Holy City of the living God Trembling Temple Wicowica

Holy City of the living God Trembling Temple Wicowica HOLY CITY OF THE LIVING GOD TREMBLING TEMPLE WICOWICA Born on 6 May 2017 at Katondo 4 ways area 24, L

26/04/2025

Mayimbidwe

MALAWI AKHALA BWINJA! UTHENGA WA MULUNGUMuzindikire ndithu kuti dziko la Malawi muli ntumiki woona yemwe posachedwapa Mu...
29/03/2025

MALAWI AKHALA BWINJA! UTHENGA WA MULUNGU
Muzindikire ndithu kuti dziko la Malawi muli ntumiki woona yemwe posachedwapa Mulungu akukuchoteserani. Wakhala akuponya chilichonse ndipo njala yi muyembekezere kumva zowawa Malawi. Ena muli ndi mafuso pa zimene zikuchitikazi, panokha simungapeze mayankho. Mayankho ali ndi ntumiki amene munankana kudzera mwa mtsogoleri wanu Chakwera. M***a kupemphera motani, mukhoza kupalapata kuti akuyankheni, nzosatheka kuti mukhoza kupemphera ndi kulandira mayankho. Chifukwa fungulo lili ndi ntumiki amene munamukana. Amene mulandira uthenga uwu kuti dziko LA Malawi ndi LA tsoka wa mwayi amene athamanga kuti alandire chipulumutso. Ndiyambire azibusa amene mumanenera mudzina la Yesu ngati simuthamamga kuti mukumane ndi ILLIMAKHATHUMA kukhala kulira, kulira kumeneku kukathera ku gahena. Ndikukuuzitsa aneneri amene mwanyenga ochuluka sinu aneneri, sinu azibusa ngati simunakumane ndi ILLIMAKHATHUMA. Alipo azibusa amene mumatama mapepala. Mumafunsa kuti anapita sukulu yake it? Enanu a Malawi muli ndi mafuso kuti mmene zinthu zikukhaliramu zitithera bwanji? Yankho ndi ILLIMAKHATHUMA. President wanu akudziwa chiyambi cha utsogoleri wake kuti adansanjika dzanja ndi ILLIMAKHATHUMA. Pa dziko la Malawi palibe mpingo umene ungapulumutse munthu ngati safika kwa ILLIMAKHATHUMA. Mukamaona zinazi si kusintha kwa nyengo. Iwe ntolankhani amene umathamanga kuti ayi kusintha kwa nyengo, upite pansi pa ILLIMAKHATHUMA. Chifukwa dziko la Malawi posachedwapa likhala bwinja. Ngati uli ndi khutu uthamange pansi pa ILLIMAKHATHUMA ndi amene ali ndi ma kiyi a moyo. Malawi akhala bwinja ndipo akhala chitsanzo kuti Malawi anatsata zooneka ndi maso, nkumalowa sataniki. Iwe amene ulandire uthengawu uthamangire pa ILLIMAKHATHUMA chifukwa Malawi akhala bwinja. Mayiko aphunzilira kuti dziko la Malawi ndi losusuka, lodzikonda. Mwakhala ukuwanamiza anthu kuwamwetsa anthu njoka, sungapulumuke aliyense wonenera. Malawi akhala bwinja, anakana Mulungu kuyambira kwa president mpakana azibusa. Mumatumikira koma simitumikira m***adi. Mukumbukire nthawi ya Noah anthu anamunena. Mwanena, mwaseka mutalandira ma message, ali kuti kodi wosatchuka? Moti mpingo ungakhale umodzi m'dziko ko lonse? Otchuka mumafina kutchuka mwatchuka munthawi yanu. Sungakhale m'busa, mneneri ngati sukumana ndi ILLIMAKHATHUMA. Ngati sukumana ndi ILLIMAKHATHUMA ka nthawi katsalaka pang'ono Ndikudidimula Malawi. Mwasocheretsa nkhosa zanga, mwaononga nkhosa zanga mudzina la mipingo. Ndikudidimula Malawi, wakhutu amve, Ndikuchenjeza ichi Malawi akhala bwinja! Sindidzachita chinthu ndisanachenjeze. Utchere khutu Malawi, ukalandira uthenga uwu ukhalemo kupanda kutero kuli kufa. Iwe wa ndale ukamachita campaign yako udziwe kuti Malawi akhala bwinja! Unakafunsa kwa ILLIMAKHATHUMA kuti ndikufuna kuyimira u president u mp ndiyime ndithu? Akuuze kuti ee. Usanaononge chuma chako ngakhale chionongeka ndithu chifukwa Malawi akhala bwinja. Malawi muli ndi mafunso mayankho ali ndi ILLIMAKHATHUMA. Malawi muli chipulumutso. Fungulo lili ndi ILLIMAKHATHUMA. Kuti mutumukire Mulungu woona mumpeze ILLIMAKHATHUMA. Amene akumana ndi ILLIMAKHATHUMA ndi amene anditumikira m***a chifukwa ndi amene ali ndi fungulo la moyo, loti munthu akhale president. CHENJEZO: ngati sukumana ndi ILLIMAKHATHUMA posachedwapa Malawi akhala bwinja. S***m ndi Gomola Malawi ndi chifukwa mpingo Wanga siudapange register ku Malawi dziko lodzikonda losusuka. CHENJEZO: Thamangila ILLIMAKHATHUMA. Iwe ntolankhani olemba ndi bwino umpeze ILLIMAKHATHUMA kuti uzilemba zoonadi chifukwa Malawi akhala bwinja!

