Radio Maria Malawi

Radio Maria Malawi RADIO MARIA is a broadcasting initiative, which was started in Italy by a group of Catholics, both priests and lay people. The radio is not commercially funded.

It aims at spreading the Good News of Jesus Christ to all people of good will.

Ndalama zokwana 35 million Kwacha ndi zomwe zinapezeka pa Mwambo wa Diner and Dance Gala ndinso fundraising yomwe inakon...
25/05/2026

Ndalama zokwana 35 million Kwacha ndi zomwe zinapezeka pa Mwambo wa Diner and Dance Gala ndinso fundraising yomwe inakonzedwa ndi gulu la Association of Former Catholic Seminarians mu mzinda wa Blantyre.

Ndalamazi zomwe ntchito yake ndi kulipilira anyamata omwe ali ndi khumbo lodzakhala ansembe ndipo pano ali m'sukulu zikuluzikulu zosulira ansembewa, zikuyembekezeka kukaperekedwa ku likulu la mpingo wa Katolika mdziko muno a Malawi Conference of Catholic Bishops (MCCB).

Mlangizi wa gululi Monsignor Henry Chikanda ati ndi okhutira ndi mmene gululi likugwilira ntchito zake kaamba koti pali kusintha kwakukulu kuchoka pa mmene gululi linayamba ntchitoyi pomwe chaka choyamba linapeza 2 million kwacha, chaka chotsatira chomwe ndi cha 2025 anapeza 10 million kwacha ndipo pano ndalamayi yakwera.

Wapampando wa gululi Dr. Maxon Ngochera wayamikira mamembala a gululi ndi onse akufuna kwabwino omwe anatengapo mbali ndi kuthandizira kuti apeze ndalamazi.

25/05/2026
Nsembe ya Ukarisitia yotsanzikana ndi malemu bambo Samuel Nawasha, ukuchitika mu tchalitchi la Zomba Cathedral.Usanayamb...
25/05/2026

Nsembe ya Ukarisitia yotsanzikana ndi malemu bambo Samuel Nawasha, ukuchitika mu tchalitchi la Zomba Cathedral.

Usanayambike mwambo-wu kunachitika mwambo owona nkhope.

Misa imeneyi akutsogolera ndi episkopi wa dayosizi ya Zomba, Ambuye Alfred Mateyu Chaima mothandizidwa ndi aepiskopi enanso omwe afika pa mwambowu omwe ndi wa arkidayosizi ya Blantyre, Ambuye Thomas Luke Msusa, wa dayosizi ya Mangochi, Ambuye Montfort Stima komanso wa dayosizi ya Mzuzu, Ambuye Yohane Suzgo Nyirenda.

Bambo Nawasha anamwalira m'mawa wa loweruka pa 23 May 2026.

Episkopi wothandizira mu arkidayosizi ya Lilongwe, Ambuye Vincent Mwakhwawa, wayamikira ansembe a chipani cha Missionary...
25/05/2026

Episkopi wothandizira mu arkidayosizi ya Lilongwe, Ambuye Vincent Mwakhwawa, wayamikira ansembe a chipani cha Missionary Community of St. Paul the Apostle (MCSPA) omwe akuyendetsa parishi ya St. Mary's Benga ku Nkhotakota mu arkidayosiziyo, kaamba ka ntchito yaikulu imene akugwira yotukula parishiyo.

Iwo ayankhula izi mkati mwa ulaliki wawo pa nsembe ya Ukaristia yomwe ili mkati padakalipano yokondwelera kuti parishiyo yakwanitsa zaka khumi ndi zitatu (13).

Pa Misa imeneyi, akhristu okwana 155 akuyembekezeka kulandira sakramenti la Ulimbitso.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Jane Ansah watsindika za kufunika kotsamira pa pemphero nthawi zonse.Dr Ansah ...
24/05/2026

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Jane Ansah watsindika za kufunika kotsamira pa pemphero nthawi zonse.

Dr Ansah amayankhula izi lero ku tchalitchi la Soche CCAP mu mzinda wa Blantyre komwe tchalitchilo limakondwelera kuti lakwanitsa zaka 30 kuchokera pomwe linachita ubale ndi tchalitchi la Shadysine la mdziko la America.

Mayi Ansah ati pemphero limayankha mafunso onse amene amakhala m'moyo wa munthu.

Parishi ya St. Patrick's Area 18 mu arkidayosizi ya Lilongwe yati loweruka likudzali pa 30 May 2026 ikhala ndi chikondwe...
24/05/2026

Parishi ya St. Patrick's Area 18 mu arkidayosizi ya Lilongwe yati loweruka likudzali pa 30 May 2026 ikhala ndi chikondwelero chakuti yakwanitsa zaka 50 chiyikhazikitsireni.

Poyankhulapo pa msonkhano wa atolankhani pomwe amafotokozera momwe zokozekera za chikondwelerochi zikuyendera, bambo mfumu wa parishiyo Bambo Kennedy Malemia ati chilichonse chili mchimake ndipo apempha onse omwe adatumikirako ku parishiyi monga ansembe, asisteri ndi akhristu eniake kuti adzakhale nawo pa mwambowu.

