNING AND BE BLESSED. ☀️

Morning Devotion: We Are Living in Borrowed Time

The Bible tells us in Psalm 90 verse 12:
“So teach us to number our days, that we may gain a heart of wisdom.”

Every new day is not guaranteed. It is only by God’s mercy that we wake up. We are truly living in borrowed time. That means today is important. Today is a chance to pray, to work hard, to love others, and to walk closely with God.

This morning, let us pray for one another. Let us use our time wisely. Let us serve God faithfully, knowing that every breath is a gift.

Please follow the link and listen to the song on TikTok about this message, “We are living in a borrowed time”:
https://vt.tiktok.com/ZS5K3GMMH/

Have a blessed morning. 🙏

Check out CHIPASULA S.D.A. YOUTH CHOIR’s video.

“I must work the works of Him who sent Me while it is day; the night is coming when no one can work.” — John 9:4This is ...
15/01/2026

“I must work the works of Him who sent Me while it is day; the night is coming when no one can work.” — John 9:4

This is our time to wake up, pray, and bring light to our city while it is still day. Let us not sleep when God is calling us to stand, to serve, and to prepare before the night comes.

👉 Follow this link and listen to our song on YouTube that carries the same message:
https://youtu.be/p_AeJWDjong?si=2ht9xLm9SkiCzbtM

Good morning ☀️

tiyeni tigwile ntchito ya Mulungu utsiku usanaze

MORNING DEVOTIONGood morning, family.Today, remember this truth:Trust God no matter how life looks.The Bible says in Pro...
14/01/2026

MORNING DEVOTION

Good morning, family.

Today, remember this truth:
Trust God no matter how life looks.

The Bible says in Proverbs 3:5–6:
“Trust in the Lord with all your heart, and lean not on your own understanding; in all your ways acknowledge Him, and He shall direct your paths.”

Life can be hard.
Sometimes we do not understand what God is doing.
But God is always in control.

Jesus also said in John 14:2:
“In My Father’s house are many mansions… I go to prepare a place for you.”

This world is not our home.
Heaven is prepared for us.
So do not be discouraged by the problems of this world.

Keep trusting God.
He knows the way.
He holds your tomorrow.

FOLLOW US

Follow us on TikTok at Chipasula SDA Youth Choir
and listen to our posts, including music.

https://vm.tiktok.com/ZMDkYgXyM/

God bless you.

Check out CHIPASULA S.D.A. YOUTH CHOIR’s video.

12/01/2026

Good morning and happy new year 2026. 🌿

Today, be encouraged by Psalm 118:13:
“I was about to fall, but the Lord helped me.”

As this new day and this new year begin, remember this:
You are here not by accident, but by God’s help.

Whatever today brings, you are not alone.
The same Lord who helped you through last year
will strengthen you, guide you, and lead you this year.

Walk into this day with hope.
Walk into 2026 with faith.

🎶 Chipasula SDA Youth Choir will soon be releasing a new song titled:
“KUNDIKANKHA” – “He helped me”
A song of testimony and hope.

Official video coming soon.
Follow us here on Facebook and on YouTube:
https://youtu.be/RfCqBp0andU?si=CWNrRK2kH0PQB_mH

Have a blessed and peaceful morning.

11/01/2026

PSALM 118:13
“I was about to fall,
but the Lord helped me.”

The past year was tough.
We were pushed.
We were tested.

But we are still standing.

Not because we are strong…
But because God helped us.

As we step into 2026,
we move with hope.
We move with faith.

The same God who helped us
will lead us.

KUNDIKANKHA
“He helped me”

Chipasula SDA Youth Choir
Video coming soon.

31/12/2025

PHUNZIRO LA SABATA SUKULU (KOTALE) MUCHIGAWO CHA AKULU

Gawo Loyamba:

Kulumikiza kumwamba ndi Dziko Lapansi Phunzirani za Yesu kuchokera m'Mabuku a Afilipi ndi Akolose

PHUNZIRO 1

Mutu: MULUNGU AMAKHALA NAFE, NGAKHALE MU NTHAWI ZOVUTA

LASABATA MASANA

PHUNZIRO LATHU MLUNGU UNO TIWERENGA KUCHOKERA MU:
Aefeso 3:1; 2 Akorinto 4:7–12; Machitidwe 9:16; Filemoni 1:15, 16; Afilipi 1:1–3.

