Akhristu olimba mchikhulupiliro

Akhristu olimba mchikhulupiliro Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Akhristu olimba mchikhulupiliro, Religious organisation, jowkim chisano Road, Blantyre.

03/02/2026

Zosatheka ndi munthu zitheka ndi Ambuye.
Usataye mtima pempherabe

02/02/2026

MADZULO ANO TIYENI TIMVETSE BWINO KUTUMA KWA AMBUYE YESU

Mateyu 10
9Musadzitengere ndalama zagolidi, kapena zasiliva, kapena zakobiri m'malamba mwanu; 10kapena thumba la kamba la kunjira, kapena malaya awiri, kapena nsapato, kapena ndodo; pakuti wanchito ayenera kulandira zakudya zace.

Pamene tawerenga Luka 22

35Ndipo anati kwa iwo, Pamene ndinakutumizani opanda thumba la ndalama, ndi thumba la kamba, ndi nsapato, munasowa kanthu kodi? Anati iwo, Iai. 36Ndipo anati kwaiwo, Koma tsopano, iye amene ali ndi thumba la ndalama, alitenge, ndi thumba la kamba lomwe; ndipo amene alibe, agulitse copfunda cace, nagule lupanga,

KODI MAU A TESU KHRISTU AKUTIPHUNZITSA CHIYANI POMVETSERA MAVERSE AWIRI AMENEWA?

21/09/2021

MIPINGO ISANU NDI IWIRI YOPEDZEKA M'BUKU LA CHIBVUMBULUTSO

Pamene ophunzira anali kusanzikana ndi Yesu Khristu pamene anali kukwera kumwamba angelo anaimba pa mbali pawo ndawauza kuti yesu adzabweranso.
(Machitidwe 1:9-11)

Ophunzirawa anadikilira ndi chidwi kuti mwina yesu abwera mu nthawi yawo koma onse anafera dzina la ambuye yesu khristu, kupatula mmodzi yohane amene anaponyedwa pa chisumbu cha patmo naona masopenya.

Iye mmasopenya, anauzidwa alembe m'buku chimene aone natumiza ku mipingo iyi:
KU efeso, ku smurna, ku pergamo, ku Tiyatira, ku sarde, ku Filadelfeya, ndi ku Laodikaya. (chibvumbulutso 1:11)

KODI MUNTHAWIYI MKUTI MIPINGO YI ILIPO?

Izi zimachitika monga ulosi wa zomwe zikudza ku tsogolo, uwu unali ulosi.

KODI MIPINGO YI IDAKHALAKODI?

Eya:
Mpingo wa efeso unakhala ko kufikira 100AD ndiwo apostolic church.

Smurna from 100-313
Pergamo 313-538
Tiyatira 538-1560s
Sarde 1560s-1790s
Filadelfeya 1790s-1840
Laodikaya 1840s- kudza kachiwiri kwa ambuye yesu khristu.

Tikhala tikusanthula mpingo umodzi umodzi kufikira Ola la ciweruzo ndi mpingo wa kumapeto.

Tisanatero mawa tizaona yesu monga wa Msembe, iye woyenda pakati pa zoikapo nyale zisanu ndi ziwiri.

Kufikira Titakumana so mawa ambuye akudalitseni.

21/09/2021

MWASWERA BWANJI WOKONDEDWA MWA AMBUYE?

Lero tiyamba Phunziro lathu la buku la chibvumbulutso chapter 1.

27/08/2021

Mwaswera bwanji abale ndi alongo konse kumene muli?
Ndili okondwa lero kulumikidzana nanu, Maka titasowana kwa nthawi yaitali.

Pozindikira kuti tili mu matsiku a kumapeto, pamene maulosi ambiri akkhala akukwaniritsidwa, choncho tiyenera kukumbutsana kuti nthawi zonse tisachoke pa mawu a mulungu.

Kuyambira mawa tikhala tikugawana mawu a mulungu, tizayamba ndi kuunikira buku la chibvumbulutso chapter 1 mpaka 22.