Iwo ati mu zaka makumi asanu zimenezi, pali zambiri zomwe zachitika pofuna kufalitsa uthenga wabwino kuphatikizapo kutsekula sukulu ya m'meram'poyamba kwa Kauma ngati njira imodzi yofuna kutukula ntchito za maphunziro.

Parishi ya St. Patrick's Area 18 yomwe inakhazikitsidwa mchaka cha 1976, ili ndi nthambi zake ziwiri zomwe ndi St. Paul Kauma komanso St. Cecilia Mgubo ndipo padakalipano parishiyo ili ndi akhristu oposa 4,500.

Akhristu okwana 182 lero akuyembekezeka kulandira sakramenti la Ulimbitso ku parishi ya Mtima Woyera mu arkidayosizi ya ...
24/05/2026

Akhristu okwana 182 lero akuyembekezeka kulandira sakramenti la Ulimbitso ku parishi ya Mtima Woyera mu arkidayosizi ya Lilongwe.

Amene akutsogolera Misa yopereka sakramentili ndi episkopi wothandizira mu arkidayosizi ya Lilongwe, Ambuye Vincent Mwakhwawa.

Unduna owona kuti pasakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo, ana, ulumali ndi chisamaliro cha anthu, wati upitilira ...
23/05/2026

Unduna owona kuti pasakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo, ana, ulumali ndi chisamaliro cha anthu, wati upitilira kuwonetsetsa kuti boma likupereka chisamaliro ndi chitetezo chokwanira kwa atsikana kuti athe kuchita bwino pa maphunziro.

Nduna mu undunawu mayi Mary Navitcha ayankhula izi lero pomwe anali mlendo wolemekezeka pa mwambo wokondwelera kuti sukulu ya sekondale ya atsikana ya Our Lady of Wisdom yomwe ili ku Limbe mu mzinda wa Blantyre, yakwanitsa zaka 105 chiyikhazikitsireni.

Pa mwambo omwewu, sukuluyi imakhazikitsanso ntchito yotolera thandizo la ndalama zosachepera 200 million kwacha zoti amangire chipinda chowerengera ndi kusungira mabuku ndinso kugula bus yomwe ophunzira pa sukuluyi adzigwiritsa ntchito.

Pamenepa iwo ati boma layika kale ndondomeko zomwe zikuwonetsetsa kuti atsikana alandire ufulu wawo wa maphunziro.

Wapampando wa komiti yoyendetsa ntchito za sukuluyi a Ignacious Banda alimbikitsa onse omwe anaphunzillrapo pa sukuluyi kuti atengepo mbali pothandiza ntchitoyi chifukwa kutero kuthandiza kuchepetsa ena mwa mavuto omwe ana amakumana nawo.

Sukulu ya Our Lady of Wisdom anayikhazikitsa mchaka cha 1921 ndipo imayendetsedwa ndi asisteri a chipani cha Daughters of Wisdom.

A Francis Haiya ndi omwe ayimire ngati phungu wa chipani cha Democratic Progressive (DPP) mdera la Machinga Mikoko, pots...
23/05/2026

A Francis Haiya ndi omwe ayimire ngati phungu wa chipani cha Democratic Progressive (DPP) mdera la Machinga Mikoko, potsatira kupambana kwawo pa chisankho chachipulula chomwe chachitika lero ku deralo pomwe agonjetsa anthu ena asanu ndi anayi.

Iwo apeza mavoti 144, a Ali Chioko apeza 61, a Blessings Hoppos apeza 1, a Lucius Taipi Hoshiwa apeza 18 ndipo a Ishmael Japan apeza 56.

Chisankho cha aphungu chidzachitika mdera la Mikoko m'boma la Machinga pa 30 June, 2026 potsatira imfa ya yemwe anali phungu wa deralo, a Jafali M***a.

Mwambo wokondwelera kuti sukulu ya sekondale ya atsikana ya Our Lady of Wisdom yakwanitsa zaka 105 chiyikhazikitsireni, ...
23/05/2026

Mwambo wokondwelera kuti sukulu ya sekondale ya atsikana ya Our Lady of Wisdom yakwanitsa zaka 105 chiyikhazikitsireni, ukuchitika lero ku malo a sukuluyi ku Limbe mu mzinda wa Blantyre.

Mwazina pa mwambowu akutsekuliranso ntchito yosaka ndalama zomangira chipinda chowerengera ndinso kugula bus yomwe ophunzira pa sukuluyi adzigwiritsa ntchito

Mlendo wolemekezeka pa mwambowu ndi nduna yowona kuti pasamakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo, ana, ulumali ndi chisamaliro cha anthu, mayi Mary Navicha.

Bambo Samuel Nawasha otumikira mu dayosizi ya Zomba, amwalira.Mkulu wa nthambi yofalitsa mauthenga mu dayosizi ya Zomba,...
23/05/2026

Bambo Samuel Nawasha otumikira mu dayosizi ya Zomba, amwalira.

Mkulu wa nthambi yofalitsa mauthenga mu dayosizi ya Zomba, bambo Steve Likhutcha atsimikiza za imfayi koma ati zambiri afotokozabe.

Mzimu wa bambo Samuel Nawasha uwuse mu mtendere wosatha.

Address

Box 408, Mangochi
Chimwala

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Radio Maria Malawi posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Place Of Worship

Send a message to Radio Maria Malawi:

Share