VESI LOLOWEZA:“Kondwerani mwa Ambuye nthawi zonse: ndibwerezanso kutero, kondwerani!” (Afilipi 4:4).

MBUSA WINA WA MPINGO WA SEVENTH-DAY ADVENTIST anamangidwa pa mlandu umene sadaupalamule. Mbusayo anakhala m’ndende pafupifupi kwa zaka ziwiri. Nthawi yoyamba, mbusayo anali wa chisoni ndi wosokonezeka. Ndi chifukwa chiyani Mulungu analola kuti chinthu choipachi chichitikire mbusayu? Kodi Mulungu samasamala za mbusayu?

Posakhalitsa mbusayu anamvetsetsa kuti Mulungu anamtumiza m’ndendemo kukapulumutsa anthu! Pamene anthu a m’ndendemo anazindikira kuti munthu ndi mbusa, anampempha kuti awalalikire. Chotero, mbusayo analalikira za Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu m’ndendemo. Iye anaperekanso mabuku okamba za Baibulo kwa anthu a m’ndendemo. Iye anabatiza andendewo nawadyetsa mgonero wa Ambuye. Mbusayo anati, “Masiku ena ndinkavutika kugwira ntchito m’ndende muno.

Koma ndinalinso ndi chimwemwe chachikulu mu mtima mwanga. Ndinali wachimwemwe pamene ndinaona Ambuye akusinthanso miyoyo ya anthu m’ndendemo. Apa ine ndinaona Ambuye akuyankha mapemphero anga.”
Anthu ankaganiza kuti Paulo ndi Sila analakwa kanthu kena, komatu iwo sadalakwe konse.

Paulo ndi Sila nawonso, anaponyedwa m’ndende. M’dindo woyang’anira ndendeyo “anawaika m’chipinda cha m’kati, namangitsa mapazi awo m’zigologolo” (Machitidwe 16:24). Iwo ali m’ndendemo, Paulo analemba makalata opita ku ziwalo za mpingo wa m’mizinda ya Afilipi ndi Akolose (werengani Afilipi 1:7 ndi Akolose 4:3).

Mulungu uno, ife tiona zimene zinachitikira Paulo m’ndende. Zowawa zimene iye anakumana nazo m’ndendemo zinampangitsa kudziwa dongosolo limene Mulungu anali nalo pa moyo wake. Chitsanzo ichi cha Paulo chitiphunzitse ife nanga kupitiriza kutumikira Mulungu ngakhale pamene tikudutsa m’nyengo zowawa.

TSIKU LOYAMBA

PAULO, MWAMUNA WOPONYEDWA M’NDENDE CHIFUKWA CHA YESU (AEFESO 3:1)

Paulo analemba makalata kwa Afilipi ndi Akolose. Makalata a Paulo amatchedwa makalata a m’ndende chifukwa iye anawalemba ali m’ndende. (Paulo ali m’ndende analembanso makalata ena opita kwa Aefeso ndi Filemoni.) Ambiri a anthu anzeru zakuya ozukuta Baibulo amakhulupirira kuti Paulo analemba makalata opita kwa Afilipi ndi Akolose ali ku Roma, pafupifupi A.D. 60–62 (werengani Machitidwe 28:16).

*Werengani Aefeso 3:1 ndi Filemoni 1. Kodi Paulo akuti chiyani za nthawi imene iye anali m’ndende?*

Paulo anapereka moyo wake wonse kutumikira Yesu. Ngati Mulungu akadafuna kuti Paulo aponyedwe m’ndende iye anali wokonzeka kukhala m’ndendemo. Paulo akutiuza chifukwa chimene iye waponyekera m’ndendemo. Iye akuti, “chifukwa cha umene ndili mtumiki wa m’unyolo, kuti mmenemo ndikalankhule molimbika, monga ndiyenera kulankhula” (Aefeso 6:20).

