Child of God

Child of God To spread the word of salvation and Revelation and also to spread the word of God and the coming of Jesus christ

26/07/2026

KUOPSA KOONERERA MAPORNOGRAPHY ( ZOLAURA)⚠️⚠️⚠️

🔴 Zolaula kapena mapor nography
👉Ndi mabuku, zithunzi, mavidiyo,,,,,,etc omwe amafotokoza kapena kuonetsa anthu osavala (aumaliseche) ndi mchitidwe wogonana pofuna kumpanga munthu kuti akopeke ndi zinthuzo ndikuti zilakolako zake zikathe kukulitsidwa.

👉 Mavidiyo ndi zinthuzi zambiri zolaura zimapangidwa ndi akumidima pofuna kugwetsa ndi kuononga akhristu komanso miyoyo yochuluka . Anthu ambiri akukathera kumoto(Hell) chifukwa Cha kuonera zolaura( mapornography)

👉Ma internet page monga ###, XNXX , XVIDIOS, WAPTRICK,,,,,ndi ena otero onsewa anapangidwa ndi akumidima ndipo akupanga zithunzi, Mavidiyo ndi zinthu Zina zolaura ngati chida chimodzi champhamvu chogonjetsera akhristu ochuluka.

^_^ Palnso ena omwe amajambula ena amalemba zolaura KOMA iwo sakudziwa kuti ali m'bugwe la satana ndipo satana akuwagwiritsa ntchito.

👂M'zolaura muli chiwanda champhamvu chomwe chimatchedwa kuti *ma********on spirit* chiwandachi chikakhala mwa munthu chimampanga munthu kuti azibunyula (ma******te) . Ukundiko kuseweretsa mariseche.

😭😭😭 Anthu ambiri lero akumaseweretsa maliseche, indedi akhristu ochuluka lero akumaseweretsa maliseche 😭😭😭

😮Kodi kuseweretsa mariseche ndikutani??

•pali mafotokozedwe ambiri monga m'nyamata ndikufotokoza ; kuseweretsa mariseche ndiko kutaya mas***m (umuna)
😭😭😭

•umakhala kuti uli ndichilakolako Cha Mphamvu chofuna kupanga chigololo, ndiye basi umayamba kutaya ma s***m pansi, limene lilitchimo, m***a kuwerenga (📖Geneses 38:8-10) pakupezeka nkhani inayake ya ana awiri a Yuda , Mwana woyamba anali Eli wachiwiri anali Onani, Ndiyeno Eli anafa nasiya Mkazi ndipo Yuda anauza Onani kuti tenga Mkazi wa M'bale wako um'balire ana M'bale wako , kuti dzina lake lake lisafafanizidwe mu Israeli. Ndipo Onani panthawi yomwe anali kugona ndi Mkazi wa M'bale wake anali kutaya pansi mas***m(umuna) kapena mbeu, kuti Mkazi uja asakhale ndi mwana , ndipo mapeto ake Mulungu anamupha Onani.

29/06/2026

*Kudziwike kuti kuli Mulungu kunjaku oyankha mapemphero* !!

*Mulungu aike poponderapo Mdalitso wako mu tsiku lalero.*

*Mulungu akupatse chisomo chako chikhale chapaderadera.

Mulungu achititse manyazi onse olondora tsogolo lako.

Mulungu azilemekeze yekha mu nyengo zako ndipo* akupambanitse mmaysero ena onse obwera moyo wako!

01/06/2026

*CHIPHUNZITSO CHA TSIKU NDI TSIKU ⏰*

Machitidwe 4:31📖 akuti, “Ndipo pamene anapemphera, malo amene anasonkhanamo anagwedezeka, ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, napitiriza kulankhula mawu a Mulungu molimba mtima.” (Machitidwe 4:31)📖 Chimodzi mwa mavumbulutso amphamvu kwambiri mu vesili ndi chakuti mpingo woyambirira sunapemphere kuchokera mu mantha, kusadzidalira, kapena kusatsimikiza za chikondi cha Mulungu pa iwo. Anapemphera ndi chidaliro chifukwa ankadziwa kuti Yesu anali atatsegula kale njira yoti ayandikire Mulungu molimba mtima kudzera mu ntchito Yake yomalizidwa pa mtanda.
Maziko a vesili ndi ofunika kwambiri. Ophunzira aja anali atangowopsezedwa chifukwa cholalikira Yesu Khristu. Atsogoleri achipembedzo ankafuna kuwachepetsa ndi kuwatsekereza pakulankhula. Kupanikizika kunali kukuwonjezeka. Kuzunzidwa kunali kukukulirakulira.

