17/08/2026
๐ ๐๐๐ก๐๐ข ๐๐ ๐๐ก๐ ๐๐๐จ๐๐๐ง๐จ๐ ๐๐๐๐ฅ๐ ๐๐จ ๐ฃ๐๐ง๐๐๐๐ก๐๐๐ฅ ๐๐๐ ๐ฃ๐ข๐ฅ๐๐ ๐ช๐๐๐๐๐
Mlendo amene akuKatumikira ku Pathfinder Camporee yoyamba ya Eastern Malawi Conference wafika mdziko muno. M'busa Bongani Ndlobvu wochokera ku Zimbabwe West Union Conference amene ndi President wa Conference-yi wafika lero kudzera pa Bakili Muluzi International Airport ku Chileka, mu mzinda wa Blantyre.
Wapampando wa achinyamata mu Malawi Union Conference Master Guide Vitumbiko Chijere Chirwa komanso atsogoleri ena a Pathfinder ndi omwe anakachingamira mlendoyu pa bwalo la ndegeli. M'busa Ndlobvu akhala mlaliki ku Camporee yonse.
Eastern Malawi Conference Pathfinder Camporee yayamba dzulo pa 16 August 2026 ndipo itha pa *22 August 2026 ku Mlangeni Campsite, Mangochi. Achinyamata oposa 500 ochokera m'madera osiyanasiyana asonkhana kuti aphunzire za uzimu, luso, ndi umodzi pansi pa mutu wakuti โSTAND STRONGโ.
Atsogoleri ati kufika kwa mlendoyu ndi chizindikiro chakuti Mulungu ali ndi dongosolo lalikulu la mibadwo yachinyamata mu Conference ino. Ma Pathfinder akuyembekezeka kupindula kwambiri ndi maulaliki, masewero olimbitsa thupi, ndi maphunziro omwe akonzedwa sabata yonseyi.
Muchithunzomo, Master Guide Ndlobvu ndi omwe avala sumumba omwe komanso buluku la khaki.
Abusa ambiri kuphatikizapo mtsogoleri wa Eastern Malawi Conference m'busa Master Guide Dr Sanned Lubani ali kuno ku Mangochi.
Wolemba : McAllan Mapinda
EMC Media