Tonse Okhulupilira Mulungu Timve Mawu A Mulungu Pano

Tonse Okhulupilira Mulungu Timve Mawu A Mulungu Pano Kutengera anthu Mu Umfumu Wa Mulungu

19/05/2026

Uthenga Wa Chipulumutso

Ndikudziwa Kuti Inuyo Mukupita Ku Church Mwina Simujombaso Komaso Mawu a Mulungu Mukuwadziwa Kwambiri Ena Amakuitanani A Khristu Mwina Ena Akuitana inuyo Kuti Atsogo Ena Ndinu Abusa Kumene Koma Muli Ndi Vuto La NTCHIMO Ubale Wanu Ndi Mulungu Sulibwino.

Mukudziwa Abale Kuti CHOLINGA Cha Mulungu Sikuti inuyo Mudzipedzeka Malo Opemphereramo Okha Ayi Tiyende Mu Chiyero Molemekedza Mawu Ake Kuti Tikhare Nawo Moyo Osatha Tione Mawuwa

2 Timoteyo 3:1-4

Koma dziwa izi: Mʼmasiku otsiriza kudzafika nthawi zoopsa kwambiri.

Anthu adzakhala odzikonda, okonda ndalama, odzitama, onyada, achipongwe, osamvera makolo awo, osayamika, wopanda chiyero.

Adzakhala wopanda chikondi, osakhululuka, osinjirira, osadziletsa, ankhanza, osakonda zabwino,

opereka anzawo kwa adani awo, osaopa zoyipa, odzitukumula, okonda zowasangalatsa mʼmalo mokonda Mulungu.

Adzakhala ndi maonekedwe achipembedzo koma mphamvu yake ndi kumayikana. Anthu amenewa uziwapewa.

Tikuona Mumawu Awa Akunena Za Matsiku Otsilidza Zonse Akunena Mawuwa Zikuchitika Matsiku ano Anthu Adzakhala Okonda Ndalama So Muone panopa Ena Asanduka ma h**e Chifukwa Cha Ndalama Ena kujoina Satanic Chifukwa Cha Ndalama Muzonse Pali Mawu Awa
2 Timoteyo 3:5
Adzakhala ndi maonekedwe achipembedzo koma mphamvu yake ndi kumayikana. Anthu amenewa uziwapewa.

Tonse Tichenjere Ndi Mawu Awa Kukhala Ndi maonekedwe Achipembedzo Koma Kuyikana MPHAMVU yake Zoona Akhristu omwa mowa Akhristu Ochita Chigololo MKAZI wake alinaye Koma kumayendaso Ndi Wamwini wake Akhristu opita ku church Atamvala kolekedzera mu Nchafu KODI NDI MTUNDU WANJI WA AKHRISTU ABADO UNO OCHITA ZOIPA?

CHOKANIKO KU NTCHIMO KHALANI AKHRISTU WOONA MTIMA OTI AMBUYE YESU AKAMATIONA ADZIKONDWERA NAFE.

CHOKANIKO KUKHALA AKHRISTU ABODZA.

12/05/2026

OLEMERA Kapena WACHUMA KOMA OSAUKA MZIMU

Ndinaona Mawu Mubuku La Chivumbulutso 3:17-19
Iwe umati: ‘Ndine wolemera, ndine wachuma ndipo sindisowa kanthu.’ Koma sudziwa kuti ndiwe wovutika, womvetsa chisoni, waumphawi, wosaona ndi wamaliseche.

Ndikukulangiza kuti ugule kwa Ine golide woyengedwa ndi moto kuti ukhale wolemera. Ugule zovala zoyera kuti uvale ndi kuphimba umaliseche wako wochititsa manyaziwo. Ndiponso ugule kwa Ine mankhwala a mʼmaso kuti uwone.

Amene ndimawakonda ndimawadzudzula ndi kuwalanga. Choncho chita changu ndipo lapa.

Mu Mawu Ali Pa Mwambawa Tikuona Ambuye Wathu Yesu Khristu Akunena Nafe Kuti Anthu Akamationa Amationa ngati ndife OLEMERA KAPENA A CHUMA KOMA AMBUYE YESU Akamationa Amationa Kuti Ndife OSAUKA. Zomvetsa Chisoni Izi

Tikamakhala Padziko pano Mulungu kumatidalitsa kumakhala nazo Zose tidzifuna AMACHITA NDI CHOLINGA KUTI MWINA TIKAONA CHIKONDI CHAKE IFESO TILAPE NDIKUKHALA MOYO OKONDWERETSA MULUNGU
Koma Ee Ndi Pamene Tikuona ngati Mulungu Atidalitsa Kuti Tikamwere mowa, tidzikachita Zibwezi Inu Satana Akukutengerani Ku Chionongeko Chonde Onani Ndi Kudzindikira Kuti Mulungu AMATIKONDA Tisiye Moyo WA Uchimo Tikhare moyo Okondweretsa Mulungu.