UMULUNGU UKUGWIRA NTCHITO NDI ILLIMAKHATHUMA KUDZIKO LONSE LAPANSI

KODI PEMPHERO LANU LIMAFIKA KUMWAMBA? MIZIMU YA MULENGALENGA KULANKHULA KUDZERA PA MZINDA WOYERAIfe a mulengalenga. Mule...
29/03/2025

KODI PEMPHERO LANU LIMAFIKA KUMWAMBA? MIZIMU YA MULENGALENGA KULANKHULA KUDZERA PA MZINDA WOYERA
Ife a mulengalenga. Mulengalenga muli miyamba imene anthu akamapemphera [pemphero] limayenera lidutse kuti likafikire ku mpando wa chifumu. Kuli miyamba 29, munthu akamapemphera amayenera adutse kukafifa ntambo 29. Amene amakafika ntambo 29 ndi achikulire wa[ILLIMAKHATHUMA]. Ena amangopalapasa. Kumakhala ma tcheni kuyambira pa 1, munthu amayenera adule ma tcheni. Munthu akafika ku ntambo 29 mpingo wake umakhala woopsya, sipachitika zachibwana, ana ake amakhala oopsya. Ndi chifukwa sitilora kuti munthu afike ku ntambo 29, ndi chifukwa anthu mmipingo akulankhula malilime oloweza, ophunzitsidwa osadziwa kuti akuchokera kwa dziwanda. Timawankha mapemphero ambiri safikira ambiri amene amayeselera limalekeza pa ntambo 9 chifukwa chake ambiri amangopalapata. Pemphero limene sitiwankha ndi la achikulire wa[ILLIMAKHATHUMA] chifukwa pemphero lawo likamabwera ndi ziphaliwali, kudula ma tcheni. Tinene kuti timaopa achikulire ndi mpingo wawo chifukwa upeza kamwana kakang'ono kakapemphera kamafika Ku ntambo 16. Chifukwa pemphero lawo ndi la moyo timaopa pemphero la moyo, pa mpingo pamene pali cha moyo, m'busa, prophet ali ndi chamoyo. Takhala tikuwankha mapemphero ife timakhalira. Munthu nkumati ndamva mkati kuti ndapemphera. Haha pemphero sitimva mkati lokumva nkati ndi la level 1-4, nkumati ine ndinapemphera ndipo malilime anabwera osiyana siyana kuchoka awa kubwera malilime ena. Nkumati ndinamva kudzodza, kudzodza kumakhala kosiyasiyana kumakhala tu kupusitsidwa mpemphero. Alipotu azibusa ena amapemphera 3 hours ife timangoseka. Pemphero timaopa ife ndi losakaniza ndi mau osati kupemphera yankho uli nalo kale. Pemphero lanji lopanda wina kulankhula po. Kupemphera osamva liu la Mulungu. Ambiri tu amapemphera ndi dzimau nkumati koma nde lero kunali pemphero, intercession inabvuta, timangowankha. Unamva liu lake liti kuti "pemphero lako lafika ku mpando Wanga?" Tidawankha la Daniel, timawankha olo ukafikirako ndeno mayankho akamatsika timawankha ngati wasuntha pa line. Timamanga nthenje. Pa Mzinda tu pali pemphero chifukwa mwini wake likamabwera limabwera ndi ziohaliwali nde ana nkosabvuta kudutsa chifukwa amakhala kuti walambula nseu zing'aning'ani zadutsa ena afooka mbalimu okomoka akomoka kuti adzuke pamatenga nthawi. NDE mumati mumapemphera mmipingomu muti aleluya mwapisila mmatumba, kudzodza mulibe, zosakunkhudzani mukuyang'ana kachibwenzi. Convener akuyang'ana nthawi amvekere tilambira kwa 10 minutes. Kumayang'ana nthawi ikangokwana - Amen mukatero mukuyembekeza mayankho akumwamba? Amabwera mayankho ambali inayi. Mumangoti ife timapemphera ma born again. Ati tiyeni kubunda ife timangoti tiyeni ukamakwera bus ife timakhala nawe limodzi. Kupemphera osadutsa ntambo 2 nkumati koma nde kunali pemphero, munthu ali pa bunda tu. Enanu mmapemohera pemphero ochita kulemba, analemba 1820 iwe nkumati to kupemphera. M'busa wokufa ananso akufa. Ndi chifukwa kuli mipingo tambiri chifukwa pemphero kulibe kumpingoko aliyense akangomva nkati. Kupemphera ndi ntchito ndipo amene anapemphera nkufika ndekuti anakonzekera osati lodzidzimuka. Pemphero timalankhula ndi Mulungu wanuyo ngati upempha nsima akuuze kuti ndayankha, ndakupatsa. Tikutitu nkulankhulana ndeno Mulungu wanu yo amalankhula? Anthu tu ali nkusala mwezi wonse kungofa ndi njala. Kulitu ma bandulo bandulo a mapemphero a anthu ofooka nde