22/08/2026
*PHUNZIRO #08 LA KOTALE MWACHIDULE KWAMBIRI*
*15th-21st AUGUST, 2026.*
_*"PAMENE YESU ANAUKA KWA AKUFA"*_
*VESI LOLOWEZA: 1 AKORINTO 15:14-17*
_*"Ndipo ngati Khristu sanaukitsidwa kulalikira kwathu kuli chabe. Chikhulupiriro chanunso chili chabe. Ndiponso ife tipezedwa mboni zonama za Mulungu; chifukwa tinachita umboni kunena za Mulungu kuti anaukitsa Khristu; amene sanamuukitsa, ngati kuli tero kuti akufa saukitsidwa. Pakuti ngati akufa saukitsidwa, Khristunso sanaukitsidwa; ndipo ngati Khristu sanaukitsidwa, chikhulupiriro chathu chili chopanda pake; muli chikhalire m'machimo anu"*_
👉🏽Mu nthawi ya Paulo anthu ena sankakhulupirira za mdzukiro.
👉🏽 Mdzukiro ndi nthawi imene akufa adzaukitsidwa pakubweranso kwachiwiri kwa Yesu Khristu
👉🏽Paulo akufuna timvetsetse choonadi cha mdzukiro
👉🏽Sabata ino tiwunikira _1 Akorinto 15_ ndi Chiphunzitso cha mdzukiro
*SUNDAY - TSIKU LOYAMBA:*
_*"KULENGEZA MDZUKIRO WA YESU"*_
*1 AKORINTO 15:1-4*
👉🏽Paulo akuyamba _1 Akorinto 15_ ndi Uthenga Wabwino
👉🏽Wakuti Yesu amatipulumutsa ku machimo
👉🏽Paulo analalikira uthenga wabwinowu kwa Akorinto
👉🏽Ndipo anthuwo anakhulupirira uthengawo
👉🏽Tsopano anayenera kugwiritsa ntchito uthengawo
👉🏽Zikatero Mulungu adzawapulumutsa _(1 Akorinto 15:1,2)_
👉🏽 Mdzukiro wa Yesu ndi gawo lofunikira kwambiri la Uthenga Wabwino
👉🏽 Paulo akuti Yesu anafera zoipa zathu monga mwa malembo _(1 Akorinto 15:3)_
👉🏽Imfa ndi mdzukiro wa Yesu zimakwaniritsa malonjezo a Mulungu a Chipangano Chakale
👉🏽_1 Akorinto 15:5-8_ akutipatsa umboni wa mu Baibulo wakuti anthu ambiri anamuona Yesu atauka kwa akufa
👉🏽Anthu amenewa Yesu akuwatchula kuti ndi _*"MBONI ZA IZI"*_ _(Luka 24:48)_
*MONDAY - TSIKU LACHIWIRI:*
_*"CHIYEMBEKEZO CHATHU CHOKHACHO"*_
*1 AKORINTO 15:9-19*
👉🏽Mu _1 Akorinto 15:9-19_ Paulo akunena chifukwa chimene sitiyenera kukana mdzukiro wa Yesu
👉🏽Popanda mdzukiro tilibe chiyembekezo
👉🏽 Amitundu ambiri kalelo sankakhulupirira za mdzukiro
👉🏽 Ndipo Paulo sankawamvetsetsa anthu okayikira mdzukirowa
👉🏽Ngati kulibe mdzukiro, Paulo ndiyetu akuti;
🔨Yesu sanauke kwa akufa
🔨 kulalikira kwathu kuli chabe
🔨 Chikhulupiriro chathu ndi chopanda pake/chopanda ntchito
🔨Ndife mboni zonama
🔨Machimo athu sanakhululukidwe
🔨Akufa adakagonabe m'manda ndipo anataika
*TUESDAY - TSIKU LACHITATU:*
_*"KHRISTU ADALI CHIPATSO CHOUNDUKULA"*_
*1 AKORINTO 15:20-23*
👉🏽 Mdzukiro wa Yesu ndi woonadi
👉🏽Choncho tikhonza kutsimikiza kuti aliyense amene anafa ali mwa Yesu.........