Koma m'malo mobwerera m’mbuyo chifukwa cha mantha, anasonkhana pamodzi ndipo anapemphera ndi chidaliro. Izi zokha zikuwonetsa china chake champhamvu chokhudza zomwe kuuka kwa Yesu kunabala mkati mwawo.
Onani zomwe sanapemphe. Sanapemphe kuti, “Mulungu, chonde tikondeni kwambiri.” Sanapemphe kuti, “Mulungu, chonde tilandireni ngati tachita bwino mokwanira.” Iwo ankadziwa kale kuti anali a Mulungu kudzera mwa Yesu Khristu. Pemphero lawo linachokera mu ubale, osati mu kusadzidalira.

Chimodzi mwa mavumbulutso akuya kwambiri mu Machitidwe 4:31📖 ndi kumvetsa kuti Mzimu Woyera amabala kulimba mtima, osati mantha. Asanauke Yesu kwa akufa, ambiri mwa ophunzira omwewa anali kubisala, ali ndi mantha, osokonezeka, komanso osakhazikika. Petro mwiniwake anakana Yesu katatu chifukwa cha mantha. Koma atakumana ndi Khristu wouka kwa akufa ndi kulandira Mzimu Woyera, zonse zinasintha. Mzimu wa Mulungu anasandutsa anthu amantha kukhala mboni zolimba mtima za Yesu Khristu. (2 Timoteyo 1:7)📖

Kugwedezeka komwe kunachitika mu vesili sikunali kwa chisangalalo cha m’maganizo kapena machitidwe achipembedzo. Kunali um

22/04/2026

MATEYU 15 : 19

**Pakuti mumtima muchokera maganizo oipa, zakupha, zachigololo, zachiwerewere, zakuba, za umboni wonama, zamwano;*

*izi ndizo ziipitsa munthu, koma kudya osasamba manja sikuipitsa munthu ai.*

________________________________________________________________________

*Kodi mtima wanu ndi OTANI nanga mumatuluka zotanii???*

Ngati nthawi zambiri mukakhala mumalingalira zosalongosoka,
Nkhawa, madandaulo, kuziimba milandu nokha kapena kumangomuda aliyense

*Dziwani kuti mukufunika mamasulidwe chifukwa mtima ndi ubongo wanu ndi zomangidwa ndi matcheni ASATANA*

*Pezani nthawi ya KUSALA KUDYA ndikupemphera kuti muumasulidwe ku zimenezi, ngati mwapemphera komabe sizikutha, pezani azitumiki amene amalalikira za ufumu wamulungu ndi mitima yoona kuti akuthandizeni mbali yosalayo*

Ambuye akudalitseni kwambiri

*  KUNENA ZIKOMO KWA AMBUYE #*Abale wanga mwa ambuye Kodi Mukudziwa kuti mau oti ZIKOMO pamaso pa Mulungu ndi ulemu wauk...
21/04/2026

* KUNENA ZIKOMO KWA AMBUYE #*

Abale wanga mwa ambuye Kodi Mukudziwa kuti mau oti ZIKOMO pamaso pa Mulungu ndi ulemu waukuru kwambiri???

zindikirani lero kuti mukathokoza pamaso pa Mulungu chifukwa cha zabwino zimene wakuchitilani zimapereka ulemelero waukulu kwambiri pamaso pake kusiyana ndi KUPEMPHA.

Ngati mukudziwa kuti muli ndi moyo chifukwa cha ambuye chonde nenani ZIKOMO, inu muli pabanja koma anzanu banja akulisowa tanenani ZIKOMO, inu muli ndi mtendere koma anzanu mtendere alibe nenani ZIKOMO, muli pa ntchito koma anzanu ntchito akuisowa nenani ZIKOMO, anzanu munabadwa Nawo limodzi lero kulibe ambuye anawatenga mwachangu Kodi simunganene ZIKOMO??, MWA anzanu onse amene munaphunzira Nawo inu nokha ndinu munalembedwa ntchito mukuchedweranji kunena ZIKOMO?

