St Denis Ssebuggwawo Parish - Chinsapo

St Denis Ssebuggwawo Parish - Chinsapo St Denis Ssebuggwawo Parish is under the Archdiocese of Lilongwe and is located at Chinsapo

MAWA MUKAPEMPHERA KUTI?Ife ku parish yathu tili ndi Chaka cha Ukalistia pamene ana akhale akuyamba kulandira sacrament l...
29/08/2026

MAWA MUKAPEMPHERA KUTI?

Ife ku parish yathu tili ndi Chaka cha Ukalistia pamene ana akhale akuyamba kulandira sacrament la Ukalistia

Misa izakhalapo imodzi nthawi ya 7 koloko mmawa

Ngati mungathe, bwerani muzapemphere nafe komanso kuzasangalala limodzi ndi ana athu pamene akuyamba kulandira ukalistia...

ZAKA ZISANU (5) ZA U EPISIKOPI Zaka zisanu zapitazo, pa 28th August 2021, Diocese ya Dedza inalandira Episikopi watsopan...
28/08/2026

ZAKA ZISANU (5) ZA U EPISIKOPI

Zaka zisanu zapitazo, pa 28th August 2021, Diocese ya Dedza inalandira Episikopi watsopano - Ambuye Peter Adrian Chifukwa

Mwambo owadzodza u Episikopi unachitikira pa bwalo la Bembeke Cathedral ku Dedza ndipo amene anawazoza u Episikopi ndi Ambuye Archbishop Thomas Luke Msusa...

Ambuye Chifukwa anasankhidwa ndi Papa Francis kukhala Episikopi wa Diocese ya Dedza pambuyo pa imfa ya Malemu Ambuye Emmanuel Kanyama.....

Happy 5th Episcopal anniversary Ambuye Peter Adrian Chifukwa

📸: Ambuye Peter Adrian Chifukwa

Photo credit: Malawi Conference of Catholic Bishops

HAPPY BIRTHDAY AMBUYE PETER ADRIAN CHIFUKWA Lero ndi tsiku limene Ambuye Peter Adrian Chifukwa anabadwa.Ambuye Chifukwa ...
27/08/2026

HAPPY BIRTHDAY AMBUYE PETER ADRIAN CHIFUKWA

Lero ndi tsiku limene Ambuye Peter Adrian Chifukwa anabadwa.

Ambuye Chifukwa ndi Episikopi wa Diocese ya Dedza komanso wachiwiri kwa wapampando wa bumgwe la ma Episikopi kuno ku Malawi la MCCB...

Ambuye Chifukwa anazozedwa kukhala Episikopi wa Diocese ya Dedza pa 28th August 2021...

Happy birthday Ambuye Chifukwa

📸: Ambuye Peter Adrian Chifukwa

TSIKU LOWAWA KU PARISH YATHULero lakhala tsiku lowawa ku parish yathu pamene Akhristu athu awiri alowa mmanda. Ambuye at...
24/08/2026

TSIKU LOWAWA KU PARISH YATHU

Lero lakhala tsiku lowawa ku parish yathu pamene Akhristu athu awiri alowa mmanda. Ambuye atichitire Chifundo...

'Tizaonanaaaaaaaaaaa, tizaonanaaaaaaaa - tizaonana mwambaaaaaaaaaa - malo aliko' 🎶🎵

Yendani bwino Mayi Maria Flora Joseph ndi Mr Andrew Kapu

Ambuye muwapatse anthu akufa chiutsiro chosatha ndipo kuyera kosatha kuwalitse maso awo...Ause ndi Mtendere...Amen

📷: Bambo Jean Kesse ndi bambo Chikumbu

THAMBO LAKUDA LATIGWERA KU PARISH YATHU Mitima yathu ndi yosweka komanso tadzadzidwa ndi chisoni chachikulu chifukwa cho...
23/08/2026

THAMBO LAKUDA LATIGWERA KU PARISH YATHU

Mitima yathu ndi yosweka komanso tadzadzidwa ndi chisoni chachikulu chifukwa chotaya Akhristu awiri ku parish yathu.

Mr Andrew Kapu atisiya dzulo mmawa ku chipatala cha Kamuzu central komwe anawagoneka. Iwo amachokera ku mphakati wa St Bakhita ndipo atisiya atadwala kwa nthawi yaitali.

Mai Maria Flora Joseph atisiyanso dzulo madzulo kuchipatala cha Kamuzu central komwe anawagoneka. Iwowa amachokera ku mphakati wa St Patrick's omwenso uli mudera limodzi ndi mphakati wa St Bakhita. Mayiwa analinso membala wa kwaya ya St Mary's yopezeka ku parish yathu.

Maliro onsewa ndi oika mmawa lolemba pa 24th August 2026 ndipo kuzakhala mwambo wa Misa ya maliro ku parish nthawi ya 10 koloko mmawa (Misa ya Malemu Maria Flora Joseph) komanso 12 koloko masana (Misa ya Malemu Mr Kapu).

Pambuyo pa mwambo wa Misa, thupi la Malemu a Kapu likaikidwa mmanda ku area 18 ndipo Malemu Flora akaikidwa ku Chinsapo 1....