Kungokumbusana, amene ali whatsap ali ndi mwayi wopangidwa add pa group imene tsiku ndi tsiku azitumiki amakhala a kulalikira mawu.

Ndipemphe chisomo cha Atate, Mwana ndi Mzimu woyera chikhale ndi tonse komwe tili.

Masalmo 141:10
Oipa agwe pamodzi mmaukonde awo kufikira nditapitilira ine.

Mateyu 4:11
Pomwepo mdierekezi anamusiya iye, ndipo angelo anadza, namtumikira iye.

Ndipempha mamasulidwe kwa onse amengidwa munsinga za matenda, kuvuta kwa banja, kusowa kwa ntchito... Masuka! Mudzina la Yesu, pamene tsiku la tsopano la yamba nyengo za tsopano so ziyambe.

Zisomo za mulungu Atate, mwana ndi mzimu woyera zikhale ndi ife tonse kuyambira lero ndi nthawi zonse... Amen

15/10/2020

Mateyu 6:33

Koma muthange mwafuna UFUMU WACE ndi CHILUNGAMO CHACE.

Pali mafunso awiri tingawalingalire:
1. Kodi ufumu wake tingaupedze kuti?
*yankho: ufumu wakumwamba uli pakati pathu.
- pakati pa wanthu amene machimo awo anamezedwa mwa madzi ndi Mzimu, ufumuwu uli pakati pawo.

2. Kodi chilungamo cha mulungu ndi chiti?
Yankho : ndicho chikondi chake chomwe anatiombola ife ndi imfa ya mwana wake wobadwa yekha, mwa madzi ndi Mzimu.

Lero anthu a kusaka chilungamo chawo kuleka cha mulungu.
Tiyeni tivomereze kuti ndife olephera ndife opanda chilungamo, koma mulungu yekha ndipo TIFUNE UFUMU WAKE NDI CHILUNGAMO CHACE.

Amen

20/02/2020

MALAMULO KHUMI AMULUNGU

Tiyeni tiunikire malamulo khumi a Mulungu amene anaperekedwa kwa Ife; Kumbukirani kuti Yesu sanadathese malamulo (Mateyu 5:17) (Agalatiya 3:24 Lamulo liri ngati nankungwi wakutifikitsa kwa Khristu)

CHOYAMBA TIYENI TIONE UDINDO WA MUNTHU KWA MULUNGU.
(Mika 6:8) Iye anakuuza, munthuwe, chomwe chiri chokoma; ndipo Yehova afunanji nawe koma kuti uchite cholungama, ndi kukonda chifundo ndi kuyenda modzichepetsa ndi mulungu wako?

MULUNGU analamula munthu kunvera chilamulo chake.
Tikawerenga AROMA 2:14,15 akutisimikizira kuti ntchito ya lamulo inalembedwa mmitima yathu.

MALAMULO AMULUNGU AMANGIDWA PA: Kukonda Ambuye Mulungu ndi mtima wathu wonse, moyo wathu wonse, mphanvu zathu zonse ndi nzeru zathu zonse ndi kukonda mnzathu monga tizikondera ife eni. (Mateyu 22:37~40)

PAMENE TIKUYANDIKIRA KU MALAMULO AMULUNGU AMENEWA; TIYENI TIONE Mawu otsogolera ku malamulo khumi a mulungu:

Eksodo 20:2 INE NDINE YEHOVA MULUNGU WAKO, AMENE NDINAKUTULUTSA IWE KU DZIKO LA AIGUPTO, KUNYUMBA YA UKAPOLO.

Mawu otsogolerawa amatiphunzitsa kuti popeza Mulungu ndi Ambuye ndi Mulungu wathu ndiponso mombolo wathu, kotero kuti tili oyenera kusunga malamulo ake.

(Luka 1:74,75) Kutipatsa ife kuti tilanditsidwa ku dzanja adani athu, tidzamtumikira Iye, opanda mantha. mchiyero ndi mnchilungamo pamaso pake, masiku athu onse.

LAMULO LOYAMBA
Usakhale nayo milungu ina koma ine ndekha.
Tiyeni mawa madzulo tikhalenso limodzi kuti tinvetsetse lamulo limeneri.

