Chapananga living waters church

Chapananga living waters church Living water church

15/05/2026

MAU ODZUKIRA

" Sichinakugwereni inu chiyeso koma cha umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi ndi chiyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako."

1 AKORINTO 10:13

Okondedwa, kupilira ndi chinthu cha mtengo wapatali, moyowu timadutsa mu zambiri koma Mulungu akuti okhala mwa Iye adzamuthandiza kupilira kuti agonjetse.

Mukhale ndi tsiku lopambana. Amen

13/05/2026

MAU ODZUKIRA

Yakobo 4:10

" Dzichepetseni pamaso pa Ambuye, ndipo adzakukwezani."

Okondedwa, nthawi zonse tiyeni tikhale anthu odzichepetsa. Mulungu adzatikweza. Mukhale ndi tsiku lopambana.

08/05/2026

*GONANI BWINO NDI MAU AWAπŸ“–08/.05/26*

*1 TIMOTHY 5:24* Zocimwa za anthu ena ziri zooneka - kale, zitsogola kunka kumlandu; koma enanso ziwatsata.

Wokondedwa tamvetserani tinapulumutsidwa mwa Chisomo komanso tikapulumuka mwa Chisomo , pakuti machimo ena awanthu ena anafika kale kumwamba akungodikira tsiku lachiweruzo , ndeutha kumanyada ndimoyo pansi pano koma osadziwa kuti machimo ako anafika kale kwa Mulungu ndipo No Reverse😭 ndeakuti ena zikuwatsata pambuyo pawo mpaka tsiku lonyamuka mdziko muno zilipambuyopo πŸ€” Satana alipantchito chochekenira machimo ziachidya aakanda Zija pano akuti ndima blesser kuiwala kuti ndi Mulungu yekha yemwe amadalitsa munthu kumvetsa chisoni kumwamba, tiyeni pemphero lakulapa lisamachoke pakamwa pathu Kuti tikapulumuke mwachisomo.

*MUKHALE NDI USIKU WACHIGONJETSO AMBUYE AKUYANG"ANIRENI*
πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™

07/05/2026

*GONANI BWINO NDI MAU AWA πŸ“–07705/26*

*Yohane 10:10*
Siikudza mbala, koma kuti ikabe, ndi kupha, ndi kuononga, Ndadza Ine kuti akhale ndi moyo, ndi kukhala nao wocuruka.

Wokondedwa Satana ndiochenjera akafuna kukuonanga choyambirira amayamba wathana kaye ndi nzeru zako, nde olo kupanga choipa umachiona ngati chabwino mchifukwa chake lero tikuona abambo kugona ndi mwana wao mkumajambula vidiyo abusa ndi mkazi wamwini mkumazijambula amakhala Satana anachotsa nzeru zaumunthu chifukwa Kwake mkupha Kuba ndikuononga , tamukakamireni Mwamuna wa Mtanda ndiyemwe alinawo moyo wochuluka Amen.

*MUKHALE NDI USIKU WOPAMBANA*
πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™

07/05/2026

*MALAMULO 10 A MULUNGU KWA ANYAMATA NDI ATSIKANA GAWO 2*

✍️ *BROTHER WANU OSCAR'S RAFAEL MWA AMBUYE*

CHIYAMBI

1. Achinyamata Kodi mwakonzeka kukonzaso moyo wanu kuti ukhale mdzanja la ambuye lero?
2. Ndemanga zanu zikuonetsa kuti mulikuwelenga mwa chidwi ndipo musaone ngati mwawelenga mwa ngozi ayi ndi Mulungu wafuna kuti muwelenge.

NDIMAKONDWELA NDIKAMAWAONA ANYAMATA AKUYENDA M'MOYO OFEWA MWA AMBUYE YESU.

KOMA ANYAMATA AMBILI NDIYAMIKA KUTI ANAMUDZIWA MULUNGU KOMA PALI ZINTHU ZINA ZONYASA ZILI MWA ANYAMATA MONGA

1. Kudzikuza ndi kufuna kutchuka
2. Mchitidwe omacheza za zibwenzi pa foni mtsikana ndi mnyamata.

Anyamata ambili ndi otumikira Mulungu koma nthawi zambili akaona kuti Mulungu Ali kuwagwilitsa ntchito amayamba kudzikuza

Ena amafuna atatchuka koma mudziwe kuti munthu ukatchuka ziwanda zimakudziwaso ndiye zimayamba kukulondora pang'ono pang'ono mpaka kufika pokugwetsa

1. Ena anati kutchuka NDI ngozi.

Mulungu atati ationetse miyoyo ya azitumiki otchuka ambili mukapeza kuti ambili anangokhala ngati botolo la (CoCa Cola)

Botolo la CoCa Cola limatha kulemba kuti CoCa Cola koma tikati

CoCa Cola timakamba zokumwa zili mkati zija koma or mutamwa za mkatizo botolo lija anthu akaliona amati

CoCa Cola

Koma Cha mkaticho chinamwedwa kale kale.

