10/08/2026
*VESI YOTSOGOLERA LERO 10 AUGUST 2026*
CHIVUMBULUTSO 14:13 Ndipo ndinamva mau ochokera Kumwamba, ndi kunena, Lemba, Odala akufa akumwalira mwa Ambuye, kuyambira tsopano; inde, anena Mzimu, kuti akapumule ku zolemetsa zao; pakuti ntchito zao zitsatana nao pamodzi.
*Kumwalira uli mwa Ambuye ndiko kumwalira Ambuye Yesu ali mpulumutsi wamoyo wako. Ukamwalira uli mwa Ambuye umakapumula ku zolemetsa za moyo uno. Koma ukamwalira usali mwa Ambuye umakakumana ndi Gahena. Kumwalira usali mwa Ambuye ndiko kumwalira usanalape machimo ndi kulandira Yesu kukhala mpulumutsi wamoyo wako. Ndi chinthu choopsa kwambiri kumwalira usali mwa Ambuye. Lapani machimo anu zenizeni, landirani Yesu kukhala mpulumutsi wamoyo wanu. Kuti mutamwalira lero kapena tsiku lina lirironse muzakhale odala kuti mukapumule ku zolemetsa za moyo uno. “Lero ndi kulapa machimo anga onse, Ambuye Yesu ndikhululukireni. Ndipulumutseni Ambuye Yesu. Kuyambira lero mukhale mpulumutsi ndi Ambuye wamoyo wanga. Zikomo Yesu pondipulumutsa, Amen!” Mwapulumuka tsopano! Khalani mwa Yesu masiku onse amoyo wanu.*
Mukhale ndi Loremba Lopambana
*Bishop WJ Ching’amba 0884507838/0999201500 Chilobwe Assemblies Of God*