AMBUYE AKUDALITSENI NONSE

31/12/2019

CHIMWEMWE CHOPAMBANA

luka 10:20
Koma musakondwere kuti mizimu idakugonjerani; koma mukondwere kuti maina anu alembedwa mmwamba.

Wokondwa ophunzira atatumidwa kukalalikira zonse zinawayenderako bwino, odwala amachira, osayenda nayenda, ziwanda nkumatulutsidwa ndipo iwo anali ndi chimwemwe!! kusangalala kuti chilichonse chinali bwino.

Atafika kwa ambuye Yesu namuuza za chimwemwe chawo kuti analibe bvuto lililonse ndipo ziwanda zimawanvera; Yesu anawauza kuti asasangalale kwambiri kuti anagonjetsa koma: asangalale kuti maina awo alembedwe mmwamba.

nchimwene, mlongo, bambo ndi mayi!!! Pamene lero tikusangalala kuti TAGONJETSA MPHANVU ZOIPA; afiti, ngozi, zigawenga, njala, ziwanda ngakhalenso matenda ndi imfa

Tikuyenera kusangalala inde sizoletsa chifukwa tadutsa muzambiri ndipo lero tili ndi MOYO, koma ndikupempheni kuti kusangalala kwathu tisangalale kuti maina athu alembedwa mu BUKU LA AMOYO!!

Chifukwa nkutheka lero usikuwu nkumasangalala kuti tachilowa ndimoyo ndipo talimbana ndi matenda koma kungotha masiku awiri okha imfa ndikutipedza, KUDI KUSANGALALA KWATHU KUDZAKHALA KWA PHINDU LANJI?!!!

Ndilinawo umboni lero kuti wogwira naye ntchito lero lomwe, wayenda yekha koma pongotha 1 hour wamwalira, @ heart attack.
Tsiku lomalidza la chaka koma zachitika izi; Popeza aliyense adzafa ndithu koma chikufunika nchakuti TILEMBETSE LERO MAINA ATHU MUBUKU LAMOYO.

Tilembetsa bwanji???

Pokhulupilira YESU KHRISTU amene ali mbuye ndi mpulumutsi wathu.

Tingamukhulupilire bwanji??

Pokhala ndi chikondi chapamulungu ndi mtima wathu wonse, nzeru zathu zonse, ndi mphanvu zathu zonse komanso pokonda Abale athu monga tizikondera ife eni.

Zisomo ndi mtendere zikhale ndi inu nonse ambuye akudalitseni

22/09/2019

NKHUMALIRO YA MAWU

MUTU: SINDIKUMUDZIWA;
luka 22:54~62
Tikawerenga chapter chimenechi tikunva za Petulo akumkana yesu kuti sakumudziwa. Tikakumbukira pamene Yesu alali kunchenjeza Petulo, iye ananena kuti " Ambuye, ine ndidzapita nanu kundende ndi kuimfa" Thupi ndilo lofuna koma mzimu ndiwo olefuka. Petulo analumbira, kuti sadzawasiya ambuye yesu ngakhale ndende ngakhale imfa.

Koma nthawi iyi petulo akumkana yesu kuti sakumudziwa!!

"Nchifukwa chani tikumkana Yesu lero? Nchifukwa chiyani tikukanika kukhalabe ndi Yesu lero?"
Simon Petulo anadzazidwa ndi mantha, amaopa kuti akangovomera kuti akumudziwa Yesu ndiye kuti nayenso aphedwa!

Nkutheka mugulu linonso a Petulo tilipo, amene tinavomera kuti "ndine khristu ndipo ndidzayenda ndi Yesu nthawi zonse" Koma ndizoona zimenezi?
Kodi lero tilikuti? Dzulo tinali kuti? Pakuti taiwala ndi kupita ku church komwe. Nkutheka wina mwa ife Neighbour wathu akuvutika kuchipatala, pofufuza abale nkupedzeka inuyo, poudzidwa za uthengawu; Tidamkana kuti ayi sindikumudziwa sichibale!! Anthu ambiri akuvutika lero kusowa owathandidza chifukwa cha yankho lakuti: "SINDIKUMUDZIWA, ngati ndi m'bale wanga? tinangoyandikana basi!"