👉🏽.......adzaukitsidwa pakubweranso kwachiwiri kwa Yesu Khristu
👉🏽Mu _1 Akorinto 15:20-23_ Yesu akutchulidwa *'Chipatso Choundukula'*
👉🏽Chifukwa chakuti Iye ali umboni kuti akufa mwa Yesu adzaukitsidwa pakubweranso kwake kwachiwiri
👉🏽Yesu adzabwezera Ufumu kwa Mulungu Atate
👉🏽Dziko lapansi lidzayambanso kulamulilidwa ndi Mulungu _(1 Akorinto 15:25-28)_
👉🏽Yesu adzadziyika yekha pansi pa ulamuliro wa Mulungu Atate _(1 Akorinto 15:28)_
👉🏽Kuti timvetsetse izi, yerekezani Yesu ndi Adam
👉🏽Yesu adakhala Adamu wachiwiriyo pofuna kupulumutsa ife ku uchimo
👉🏽Iye adzadzipereka kutumikira Atate zinthu zimene Adamu oyambayo sanachite.
*WEDNESDAY - TSIKU LACHINAYI:*
_*"THUPI LATSOPANO"*_
*1 AKORINTO 15:36-41*
👉🏽Mu ndime iyi👆🏽, Paulo akufotokoza mwachidule za thupi lowukitsidwa
👉🏽Paulo akuyamba uthenga wake waufupi ndi mafunso awiri _(1 Akorinto 15:35):_
🔨1.Akufa aukitsidwa bwanji?
🔨2.Ndipo adza nalo thupi lotani?
👉🏽Mafunsowa akuyankhidwa mu _1 Akorinto 15:36-40_
👉🏽Thupi loukitsidwa ndi limene Yesu adzatipatse tikadzaukitsidwa kwa akufa
👉🏽Paulo wagwiritsa ntchito zitsanzo zitatu pofotokoza zimene zidzachitike pa mdzukiro;
1. Paulo akuyerekeza thupi ndi mbewu
👉🏽Mbewu ikadzalidwa imayenera kufa isanamere
👉🏽 kusintha kumeneku ndi chozizwa cha Mulungu
2. Paulo akufotokoza za mmene Mulungu amaperekera matupi osiyanasiyana kwa anthu ndi nyama
👉🏽Awa ndi matupi amene tikukhala nawo panowa.
👉🏽mu njira yomweyo Mulungu adzatipatsa matupi atsopano kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano
3. Paulo akufotokoza za matupi amene tidzakhale nawo tikadzauka kwa akufa _(1 Akorinto 15:40-42)_
👉🏽Paulo akuti tidzakhala ndi matupi a ulemerero
*THURSDAY - TSIKU LACHISANU:*
_*"CHIGONJETSO CHATHU CHOTSIRIZA KUGONJETSA IMFA"*_
*1 AKORINTO 15:54-57*
👉🏽Mu _1 Akorinto 15:50_ Paulo akubwera ndi Chiphunzitso chachilendo
👉🏽 _*"koma ndinena ichi abale, kuti thupi ndi mwazi sizingathe kulowa Ufumu wa Mulungu........"*_
👉🏽Akhristu ambiri amaganiza kuti Paulo akuti kumwamba tidzakhala anthu opanda matupi
👉🏽Komatu Paulo sakuphunzitsa choncho
👉🏽Mu _1 Akorinto 15:42-49_ Paulo akuyerekeza matupi omwe tili nawowa
👉🏽Ndi matupi amene adzaukitsidwe
👉🏽Matupi omwe tili nawowa anaonongedwa ndi uchimo komanso amafa
👉🏽Koma thupi loukitsidwa lidzakhala lopanda uchimo
👉🏽Komanso lidzakhala lamuyaya _(1 Akorinto 15:50)_
👉🏽Paulo wagwiritsa ntchito mawu oti, _*"thupi ndi mwazi"*_
👉🏽kutanthauza matupi amene tili nawo panowa
👉🏽Ndi chifukwa chake ayenera kusinthidwa mkamphindi pakubweranso kwachiwiri kwa Yesu Khristu
*FRIDAY - TSIKU LA CHISANU NDI CHIMODZI:*
_*"KUOMBA NKOTA"*_
🔨Ambiri mwa anthu a Mulungu anamwalira pamene matupi awo anali odwala
🔨Koma pa nthawi ya mdzukiro adzaukitsidwa Ndi matupi a thanzi Ndi a mphamvu zamuyaya.
*A M E N 🙏*
_Tikukufunirani nonse Sabata lopambana lodzadza ndi madalitso ochokera kwa Yehova Mulungu wakumwamba._
_Ndife abale anu ndi mlongo wanu mwa Khristu Yesu Ambuye wathu;_
*SSLS TEAM:*
*Jimmy HB Njiragoma Phiri*
_+265 888 611 266_
*Hudson Nkumbira Gama*
_+265 888 481 718_
*Mrs Edina Kholowa*
_+258 841 102 715_
*Donald Katete*
_+265 888 598 149_