DAILY Strength.

DAILY Strength. The only site where you get spiritual strength when deeply troubled with the world.

16/05/2025

Let's invest in humanity..

27/02/2023

*BE SELF ESTEEMED AND TRUST IN GOD ONLY.*

In the story of Jesus Christ's journey to Jairus for a healing mission which suddenly turned into a resurrection mission, I learn alot.

When Jesus christ approached Jairus's home, some mocked Him saying, no impact for His coming would occur because the daughter was already dead, but instead, Jesus Christ ignored the mock and just proceeded by taking James, John and Peter together with the child's parents and they got into the house and the mission was a success.

This simply teaches me that, not all the words uttered are to be attended, some are meant to be ignored for our mission to be a marvel.
It also raise an insight, that, not all people who claim to be with you in the journey are your friends.
For a mission to be a success, we need to have mature, serious and real friends with sense of humor.

Sometimes we force ourselves into people who don't value and trust us and they end up in discouraging all our missions.

If Jesus chose those to be close to Him, be wise as well, choose those to be close to you because even those who were overthrown/defeated in life, the principal reason was because they associated themselves with enemies.

Behold, I send you forth as sheep in the midst of wolves: be ye therefore wise as serpents, and harmless as doves.
(KJV Matthew 10:16).

May God grant us wisdom of digesting things for our eternal betterment.

evangelistkawalangathoughts2023@praisetelevision.

18/05/2022

!!

"Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ndi mu Yudeya monse, ndi mu Samariya, ndi kufikira malekezero ake a dziko"
(Macitidwe 1:8).

Nthawi zambiri anthu timafuna kumtumikira Mulungu ndi mtima wathu wonse ndi kucita zopambana pa utumiki.. Koma comwe cimatisowekera ndico kuitana mwini utumikiwo amene ali Mulungu ndi kumulandira Yesu kukhala Mbuye ndi mpulumutsi wa moyo wathu.

Yesu kristu powasiya ophunzira ace kuti apitirize utumiki wace, anawauza kuti, "Mudzalandira mphamvu, mzimu woyera atadza pa inu."
Dziwani palibe utumiki omwe ungakhale successful in terms of transforming people's lives to christ and resulting into a salvation ngati Mzimu woyera tamupanga neglect/ kumkana.

Taonapo ambiri akukana dzina la Yesu poopa kunyozedwa ngakhalenso kuphedwa, zonsezi ndi kusowa kwa Mzimu woyera cifukwa ndi Yekhayo amapatsa mphamvu ndi cirimbikitso.

Ngati inu ndiine tikufuna kupita citsogolo ndi utumiki omwe anatipatsa Mulungu ndi kusafooka pokweza dzina lake kukafikira ku malekezero a dziko ndi kumapeto a nthawi kufikira Yesu adze, tiitanire pa Mzimu woyera cifukwa;

"Mulungu ndiye mzimu; ndipo omlambira Iye ayenera kumlambira mumzimu ndi m'choonadi."
(Yohane 4:24).

31/03/2022

Ephraim waphatikana ndi mafano, mlekeni Hosea 4:17

22/05/2020
12/04/2019

NDINGATHAWIRE KUTI?

Mkulu wina olemba ndi kutsindikiza mabuku, otchedwa William Shakespeare, analemba buku lina lotchedwa, "Julius Caesar."

Mu bukuli muli nkhani ya mkulu wolamula wakale wa kudziko la Rome otchedwa Julius Caesar amene nthawi ya ulamuliro wace anali wokondedwa.
Koma kamba ka ndale ndi akuluakulu ogwira nao ntchito, guru la ogwira nao ntchito (senators) linapanga upo wofuna kupha mtsogoleriyu ndipo ciwembuci cinapangidwa kuti cikacitikire ku malo a zokambirana monga ikhalira parliament yomwe kwa iwo imatchedwa capitol.

Mkazi wace analota maloto omucenjeza kuti asapite kumalowo, koma Iye monga mtsogoleri anacita makani kuti apita basi potengera kuti iye amati nkokakambirana zokweza dziko.
Mkulu wina wolosera ndi kulota za mtsogolo (Sooth sayer) naye anafuna kupereka uthengau panjira pomwe panali namtindi wa anthu ofuna kumuona pomwe anali kupita ku capitol, koma analephera kutero kamba ka namtindiwu kotero Caesar anakafika ku capitol komwe kunali zokambirana za akuluakulu a boma.

Zokambirana ziri mkati, mkulu otchedwa Cassius anafunsa funso kwa Caesar kotero Caesar poyankha, m'modzi wa mguru la ma senators otchedwa Casca anadzipsetsa mtima mwadala monga mwa cikonzero cao (Conspiracy) kotero anasolola lupanga lace nalankhula mau kuti, "Manja anga, ndilankhulire" (Let my hands speak for me) kotero anagwaza nalo pamtima pa Julius Caesar amene anaferatu pomwepo.