Okondedwa popedza kunalembedwa kuti wokana Khristu adzabwera, koma alipo ngakhale TSOPANO LINO!
Tikuyenera kukhala ndi chikondi chenicheni, achifundo, komanso okhulupilira mulungu.

Tidzazizimuka tsiku la chiwerudzo Ambuye Yesu akuti; "ndinali wanjala koma sunandidyetse, wamaliseche sunandiveke, wachisoni koma sunandipukuta misonzi yanga!!"
Koma ife tidzati " Ambuye ndinakumana nanu kuti?"

Tisakhale ngati Petulo okondedwa, amene anayenda naye, anadya naye, koma OSAMUDZIWA. Zonvetsa chisoni!

Pempho langa masana ano nlakuti, musamukane yesu, musamukanidze yesu, musamumane yesu, Nzanu akukupemphaniyo ndi ambuye amenewo, tiwasamale a umphawiwo, amasiyewo.

24/07/2019

tumidzani uthenga okuti ADD ku 0881248982 kuti mupangidwe add ku group ya zauzimu ( KUYENDA NDI YESU WHATSAP GROUP)

ngakhale titachita ntchito zotani… koma chopambana kwambiiri ndi KUNVETSERA MAWU A UTHENGA WABWINO.

24/07/2019

CHIKHULUPILIRO

AHEBRI 11:1~3

Koma chikhulupiliro ndicho chikhazikitso cha zinthu zosapenyeka. Pakuti momwemo akulu amachitidwa umboni. Ndi chokhulupiliro tizindikira kuti maiko ndi a mmwamba omwe anakonzedwa ndi mawu amulungu , kotero kuti zinthu zopenyeka sizinapangidwa zochokera mwa zoonekazo.

Nkutheka mmawa uno tataya mtima chifukwa cha nkhawa za moyo uno, ena TIKUKAIKA KUTI TIDZAPEDZA NTCHITO? TIDZAPEDZA BANJA? TIDZAMANGA NYUMBA?

Tikuyenera kukhala ndi chikhulupiliro kuti mwa mulungu ndizotheka.
NDIMAWU OKHA WINA LERO AKUMASULIDWA MU NSINGA ZAKE.

Timadziwa kuti mawu amulungu amapatsa moyo, "PEMPHANI NDIPO CHIDZAPATSIDWA KWAINU, GOGODANI ADZAKUTSEKULIRANI, FUNAFUNANI NDIPO MUDZAPEDZA.

Pali chinsisi chimodzi kuti pamene tili ndi chikhulupiliro, tikhalenso tikugwira ntchito YOFUNAFUNA, YOGOGODA ndi KUPEMPHA KWA ATATE AKUMWAMBA. chifukwa mwa mawu akuti WOSAGWIRA NTCHITO ASADYE. ( 2 atesalonika 3: 10&11)

Ambuye adalitse tonse pamene tikupempha kwa atate mwa chikhulupiliro…… amen

18/07/2019

Kwapatsidwa kusankha kwa ife, kupedza moyo kapena imfa. Koma mulungu safuna mmodzi wa ife kuti aonongeke, nchifukwa anatumidza mwana wake padziko lapansi kuti yense okhulupilira iye asataike koma akhale ndi moyo osatha.

Ndipo pakukwera kumwamba mbuyeyo anati: "ndikutumizirani nkhose ndiye mzimu oyera"

Agalatiya 5:16&17
mzimu asutsana nalo thupi kuti lisachite zofuna zake.

Tiyeni tinvere kulankhula kwa mzimu oyera mkati mwathu posutsana nalo tchimo lathu kuti tikalandire moyo osatha, omwe anatilonjeza. amen

Address

Jowkim Chisano Road
Blantyre

Telephone

+265881248982

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Akhristu olimba mchikhulupiliro posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share