Child of God

Child of God To spread the word of salvation and Revelation and also to spread the word of God and the coming of Jesus christ

22/04/2026

MATEYU 15 : 19

**Pakuti mumtima muchokera maganizo oipa, zakupha, zachigololo, zachiwerewere, zakuba, za umboni wonama, zamwano;*

*izi ndizo ziipitsa munthu, koma kudya osasamba manja sikuipitsa munthu ai.*

________________________________________________________________________

*Kodi mtima wanu ndi OTANI nanga mumatuluka zotanii???*

Ngati nthawi zambiri mukakhala mumalingalira zosalongosoka,
Nkhawa, madandaulo, kuziimba milandu nokha kapena kumangomuda aliyense

*Dziwani kuti mukufunika mamasulidwe chifukwa mtima ndi ubongo wanu ndi zomangidwa ndi matcheni ASATANA*

*Pezani nthawi ya KUSALA KUDYA ndikupemphera kuti muumasulidwe ku zimenezi, ngati mwapemphera komabe sizikutha, pezani azitumiki amene amalalikira za ufumu wamulungu ndi mitima yoona kuti akuthandizeni mbali yosalayo*

Ambuye akudalitseni kwambiri

*  KUNENA ZIKOMO KWA AMBUYE #*Abale wanga mwa ambuye Kodi Mukudziwa kuti mau oti ZIKOMO pamaso pa Mulungu ndi ulemu wauk...
21/04/2026

* KUNENA ZIKOMO KWA AMBUYE #*

Abale wanga mwa ambuye Kodi Mukudziwa kuti mau oti ZIKOMO pamaso pa Mulungu ndi ulemu waukuru kwambiri???

zindikirani lero kuti mukathokoza pamaso pa Mulungu chifukwa cha zabwino zimene wakuchitilani zimapereka ulemelero waukulu kwambiri pamaso pake kusiyana ndi KUPEMPHA.

Ngati mukudziwa kuti muli ndi moyo chifukwa cha ambuye chonde nenani ZIKOMO, inu muli pabanja koma anzanu banja akulisowa tanenani ZIKOMO, inu muli ndi mtendere koma anzanu mtendere alibe nenani ZIKOMO, muli pa ntchito koma anzanu ntchito akuisowa nenani ZIKOMO, anzanu munabadwa Nawo limodzi lero kulibe ambuye anawatenga mwachangu Kodi simunganene ZIKOMO??, MWA anzanu onse amene munaphunzira Nawo inu nokha ndinu munalembedwa ntchito mukuchedweranji kunena ZIKOMO?

OLO mulibe BANJA, ntchito business, ana, NDALAMA, kapena mukudwala, kapena sizikuyenda, KAPENA anthu amangokudani komabe mulinacho chifukwa chakunena ZIKOMO pamaso pa Mulungu,, chifukwa choti moyo wanu ndi m'dalitso kale.

muwerenge Luka 17:11-19 MASALMO 92:1 MASALMO 103:1-4.

AMBUYE YESU LERO MUKUMBUKILE ANA ANU ALIYENSE AMENE WANENA * # KWA INU # #* NDIPO MUKWANILITSE CHOSOWA CHAKE CHIFUKWA WINA AKUNENA ZIKOMO KOMA AKUDUTSA MUNYENGO ZOWAWA CHONDE MKUMBUKILENI NDIKUMULEMBA DZINA LAKE M'BUKU LA MOYO SOPANO.

Ambuye akudaliseni nonse ana Mulungu wa Moyo.

TIKUMANE PA 31 DECEMBER KWA INU NONSE OKHALA M'BOMA LA THYOLO NDI MADERA OZUNGULIRA
18/12/2025

TIKUMANE PA 31 DECEMBER KWA INU NONSE OKHALA M'BOMA LA THYOLO NDI MADERA OZUNGULIRA

*CHIDZIWITSO CHA PADERA KOMANSO PEMPHO KWA NONSE OMWE M'MADALISIKA NDI NYIMBO ZA PASTOR FYSON!**MOTHANDIZIDWA NDI AMBUYE...
18/12/2025