Paulo sanaponyedwe m’ndende iye anayenera maulendo nalalikira Uthenga Wabwino. Iye anakumana ndi mipingo komanso anaphunzitsa atumiki ogwira ntchito ya Mulungu. Mwinanso Paulo ankadzifunsa modabwa, “kodi chifukwa chiyani ndili m’ndende? Inetu ndikadakhala mfulu ndikadagwira ntchito zambiri ya Mulungu!”
Kutsogolo kwake, Paulo analowanso m’ndende kachiwiri.

Iye ali m’ndendemo, analemba 2 Timoteo. Chotero, Paulo ali m’ndende analemba pafupifupi makalata asanu a m’Chipangano Chatsopano.
Paulo sakutiudza dzina la mzinda komwe iye anaponyedwa m’ndendeko. Akatswiri ena ozukuta Baibulo amati Paulo anaponyedwa m’ndende mu mzinda wa Efeso kapena Kaisareya. Koma umboni woti Paulo anaponyedwa m’ndende mu Efeso m’Baibulo mulibe. Koma pali umboni woti Paulo anali pa choopsa pa ulendo wake woyamba wa ku Kaisareya.

Koma pamene iye analemba makalata yake yopita kwa Afilipi, ndi pamene iye anali pa choopsa chachikulu (werengani Afilipi 1:20 ndi Afilipi 2:17). Kalata ya Paulo yopita kwa Afilipi ikutisonyeza komwe iye anaponyedwa m’ndende. Koyamba, Paulo akunena za nyumba ya chifumu yapaderadera. Nyumba ya chifumu imeneyi ikhoza kutanthauza kunyunmba kwa kazembe. Yesu anatengedwa kupita ku nyumba ya mfumu mu Yerusalemu komwe anaweruzidwa ndi Pilato (Mateyu 27:27; Yohane 18:33).

Pamene pa mlandu wa nyumba ya mfumu ndi ndende ya Kaisareya komwe Paulo anatumizidwa kukakhala (Machitidwe 23:35). Koma Paulo sakugwiritsa ntchito mawu oti “nyumba ya mfumu yapadera” kukamba za malo ayi. Iye akugwiritsa ntchito mawuwa kunena za anthu. Iwo onse “m’bwalo lonse la alonda ndi kwa onse ena” amena anamva za Yesu (Afilipi 1:13).

Alonda amenewa anali asilikali odziwa nkhondo kwambiri m'gulu la Chiroma. Iwo anali kuteteza mfumu ya Roma komanso kuyang’anira andende.
Kachiwiri, Paulo anatumiza malonje ochokera kwa oyera mtima, ponena kuti, “oyera mtima onse alankhula inu, koma makamaka iwo a banja la Kaisara” (Afilipi 4:22). Chotero, izi zikuonetsa kuti Paulo analemba kalata yake yopita kwa Afilipi ali m’ndende ya ku Roma. Iye anali kulumikizana ndi anthu amene ankakhala ndi kugwira ntchito ku nyumba ya mfumu.

TSIKU LACHIWIRI

PAULO MU NSINGA (2 AKORINTO 4:7-12)

Pamene Paulo ali ku Makedoniya, akuti iye anaponyedwa m'ndende nthawi zochuluka (2 Akorinto 6:5; 2 Akorinto 11:23; 2 Akorinto 7:5). Nthawi yoyamba imene Paulo anaponyedwa m'ndende kunali ku Filipi (Machitidwe 16:16-24). Paulo anaponyedwanso m'ndende ya ku Yerusalemu, koma kwa nthawi yochepa. Ndipo kenaka iye anaponyedwanso m'ndende ya ku Kaisareya.

Palinso pena pamene Paulo akunena zokhudza kuponyedwa kwake mu "ndende" (Filemoni 1:10, 13). Pamene Paulo anali m'ndende ya ku Roma, iye anali kukhala m'nyumba. M'nyumbamo, Paulo anamangiriridwa kwa msirikali. Msirikali ameneyu anali wa gulu la asirikali a paderadera, omwe anali akatswiri odziwa nkhondo kwambiri m'gulu la ankhondo a Chiroma. M'chaka cha A.D. 300, nayenso Mkhrisitu wina wotchedwa Ignatius anamangiriridwa kwa msirikali wa Chiroma.