So Tilingalire Mawuwa Abale Mozama Kumakhala nazo Zose Koma Kusowekera U MULUNGU Pa Moyo wanu Nde Ndinu Omvetsa Chisoni INU Talingalirani Za Yobu Anali OLEMERA KOMA OMUOPA MULUNGU KUYENDA MU CHIYERO Yobu 1:1,3
Mʼdziko la U*i munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.

ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.

So Satana Asakunamidzeni Kuti Mukakhala NDI CHUMA Simungayende Muchiyero

So Kukhala Ndi Zonse Koma Kusowekera U MULUNGU NDINU A TSOKA KWA MULUNGU NDINU OMVETSA CHISONI
Kwa Anthu Ndinu Abwana Ee Ndinu Olemekedzeka Koma Kwa Mulungu Ndinu Ovutika aumphawi Omvetsa Chisoni

Nde Pali Enaso Ndife OSAUKA Kuthupi Ndithu Koma Kusowekera U MULUNGU Nde Ndife Atsoka TSOKA Zedi

Kuthupi Chuma Chavuta Kumbalitso Ya Mulungu Yavutaso Eee Ndekuti Ndinu Angozi Ngozi

NKHANIYI NJAKUTI TITEMBENUKE MTIMA TILAPE TISIYE MACHINO

Chivumbulutso 3:18-19
Ndikukulangiza kuti ugule kwa Ine golide woyengedwa ndi moto kuti ukhale wolemera. Ugule zovala zoyera kuti uvale ndi kuphimba umaliseche wako wochititsa manyaziwo. Ndiponso ugule kwa Ine mankhwala a mʼmaso kuti uwone.

Amene ndimawakonda ndimawadzudzula ndi kuwalanga. Choncho chita changu ndipo lapa.

Khalani osimikidzika mtima Kuti Mulungu AMATIKONDA Lapani Tikalowe Mu Umfumu Wakumwamba

Ambuye Akudalitseni Nose Zikomo

11/05/2026

TISITHE MULINGO WA CHIKHULUPILIRO MWA AMBUYE WATHU YESU

Tikapanga chisakho Choyenda Ndi Ambuye Wathu Yesu Khristu Mayesero Ngochuluka Koma Mawu anena Kuti

Mateyu 10:22
Anthu onse adzada inu chifukwa cha Ine, koma iye amene apirira mpaka kumapeto, adzapulumuka.

Mateyu 24:11-13
ndipo aneneri onama ambiri adzaoneka ndi kunyenga anthu ambiri.

Chifukwa cha kuchuluka kwa zoyipa, chikondi cha ambiri chidzazirala,

koma wopirira kufikira chimaliziro adzapulumuka.

Tikuona Mu Ma chaputawa Kuti Amene Adzapulumuka Ndi Amene Adzapilira Mpaka Chimaliziro So Ifeyo Monga A Khristu tikuyenda Bwanji?

Ndi Ntchimo Lanji Limene Tikukanika Kulisiya Limene Latikakamira Kuti litifikitse ku Chionongeko.

Simunachedwe Ayi Mene Mukumva Uthengawu Utifikise Kukutembenuka mtima koona Yesu natifera Kuti Ife Tikhare Nawo Moyo Osatha Komaso Tiyende Mu Chiyero.

Chokaniko ku khala Khristu Ophatikiza Pena Mupephere Pena Kunyengaso Azimayi A mpingoso momo Ayi Satana tikane Pa Moyo Wathu

Khalani Okhulupilika Mpaka Chimaliziro Kuti Tikapulumuke

Ambuye Akudalitseni Nose Zikomo

09/04/2026

CHENJENZO

Nthawi Ikupita Koma Tikuti Ife OKHULUPIRIRA YESU KHRISTU Pamene Tikuyendabe Mu Uchimo Ku 2 Timoteyo 3:1-5 Akuti

Koma dziwa izi: Mʼmasiku otsiriza kudzafika nthawi zoopsa kwambiri.
Anthu adzakhala odzikonda, okonda ndalama, odzitama, onyada, achipongwe, osamvera makolo awo, osayamika, wopanda chiyero.
Adzakhala wopanda chikondi, osakhululuka, osinjirira, osadziletsa, ankhanza, osakonda zabwino,
opereka anzawo kwa adani awo, osaopa zoyipa, odzitukumula, okonda zowasangalatsa mʼmalo mokonda Mulungu.
Adzakhala ndi maonekedwe achipembedzo koma mphamvu yake ndi kumayikana. Anthu amenewa uziwapewa.