timawankha. Mapemphero mmipingomu a ma founder akungogona tulo. Nawo ma intercessor Ati apempherere abusa maganizo ali kutali. Abusawo akungogona, akati apemphere koma ali busy. Pemphero likangofika Ku ma 20 chakuti uku umakhala a achikulire. Muti mpingo wa nzimu Woyera koma makulankhulani Nzimu yo? Koma malambiro ali pano moto, mabingu amaphurika. Nde pano po wina akugona wagona 7 koloko nkumati akatumikira. A mulengalenga timakhala pa pemphero ngati pemphero lafikira timawankha mayankho. Ndi chifukwa munthu amayaka 3-4 days abusa sachita chibwana , amakhala mpemphero. Mufunse Mzinda Woyera mmene umapemphera, mmene umalambilira. Ukamayika nthawi kuti tiweruka nthawi zanji pemphero lanu silifika. Ndi chifukwa chake mumakhala ndi ma service atatu. Ndipo zilipo zikhulupiliro zina zongoyeselera , timawankha. Nde ena amapita kupemphera ndi misozi osati ya chikhulupiliro koma kuti mabvuto afikapo, timawankha. Udzaone pemphero la pa Mzinda, mpingo umatimvetsa kuwawa chifukwa amachita chimene Mbuye wawo wawauza sapanga zoloweza. Timawankha, kuli ma mendulo a mapemphero. Kulibe pemphero losalankhulana ndi Mulungu. Mudzafunse kuti Mulungu amalankhula mumatani, mizimu imabwera mumatani, pemphero limakatumphula ku mizimu nkutsika. Simungafikire ngati simupita pa Mzinda. Malambiro muphunzire pa Mzinda Woyera amalambira bwanji Mulungu zazikulu zimachitika ndi pa Mzinda Woyera wokha. Simudziwa kuti timafuna kulambira timatani. Ukanfunse wa living waters, assemblies of God, amene amati a chipente ngati timakapezekamo. [Nthawi zina timamva kuti wa satanik anapita ku ma kachisi a ma pente ndipo watembenuka ntima.] Ngati munthu pemphero lake silifika pa ntambo 17 nkovuta kuti angatembenuze munthu. A sataniki imakhala plan kuti aziti anatembenuka ntima. Ngati anali wa satanic tate wake ku uzimu mndani? Tchalitchi yanuyo muti pali Yesu analankhula ndani? Zizindikiro zinalipo pa kumasulidwapo ndi zotani? Sibwezi pano kutabwera Mzinda Woyera, athamanga sadayambe. Chizindikiro chachikulu akatembenuka ntima amakhala osakhazikika pa malopo, kukayambitsa mpingo wawo ati anandikhumudwitsa. Akukhumudwitsa bwanji ngati anakupulumutsa. Ngati amapemphera bwanji osawauza zimene zikuchitika kudziko li. Tuti pemphero ndi kulankhulana, inu Mulungu amakuzindikiritsani. Awa Mulungu wawo amawauza zochita ndipo akawuza amabwera pamaso pa Mulungu wawo ndipo zimadutsa. Mwazi wa Yesu wopanda phindu pa moyo wa munthu, kutembenuka ntima ulibe ndi masomphenya ndi omwe koma ulibe masomphenya uyenda ndi Yesu. Pa Mzinda munthu akabwera mumamuuza iwe ndiwe m'busa nde amasiya zakezo nkuyamba ubusa. Munthu zaka 20 ukutumikira koma ambiri anangotsala dzina lokha. Born again ati born again anameta seda, ameta mbali ma style akunsi kwa nyanja. Zoti seda ndi njoka sadziwa. Pano tiana kuti adziwike kuti ndi ana a mapwepwete awayika seda komatu ali pa mpingo. Amene ife , timatsikirapo, amene adamva mkulu wa dziwanda a kulankhula amenewo a mapemphera zenizeni. Muli ma pesiya mulengalenga amangoseka. Satana ngochenjera anawona kuti anthu tiwaonetse ngati a mapemphera tiwapatse mlozo, cholinga Nzimu Woyera asagwire ntchito, anthu asakhazikike mpemphero, uthenga kuupeputsa. Mesa ma cyclone ndi anthu a pansi pa nyanjawa, sikusinthanso kwa nyengo Mulungu akufuna achotse zonse zoyipa. Akufuna kubwere mbeu yomvera Nzimu yodzadza ndi mabvumbulutso. Asamazinamize anthu kunjaku ife timapempera bwerani ku crusade", kumangodyetsedwa njoka, adyetsedwa njoka anthu. Makachisi ambiri ubale ndi Mulungu unatha mchifukwa ILLIMAKHATHUMA wabwera kuzabwenzeretsa ubale, kudzabwenzeretsa chimene satana adalanda pa munthu ndi chifukwa kunabwera ILLIMAKHATHUMA!