*CHIDZIWITSO CHA PADERA KOMANSO PEMPHO KWA NONSE OMWE M'MADALISIKA NDI NYIMBO ZA PASTOR FYSON!*

*MOTHANDIZIDWA NDI AMBUYE YESU NKHILISTU MNAZALAYO INE PASTOR FYSON NDIKHALA NDIKUCHITA LAUNCH NDIKUTULUTSA ALBUM YANGA YA TSOPANO YACHITATU, KUCHOKERA PAMUTU WOTI: (YESU AKUBWERA)*

*CHONCHO ITULUKA PA 01 JANUARY 2026 MAMAWA IKAZANGOTHA OVER NIGHT YOCHOKA KU 31 DECEMBER*

*MWAICHI NDIKUPEMPHANI MWA ZISOMO ZA AMBUYE KUCHITA SUPPORT NYIMBO ZIMENEZI KUTI TIJAMBULENSO ZINA POSACHEDWAPA, NDIPO PA TSIKULI KUKAKHALA MA FLASH A NYIMBO ZIMENEZI KOMANSO MA MEMORY CARD NDIPO MEMORY CARD YA NYIMBOYI IZIKAGULISIDWA PA MTENGO WA K7000 KOMANO INU MUNGATHE KUKACHITA MOPOSERA APO MALINGANA NDI KUKHUMBA KWA M'TIMA WANU*

*KWA OMWE MULI KUTALI NDIPO SIMUNGATHE KUFIKA, MUKHONZA KUTENGAPONSO MBALI PA LAUNCH IMENEYI POTHANDIZIRA NDI KANGACHEPE KANU NDIPO NYIMBO MUZALANDIRA KUZERA PA PHONE YANUYO MU NJIRA YA WHATSAPP*

KUMBUKILANI KUTI NYIMBO ZA PASTOR FYSON SIZIMAGULISIDWA NDIPO NTHAWI ZONSE ANTHU AMALANDIRA KWA ULELE KOMANO IYI NDI Launch yofuna kupeza THANDIZO kuti tijambulenso album ina posachedwapa. Munkhonza kugwiritsa ntchito ma number awa pofuna kuthandizira album launch imeneyi 0884453937/0993982982 akatero nyimbo zanu muzalandira.
Ambuye akudaliseni kwambiri

11/09/2025

MMENE MUMAONERA SI MMENE MULUNGU AMAONERA

Mtendere wa Ambuye wathu Yesu Khristu wamoyo kaya Ambuye Yesu akusamalirani bwanji? Kukakhala kuno chisomo chake mchokwanira.

1 Samueli 16:6-7 Ndipo kunali, pakufika iwo, iye anayang'ana pa Eliyabu, nati, Zoonadi, wodzozedwa wa Yehova ali pamaso pace. Koma Yehova ananena ndi Samueli, Vsayang'ane nkhope yace, kapena kutalika kwa msinkhu wace, popeza Ine ndinamkana iye; pakuti Yehova saona monga aona munthu; pakuti munthu ayang'ana cooneka ndi maso, koma Yehova ayang'ana mumtima.

Okondedwa tikuona Samueli akupita mmudzi ufuna kukasankha mfumu monga momwe anamulamulira Yehova, komatu posankha iye amayang'ana mwa thupi monga mwa maonekedwe koma Yehova akuwakana . Dziwani kuti mmene munthu amaonera si mmene Mulungu amaonera ayi, munthu amangoyang'ana za kunja kokha koma Mulungu amathanso kuyang'ana za mumtima. Anthu ambiri timaluza zinthu zabwino chifukwa chofera maonekedwe, azibambo ambiri akuvutika mmabanja anakwatira mkazi osatha kuphika ngakhale ndi kuchapa komwe kufera maonekedwe, dziwani kuti ngakhale botolo la mowa litakongola koma mkatimo muli zoipa basi, ena anakwatiwa ndi mamuna omenya kufera handsome lero akuzunzika ndi ululu ,ena chifukwa ndi handsome nthumba sanadziwe kuti ndalamazo ndi zokhwimira pano akuvutika kusambitsa njoka ....Ambuye atithandize dziwani mmene inu mumaonera si mmene Mulungu amaonera ayi, ambiri akunong'oneza bondo chifukwa makolo amkawauza koma kusamva.