Imfa itacitika, cinawatsalira ndi nzeru yokaliuzira dziko kuti imfa ya mtsogoleri wao yabwera bwanji kotero anamemeza dziko lonse kukakumana malo otchedwa Market Square.
Mu kukambirana kwao, anauzana kuti asakanene bodza koma kunena zoona kuti iwo amupha pofuna kupulumutsa dziko ku nkhanza ndi kudzikonda kwace kotero alole kuti pasankhidwe mtsogoleri wina.

Izi zitakonzeka, ndikulengezedwa, mbiri ya imfa ya Julius Caesar inali ponseponse ndipo mkulu wina otchedwa Mark Antony, anapempha kuti akalankhule pa malirowo.
Mark Antony anali mnzace wa Julius Caesar amene amauzana naye zinsinsi zambiri ngakhale Mark Antony sanali mgulu la olamulira ndipo guru iri la upandu linalamula kuti Mark Antony akalankhule kumapeto koma asakalankhule zowapacika ai.

Pa mwambowu, akuluakulu aboma monga Marcus Brutus, Cassius ndi Caius Ligarius analankhula ndipo anthu anaombera mmanja kuti zoona Caesar anayeneradi kufa ndithu cifukwa mu umboni wao, ananena kuti, Caesar anali Mtsogoleri odzikundikira cuma amene sakhudzidwa ndi kusowa kwa anthu mdziko lace kotero iwo atenga risk yomupha kuti apereke ufulu kwa anthu wamba.
Izi zinawakomera anthu omwe anaimba nthungululu ndi kuombera mmanja uku mtembo wa Caesar usanafike pamalopo.
Mwadzidzidzi, Mark Antony anafika pamalopo ndi mtembo wa Caesar ataukulunga nauika pamsanja pomwe amalankhulira ndi kuyamba kulankhula uku akulu onse aboma ndi aupanduwa akunyamuka.

Mmau ace, Mark Antony anangoti, "Ndabwera kudzaika m'manda Caesar osati kudzamutamandira" (I've come to burry Caesar, not to praise Him).
Komabe ndinayenera kukuuzani za ma plan a mu will ya Caesar.
Caesar anaika cuma capadera cothandizira inu mdzaka za mtsogolomu ndipo mbali ya malo ambiri anapereka kwa anthu inu ovutika.
Pali zabwino zambiri zomwe Caesar amakukonzerani zomwe ngakhale wamwalira, zinthuzi muziona zikukucitikirani.

Mau awa, anautsa mkwiyo wa anthu omwe analingalira kuti, nkutheka guru la akuluakulu a boma lija, lapha Caesar osati pa zifukwa zomwe amanenazo ai, koma kufuna udindo wace kotero anthu a dziko la Rome anapsa mtima nalonjeza kusaka aliyense payekhapayekha wacita nao ciwembuci ndi kumuphanso.

Mguru la akuphali munali mkulu wina wosatchuka otchedwa Pindarus ndipo Iye podziwa kuti kalikonse katha kucitika, anathawira kuphiri komwe ali pamwamba pa phiriri amaona zonse zocikika pa Market Square ndipo mkwiyo wa anthu amatha kuuona kuti anthu akubalalika nasakasaka malo onse omwe angathe kupeza akuluakulu akuphawa.
Mantha atamugwira, anadziwa kuti, nkosathekanso kubwerera kunyumba kwace cifukwa anaona nyumba zina za akuluakuluwa zikuyatsidwa moto ndipo anadziwa kuti kubwerera kwa Iye ndi cionongeko.
Atakhala n'kusowa nzeru, analankhula mau onena kuti;
"FAR FROM THIS COUNTRY, PINDARUS SHALL RUN, WHERE NO ROMAN, BUT, SHALL TAKE NOTE OF HIM."

Iri linali lingaliro lomwe linamufikira kuti, kutali ndi dziko lace la Rome, Iye akuyenera kuthawira kuti pasapezekenso wina ozindikiranso za komwe wapita.
Konsekutu kunali kusowa ndi kuusakasaka mtendere polingalira za kupalamula komwe anapalamula ndipo anaziona kuti palibenso pobisalika mu dziko la Rome angathe kukhala, koma kupita kutali zedi kuti pasapezeke omupeza ndi kumupha.

Ambiri lero tiri mdziko la cilendo osati mwa kufuna ai, koma kamba ka mavuto omwe tinawapalamula kwathu.
Ena tinathawa milandu ya kupha, kuba angakhalenso milandu ya zigololo yomwe mwa njira ina iriyonse ikanaphetsa miyoyo yathu.
Ena tikunema pano tinathawa mavuto a banja, ena ngongole zitafika povuta zomwe manjira ina iriyonse zimapereka citonzo komanso ciopsezo ku moyo wathu.
Koma ngakhale titathawa motani pamaso pa nyengo zimenezi, malo alionse amene timathawirawo sitipezabe mtendere, zonsezi ndi cifukwa cakuti, tathawa pamaso pa Mulungu.