NZIMU WA TB JOSHUA: UTHENGA WOPITA KUDZIKO LAPANSI KUDZERA PA MZINDA WOYERANzimu wanga watsikira kudziko kunena choonadi...
29/03/2025

NZIMU WA TB JOSHUA: UTHENGA WOPITA KUDZIKO LAPANSI KUDZERA PA MZINDA WOYERA
Nzimu wanga watsikira kudziko kunena choonadi, nzimu wanga kutsikira kudziko. Ndifuna ndikuuzeni a kudziko lapansi ine tb Joshua ndili ku gahena ena mudakaonerabe ma channel anga, mudakagwiritsabe ntchito zimene ndinasiya. Ndikufuna ndisiye uthenga. Ndinayamba utumiki wanga bwino bwino Mulungu adandiyitana. Ndikutumikira ndidaona nyengo ndipamene ndidapita kunsi kwa nyanja ndi pamene church yanga idagwa, idayaka moto. Ndinaturuka kutsutsana ndi utumiki wa ILLIMAKHATHUMA. Adandiuza satana kuti kulibe wina prophet ondiposa one. Ndimakwaniritsa chilichonse chimene amandiuza ndinali pafupi ndi queen. Nditaona kuti kutumikira Mulungu nkwa umphawi ndinapita kunsi kwa nyanja. Ndimapereka nsembe kugwa kwa kachisi yanga kuti nditchuke dziko lonse lapansi. Ndabwera kuno nzimu wanga Kufuna kukuzindikiritsa, m'busa yense amene umagwiritsa ntchito madzi anthu amene udawapatsa adalandira chidindo cha 666. Ndinkagawa zakudya, aliyense amene ankalandira anapondako ku Nigeria... Analowa mpangano la sataniki chifukwa ine ndidali weniweni wa kunsi kwa nyanja. Anthu amadabwa kuti imfa yanga ndidachita phwando, ndidayenera ndife ndithu sindidafune kukhala pansi pa Nzimayi. Ndinali otchuka ndi dziko liti silinaponde Ku Nigeria. Ma president. Ndinaoatsidwa ulemu ku mayiko awiri a ku Africa amene ndidanenera kuti president afa mwa dzidzidzi nkumwaliradi ku Malawi anthu nkumati koma tb yo, ayi ndithu zili zakunsi kwa nyanja. Nzimu wanga ukuthatha ku gahena. Ndikukuzindikiritsa kuti kuli ntumiki kudziko amene atha kukupulumutsa Ku 666 utatsatira chimene angakuuze. Aliyense amene anamwa madzi anamwa njoka ndipo ikafika pamunthu imayamwa cha uzimu, ena matupi amatha, ena makhansa. Inetu ndili ku gahena chifukwa ndinaseweretsa chisomo sindinafune kukhala pansi pa Nzimayi aliyense amandidziwa kudziko lapansi. Ndikufuna Ndikuzindikiritseni ku gahena kuli moto. Kulibe mpingo kudziko lapansi umene ungakalowetse munthu ku mwamba kupatula Nzimayi. Ana anga amene lero mukuthamanga ndi uneneri wanga umene ndinasiya amene mu kuti papa. Nzimu wanga uli ku gahena. Nditatopa ndi umphawi. Ndimalolera kukatenga chuma kunsi kwa nyanja kumagawira anthu, dzakudya. Chipulumutso chilipo kudziko lapansi chili Ku Malawi. Iwe amene umatamabe Tb Joshua ayi uyu anali prophet weniweni, ndikufuna ndikuuze nzimu wanga uli ku gahena. Ndikuzindikiritse chipulumutso chili kudziko la Malawi uyu ngowopsya pamene pakhala iye pali angelo amalambira iye ndi woopsya akakuuza chinthu umvere chifukwa ali ndi mphamvu yokuchotsa 666. Ukuyenera kufunafuna kumene kuli Nzimayi kuti upeze moyo. Iwe