1 Samueli 16:11-12 Ndipo Samueli anati kwa Jese, Ana anu ndi omwewa kodi? Nati iye, Watsala wina, mng'ono wa onse, ndipo taonani, iye alikuweta nkhosa. Ndipo Samueli anati kwa Jese, Tumiza munthu akamtenge; pakuti ife sitidzakhala pansi kufikira iye atadza kuno. Ndipo anatumiza munthu, nabwera naye. Tsono iye anali wofiirira, ndi wa nkhope yokongola, ndi maonekedwe okoma. Ndipo Yehova anati, Nyamuka umdzoze, pakt ndi ameneyu.

Zindikirani kuti Mulungu amagwiritsa ntchito zinthu zooneka zopanda pake koma amazilemekeza,
099729921 Jones KACHULU

07/09/2025

TSIKU LINALAKE LIDZAKHALA LOMALIZA TIDZAFUNE TISADZAFUNE

AMAYI ABAMBO NYAMATA MSUNGWANA KODI WAKONZA UBARE WAKO.NDIMULUNGU

DZIWANITU KUNALEMBEDWA KUTI
Luka 12:9 koma iye wondikana ine pamaso pa anthu, iye adzakanidwa pamaso pa angelo a Mulungu.

MUKUWONEKA OCHENJERA LERO MUKUMKANA MULUNGU KAMBA KAMACHITIDWE ANU KOMATU TSIKULINA LIDZAKHALA LOYAMBA KULIRA KOMA KOSALEKEZA MUCHIZUNZO CHOOPSA KOMA PANO.
MUKAMAMVA MAWU AMULUNGU KUMAWATENGA NGATI OPANDA PAKE KOMATU TSIKU LINALAKE MUDZAMFUNA MULUNGU KOMA DNTHAWI IDZAKHALA KUTI YATHA

Mlaliki : 8 :8-8
8. Palibe munthu amene ali ndi mphamvu yolamulira mpweya wa moyo kuti athe kuwusunga, choncho palibe amene ali ndi mphamvu pa tsiku la imfa yake. Nkhondo sithawika; tsono anthu ochita zoyipa, kuyipa kwawoko sikudzawapulumutsa.

Ahebri 9:27 Ndipo popeza 8 kwaikikatu kwa anthu kufa kamodzi, ndipo 9 atafa, ciweruziro;

MULUNGU WAPEREKA NTHAWI KWAM'BALE IWE CHITA CHANGU KUKONZA MOYO WAKO

MUNALI NDIINE KAPOLO NZANU KUCHENJEZABE KUTI OGONAYO ADZUKE MALINGANA NDINTHAWI

0996729921

06/09/2025

KUSIYANA KWA AMOYO NDI AKUFA*

*Dziwani okondedwa kuti munthu yemwe wafa sangalape,ngakhale titapempherela mwezi wonse Sizingatheke kuti akhale wolungama ngati munthuyo anafa ndi Uchimo*

*Uthenga ukamalalikidwa umapita kwa amoyo,ndipo womwalira sanganene AMEN Kuti wamva Uthenga womwe walalikidwa pa maliro ake,koma amoyo.choncho ife amoyofe tiyeni pomwe tikumva tilape,chifukwa likubwera tsiku lomwe tidzakhale akufa ndipo mwayi wolapa sudzapedzeka.*

*Chifukwa akufa salemekedza Yehova komanso wakufa sadziwa kanthu Bii,lapa pomwe ulimoyo ndikufa chidzudzulo AMEN*

Uthenga ukafika ulaswa Moyo musati awa amandikhumba ayi chachikulu ndi kungolapa basi.... bible limati Ngati wamva mau musaumitse mtima muloleranji kufa mmachimo Anu?

Sizoti anthu akamadzudzula tchimo Amakhala kumwamba akukanizako kapena akukukanizani zabwino zapadzikoli ayi Koma amakufunirani zabwino Kuti pokutha pa Moyo uno mukapeze Moyo osatha

Mwayi muli nawo lero wa kulapa dziwani za mawa sizimadziwika

Dziwani Kuti palibe kodetsa kadzalowe mu ufumu wa Mulungu analipo ena amkati ndilapa mawa Koma zachsoni mawa sanafike lingalirani za Moyo wanu lero

*MUKUDZIWA CHANI ABWENZI*

Pena ukadya mmawa,kudya masana,,kudwala sukudwala,ndalama nthumba zilimo

Pena mtima umakunamiza kuti zinthu zilibwino,,ndipo zimaoneka ngati kwina kulikonse zilibwino.