Pofofokoza za izi, Ignatius anati khalidwe la asirikali amenewa linali loipa ngati "nyama za kuthengo. Iwo akachitiridwa zabwino ndi anthu ndi pamene amaonetsera kwambiri khalidwe lawo loipalo." -Michael W. Holmes, mkozi wa, The Apostolic Fathers (Grand Rapids, MI: Baker Academic, 2007), tsamba 231, mawuwa ndi okonzedwanso. Izi zikusonyeza kuti moyo wa m'ndende unali wovuta kwambiri.

*Kodi ndi chiyani chimene chinampangitsa Paulo kukhalabe wolimba mtima m'mavuto ake a mu nyengo zokhomazo? Werengani 2 Akorinto 4:7-12 kuti mupeze yankho.*

Pamene zinthu zafika povuta, nthawi zonse Paulo amakhala munthu wa chiyembekezo ndi chikhulupiriro. Chiyembekezo ndi chikhulupiriro chake zinali kumulimbikitsa kukhalabe munthu wamphamvu. Satana anachita chilichonse chomwe akadatha kumumvetsa nacho Paulo kuwawa ndi kumutayitsa chiyembekezo. Koma Paulo anadziwa kuti nthawi zonse Mulungu anali ndi iye.

*Kodi ndi madalitso anji auzimu amene anamuthandiza Paulo kukhalabe wolimba mtima mu nthawi ya masautso? Werengani 2 Akorinto 6:3-7 kuti mupeze mayankho.*

Kawiri kawiri, ife timaona zolakwika zathu zakale ndipo timadziwa kuti ndife ofooka. Timaona zinthu zoopsa zimene zikuchitika pa malo otizingulira ndipo sitikhalanso ndi chiyembekezo. Mu nthawi zoterozi, kuti ife tipeze chipambano timayenera kukumbukira mphatso zonse zimene Mulungu amatipatsa. Baibulo ndilo imodzi ya mphatso zofunikira kwambiri zimene Mulungu amatipatsa.

Ilo limatithandiza kuphunzira kuchokera ku zolakwika za ena. Kuchokera m'Baibulo ife timaphunziramo za mmene anthu ena anagonjetsa mu nkhondo yolimbana ndi choipa. Mulungu amatipatsanso Mzimu Woyera. Mzimu Woyera "amatithandiza kukhala moyo wofunana ndi wa Mpulumutsi. Mzimu amapanga moyo wathu kukhala moyo wopanda chodetsa ndi wa chiyero.

Iye amatithandiza kuti m'mitima mwathu tikhale ofanana ndi Mulungu. Yesu anatipatsa Mzimu Wake kuti atithandize m'mitima mwathu kugonjetsa mu nkhondo yolimbana ndi uchimo komanso choipa. Mzimu amatithandiza mpingo wa Mulungu poudzaza ndi moyo wa chiyero komanso chikondi Chake." -Ellen G. White, The Desire of Ages, tsamba 671, mawuwa ndi okonzedwanso.

TSUKU LACHITATU

PAULO MU FILIPI (Machitidwe 9:16)

Paulendo wake wachiwiri wokalalikira Uthenga Wabwino, Paulo anayenda ndi Timoteo komanso anzake ena. Posakhalitsa, Mzimu akuletsa Paulo kuti asaolokere ku Asiya (Asia Minor) (Machitidwe 16:6). Asia Minor lero amatchedwa Turkey. Usiku umenewo, Paulo akulota loto. Mu lotolo, iye akuona munthu wina wochokera ku “Makedoniya.

Munthuyu adaima pamenepo nanena kwa Paulo, "muolokere ku Makedoniya kuno, mudzathitangate ife'” (Machitidwe 16:9). Pomwepo, Paulo ndi anzakewo anayenda pa nyanja kuchokera ku Trowa. Pa ulendowo Paulo anali ndi Sila, Timoteo, ndi Luka. Luka anawapeza anazekwo ku Trowa (Machitidwe 16:11). Paulo ndi anzake wo anayenda pa nyanja kupita ku mzinda wina wa m'dziko la Greece. Koma kumeneko iwo sanalalikire. Ndipo gululo linapita ku Filipi.