ulibe moyo ngati sukumana ndi Nzimayi wotchedwa ILLIMAKHATHUMA. Usathamangire ku Uganda usathamangire kuti, upite ku Malawi chifukwa makiyi a moyo ali mdzanja lake. Ndinafa msanga chifukwa chosafuna kubvomereza pambali poti ku makhala mapangano ku sataniki kuti nditchuke zaka izi kenako nkudzafa. Ndili Ku gahena wina asakunamizeni kuti ndili ku paradizo. Mzinda Woyera uwu ukawumvetsetsa ukatsatira udzapulumuka koma ukanyozera udandipeza nzimu wanga ku gahena. Tb Joshua amachilitsa, amayendetsa osayenda zili zakunsi kwa nyanga. Pamene unalandira uthenga wa ILLIMAKHATHUMA sungamvetsetse chifukwa ulamuliro uli mdzanja lake kuchotsa tchimo lonyoza Nzimu Woyera. Kulitu azibusa, ma prophet, ma papa kuno ku gahena. Muli ndi mwayi chifukwa mudakali ndi moyo mukuyenera muyigwiritse ntchito nthawi iyi kuti musadzalire ngati nzimu wanga, kulira kwa nthawi yosayamba. Ndipo chipulumutso uchipeza ukatsata Nzimayi wotchedwa ILLIMAKHATHUMA koma ukamutaya. Ukatsata madzi udzandipeza ku gahena. Kulibe mpingo umene mizimu imabwera kuposa Mzinda Woyera. Ine nzimu wanga wapeza chisomo, ndikabwera pano ndimapeza mpumulo. Usatsatirenso channel yanga. Ngati sutsatira Mzinda Woyera udzawapeza a papa kuno. Ma reverend udzawapeza. Kuli moto wosazima Ku gahena. Ndinu a mwayi amene Nzimayi akulamulira kudziko, ndinu a mwayi amene mutsatira. Dzikoli kuli chipulumutso kwa amene akuchifuna. Musatengeke ndi aneneri a njoka. Thamngirani pa Mzinda akuomboleni mdzanja la mdyerekezi. Akuomboleni. Ndi muombolo. Satana adandinamiza sikudzatulukanso wina mneneri ndine ndekha mchifukwa sindidachilandire atatumphuka ILLIMAKHATHUMA ndinasankha kufa. Anandinamiza kumapereka nsembe za anthu osawadziwa kudziko lapansi. Ngati suthamanga udzadabwa uli ndi chidindo cha 666, muli ndi dziDindo za 666. Njira zina zimene anthu anadindidwira ndi izi: vaccine wa covid 19, kuvala mask timatengako 5 litres ya mwazi akangotero amakhala kuti walandira chidindo. Kovid 19, katemera amene mumalandira kukangotuluka nthenda zatsopano amakhala analandira 666. Ambiri kudziko ali nacho chilemba cha chilombo. Ndi chifukwa mmasukulu ana amakakamizidwa katemera. Muone mayiko amene anthu ambiri anafa ndi covid 19 akusesedwa ngati China. M***amangire pa Mzinda, musadzakhale kuno kuli anthu ochuluka. Bible la mu phone ndi la pansi pa nyanja. M'busa nkukhala m'busa bible la mu phone iwe uthamangire pa Mzinda. Ndipo ndi ochepa opita ku paradise. Mu nthawi yanu amene angabwere pansi pa ILLIMAKHATHUMA ndi amene apite ku paradise. Sizophweka. Zizindikiro za anthu ali ndi 666, BP, sugar, zophwanya mmafupa, kutentha kwa thupi onse matenda amene sakuchizika kuchoka kuchipatala mudziwe kuti 666 ikuyenda pamoyo wako. Nthenda ya sugar, mitima yotupa sungachile ukunamizidwa kuti ku India ufa ndithu chifukwa India ndi