Lingalirani za Moyo wanu pakuti tsiku lokutengani Mulungu simukulidziwa

AMBUYE AKUDALITSENI NONSE
M'BALE WANU MWA AMBUYE JONES KACHULU

0996729921 kuti mupezeke pa ma group athu a pa whatsapp

06/09/2025

CHIFUKWA CHANI MPEPHERO LANU SILIKUYAKHIDWA?.

KOMA ZOIPA ZANU ZAKULEKANITSANI INU NDI MULUNGU WANU NDIPO MACHIMO ANU ABISA NKHOPE YAKE KWA INU KUTI IYE SAKUMVA. YESAYA 59: 2.

PAMENE TIKUFIKA PAMASO PA MULUNGU TIONESESE TALAPA MACHIMO ATHU CHIFUKWA KWALEMBEDWA PALIBE OLUGAMA INDE PALIBE MODZI OLUGAMA AROMA 3:10.
KWALEMBEDWA TIZIKHALA OYERA POPEZA MULUNGU WATHU NDI OYERA 1PETRO 1:16
CHONDE TIKAMAFIKA PAMASO PAMULUNGU CHONDE TILAPE MCHIMO LILILONSE NDIPO TIKALAPA TISACHIMWENSO .
KOMA SUNGANI CHIRICHONSE CHIMENE MULUNGU ANAKUUZANI .NDIPO MULUNGU NDI OKONZEKA KUYAKHA MPEPHERO LAKO.
NGATI UKUONA KUTI YAKHO LAKO LACHEDWA DIKIRABE PA MULUNGU CHIFUKWA SACHEDWA SAFULUMIRA.

KAPENA PANGANI FASTING MULUNGU AYAKHA NDITHU MPEPHERO LANU KOMANSO ONESESANI KUTI ZOPEMPHA ZANU ZOBVOMEREZEKA PAMASO PA MULUNGU OSATI KUMUYESA.

BVUTO LOMWE MUKUDUTSAMOLO MULUNGU AYAKHA NKHALANI NDI CHIKHULUPIRIRO BASI PEMPHERANI KOSALEKEZA .

LIMBIKANI MWA MULUNGU CHOONADI CHIFUKWA NDI CHOVALA CHOMWE MULUNGU AMAFUNA.NDIPO MAPEMPHERO ATHU AZAYAKHIDWA MOSAVUTA.
LAPANI MACHIMO ANU KUTI MULANDIRE CHISOMO CHA AMBUYE WATHU YESU KHRISTU NDI MPHAMVU YA MZIMU OYERA. POPEZA YESU KHRISTU AKUBWERA POSACHEDWA.

MTENDERE WA AMBUYE WATHU YESU KHRISTU UKHALE NANU.
M'BALE WANU MWA AMBUYE JONES KACHULU 0996729921

06/09/2025

NDILAPABE UJA WAMWALIRA

Chichewa Bible

“Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”

Marko 1:15

Nthawi ndiye yatha, ufumu wa kumwamba wayandikira, zizindikiro zikuoneka ndi maso, maliro tsiku ndi tsiku, ngozi zili ponse ponse. Zonse izi zikutibweretsera ponena kuti tikhale okonzeka ndinso osamala.

Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino umene atumiki a Mulungu akutumikira lero, tikhale ngati anamwali ochenjera asanu amene anasunga mafuta kuti aonjezere. Zinali zowawa kuti anamwali asanu oyamba aja anazisunga kwa zaka zambiri koma mwatsoka anakopeka mtima ndi za nziko ndipo analephera kusunga chiyero chawo, mmalo mwake anaonongeka, sanazisungire mafuta kuti nyali zawo zikazima athe kuonjezera ndi kuyatsanso.

