11/09/2025
MMENE MUMAONERA SI MMENE MULUNGU AMAONERA
Mtendere wa Ambuye wathu Yesu Khristu wamoyo kaya Ambuye Yesu akusamalirani bwanji? Kukakhala kuno chisomo chake mchokwanira.
1 Samueli 16:6-7 Ndipo kunali, pakufika iwo, iye anayang'ana pa Eliyabu, nati, Zoonadi, wodzozedwa wa Yehova ali pamaso pace. Koma Yehova ananena ndi Samueli, Vsayang'ane nkhope yace, kapena kutalika kwa msinkhu wace, popeza Ine ndinamkana iye; pakuti Yehova saona monga aona munthu; pakuti munthu ayang'ana cooneka ndi maso, koma Yehova ayang'ana mumtima.
Okondedwa tikuona Samueli akupita mmudzi ufuna kukasankha mfumu monga momwe anamulamulira Yehova, komatu posankha iye amayang'ana mwa thupi monga mwa maonekedwe koma Yehova akuwakana . Dziwani kuti mmene munthu amaonera si mmene Mulungu amaonera ayi, munthu amangoyang'ana za kunja kokha koma Mulungu amathanso kuyang'ana za mumtima. Anthu ambiri timaluza zinthu zabwino chifukwa chofera maonekedwe, azibambo ambiri akuvutika mmabanja anakwatira mkazi osatha kuphika ngakhale ndi kuchapa komwe kufera maonekedwe, dziwani kuti ngakhale botolo la mowa litakongola koma mkatimo muli zoipa basi, ena anakwatiwa ndi mamuna omenya kufera handsome lero akuzunzika ndi ululu ,ena chifukwa ndi handsome nthumba sanadziwe kuti ndalamazo ndi zokhwimira pano akuvutika kusambitsa njoka ....Ambuye atithandize dziwani mmene inu mumaonera si mmene Mulungu amaonera ayi, ambiri akunong'oneza bondo chifukwa makolo amkawauza koma kusamva.
1 Samueli 16:11-12 Ndipo Samueli anati kwa Jese, Ana anu ndi omwewa kodi? Nati iye, Watsala wina, mng'ono wa onse, ndipo taonani, iye alikuweta nkhosa. Ndipo Samueli anati kwa Jese, Tumiza munthu akamtenge; pakuti ife sitidzakhala pansi kufikira iye atadza kuno. Ndipo anatumiza munthu, nabwera naye. Tsono iye anali wofiirira, ndi wa nkhope yokongola, ndi maonekedwe okoma. Ndipo Yehova anati, Nyamuka umdzoze, pakt ndi ameneyu.
Zindikirani kuti Mulungu amagwiritsa ntchito zinthu zooneka zopanda pake koma amazilemekeza,
099729921 Jones KACHULU