OLO mulibe BANJA, ntchito business, ana, NDALAMA, kapena mukudwala, kapena sizikuyenda, KAPENA anthu amangokudani komabe mulinacho chifukwa chakunena ZIKOMO pamaso pa Mulungu,, chifukwa choti moyo wanu ndi m'dalitso kale.

muwerenge Luka 17:11-19 MASALMO 92:1 MASALMO 103:1-4.

AMBUYE YESU LERO MUKUMBUKILE ANA ANU ALIYENSE AMENE WANENA * # KWA INU # #* NDIPO MUKWANILITSE CHOSOWA CHAKE CHIFUKWA WINA AKUNENA ZIKOMO KOMA AKUDUTSA MUNYENGO ZOWAWA CHONDE MKUMBUKILENI NDIKUMULEMBA DZINA LAKE M'BUKU LA MOYO SOPANO.

Ambuye akudaliseni nonse ana Mulungu wa Moyo.

TIKUMANE PA 31 DECEMBER KWA INU NONSE OKHALA M'BOMA LA THYOLO NDI MADERA OZUNGULIRA
18/12/2025

TIKUMANE PA 31 DECEMBER KWA INU NONSE OKHALA M'BOMA LA THYOLO NDI MADERA OZUNGULIRA

*CHIDZIWITSO CHA PADERA KOMANSO PEMPHO KWA NONSE OMWE M'MADALISIKA NDI NYIMBO ZA PASTOR FYSON!**MOTHANDIZIDWA NDI AMBUYE...
18/12/2025

*CHIDZIWITSO CHA PADERA KOMANSO PEMPHO KWA NONSE OMWE M'MADALISIKA NDI NYIMBO ZA PASTOR FYSON!*

*MOTHANDIZIDWA NDI AMBUYE YESU NKHILISTU MNAZALAYO INE PASTOR FYSON NDIKHALA NDIKUCHITA LAUNCH NDIKUTULUTSA ALBUM YANGA YA TSOPANO YACHITATU, KUCHOKERA PAMUTU WOTI: (YESU AKUBWERA)*

*CHONCHO ITULUKA PA 01 JANUARY 2026 MAMAWA IKAZANGOTHA OVER NIGHT YOCHOKA KU 31 DECEMBER*

*MWAICHI NDIKUPEMPHANI MWA ZISOMO ZA AMBUYE KUCHITA SUPPORT NYIMBO ZIMENEZI KUTI TIJAMBULENSO ZINA POSACHEDWAPA, NDIPO PA TSIKULI KUKAKHALA MA FLASH A NYIMBO ZIMENEZI KOMANSO MA MEMORY CARD NDIPO MEMORY CARD YA NYIMBOYI IZIKAGULISIDWA PA MTENGO WA K7000 KOMANO INU MUNGATHE KUKACHITA MOPOSERA APO MALINGANA NDI KUKHUMBA KWA M'TIMA WANU*

*KWA OMWE MULI KUTALI NDIPO SIMUNGATHE KUFIKA, MUKHONZA KUTENGAPONSO MBALI PA LAUNCH IMENEYI POTHANDIZIRA NDI KANGACHEPE KANU NDIPO NYIMBO MUZALANDIRA KUZERA PA PHONE YANUYO MU NJIRA YA WHATSAPP*

KUMBUKILANI KUTI NYIMBO ZA PASTOR FYSON SIZIMAGULISIDWA NDIPO NTHAWI ZONSE ANTHU AMALANDIRA KWA ULELE KOMANO IYI NDI Launch yofuna kupeza THANDIZO kuti tijambulenso album ina posachedwapa. Munkhonza kugwiritsa ntchito ma number awa pofuna kuthandizira album launch imeneyi 0884453937/0993982982 akatero nyimbo zanu muzalandira.
Ambuye akudaliseni kwambiri

Address

Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Child of God posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share