Ndilapabe uja wamwalira!! Mkutheka kuti uthenga wabwino mukulalikidwa tsiku ndi tsiku pa radio, pa phone, pa kanema, ku msika koma inu mukuti ndidyerere kaye ndizalapabe. Pamene ukuti ndizalapabe ukukhala ngati munthu wachuma uja amene anati lero ndi tsiku langa loti ndisangalare ndivine ndi anzanga ndipo timwerere osadziwa kuti akamaliza chisangalalo chake imfa ikumutenga usiku omwewo ndipo kumwamba ku kunena kuti kapolo opusa iwe ukanadziwa kuti usiku uno moyo wako utengedwa sibwenzi utapanga zimene wachita iwezo kapolo opusa iwe. Ndilapabe uja wamwalira.!!!

Ambiri tilipo lero tili ngati munthu mwini chuma uyu amene zosangalatsa za pa dziko lino lapansi ndiye kudya kwanu, amene mtendere wanu wadzadza ku ma bwalo onyoza, amene chuma chanu chimathandizira zoipa basi. Pamene chisangalalo chachuluka mpamene imfa ikugogoda, ndilapabe uja wamwalira.

Palibe akudziwa tsiku la imfa yake kuti lidzakhala lotani/ Chimaliziro chake chidzakhala motani?
Kunali kwabwino lero kt tiyende okonzeka tisunge mafuta mu nyali zathu kuti ngati angabwere modzidzimutsa tizatha kugwiritsa ntchito mafuta amene tasunga aja pakuti nthwi ndye yatha.
AMBUYE AKUDALITSEN
M'BALE WANU MWA AMBUYE JONES KACULU0996729921

01/09/2025

KUNJA KUMACHA NGAKHALE MDIMA UNGAKULE BWANJI MAWA LIMAFIKA

MUSADERE NKHAWA ZA MAWA CHIFUKWA ZA MAWA AMADZIWA NDI MULUNGU LERO TADZUKASO NDI CHIMWEMWE NDI UMBONI OGWIRIKA

yeremiya 29:11 pakuti ndidziwa malingaliro amene ndilingiririra inu ati yehova, malingaliro a mtendere si a choipa akukupatsani inu adzukulu chiyembekezo.

Okondedwa ngati anthu tikusautsika lero ndi Chifukwa cha tsogolo lathu limene sitinalifike komaso sitimadziwa kuti tidzafikako, kuphunzira konseku mpaka kukafika kunja kuti mtsogolo adzakhale abwana, kusiya ntchito ya Mulungu kumapita maiko ena konseku kufuna kukapeza Mtendere wa mtsogolo, kumana anthu zakudyaku kumalingalira kuti nanga mawa ine ndidzatani ukatha?

Okondedwa Mulungu akupereka chiyembekezo, Akuti akuziwa malingaliro anu Ndipo Ali ndi ma plan abwino amoyo wanu ngakhale ndi zidzukulu zanu zomwe, malingaliro a mtendere si a choipa Ayi koma anthu talephera kukhulupirira ndi kumumvetsa Mulungu.

Lero anthu akujomba ku church kupita kukapanga business kufuna chakudya cha tsiku lina, lero anthu akuphana kufuna zinthu za tsiku lina Ali ndi chimanga chilichonse Ali nacho dzanja lili PA tsaya kulingalira kuti fertilizer akamutenga kuti? Okondedwa musadere nkhawa Mulungu akulonjeza kuti Ali nawo malingaliro a mtendere si a choipa ayi pamoyo wanu

Mwina mwana wasankhidwa ku secondary koma fees sikudziwika kuti ichokera kuti? Mwina muli ndi ulendo ofunikira koma transport simukudzwa ichokera kuti? Mwina muli ndi nkhawa yanji komatu Mulungu ali nawo ma plan abwino amoyo wanu dziwani kuti kukusungani ndi moyo wakusungani ndi cholinga,

Afilipi 4:6 musadere nkhawa, chachikulu mudalire Mulungu Chifukwa Ali ndi ma plan abwino a moyo wanu, ena mwina ntchito yatha, banja akuthamangitsani Chifukwa chosowa mwana, ena abale akuthamangitsani mu dzina LOTI akusungani kwakwana, dziwani kuti Mulungu Sataya wake Ndipo zonse zachitika ndi cholinga kuti ukulu wake uwoneke komanso dziko lidziwe kuti Kuli MULUNGU

0996729921

Address

Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Child of God posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share