Tikupepesa akubanja komanso Akhristu onse chifukwa chotaya Akhristu anzawo...

Tipemphere kwa Mulungu kuti atichitire Chifundo munyengo zowawitsazi....

Kupempherera anthu akufa....

Ambuye muwapatse anthu akufa chiutsiro chosatha ndipo kuyera kosatha kuwalitse maso awo...ause ndi mtendere....Amen

📸: Malemu Mr Kapu komanso Malemu Maria Flora Joseph

ANA A UKALISTIA ALANDIRA UBATIZO Wakulaaaa Ekleziaaaaaa Wakulaaaaa Lerooooo 🎶🎵🎼 Lero ana okwana alandira sacrament la ub...
23/08/2026

ANA A UKALISTIA ALANDIRA UBATIZO

Wakulaaaa Ekleziaaaaaa Wakulaaaaa Lerooooo 🎶🎵🎼

Lero ana okwana alandira sacrament la ubatizo pokozekera kulandira ukalistia Lamulungu likubwerali....

Bambo Jean Kesse MAfr ndi amene anatsogolera mwambo wa Misa

Anawatu alowa mmbumba yake ya Eklezia

Wakulaaaaa Ekleziaaa Wakulaaaa Lerooooo 🔥🔥🔥🔥🔥

23/08/2026

MISA LERO PA 23/026 LAMULUNGU LA 21 PA CHAKA

MAIN CELEBRANT IS FR GUELORD MAHONGOLE MAFR

TIYENI TIPEMPHERE LIMODZI

MBINDIKIRO WA MABANJA Mbindikiro wa mabanja uli mkati ku parish yathu ndipo amene akutsogolera mbindikiro umenewu ndi ba...
22/08/2026

MBINDIKIRO WA MABANJA

Mbindikiro wa mabanja uli mkati ku parish yathu ndipo amene akutsogolera mbindikiro umenewu ndi bambo mfumu athu Fr Jean Kesse pamodzi ndi banja la a Maxwell...

Cholinga cha mbindikiro umenewu ndi kuzamitsa Chikondi Pakati pa mabanja a chikhristu mmparish yathu...

Mabanja osiyanasiyana akutenga nawo gawo pa mbindikiro umenewu.

📸: Mbindikiro wa mabanja

CHILDRENS CONGRESS - ARCHDIOCESE OF LILONGWE Ana a tilitonse okwana 15 kuchokera ku parish yathu lero anyamuka ulendo ok...
21/08/2026

CHILDRENS CONGRESS - ARCHDIOCESE OF LILONGWE

Ana a tilitonse okwana 15 kuchokera ku parish yathu lero anyamuka ulendo okakhala nawo ku mnsonkhano wa ana (Childrens Congress) omwe wakonzedwa ndi Archidiocese yathu ya Lilongwe komanso ofesi ya ma utumiki a apapa ya PMS.

Asananyamuke ulendowu, bambo mfumu athu anatsogolera nsembe ya misa yowapempherera anawa pa ulendo wawo komanso kuti akakhale ndi msonkhano opambana.

Ana pafupifupi 700 kuchokera mma parish osiyanasiyana akuno ku Archdiocese ya Lilongwe akuyembekezeka kukakhala nawo pa mnsonkhanowu.

Mnsonkhanowu ukachitikira ku St Anne's Guilleme Parish ku Mchinji ndipo uyamba lero pa 21st August mpaka lamulungu pa 23rd August 2026. Mutu wa mnsonkhano umenewu ndi: ANA KHALANI AMODZI MWA KHRISTU, OGWIRIZANA MU UTUMIKI.

Tiyeni tiwafunire mafuno abwino ana athu ndipo tiwapempherere kuti msonkhano wawo ukhale opambana....

LUNCH HOUR REFLECTIONKUKHALA A CHIFUNDO NDI A CHIKONDI"Khalani achifundo, monga Atate anu ali achifundo" [Luka 6:36]…..T...
20/08/2026

LUNCH HOUR REFLECTION

KUKHALA A CHIFUNDO NDI A CHIKONDI

"Khalani achifundo, monga Atate anu ali achifundo" [Luka 6:36]…..

Tikuyenera kukhala anthu chifundo, okoma mtima, komanso a chikondi kwa anzathu nthawi zonse.

Tikuyenera kuchitira chifundo anzathu ngakhale kwa iwo omwe akuoneka ngati ndi osayenerera kulandira chifundo chimenecho.

Tiyeni tiwakonde anzathu posayang’anira zolakwa zakale ndipo tiwaonetse chikondi osati kubwezera choipa.

Mulungu atithandize kuti tizikhala achifundo komanso achikondi nthawi zonse...Amen….

Masana abwino kwa inu nonse......

Address

Box 104, Lilongwe ; Along The Kachere Street/Chinsapo 1
Lilongwe

Telephone

+265998616914

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when St Denis Ssebuggwawo Parish - Chinsapo posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Place Of Worship

Send a message to St Denis Ssebuggwawo Parish - Chinsapo:

Shortcuts

Share

Category