Filipi unali "mudzi wa ku Makedoniya, waukulu wa m'dzokomo." (Machitidwe 16:12). Filipi unalinso mzinda wolemekezeka kwambiri pakati pa mizinda ya ufumu wa Roma. Anthu okhala mu Filipi adali ndi ufulu woponya voti pa chisankho kapena kukhala ndi malo a munthu mwini mofanana ndi nzika za Roma zomwe zinkakhala mu Italy. Ndiponso Afilipi sankalipira misonkho ina. Aliyense wobadwira mu mzinda wa Filipi anali nzika yeni yeni ya ufumu wa Roma.

Filipi anali malo wofunikira kwambiri womwe anthu amaima ndi kupumula pa ulendo wopita ku Via Egnatia. Via Egnatia unali msewu wofunikira kwambiri wolumikiza Roma ndi maiko a kummawa. Chotero, Paulo adafuna kukhazikitsa mpingo mu Filipi. Mpingo wa mu Filipi ukadathandiza Paulo ndi gulu lakelo kulalikira Uthenga Wabwino ku mizinda ina yapafupi. Ina ya mizinda imeneyi ikuphatikizira Amfipoli, Apoloniya, Atesalonika ndi Bereya (werengani Machitidwe 17:1, 10).

Mu nthawi ya Paulo, Afilipi anali kulankhula chilankhulo cha Chilatini. Koma ku misika ndi m'mizinda yozungulira anthuwo anali kulankhula Chihelene. Luka akutiuza mmene Paulo ndi gulu lakelo analowera mu gulu la anthu amene anali kupemphera mphepele mwa mtsinje. Kumeneko, Lidiya pamodzi ndi antchito ake ndi ena okhala nawo m'nyumba mwake, analowa Chikhrisitu (Machitidwe 16:13-15). Lidiya anali mkazi wochita malonda amene ankagulitsa nsalu za chibakuwa.

Lidiya anagwiritsa ntchito ndalama zake kuthandiza ntchito ya Mulungu imene Paulo ankagwira. Mu nthawi yomwe Paulo ndi Sila anali mu Filipi, iwo kwambiri anakhala m'ndende. Kukhala kwawo kwa ndendemo kunapangitsa mdindo woyag'anira ndende kulowa Chikhrisitu. Anthu onse a panyumba pake, nawonso analowa Chikhrisitu!

Mzinda wa Filipi unali wofunikira kwambiri ku mpingo wonse. Mpingo wa mu Filipi unathandiza anthu a Mulungu kufalitsa Uthenga Wabwino ku Ulaya. Kumena zoona, Paulo ndi gulu lake anasautika chifukwa cha chikhulupiriro chawo mu Filipi. Mulungu akhoza kugwiritsa ntchito masautso athu ndi cholinga chofuna kukhudza mitima ya anthu ndi Uthenga Wabwino.

*Werengani Machitidwe 9:16. Kodi vesili likutithandiza bwanji kumvetsetsa masautso amene Paulo anakumana nawo? Nanga nafenso likutithandiza motani?*

TSIKU LACHINAYI

PAULO NDI KOLOSE (Filemoni 1:15, 16)

Baibulo silikunena kuti Paulo anafikapo mu mzinda wa Kolose. Koma ife tikudziŵa kuti Epafra ndi amene anakhazikitsa kumeneku (Akolose 4:12). Epafra anali munthu woyamba kulalikira Uthenga Wabwino wa Yesu mu mzinda wa Kolose (Akolose 1:7). Funso nkumati, kodi Epafra analowa bwanji Chikhristu? Kunena zoona, ife sitikudziwa. Mwina Epafra analowa Chikhristu nthawi imene Paulo anali kukhala mu mzinda wapafupi, wotchedwa Efeso, pakatikati pa zaka za A.D.-50.

