29/05/2026
TODAY'S REFLECTION ON CUNIMA'S GRADUATION
29/05/2026
..Usiku ungatalike bwanji, koma kunja kumacha basi.....
Pali nthawi zina timaona ngati tikutaya nthawi kapena Mulungu akuchedwa kuyankha mapemphero athu. Komatu AYI... Chilichonse chimakhala ndi nthawi yake ndipo munthawi yake Mulungu amakwaniritsa..
Atatha ena zaka zinayi, ena zaka zitatu akuphunzira, lero amaliza maphunziro awo ndipo alandira ma diploma ndi ma degrees. Ena amachezera kuwerenga, ena kudzuka mbandakucha cholinga azakwaniritse khumbo lawo.
Ena anali ndi nkhawa kuti ulendowu watalika, kapena ndalama za fees ndizipeza bwanji, ena mkumati koma zitheka? Koma lero zonse zatheka....Imeneyi ndi nthawi ya Mulungu...
Tizikhala odekha ndi odikira mwa chiyembekezo ndi chikhulupiriro....
Lero tikufunira mafuno abwino onse amene amaliza maphunziro awo ku sukulu ya Catholic University of Malawi
Pitani mukatumikire dziko mwa toto moyo ndi kukasintha miyoyo ya anthu...
Mulungu akutsogoleleni pamene mukhale mukasaka mwayi wantchito komanso ena pamene mukhale mukupitiriza maphunziro anu
Congratulations....
📹: Ena mwa ophunzira pamwambo wa graduation ku Nguludi