Seventh day adventist Chitala church

Seventh day adventist Chitala church Afilipi 4:4 Kondwelani mwa ambuye nthawi zonse kotero ndibwerezanso kondwerani.

05/06/2026

HAPPY SABBATH

28/05/2026
17/05/2026

Big shout out to my newest top fans! Adam Golden, Thomas Likome, Elizah Madi

27/04/2026

MULUNGU SADZAKUIWALANI

09/04/2026

CHIVUMBUKUTSO 3 vs 29- 22.
Onse amene ndiwakonda, ndiwadzudzula ndi kuwalanga, potero chita changu, nutembenuke mtima. Taona, ndaima pakhomo, ndigogoda wina akamva mau anga nakatsegula pakhomo, ndidzalowa kwa iye, ndipo ndidzadya naye, ndi iye ndi lne. Iye wakulakika, ndidzampatsa akhale pansi ndi lne pa mpando wachifumu wanga, monga lnenso ndinalakika, ndipo ndinakhala pansi ndi Atate wanga pa mpando wachifumu wake. Iye wakukhala nalo khatu amve chimene Mzimu anena kwa Mpingo. Mulungu akudalitseni pamene mukulingalira mau amenewa. Amen!!!

07/04/2026

Mu zikambirana za dzulo pa counseling m’busa Orlac Mozalande anaphunzitsa ophunzira pa kutu wakuti “SMART – How to live a successful life in youthhood.”

M’mawu ake, m’busayu anatsindika kuti kukhala opambana mmoyo ndi chisankho. Iye anafotokoza kuti munthu akhoza kusankha kukhala wosauka kapena wopambana potengera zisankho zake za tsiku ndi tsiku.

Abusa a Mozalande analangiza achingamata kuti akuyenera kutsatira mawu oti SMART motere:

S – Select friends wisely (Sankhani abwenzi mwanzeru)
Achinyamata analangizidwa kusankha abwenzi omwe ali ndi malingaliro abwino komanso amene angathandize kukweza tsogolo lawo. Ananenanso kuti pali anthu a great minds, average minds, ndi low minds, choncho kusankha bwino abwenzi n’kofunika kwambiri.

M – Manage time (Gwiritsani ntchito bwino nthawi)
Nthawi inafotokozedwa ngati moyo komanso ndalama. Munthu aliyense ayenera kukhala ndi dongosolo la tsiku ndi tsiku (timetable) ndi kupewa kuwononga nthawi pa zinthu zopanda phindu. Ananenanso kuti kusagwiritsa ntchito bwino nthawi kumabweretsa kulephera mmoyo.

A – Attention to urgent and important matters
Achinyamata ambiri amalakwitsa posadziwa choyenera kuchita choyamba. M’busayu ananenanso kuti zinthu monga maphunziro sizingadikire, pamene zina monga banja zingadikire. Kusankha bwino zofunika kuchita pa nthawi yake kumathandiza kupambana.

R – Respect (Kulemekeza)
Ulemu unatchulidwa ngati chinsinsi chachikulu cha kulumikizana (connections). Achinyamata analangizidwa kulemekeza aliyense chifukwa tsogolo limadalira mmene munthu amachitira anzake. Kusowa ulemu kungalepheretse munthu kupeza ntchito, ubwenzi wabwino, kapena mwayi wina wabwino.

T – Tell God in prayer

KUKHALA MU PEMPHEROPa tsiku lachiwiri la Youth Week of Prayer wa Seventh-day Adventist Church, achinyamata ochokera ku B...
06/04/2026

KUKHALA MU PEMPHERO

Pa tsiku lachiwiri la Youth Week of Prayer wa Seventh-day Adventist Church, achinyamata ochokera ku Balaka East, Balaka North komanso Balaka Main asonkhana popitiriza kumva mawu a Mulungu.

Ulaliki unalalikidwa ndi m’busa Orlac Mozalande pa mutu wakuti “Prayer in Action” (Pemphero pa Kuchita).

M’busayu anafotokoza kuti Yesu ndi chitsanzo pa moyo wa pemphero, potengera Marko 1:35 pamene ankadzuka m’mawa kupemphera.

Iye ananenanso kuti pemphero ndi njira yolumikizirana ndi Mulungu, komwe timapereka zosowa ndi nkhawa zathu.

Achinyamata analimbikitsidwa kukhala okonda pemphero chifukwa moyo wopambana umafunikira kulumikizana ndi Mulungu. Zinthu zonse monga sukulu, ntchito, ndi bizinesi ziyenera kuyikidwa mu pemphero kuti zipambane.

M’kulimbikitsa, anatchula zitsanzo za Nehemiya ndi Danieli, omwe anapemphera n’kupeza mayankho kwa Mulungu. Izi zikuwonetsa kuti zimene munthu sangathe, Mulungu amatha, ndipo pemphero limathandiza kukwaniritsa zolinga.

Pomaliza, abusa anatsindika kuti pemphero liyenera kuphatikizidwa ndi zochita. Achinyamata ayenera kugwira ntchito limodzi ndi kupemphera, chifukwa kupambana kwawo kuli mu kudalira Mulungu.
Msonkhanowu ukupitirirabe mpaka Sabata lomwe likubwerali.

Wolemba:
Esau Banda
.

KHALANI A SODZI A ANTHUAchinyamata mu mpingo wa Seventh-day Adventist Church, m’boma la Balaka ochokera ku Balaka East, ...
05/04/2026

KHALANI A SODZI A ANTHU

Achinyamata mu mpingo wa Seventh-day Adventist Church, m’boma la Balaka ochokera ku Balaka East, Balaka North komanso Balaka Main Church.Lero pa 5 April 2026,awalimbikitsa kusiya za dziko ndi kukhala asodzi a anthu.

Uthengawu unaperekedwa ndi Pastor Orlac Mozalandi, abusa ochokera mu chigawo Cha Namwera, pa kutsegulira Youth Week of Prayer yomwe ikuchitikira pa Balaka Main Seventh-day Adventist Church.

Polalikira pa mutu wakuti “ *Kukhala Msodzi wa Anthu* ,” abusawa anawerenga m’buku la Uthenga Wabwino malinga ndi Marko 1:16–17, pomwe Yesu anayitana anyamata kuti asiye ntchito zawo n’kumutsatira kuti akhale asodzi a anthu. Iwo anafotokoza kuti Mulungu amaitana aliyense wokonzeka, ndipo achinyamata ayenera kutumikira Iye kulikonse komwe ali monga m’sukulu, kuntchito kapena m’malonda.

Komabe, ananenetsa kuti zimenezi sizingatheke popanda kuwerenga Baibulo ndi kupemphera nthawi zonse.
Anachenjezanso achinyamata kuti apewe zochita zoipa monga kugwiritsidwa ntchito pa ndale ndi zinthu zopanda pake, ndipo analimbikitsa kuti ino ndi nthawi yabwino yoyamba kutumikira Yesu.

Msonkhanowu ndi wa masiku 7 ndipo udzatha Loweruka lomwe likubwerali,lomwe ndi tsiku Sabata.

Wolemba :
Esau Banda
.

Address

Along Nkhotakota
Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Seventh day adventist Chitala church posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share