22/09/2019
NKHUMALIRO YA MAWU
MUTU: SINDIKUMUDZIWA;
luka 22:54~62
Tikawerenga chapter chimenechi tikunva za Petulo akumkana yesu kuti sakumudziwa. Tikakumbukira pamene Yesu alali kunchenjeza Petulo, iye ananena kuti " Ambuye, ine ndidzapita nanu kundende ndi kuimfa" Thupi ndilo lofuna koma mzimu ndiwo olefuka. Petulo analumbira, kuti sadzawasiya ambuye yesu ngakhale ndende ngakhale imfa.
Koma nthawi iyi petulo akumkana yesu kuti sakumudziwa!!
"Nchifukwa chani tikumkana Yesu lero? Nchifukwa chiyani tikukanika kukhalabe ndi Yesu lero?"
Simon Petulo anadzazidwa ndi mantha, amaopa kuti akangovomera kuti akumudziwa Yesu ndiye kuti nayenso aphedwa!
Nkutheka mugulu linonso a Petulo tilipo, amene tinavomera kuti "ndine khristu ndipo ndidzayenda ndi Yesu nthawi zonse" Koma ndizoona zimenezi?
Kodi lero tilikuti? Dzulo tinali kuti? Pakuti taiwala ndi kupita ku church komwe. Nkutheka wina mwa ife Neighbour wathu akuvutika kuchipatala, pofufuza abale nkupedzeka inuyo, poudzidwa za uthengawu; Tidamkana kuti ayi sindikumudziwa sichibale!! Anthu ambiri akuvutika lero kusowa owathandidza chifukwa cha yankho lakuti: "SINDIKUMUDZIWA, ngati ndi m'bale wanga? tinangoyandikana basi!"
Okondedwa popedza kunalembedwa kuti wokana Khristu adzabwera, koma alipo ngakhale TSOPANO LINO!
Tikuyenera kukhala ndi chikondi chenicheni, achifundo, komanso okhulupilira mulungu.
Tidzazizimuka tsiku la chiwerudzo Ambuye Yesu akuti; "ndinali wanjala koma sunandidyetse, wamaliseche sunandiveke, wachisoni koma sunandipukuta misonzi yanga!!"
Koma ife tidzati " Ambuye ndinakumana nanu kuti?"
Tisakhale ngati Petulo okondedwa, amene anayenda naye, anadya naye, koma OSAMUDZIWA. Zonvetsa chisoni!
Pempho langa masana ano nlakuti, musamukane yesu, musamukanidze yesu, musamumane yesu, Nzanu akukupemphaniyo ndi ambuye amenewo, tiwasamale a umphawiwo, amasiyewo.