Adamunso atalephera kumvera macenjezo a Mulungu posadya zipatso za mtengo oletsedwawo, tikupeza kuti atangodya cipatso ca pakati pa munda, Adam ndi Hava anadziona kupelewera pamaso pa Mulungu kotero nthawi yomwe Mulungu anali kuwaitana, iwo sanafune kuyankha koma kuthawa ndi kubisala (Gen 3: 8-10).
Koma ngakhale anabisala, Mulungu diso lace limawaonabe.

Ndidzapita kuti kuzembera mzimu wanu? Kapena ndidzathawira kuti kuzembera nkhope yanu? Ndikakwera kunka kumwamba, muli komweko; kapena ndikadziyalira ku Gehena , taonani, muli komweko.
(MASALMO 139:7‭-‬8).

Tingathe kuthawira kuli konse, komabe consciece yathu ndi imene imatisaka ndipo timakhalabe anthu ozunzika mumtima.
Tinayenera kudziwa kuti, tonsefe ndi ocimwa ndi operewera pamaso pa Mulungu kotero, kuthawa anthu a dziko lapansi kapenanso nyengo za dziko lapansi sikungatipindulire, koma kuthawira kwa mwini opereka moyoyo.

Ndipo ndinena kwa inu, abwenzi anga, Musaope iwo akupha thupi, ndipo akatha ichi alibe kanthu kena angathe kuchita. Koma ndidzakulangizani amene muzimuopa; taopani Iye amene atatha kupha ali ndi mphamvu yakutaya ku Gehena , inde, ndinena ndinu opani ameneyo.
(LUKA 12:4‭-‬5)

Ndikufuna ndilankhule ndi moyo wa wina lero amene akusautsidwa mu njira zosiyanasiyana ndipo akulakalaka atangosowa, kufa ndipo sakuonanso cifukwa cokhalira ndi moyo lero kuti, kulibe kwina komwe ungathe kuthawira, koposa kwa Mulungu.

Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m'masautso.
(MASALMO 46:1)

Anthu athawirapo maiko ocuruka kamba ka zovuta za mdziko lao monga njala, nkhondo ndi zina zocuruka natchulidwa ma refugee kumeneko, koma kumaiko konseko anathawirako, sanakhale mwaufulu cifukwa zovuta sizimati zawapeza liti, koma refugee camp yopambana yomwe inu ndiine tingathawireko mmasautso athu, ndiye kwa Mulungu.

Dzina la Yehova ndilo nsanja yolimba; wolungama athamangiramo napulumuka.
(MIYAMBO 18:10)

Mulungu akudalitseni pamene mukutsinkhatsinkha zosankha kwa Mulungu yekha monga kothawirako mnyengo zanu zonse.

Evangelistkawalanga@dailystrength2019.

12/04/2019

NJALA

Mdziko la South Africa, ca ku madzulo kwace maka mdera lotchedwa capetown caka cathaci kunacitika cinthu cina comwe cinandiphunzitsa kufufuza m'malemba.

Dera la Capetown lazunguliridwa ndi nyanja zikuru-zikuru za mcere (Oceans) za Atlantic komanso Indian zomwe ziri ndi madzi ocuruka zedi .
Koma ngakhale izi ziri comweci, adzanyengo analengeza kuti mderali madzi avuta ndipo kukhala cilala ca madzi.

Zinali ngati mphekesera, koma popita pa nthawi tinaona kuti nthawi yoikika kuti mvula igwe, siinagwe kotero kucuruka kwa madzi mmadziwe osungilamo kunayamba kutsika mpaka kufika pa ciopsezo.

Boma silinakhale cete, linayamba campaign ya kudziwitsa anthu okhala mderali za coopsa comwe cinali nkudza kuti ngati nkotheka, ayesetse kukonzekera ndi kusamalira madzi omwe alipo.

Ndinadzionera ndekha ndi maso municipality ya Capetown ikulengeza paliponse za kasamalidwe ka madzi.
Ukapita ku Quick spar, Pick and Pay, shoprite ndi ma shop ena akuru akuru, umapeza ma poster aakuru bwino olemba za kasamalidwe ka madzi koyenera.
Mpaka zinafika poti mlingo unaikidwa wa kaonongedwe ka madzi pa tsiku kuti atleast 50litre pa tsiku pa khomo liri lonse ndipo ngati umagwiritsa ntchito washing machine, dish wash machine, shower ndi zida zina zotaya madzi, kunalamulidwa kuti zicepetsedwe.

