Pastor Vincent Mtira

Pastor Vincent Mtira Senior Pastor at Glory to God Ministries (GGM), an interdenominational Ministry, devoted to nurturing souls and building a people grounded in faith and love.

Tsogolo komanso Kuchita bwino m'moyo ndi ulendo. Mau a Mulungu amaphunzitsa mfundo zoyenera kutsatira kuti tikafikire ku...
30/04/2026

Tsogolo komanso Kuchita bwino m'moyo ndi ulendo. Mau a Mulungu amaphunzitsa mfundo zoyenera kutsatira kuti tikafikire kutsogolo komanso Kuchita bwino kwathu.

Loweruka lino tiphunzira za mfundo zoyenera kutsatira kuti tikafikire kutsogolo lathu. Tidzaphunziranso za "Yetser Anointing" kudzodza komwe kumupangitsa Munthu kuchita bwino.

Itanani abale ndi anasi ndipo pangani chiganizo chopezeka mu Service imeneyi ndipo moyo wanu udzapindula kwambiri.

Okondedwa mwa Ambuye, muchilengedwe chonse mulibemo chinthu cha mphamvu kuposa Mawu a Mulungu otsogozedwa ndi mphamvu ya...
24/04/2026

Okondedwa mwa Ambuye, muchilengedwe chonse mulibemo chinthu cha mphamvu kuposa Mawu a Mulungu otsogozedwa ndi mphamvu ya nzimu oyera.

Loweruka lino sindikungophunzitsa Mawu a Mulungu chabe komanso nditsiku limene zinsinsi zokafikira tsogolo lanu zikuvumbulutsidwa.

Bwerani ndipo uzani abale ndi anasi. Moyo wanu upindula koopsa.

18/04/2026

Saturday Service with Pastor Vincent Mtira 📌

Yakobo 5:13 Kodi alipo wina mwa inu amene ali pa mavuto? Apemphere.Tikakumana ndi vuto tiyeni tisachedwe ndi kumangodand...
17/04/2026

Yakobo 5:13 Kodi alipo wina mwa inu amene ali pa mavuto? Apemphere.

Tikakumana ndi vuto tiyeni tisachedwe ndi kumangodandawula, kulira , kapena kufotokozera mtundu wa anthu. Tikakumana ndi vuto,tiyeni tipemphere. Mulungu amalanditsa anthu kumavuto.

Chikhristu sichingatheke popanda Mawu a Mulungu. Loweruka lino ndiphunzitsa pa Mutu woti mphamvu ya Mawu a Mulungu. Ndif...
16/04/2026

Chikhristu sichingatheke popanda Mawu a Mulungu. Loweruka lino ndiphunzitsa pa Mutu woti mphamvu ya Mawu a Mulungu. Ndifotokozera zinthu zogwirika 10 zimene Mawu amulungu amachita akalowa m'moyo wa Munthu.

Ichi ndi chiphunzitso chofunikira kwambiri, itanani abale ndi anasi ndipo bwerani kuti mudzakumane ndi mphamvu ya Mawu a Mulungu.

LINGALIRO LA LERO: 📌 2 Akorinto 4:13 Kwalembedwa kuti, “Ndinakhulupirira; nʼchifukwa chake ndinayankhula.” Popeza ife ti...
14/04/2026

LINGALIRO LA LERO: 📌
2 Akorinto 4:13
Kwalembedwa kuti, “Ndinakhulupirira; nʼchifukwa chake ndinayankhula.” Popeza ife tili ndi mtima womwewo wokhulupirira, ifenso timakhulupirira ndi kuyankhula,

CHILIMBIKITSO: Yakhulani zimene mukukhulupirira osati zimene mukuwona. Zomwe mumayankhula mwa chikhulupiriro ndizimene zimachitika.

KUCHITA MAWU: Lero lonse muyankhule Chimene mukufuna mutachiwona chikuchitika pa moyo wanu mudzina la Yesu khristu

11/04/2026

Saturday Service with Pastor Vincent Mtira | How to Neutralize Curses

❗Join Us for a Special Saturday Service❗Okondedwa, ngakhale Kuti Munthu akalandira Yesu amakhala omasuka kumatemberero, ...
10/04/2026

❗Join Us for a Special Saturday Service❗

Okondedwa, ngakhale Kuti Munthu akalandira Yesu amakhala omasuka kumatemberero, pali zinthu zina zimene zimapangitsabe kuti Munthu apezeke pansi pa mphamvu ya matemberero. Mwazina, mphamvu ya matemberero imapangitsa nyengo kukhala zovuta ndinso kuti zinthu zisamakuyendere bwino.

Lowerukalino, ndikuphunzitsa za zomwe zimapangitsabe akhristu kupezeka pansi pa matemberero komanso momwe tingatulukire mumatemberero ndi kulowa mphamvu ya m'dalitso wa Moyo wathu.

Awuzeni Abale ndi Anansi za Service Yi.

LINGALIRO LA LERO: 📌 -Ndi Abusa Vincent Mtira Maliro 3:37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavo...
09/04/2026

LINGALIRO LA LERO: 📌
-Ndi Abusa Vincent Mtira

Maliro 3:37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?

Pemphero Langa pa Inu: 🙏
Mawu aliwonse athemberero oyankhulidwa ndi oyipa pa moyo wanu, sangakwaniritsike, mudzina la Yesu khristu.

Nanuso Pempherani motelo. Hallelujah

06/04/2026

Easter Conference 2026 | Breakthrough Service | Easter Monday Service

Easter Conference yathu ikutha lero ndipo Service ya Kubowoleza iyamba Nthawi ya 1 Koloko Masana Uno🙏Pali Chisomo chapad...
06/04/2026

Easter Conference yathu ikutha lero ndipo Service ya Kubowoleza iyamba Nthawi ya 1 Koloko Masana Uno🙏

Pali Chisomo chapadeladela chomwe chitasike lero pakati pathu chakubowoleza mmagawo onse a moyo, iyi ndi Imodzi mwa ma service ofunikila kwambiri pa Moyo Wanu.

Chifukwa cha chiwukitso cha Yesu Nkhristu m'manda, mphanvu yachiwukitso yomweyo ifike pa moyo wanu lero ndikuwukisa zomwe zinafa m'moyo mwanu mudzina la Yesu.

Awuzeni ndikwayitanila Abale ndi Anansi!

Moni okondedwa mwa ambuye, tikumaliza nsonkhano wathu wa Easter Lolembalino  ndi service ya chiwukitso ndi kubowoleza. K...
05/04/2026

Moni okondedwa mwa ambuye, tikumaliza nsonkhano wathu wa Easter Lolembalino ndi service ya chiwukitso ndi kubowoleza. Kuyambira 1:00pm- 4:00pm.

Kwa amene tikufuna kubowoleza mugawo lililonse, bwerani ndichikhulupiriro ndipo mudzalandira chosowa chanu.

Address

Blantyre

Telephone

+265888752503

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Pastor Vincent Mtira posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Place Of Worship

Send a message to Pastor Vincent Mtira:

Share