13/05/2024
TISAMAIWALE IZI AKATOLIKA ANZANGA MMAWA ULIWONSE
👇🏼👇🏼👇🏼👇🏼👇🏼
✝
PEMPHERO LA M'MAWA.
Mulungu wanga, ndipereka kwa inu, ndi chithandizo cha Maria Woyera, zanga zonse , ntchito zonse ndidzazichita lero lomwe, ndi mafuno ndi maganizo anga onse.
Ndifunitsa kuchita kufuna kwanu kokha. Mundithandize kufikira nthawi yogona.
Amen 🙏
✝
ATATE ATHU
Atate athu muli m'mwamba dzina lanu liyeretsedwe ufumu wanu udze, kufuna kwanu kuchitidwe , monga kumwamba choncho pansi pano.
Mutipatse ife lero chakudya chathu cha lero, mutikhululukire ife zochimwa zathu monga ifenso tikhululukira adani athu, musatisiye ife m'chinyengo, koma mutipulumutse ife kwa zoipa.
Amen 🙏
✝
KUMVERA KWA APOSTOLI.
Ine ndimvera Mulungu Atate amphamvuzonse, amene adalenga dzilo lakumwamba ndi Dziko lapansi pino, ndipo Yesu Khristu , Mwana yekha, Ambuye athu amene adaikida m'mimba ndi Mzimu Woyera, nabadwa mwa Maria Virgo, adasauka kwa Ponsio Pilato, adampachika pamtanda adamwalira, adamuika m'manda, adatsikira kwa akufa, ndipo tsiku lachitatu lake adauka kwa akufa, adakwera Kumwamba, ndipo akukhala ku dzanja lamanja lA Mulungu Atate amphamvuzonse, adzafumira ko.weko kudzaweruka amoyo ndi akufa.
Ndimvera Mzimu Woyera, Eklezia Katolika Woyera, chiyanjano cha anthu oyera, chikhululukiro cha machimo, thupi lidzauka, ulipo moyo wosatha.
Amen. 🙏
✝
TIKUONENI MARIA
Tikuoneni Maria wachaulere chodzaza, Ambuye ali nanu, ndinu wodala kopambana akazi onse, ndipo ngodalanso Mwana wanu Yesu.
Maria Woyera, Amai a Mulungu, mutipempherere ife ochimwa, tsopano ndiponso pa nthawi ya kufa kwathu.
Amen 🙏
✝
KULAPA
Mulungu wanga, ndilapa, ndileka zakwaipa zanga zonse, chifukwa ndinu wabwino ndi wokondeka ndithu ndi wolanga anthu ochimwa.
Mundithandize ndi chaulere chanu kuti ndisachimwenso.
Amen 🙏
✝
KUMVERA
Mulungu wanga ndimvera mau anu onse, monga *Eklezia Katolika* awamvera, nawaphunzitsa, ndimvera iwo chifukwa ndinu Mulungu woona ndipo *Eklezia* wanu sangathe