So Tikuona Umu Za Matsiku Otsiliza Za Makhalidwe Amene Anthu Adzakhala Nawo Apa Tikuchenjedzedwa Kuti Tidziyendabe Mu Chiyero Osati Kukhala ndi Maonekedwe Achipembedzo Mphamvu Yake Titayikana Iyayi Zokhumba Zathu Zongokondweretsa Thupi Zakathawi Kochepa Chilango Chake Chamuyaya Sibwino Kumachimwa Choonadi Mukuchidziwa Ndi Chifukwa AHEBERI 10:26-31

Ngati ife tipitirira kuchimwa mwadala pamene tikudziwa choona, palibenso nsembe ina imene ingaperekedwe chifukwa cha machimo athuwo.

Koma kumangodikira kokha ndi mantha chiweruzo ndiponso moto woopsa umene udzawononga adani a Mulungu

Aliyense amene amakana malamulo a Mose amaphedwa popanda nʼchifundo chomwe, malingana pali mboni ziwiri kapena zitatu.

Koposa kotani nanga ululu wachilango chimene adzalandire munthu amene amapeputsa Mwana wa Mulungu, amene amayesa magazi a pangano, amene anamuyeretsa, kukhala chinthu chodetsedwa, ndi kunyoza Mzimu wachisomo?

Pakuti timadziwa amene anati, “Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.” Iye anatinso, “Ambuye adzaweruza anthu ake.”

Nʼchinthu choopsa kugwa mʼmanja a Mulungu wamoyo.

CHENJENZO Kwa Ifeyo Ndi Limeneli Sitinadziwe Choonadi Kuti Tidzipitilidzabe Kumachimwa Iyayi Ndi Nthawi Yoyenda Muchiyero Monga Mawu Anena Ndi Koopsa Kugwa Manja A Mulungu Wamoyo Akutiso Moto Oopsa Udzawaononga Adani A Mulungu Amene Sachita Chifuniro Chake.

Ndinaona Chinachake Ku Aefeso1: 4-6 ZA CHIKONDI CHACHIKULU CHA MULUNGU PA IFEYO

Dziko lapansi lisanalengedwe, Mulungu anatisankhiratu mwa Khristu kuti tikhale oyera mtima ndi wopanda cholakwa pamaso pake. Mwa chikondi chake,

Iye anakonzeratu kuti ife titengedwe ngati ana mwa Yesu Khristu, molingana ndi kukonda kwake ndi chifuniro chake.

Anachita zimenezi kuti tiziyamika ulemerero wa chisomo chake, umene watipatsa kwaulere mwa Khristu amene amamukonda.

Tikuona Kuti Mulungu Chifuniro Chake Choti Ifeyo Tikhale Oyera Mtima Tiyende Mokondweretsa IYE

AMBUYE AKUDALITSENI KOMA PANGANI SHARE CHONDE

03/04/2026

Atate Mudzina La Yesu Ndikupemphani Kuti Mu Tipatse Mzimu Wakumvetsetsa Mawu Anu Kuti Tikathe Kukula Moyo Wathu Wa Umzimu Ndi Kusitha Mulingo Wachikhulupiriro Ndipempha Mudzina La Yesu Amen.

Ndinali Pheee Kulingalira Za Umfumu Wakumwamba Maka Pa Chaputa Cha Mateyu 7:13-14
Pali Mawu Awa Inuso Lingalirani Kwambiri Tiudzeni Pokometa

Mateyu 7:13-14
“Lowani pa chipata chopapatiza. Pakuti chipata cholowera kuchiwonongeko nʼchachikulu ndipo msewu wake ndi waukulunso. Ndipo anthu ambiri amalowera pamenepo.

14 Koma chipata ndi chopapatiza ndi msewu ndi waungʼono umene utsogolera anthu ku moyo wosatha ndipo ndi owerengeka okha amene ayipeza njirayo.