Chifukwa cha ntchito ya Paulo “kotero kuti onse akukhala m’Asiya anamva mawu Ambuye, Ayuda ndi Ahelene” (Machitidwe 19:10; yerkezani ndi Machitidwe 20:31). Buku la Chivumbulutso likutiuzanso kuti otsatira a Mulungu analalika Uthenga Wabwino ponse ponse mu Asiya (Chivumbulutso 1:4). Kodi ndi chifukwachi chiyani iwo anapambana? Yankho ndi loti, chifukwachi cha ulaliki wa Paulo.

Anthu anamva uthenga woyamba kuchokera kwa Paulo mu Efeso. Efeso unali mzinda wofunika kwambiri mu Asiya komanso ku doko lalikulu, chotero, Epafra ananva Paulo akulalikira mu Efeso. Iye anakhalanso mmodzi wa anthu ogwira ntchito limodzi ndi Paulo. Ndipo kenaka Epafra anabwerera kwawo ku Kolose nalalikira Uthenga Wabwino kumeneku.
Mzinda wa Kolose uli pa mtunda wa zipumulo khumi ndi mphambu zisanu (15) kum’mera cha kum’mwera kwa Laodekaya.

Anthu a zotumbatumba tsopano ayamba kukumba mu mzinda wa Kolose. Chotero, kufikira lero ife sitikudziwa zambiri zokhudza mzindawu. Tikudziŵa kuti mu mzindawu munali kukhala Ayuda pafupifupi 10,000. Ndalama zachitsulo za ku Kolose zimasonyeza kuti mu mzindawu munali anthu opembedza milungu yochuluka kwambili.

Chotero, Akhristu anali kukumana ndi mavuto ochuluka polalikira Uthenga Wabwino mu mzindawu. Komanso, mu mzinda umenewu zinali zowuta kwa Akhristu kukhala moyo womvera Mulungu. Filemoni anali mmodzi wa Akhristu amene anakhalabe mu Kolose. Mwina Filemoni analowa Chikhristu mu nthawiyi yofanana ndi Epafra.

*Werengani Filemoni 1:15, 16. Werenganinso Akolose 4:9. Kodi Paulo anampempha Filemoni kuchitira Onesimo chiyani?*

Lamulo la Chiroma linati Paulo anayenera kubweza Onesimo kwa mbuye wake, Filemoni. Koma Paulo anapempha Filemoni kuchitira Onesimo chifundo. Onesimo anali kapolo wa Filemoni. Koma Paulo anapempha Filemoni kuti amtenge Onesimo monga mbale wake mwa Yesu Khristu (Filemoni 1:16).

*Kunena zoona, ukapolo ndi chinthu choipa. Ife tikadakonda kuti Paulo auze Filemoni amasule Onesimo kukhala mfulu. (Mu nthawiyi ukapolo mu America, Ellen G. White anauza Akhristu a mpingo wa Seventh-day Adventist kuti asamatsatira lamulo lokhudza kapolo wothawa mbuye wake. Lamuloli linkalamula anthu kubweza akapolo othawa kwa ambuye awo.) Momwemo, kodi ife tingafotokoze motani ganizo la Paulo lopita kwa Filemoni?*

TSIKU LACHISANU

MIPINGO MU FILIPI NDI KOLOSE (Afilipi 1:1–3)

*Werengani Afilipi 1:1–3 ndi Akolose 1:1, 2. Kodi Baibulo likutiuza chiyani zokhudza mipingo ya mu Filipi ndi Kolo­se? Nanga ndi chifukwa chiyani chidzivitsoche chili chofunikira kwambiriri?*

Paulo m’makalata ake kawirikawiri akupereka malonje kwa Akhristu powatchula monga oyera mtima. Chifukwa chake ndi choti iwo anali atabatizidwa mu mpingo. Ubatizo unali kusonyeza kuti iwo anali olekanitsidwa ndi njir­a za moyo wawo wakale nakhala anthu a Mulungu apadera. Namonso mu Chipangano Chakale, Mulungu anasankha Aisrayeli kukhala anthu Ake apadera.

