St Denis Ssebuggwawo Parish - Chinsapo

St Denis Ssebuggwawo Parish - Chinsapo St Denis Ssebuggwawo Parish is under the Archdiocese of Lilongwe and is located at Chinsapo

29/05/2026

TODAY'S REFLECTION ON CUNIMA'S GRADUATION

29/05/2026
..Usiku ungatalike bwanji, koma kunja kumacha basi.....

Pali nthawi zina timaona ngati tikutaya nthawi kapena Mulungu akuchedwa kuyankha mapemphero athu. Komatu AYI... Chilichonse chimakhala ndi nthawi yake ndipo munthawi yake Mulungu amakwaniritsa..

Atatha ena zaka zinayi, ena zaka zitatu akuphunzira, lero amaliza maphunziro awo ndipo alandira ma diploma ndi ma degrees. Ena amachezera kuwerenga, ena kudzuka mbandakucha cholinga azakwaniritse khumbo lawo.

Ena anali ndi nkhawa kuti ulendowu watalika, kapena ndalama za fees ndizipeza bwanji, ena mkumati koma zitheka? Koma lero zonse zatheka....Imeneyi ndi nthawi ya Mulungu...

Tizikhala odekha ndi odikira mwa chiyembekezo ndi chikhulupiriro....

Lero tikufunira mafuno abwino onse amene amaliza maphunziro awo ku sukulu ya Catholic University of Malawi

Pitani mukatumikire dziko mwa toto moyo ndi kukasintha miyoyo ya anthu...

Mulungu akutsogoleleni pamene mukhale mukasaka mwayi wantchito komanso ena pamene mukhale mukupitiriza maphunziro anu

Congratulations....

📹: Ena mwa ophunzira pamwambo wa graduation ku Nguludi

25/05/2026

TODAY'S REFLECTION
25th MAY 2026

KUTUMIKIRA AMBUYE

Kodi timamutumikira bwanji Ambuye?

Timathandizira bwanji kuti chipembedzo chiyende bwino komanso kuwathandiza anthu kupemphera bwino?

Pa moyo wathu wa Chikhristu tikuyenera kukhala otakataka potumikira Ambuye pa parish yathu, ku mphakati, kaya Church ngakhalenso ku diocese/archdiocese.

Mu mpingo wathu tili ndi mabungwe osiyanasiyana amene tingathe kulowa kuti tizitumikira Ambuye komanso mpingo.

Kodi inu ku parish yanu, church, mphakati kapena Diocese/Archidiocese mumatumikira Ambuye motani?

Choir? Owerenga? Achipembezo? Youth? Scout? YCW? CWA kapena CMA? .....

Tatiuzeni

Mukhale ndi usiku opambana

📹: Maria Rosa Choir - St Denis Parish Chinsapo kunyadira utumiki wawo mmaimbidwe...

Our parish schedule for this week
25/05/2026

Our parish schedule for this week

24/05/2026

UTHENGA WAPADERA WA LERO LA MULUNGU LA CHAKA CHA PENTEKOSITE

Bambo Jean Kesse MAfr - Bambo Mfumu

LAMULUNGU LA PENTEKOSITE Kwanuko linali bwanji tsiku la lero la kutsika kwa Mzimu Woyera....Kuno kwathu kunali bwino zed...
24/05/2026

LAMULUNGU LA PENTEKOSITE

Kwanuko linali bwanji tsiku la lero la kutsika kwa Mzimu Woyera....

Kuno kwathu kunali bwino zedi ndipo mwambo wa Misa anatsogolera ndi bambo mfumu athu bambo Jean Kesse MAfr.....

Mu ulaliki wawo bambo Kesse atipempha kuti pamene talandira mzimu Woyera lero, tikuyenera kusinthika..."Ngati munali akuba, lero musiye chifukwa mwalandira mzimu Woyera. Ngati munali ankhanza kwa ena, mukuyenera kusinthika lero chifukwa mzimu Woyera uli mwa Inu" ......

A bungwe la Charismatic ndi amene anatsogolera chipembedzo komanso kupereka mphatso zapaguwa.....

Kodi kwanuko zayenda bwanji?

Ansembe anu alalika zotani lero? Mau amene anakugwirani mtima ndi otani.....

Tsiku lopambana kwa Inu nonse

📸: Ma membala a bungwe la Charismatic pa mwambo wa Misa wa lero....

24/05/2026
24/05/2026

PENTECOST SUNDAY 🔥 - MAIN CELEBRANT IS FR JEAN KESSE

LAMULUNGU LA PENTEKOSITE MUKAPEMPHERA KUTI?Kuno kwathu ndinu olandiridwa ndipo Misa zizakhalapo zonse ziwiri; 6am ndi 8a...
23/05/2026

LAMULUNGU LA PENTEKOSITE MUKAPEMPHERA KUTI?

Kuno kwathu ndinu olandiridwa ndipo Misa zizakhalapo zonse ziwiri; 6am ndi 8am komanso tizakhala tikujambula mwambo wa Misa LIVE pa page yathu ino..
....Bwerani kuti tizalandire mphatso za mzimu Woyera...
...Iche tupochere mbaso dya msimu weswera..
..Zaninge muzakapokere chawanangwa cha mzimu utuwa....

🔥 🔥 🔥 🔥

TODAY'S REFLECTION KODI TIMAWAPEMPHERERA ATUMIKI ATHU?  23rd MAY 2026Mumpingo wathu wa Katolika tili ndi atumiki osiyana...
22/05/2026

TODAY'S REFLECTION

KODI TIMAWAPEMPHERERA ATUMIKI ATHU?