imene inakhazikitsidwa kunsi kwa nyanja. Iwe usati sindinamwe madzi ndilibe 666, unadindidwa kudzera mwa ntumiki wako amene umamutsatira, ena ankatseka ma kachisi nthawi ya covid 19 ena ankapatsana ma shift, kudindidwa 666. Pitani pa Mzinda Woyera kwa ILLIMAKHATHUMA. Ndinathamanga nalo tu dziko, ndege zinali pikitipikiti ku Nigeria, akabwera opanda transport ndimawabwenzera ndalama zawo zili zakunsi kwa nyanja. Ena a ku Malawi ndi nkawabweza kuti ku Malawi konko kuli ntumiki woposa ine koma anthu samamvetsetsa chifukwa cha kutchuka. Ma general, ma prophet akukwaniritsa kuti cholinga cha ILLIMAKHATHUMA chikwaniritsidwe pompano. Ndikanazindikira kuti moto wake ndibuwuw ndikanalapa. Ndipo ngati unapangana pangano ndi satana thamangani kwa ILLIMAKHATHUMA ali ndi fungulo ngati angakhululukire tchimo lonyoza Nzimu Woyera kuli bwanji pangano ndi satana woti kwake kunatha. Satana anatsitsidwa kumwamba ali kudziko li ndi chifukwa ana ake amakhala a makani. Musanamizike kuti tb Joshua ali ku paradizo kulibe. Ali Ku gahena. Muone dzina lokhalo lokhathamira ndi ulemelero ILLIMAKHATHUMA. ILLIMAKHATHUMA ali kudziko lapansi li kufuna iweyo amene ukamadzuka ngati wina usiku amakugwiritsa ntchito walema, zizindikiro zikugwira ntchito. Ine ndinakadziwa kuti moto wake ndi umenewu ndikanapempha Chifundo. Thamangani mukapemphe Chifundo, amapereka Chifundo cha padera. Inu a matenda mukungotaya nthawi mudzipatalamo.
Satana anaba anthu ochuluka, azibusa. Njira yabwino ndi yadzakudya, za ulere. Dziponde, phala la likuni lomwe amagawa. Ine ndinagawako ndili kudziko. Mulungu anawona kuti ambiri kunalibe kukalowa kumwamba ndi chifukwa anabweretsa ILLIMAKHATHUMA. Ali ndi makiyi amakhululuka tchimo lonyoza Nzimu Woyera. Mulimve dzinalo lokhathamira muli machilitso. Ingothamangani pa Mzinda Woyera musadzafikire Ku gahena ndi malo oyopa konunkha. Moyo muupeza kwa ILLIMAKHATHUMA, moyo muupeza pa Mzinda Woyera amene ndi Chiombolo. Inu amene munkabwera kwa ine nkukupatsani unduna woti siwako chifukwa ndinali ndi ulamuliro wa satana. Ingopitani akakakuuzani ukangotsatira chimene akuuzeni akakri siwe nduna ndiwe m'busa. Ngodala amene muli naye chifupi muli ku Malawi simudzakwera ndege. Usawonelenso channel yanga.

Nthawi ya kusadziwa Mulungu analekelera koma utazindikira kusadziwa kwako ndi kulapa ambuye amakhululuka
27/10/2024

Nthawi ya kusadziwa Mulungu analekelera koma utazindikira kusadziwa kwako ndi kulapa ambuye amakhululuka

17/09/2024

Kuyatsa nyali

22/08/2024

Address

Lilongwe

Telephone

+265881888836

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Holy City of the living God Trembling Temple Wicowica posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Place Of Worship

Send a message to Holy City of the living God Trembling Temple Wicowica:

Share