Mulungu analamula ana a Israyeli kulandira mdulidwe monga chizindikiro. Mdulidwe unkachitika pa ana aamuna a Israyeli. Chizindikiro chimenechi chinkasonyeza kuti Aisrayeli anali olekanitsidwa ndi anthu a mitundu ina, ndiponso iwo anali anthu a mwini Wake Mulungu. Iye ankawatenga iwo monga chuma chake chapadera. Iye anafuna Aisrayeliwo akhale oyera (Eksodo 19:5, 6; yerekezerani 1 Petro 2:9, 10).

Momwemonso, Mulungu akufuna Akhristu nawonso akhale oyera. Ubatizo umasonyeza kuti ife ndi a Mulungu mwini.
Tiyeni tiyerekezere malonje a Paulo m’kalata yake yopit­a kwa Akhristu mu Filipi ndi malonje a m’kalata yake yopita kwa Akhristu a mu Kolo­se. Paulo akulemba makalata ake kwa akulu akulu a mu Filipi, pamodzi ndi “oyang’anira ndi atumiki” a mpingo (Afilipi 1:1). Paulo akulem­banso kwa “oyera mtima onse mwa Khristu Yesu” amene akukhala mu Kolo­se (Akolose 1:2).

Pamene Chipangano Chatsopano chikunen­a za “abale okhulupirika,” ife timawerenga anthu amene awo amene akugwira ntchito ya Mulungu yapadera mu mpingo (werengani Aefeso 6:21; Akolose 4:7; ndi 1 Petro 5:12). Chotero, Paulo akulankhula kwa ziwalo za mpingo pamodzi ndi akulu a mpingo mu Filipi ndi mu Kolo­se. Mu zigawo zina za Baibulo, ife timamva za ntchito ya Mulungu imene akulu ampingo akugwira mu mpingo (Werengani 1 Timoteo 3:1–12 ndi Tito 1:5–9).

Ntchito zosiyanasiyanazi zimathandiza kumvetsetsa kuti utsogoleri unali chinthu chofunikira kwambiri mu mpingo wa Mulungu kuyambira kumayambiriro kweni kweni.
Paulo anaphunzitsa ntchito Timoteo, Epafra, ndi Akhristu ena kukhala atsogoleri a mipingo ya kwawo. Paulo ankadziwa kuti kuphunzitsa atsogoleri inali ntchito yofunika kwambiri. Akulu a mpingo anathandiza Paulo kulalikira Uthenga Wabwino m’mizinda. Paulo anali ndi ndondomeko yolalikira Uthenga Wabwino komanso kupereka upangiri kwa atsogoleri a mpingo.

N’choncho atsogoleri amene anayambitsa mpingo wathuwu wa Seventh-day Adventist anatsata dongosolo lomweli. Zaka zambiri zakumbuyo, Paulo asadalembe makalata ake opita ku mipingo ya Filipi ndi Kolo­se, mpingo wa mu Yerusalemu unali kutsata kale dongosolo limeneli (werengani Machitidwe 6:1–6 ndi Machitidwe 11:30). Mpingo wa mu Yerusalemu “unali chitsanzo cha utsogoleri kuti mipingo ina itsatire.”—Ellen G. White, The Acts of the Apostles, tsamba 91, mawuwu ndi okonzenso.

TSIKU LACHISANU NDI CHIMODZI

KUPITIRIZA PHUNZIRO:

“Mulungu anasankha inu kuti mupulumutsidwe. Iye akufuna kukukupangani inu kukhala woyera. Chikhulupiriro chanu mu choonadi cha Baibulo chidzikupangani kukhala oyera. Chotero, khalani amphamvu… Ngati mumvera Mulungu, anthu adzalimbana nanu chifukwa cha chikhalupiriro chanu. Inu musakwiye pamene wina wakuputani. Musamabwezera. Khalani olimba mwa Yesu.

Inu musadalaule pa zimene zina akukunenani. Inutu simukuyenera kuwaletsa kuchita zimene akufuna kuchita. Ntchito yanu ndi yochotsa kunyada konse mu mtima mwanu. Chitani ntchito imeneyi ndi mtima wanu wonse komaso mphamvu zanu zonse. Inu simukuyenera kugwetsedwa mphwayi. Khulupirirani mwa Mulungu. Kodi ntchito yanu ndi ntchito yofunikira bwanji? Mwina inu simungathe kudziwa yankho la funsoli m’moyo uno. Komabe panopa inu mukhoza kudziwa mtengo wa moyo wanu: Mulungu anapereka Mwana Wake kuti akupulumutseni.