23rd MAY 2026

Mumpingo wathu wa Katolika tili ndi atumiki osiyanasiyana amene amatitsogolera komanso kutithandizira mmoyo wathu wa uzimu wa tsiku ndi tsiku.

Ma bishopu, Ansembe, Adikoni, Abulazala komanso Asisitere ndi atumiki amene Mulungu anawasankha komanso kuwapatula kuti azititumikira ku ma church komanso mmalo osiyanasiyana.

Atumiki ena monga ma mishonale amachoka madera kapena maiko awo kukatumikira dera kapena dziko lina. Uku kumakhala kuzipereka kotheratu....

Atumiki a Mulunguwa nawonso ndi anthu ndipo amafuna mapemphero athu nthawi zonse. Mapemphero athu amawathandiza moyo wawo wa tsiku ndi tsiku komanso amawathandiza kukhala olimba pa utumiki wawo..

Tsiku ndi tsiku tikamapemphera tiyeni tiziwakumbukira atumiki a Mulungu mmapemphero athu....

Mwapadera tiwapempherere Abulazala 13 amene mawa akhale akuzozedwa udikoni ku Zomba - Zabwino zonse and congratulations

Usiku wabwino kwa nonse

📸: Mabulazala amene akulandira udikoni mawa ku Zomba

TODAY'S REFLECTION - 21st MAY 2026.....KODI TIMAPITA KU CHURCH CHIFUKWA CHIYANI?....Anthufe timapita ku church ndi zolin...
21/05/2026

TODAY'S REFLECTION - 21st MAY 2026
.....KODI TIMAPITA KU CHURCH CHIFUKWA CHIYANI?....

Anthufe timapita ku church ndi zolinga zosiyanasiyana. Cholinga chathu choyamba nkukhatokoza Mulungu ndi msembe yathu; Timapita kukapemphera, kukathokoza, kukapepesa kwa Mulungu komanso kukapempha zosowa za moyo wathu wa tsiku ndi tsiku...Izitu ndi zina mwa zolinga zenizeni zokapezekera munyumba ya Ambuye kapena kuti ku church..

Ena timapita ku church opanda zolinga zeni zeni ndipo mapeto ake timabwerera kunyumba chimodzimodzi opanda kusinthika mmoyo wathu wa uzimu....

Ena timapita kuti tikacheze ndi anzathu kapena tikawaonetse zovala zatsopano zomwe tagula ndipo kutifunsa kuti mwamvako zotani ku church sitimayankha kanthu ndipo timangoti "iiii koma kunabeba"....Ku church simalo okacheza AYI....inde m***a kucheza ndi anzanu pamene tamaliza kupemphera choncho macheza asamakhale mu church ayi.....ndi nyumba ya Mulungu yofunika ulemu wake....

Ndiye pali kagulu kena kopita ku church kukasokoneza anzawo....monga kulowa mochedwa ndi nsapato za gogoda mkumasokosa church chonse...ena ma phone mkumasokosa mu church mwinanso panthawi imene abambo akulalika...Izi sizolinga zabwino zopitira ku church...

Palinso kagulu kena kokonda kutulukatuluka mu church mkumakacheza panja pamene mwambo wa Misa kapena mapemphero uli mkati...Izitu Mchimodzimodzi kukhala kunyumba mkumacheza...

Tizindikire kuti church ndi nyumba ya Mulungu yofunika ulemu wake monga kavalidwe koyenera, kuyenda mwa ulemu, kutsatira dongosolo lonse moyenera komanso ngati mkotheka kutenga nawo gawo muzochitika.

Tikuyeneranso kudziwa kuti church ndi malo oyera - osasewera mu church ndipo makolo titenge udindo oonetsetsa kuti ana athu akuphunzitsidwa mmene angaperekere ulemu mu church...

Potsiriza, pali kagulu kena kamene kamapita ku church pokhapokha ku church kukhale zabwino zokha zokha...AYI...Tiyeni tizipita ku church munyengo zonse popeza ndi nyumba ya Ambuye kumene titha kukatula nkhawa zathu. Tisaope kulowa mu church mkukacheza ndi Ambuye ikhala mu sacrament la Ukalistia...Tisaope kulowa mu church ndikukapemphera - ndi nyumba ya Atate athu..

📸: Church cha St Denis Ssebuggwawo Parish Chinsapo

HAPPY BIRTHDAY BAMBO GUELORD MAHONGOLE Mwezi uno wa May, ma birthday atipanikiza ku parish yathu..Lero tikukondwerera ku...
20/05/2026

HAPPY BIRTHDAY BAMBO GUELORD MAHONGOLE

Mwezi uno wa May, ma birthday atipanikiza ku parish yathu..

Lero tikukondwerera kubadwa kwa abambo mnthandizi a parish yathu Bambo Guelord Mahongole.

Bambo Mahongole amachokera ku St Francis Xavier Parish mu Archidiocese ya Bukavu mdziko la Democratic Republic of Congo

Padakali pano iwowa ali kumudzi kwawo ku DRC ku holiday kumene adapita kukacheza ndi makolo komanso achibale

Happy birthday Abambo

Address

Box 104, Lilongwe ; Along The Kachere Street/Chinsapo 1
Lilongwe

Telephone

+265998616914

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when St Denis Ssebuggwawo Parish - Chinsapo posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Place Of Worship

Send a message to St Denis Ssebuggwawo Parish - Chinsapo:

Share

Category