23/05/2026
*YOTSOGOLERA LERO 23 MAY 2026*
Genesis 37:18 Abale ake aja anamuonera patali. Ndipo asanafike nʼkomwe kumene kunali iwo kuja, anayamba kale kumupangira chiwembu choti amuphe.
*Ukamamva kuwawa ndi chipambano cha munthu wina dziwa kuti uli ndi nsanje, kaduka ndi nkhwidzi ndi munthuyo. Ukamakondwera kuchokera pansi pa mtima wina akamachita bwino, ndiye kuti mwa iwe mulibemo nsanje, kaduka ndi nkhwidzi. Abale ake a Yosefe amamva kuwawa ndi maloto ake mpaka anamugulitsa chifukwa cha nsanje, kaduka ndi nkhwidzi. Palibe choipa chimene Yosefe adachitira abale kuti mpaka aganize zomupha kenako ndi kumugulitsa ngati kapolo. Nsanje, kaduka ndi nkhwidzi zimapha. Samala ndi anthu owawuza maloto, mapulani ndi chipambano, kuwopa ungauze anthu a nsanje, kaduka ndi nkhwidzi. Anthu a nsanje palibe chaphindu chimene amachita. Paja nkhuku ya nsanje simaswa. Abale ake onse a Yosefe palibepo amene anapanga chaphindu. Chifukwa nsanje, kaduka ndi nkhwidzi zimakodola matemberero, masoka ndi minyama. Lekani nsanje, kaduka ndi nkhwidzi kuti musaphe tsogolo lanu. Celebrate the success of others while you are praying and working hard for your success. “Ambuye Yesu ndimasuleni ku nsanje, kaduka ndi nkhwidzi. Amen!”*
Mukhale ndi Loweruka Lopambana
*Bishop WJ Ching’amba 0884507838/0999201500 Chilobwe Assemblies Of God*