Ndikufuna mtanthauzenji

1. Azitumiki ambili chauzimu Chao chinadyedwa ndi satana koma amatumikilabe amachita zozwizwabe koma chonsecho anagwa kale kale koma popeza anavala suti ya MTUMIKI anthu amangoti mtumiki

Ndinamva chisoni tsiku lina mtumiki wina amatumikira koma ataona kuti uthenga wake anthu sakupanga comment anatsazika pa group ATI mwina anthunu simukundifuna.

Aiwara kuti

1. Yelemiya anatumiki mwa mphavu koma palibe omulondora
2. Eliya, Paulo, Stefano NDI azitumiki ambili amene amatumikira koma opanda anthu kuwalondora koma
3. Kuwanyoza NDI kuwaponyera zingwe amangidwe.

Ngati ndiwe mnyamata m'modzi omafuna kutchuka dziwa kuti

1. Suzazindikira utumiki wako ayi koma ozangopanga copy mauthenga a ena ndik

07/05/2026

MAU ODZUKIRA

Yohane 14:1

" Mtima wanu usavutike; mukhulupilire Mulungu, khulupilirani Inenso."

Okondedwa, ambiri tadzuka ndi nkhawa komanso madandaulo, koma mawu-wa akutilimbikitsa kuti tisadere nkhawa ndi kudandaula konse, tikhulupilire Mulungu, tikhulupilire Yesu Khristu. Zinthu zikhala bwino. Amen

06/05/2026

*GONANI BWINO NDI MAU AWA πŸ“–06/05/26*

*Yohane 10:10*
Siikudza mbala, koma kuti ikabe, ndi kupha, ndi kuononga, Ndadza Ine kuti akhale ndi moyo, ndi kukhala nao wocuruka.

Wokondedwa Satana Kwake mkuba kupha ndi kuonga , mzosasabwitsa lero imfa zaachinyamata odzipha ikuchuluka fukwa Satanayo amabweretsa timavuto tina tosadziwika bwino ndeamaperekanso solution ali bola ungodzipha tu basi ukapume😭 pamene ndekuti wakuba , wakuononga komanso kumupha pakamodzi , tamverserani kulibe mpumumulo kwa onse odzipha okha olo pena timanamizana kuti andipangitsa izi ndiawo ndekuti machimo anga onse apita kwaiwo mmmmm lapani mulandire Yesu lero kudzipha si solution.

*MUKHALE NDI USIKU WOPAMBANA*
πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™

05/05/2026

*GONANI BWINO NDI MAU AWAπŸ“–05/.05/26*

*1 YOHANE 2:17*
Ndipo dziko lapansi lipita, ndi cilakolako cace; koma iye amene acita cifuniro ca Mulungu akhala ku nthawi yonse.

Wokondedwa tiuzane Chilungamo apa kuti wonse okonda dziko lino lapansi kukonda zokondweretsa moyo uno kuiwala Namalenga Mwini moyo Mwini zonse adzatha psiti 😭 . Tiyeni tikonde komanso kufunafuna moyo wosatha. Nthawi yosiya machimo ndikulapa ndiyomweino pamene Ambuye alipa mpando wakukhululula.

*MUKHALE NDI USIKU WOPAMBANA AMBUYE AKUFUNGATIRENI*
πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™

04/05/2026

*GONANI BWINO NDI MAU AWAπŸ“–04/.05/26*

*1 YOHANE 2:15* Musakonde dziko lapansi, kapena za m'dziko lapansi. Ngati wina akonda dziko lapansi, cikondi ca Atate siciri mwa iye.

Wokondedwa munyengo tikudutsayi ndiyofuni osatekeseka ndizamdziko lino chifukwa satana naye alipachintchito chobweretsa zokoma zamdziko koma zilizakuchionongeko tsoka kwaiye okonda zapansi pano chifukwa kumwamba kulibe chake.

*MUKHALE NDI USIKU WOPAMBANA AMBUYE AKUSAMALIRENI*
πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™

02/05/2026

*GONANI BWINO NDI MAU AWAπŸ“–02/.05/26*

*1 YOHANE 2:1*
Tiana tanga, izi ndikulemberani, kuti musacimwe. Ndipo akacimwa wina, Nkhoswe tiri naye kwa Atate, ndiye Yesu Kristu wolungama;

Wokondedwa inu ana a Mulungu wamoyo , ana a Yaweh inu imvani mau a Yehova Kuti musachimwe, ndipo mukachimwa mwangozi thamangilani pamtanda wa Yesu Khristu wolungama amene amatha kukhululuka machimo onse ndikuiwala , ndipo sakumbukanso, pomwe ukachimwira munthu nzako mkumupepesa mawa amadzakukumba ali mwaiwala Chaka chakuti munandipangila zakuti ndipo ndinakukhululukirani , chikondi chamunthu chimatha koma cha Mulungu mchamuyaya hallelujah.

*MUKHALE NDI USIKU WOPAMBANA AMBUYE AKUFUNGATIRENI*
πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™

Address

Chikwawa

Telephone

+265888878036

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Chapananga living waters church posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share