Izi zikuwonetsa kuti inu ndi a mtengo wapatali kwambiri…”
“M’Khristu woona aliyense adzadutsa m’nyengo zovuta. Satana adzayesetsa kukulepheretsani kukhala ofanana ndi Khristu mu mtima mwanu. Koma yang’anani ku mtanda. Pamene tikukayang’ana ku mtanda, ife tidzapambana. Yesu akutiphatsa lonjezo ili: ‘Sindidzakusiya konse, ngakhale kukutaya, sindidzakutaya ndithu.’ (Ahebri 13:5). Ndipo ‘onani, Ine ndili pamodzi ndi inu masiku onse, kufikira chimaliziro cha nthawiyi ya pansi pano’ (Mateyu 28:20).”—Ellen G. White, mu The Youth’s Instructor, November 9, 1899, mawuwu ndi okonzenso.

MAFUNSO OKAMBIRANA:

*1. Paulo anaponyedwa m’ndende nthawi zochuluka. Iye sanalakwe kena kalikonse. Kodi inu mumamva bwanji ngati anthu ena akukuchitirani zinthu zopanda chilungamo kapena kukuchitirani nkhaza? Nanga ndi malonjezo ati a m’Baibulo amene amakuthandizani mu nthawi zovutazi?*

*2. Tertullian anali mtsogoleri wa mpingo wa Chikhristu woyambirira. Pamene Aroma anali kuvulaza ndi kupha Akhristu, Tertullian analankhula mawu awa, “Nthawi imene inu mukupha ambirimbiri pakati pathu, ndi pamene chiwerengero chathu chimanka chikulira—kulira. Mwazi wa ophedwawo uli ngati mbewu.” Pa nthawi yokhayokhayo, mtopola umene unkachitikira Akhristu nthawi zina unkapangitsa kuti ntchito ya Mulungu ikhale yovuta kalero, komanso ngakhale lero. Kodi ife tichite chiyani kuti tithandize Akhristu amene akuchitidwa ntopola chifukwa cha chikhulupiriro chawo?*

*3. Taganizireni za mmene Paulo anavutikira. Tsopano werengani vesi loloweza la mlungu uno. Kodi mawu oti, “kondwerani mwa Ambuye nthawizonse” akutanthauza chiyani? (Afilipi 4:4). Nanga ife tingakondwerera bwanji mwa Ambuye nthawi zonse? Nanga bwanji pamene wokondedwa wanu wadwala kapena kumwalira kumene? Kapena pamene mwachotsedwa ntchito? Kapena pamene mukumva ululu woopsa kwambiri? Ife monga Akhristu, kodi ndi chiyani chimene chiyenera kutipanga kukhala okondwera nthawi zonse?*

MATHERO A PHUNZIRO LATHU.

Bronnex C PHIRI MPESA SDA DURBAN In list 3 items

 Chipasula Seventh Day Adventist Church
20/12/2025


Chipasula Seventh Day Adventist Church

🎶CHORAL SABBATH🎶Join us at Seventh Day Adventist Church, Chipasula for a powerful Choral Sabbath, under the theme:“Tidza...
17/12/2025

🎶CHORAL SABBATH🎶

Join us at Seventh Day Adventist Church, Chipasula for a powerful Choral Sabbath, under the theme:
“Tidzayimba Kumwamba Nthawi Zonse”

📅 Saturday, 20th December 2025
⏰ 07:30 AM – 04:30 PM

Be blessed by uplifting music from inspiring guest groups and a life-changing message by Elder Maxwell Kazako.
Come and worship, sing, and be renewed in the presence of the Lord.

You are all invited to attend.

Address

P O Box 30987
Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Chipasula Seventh Day Adventist Church posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Place Of Worship

Send a message to Chipasula Seventh Day Adventist Church:

Share