Mwaona Mawuwa Sopano Pali Zipata Ziwiri

Choyamba Cholowera Kuchionongeko Ichiso Akuti Chachikulu Ndipo Anthu Ambiri Akulowa Pamenepo

Chachiwiri Chipata Chopapatiza Koma Cholowera Ku Moyo Wosatha Ndipo ndi Anthu Owerengeka Ayipeza Njirayo

Funso Kumati Chifukwa Chani Anthu Ambiri Akulowa Pa Chipata Chonka Ku Chionongeko? Chifukwa Iwo Akusatira Zokhumba Mtima Wawo Zosangalasa Thupi Lawo Monga Chigololo Munthu Wokwatiwa Kumayenda Ndi Enaso Kumati Kusangalala Zanga Walowa pa Chipata Chonka Ku Chionongeko Kupha Munthu Zako Kamba Ka Chuma Kudzikonda Inuyo Muka Ku Chionongeko Ndithu Mukamakhala Moyo Osasamala za Mulungu Ziwani mukako ndi Ku Chionongeko.

Chifukwa Chani Chipata Cholowera Ku Moyo Osatha Chili Chopapatiza?
Chifukwa Munthu Sakhala Moyo Wokondweretsa Iye Mwini Ayi Koma Moyo Wokondweretsa Mulungu Ndicho Chifukwa Yesu Anati
Luka 9:23-24
Ndipo Iye anawuza onse kuti, “Ngati wina aliyense akufuna kutsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kusenza mtanda wake tsiku ndi tsiku nʼkumanditsata Ine.

Popeza aliyense amene akufuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene adzataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupulumutsa.

Mwaona Abale Sizoti Kumakhala Moyo Monga Mufunira Kumati Muli Mwa Ambuye YESU Iyayi Kanidzani Moyo Wanu Kudzadziko Lapasi Khalani Moyo Wochita Chifuniro Cha Ambuye Yesu Pakuti IYE Anafa Kuti Ifeyo Tidzikhala Moyo Wachiyero.

Gawani Chonde Gawani Uthengawu
Ambuye Yesu AKUDALITSENI Nonse Amen.

29/03/2026

KUDZIWA MULUNGU

Danieli 11:32
Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, KOMA anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika Mtima Nadzachita Ndi Mphamvu

Mongaso Daniel Pakuti Anadziwa Mulungu Amene Amamtumikira Sanalambire Fano KOMA Mu M'malo Mwake Analambira Mulungu Sanachitematha Ndi Mikango Ayi.

So Kodi Inuyo Mukudziwa Mulungu Wanu?
Yankho .....................

Ngati Mukudziwa Tiyeni Tikhare Moyo Okondweretsa Iye
1 Petro 1:15-16
15 Koma monga amene anakuyitanani ndi woyera, inunso khalani oyera mtima mʼmakhalidwe anu wonse.

16 Pakuti, kwalembedwa kuti, “Khalani oyera mtima, chifukwa Ine ndine Woyera.”

Mudziwe Kuti Chiyero Chotiyeneredza Kukalowa M'malo Otatulika a atate Wakumwamba pakuchita Chifuniro Chake.

ZIKOMO AMBUYE AKUDALITSENI

29/03/2026
04/03/2025

Chonde tikhare okhulupilika pa maso a Mulungu nthawi zonse Pakuti Mawu anena Kuti

Chivumbulutso 2
25 Inu mungogwiritsa zimene munaphunzira basi, mpaka Ine ndidzabwere.

26 Amene adzapambana ndi kuchita chifuniro changa mpaka kumapeto, ndidzamupatsa ulamuliro pa mitundu yonse ya anthu.

27 Adzayilamulira ndi ndodo yachitsulo ndipo nadzayiphwanyaphwanya ngati mbiya. Ulamuliro umenewu ndi omwe ndinalandira kwa Atate anga.

28 Ine ndidzamupatsanso nthanda, nyenyezi yowala mʼmamawa ija.

So khalanibe chikhulupiliriro ndi kukhulupilika Kwa Atate Mwini Moyo

29/12/2024

Aroma 8:8

Ndipo anthu amene amalamulidwa ndi khalidwe lauchimo sangathe kukondweretsa Mulungu.

Tikhare Okhulupirika Pa Maso A MULUNGU Ndi Ochita mawu Ake Kuti Tipambane
03/12/2024

Tikhare Okhulupirika Pa Maso A MULUNGU Ndi Ochita mawu Ake Kuti Tipambane

Address

Nyungwe
Karonga

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Tonse Okhulupilira Mulungu Timve Mawu A Mulungu Pano posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share