Tinadzionera tokha anthu akumvera pocotsa garden zao za maluwa, nkuika paving kukana kuononga madzi pothirira maluwawo.
Onse okhala ndi pool komanso whirlpool bath mnyumba zao, ,nyengo iyi, anasiya kugwiritsa ntchito, enanso anakwirira ndi kucotsa cifukwa boma kuona ukuonongera madzi poika mu pool omwe ena akanamwa, limatha kukuitanira kubwalo la milandu komwe cilango cace cinali ca ndiwe yani.

Zonsezi zinapangitsa anthu kudziwa ubwino wa madzi kuti madzi ndi moyo kotero aliyense anatenga udindo wa kumvera komanso kusamaladi madzi.
Izitu zikundikumbutsa moyo wa kwathu ku Malawi komwe m'dzaka zina m'mbuyomo kunagwa njala/cilala.
Njala imene anthu ena amakakumba nayo dzikhawo kuti adye kuli kusowa pogwira ndipo ambiri mwa abale athu anamwalira.
Ena makolo athu amatikumbutsa za njala ya 1940 ndi zaka zina ndipo tikamamva ndi kukumbukira za izi, timadziwadi kuti njala n'cirombo.

Ngati dziko limatha kuticenjeza za zinthu zobwera, ife nitimvera kuti nyengozo pofika tikapyole, kulibwanji mau a Mulungu ncifukwa ninji sitimvera?
Kodi munthu ndi Mulungu, amene ife tikanamumvera ndi ndani?
Ngati ife timaopa njala ya kuthupi yomwe imangopulumutsa cibvundici, nanga bwanji sitisamala za mau a opereka moyo kuti potha moyowu tikapulumuke?

Taonani, akudza masiku, ati Ambuye Yehova, akuti ndidzatumiza njala m'dzikomo, si njala ya mkate kapena ludzu la madzi, koma njala ya kumva mau a Yehova. Ndipo adzayendayenda peyupeyu kuyambira kunyanja kufikira kunyanja ndi kuyambira kumpoto kufikira kum'mawa; adzathamangathamanga kufunafuna mau a Yehova, koma osawapeza. Tsiku lomwelo anamwali okongola ndi anyamata adzakomoka nalo ludzu.
(AMOSI 8:11‭-‬13)

Baibulo nalo likuticenjeza za njala ndi cilala zomwe zidzaoneke.
Njala iyi sinjala yomwe timatha kupita dera lina nkukapezako thandizo, zolembera zikutionetsera kuti, sikudzakhala kwina kothawira ndipo anamwali onse ooneka okongola, ndi dziphona za dzitho zidzakomoka ndi njala komanso ludzu.

Kodi mumadziwa kuti munthu sakhala ndi moyo ndi cakudya cokha, koma ndi mau a Mulungu?
(Mat 4:4).
M'madziwa kuti mau omwe tikumva lerowa ndi moyo?
Nanga mukudziwa kuti mau omwe tikuwaseweretsa lerowa, liripo tsiku lina lomwe tidzawafune, kuwasakasaka kuti atitsitsimutse, kutipatsa ciyembekezo komanso moyo, koma sadzapezeka?

lirani monga makanda alero mkaka woyenera, wopanda chinyengo, kuti mukakule nao kufikira chipulumutso;
(1 PETRO 2:2)

Ife ndiife ana a Mulungu, tinayenerea tidzifuna coonadi ca Baibulo ndi kucigwiritsa ntchito monga makanda omwe akangobadwa amalilira mkaka wa mai awo kuti akule.
Kodi ife tikula bwanji muuzimu ngati sitikufunafuna kumva coonadi ca Baibulo?

Mwai tiri nao wa kugwiritsa ntchito coonadi comwe tiri naco lero koma ngati sititero, ndithu tidzathamanga peyu-peyu kumpoto mpaka kummwera, kummawa kufikira kumadzulo angakhale kunyanja ina kufikira kunyanjanso ina kufunafuna mau a Yehova momwe muli moyo koma sadzapezeka.

Yesu anati kwa iwo, Ine ndine mkate wamoyo; iye amene adza kwa Ine sadzamva njala, ndi iye amene akhulupirira Ine sadzamva ludzu nthawi zonse.
(YOHANE 6:35)

Odala amene akumva njala ya mau lero, cifukwa ikamadzafika nthawi yomwe Yehova adzaponya njalayi mdziko, iwo adzakhala wokhuta, sadzamva njala konse.
Mulungu atithandize kuyambanso kugwiritsa ntchito coonadi ca Baibulo kuti pobwera mwana wace Yesu Kristu, adzatipeze tiri Oyera ndi kuti tikapulumuke.

Mulungu akudalitseni lero pamene mukupanga cisankho comva mau a Mulungu.

Address

Blantyre

Telephone

+27780998427

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when DAILY Strength. posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Place Of Worship

Send a message to DAILY Strength.:

Share