Chilobwe Assemblies Of God Christ Tabernacle

Chilobwe Assemblies Of God Christ Tabernacle Christ Tabernacle church exists to worship God and serve lives

23/05/2026
23/05/2026

*YOTSOGOLERA LERO 23 MAY 2026*
Genesis 37:18 Abale ake aja anamuonera patali. Ndipo asanafike nʼkomwe kumene kunali iwo kuja, anayamba kale kumupangira chiwembu choti amuphe.

*Ukamamva kuwawa ndi chipambano cha munthu wina dziwa kuti uli ndi nsanje, kaduka ndi nkhwidzi ndi munthuyo. Ukamakondwera kuchokera pansi pa mtima wina akamachita bwino, ndiye kuti mwa iwe mulibemo nsanje, kaduka ndi nkhwidzi. Abale ake a Yosefe amamva kuwawa ndi maloto ake mpaka anamugulitsa chifukwa cha nsanje, kaduka ndi nkhwidzi. Palibe choipa chimene Yosefe adachitira abale kuti mpaka aganize zomupha kenako ndi kumugulitsa ngati kapolo. Nsanje, kaduka ndi nkhwidzi zimapha. Samala ndi anthu owawuza maloto, mapulani ndi chipambano, kuwopa ungauze anthu a nsanje, kaduka ndi nkhwidzi. Anthu a nsanje palibe chaphindu chimene amachita. Paja nkhuku ya nsanje simaswa. Abale ake onse a Yosefe palibepo amene anapanga chaphindu. Chifukwa nsanje, kaduka ndi nkhwidzi zimakodola matemberero, masoka ndi minyama. Lekani nsanje, kaduka ndi nkhwidzi kuti musaphe tsogolo lanu. Celebrate the success of others while you are praying and working hard for your success. “Ambuye Yesu ndimasuleni ku nsanje, kaduka ndi nkhwidzi. Amen!”*

Mukhale ndi Loweruka Lopambana
*Bishop WJ Ching’amba 0884507838/0999201500 Chilobwe Assemblies Of God*

12/05/2026

*TODAY’S KEY VERSES 12 MAY 2026*
Luke 9:28-29 About eight days after Jesus said this, he took Peter, John and James with him and went up onto a mountain to pray. As he was praying, the appearance of his face changed, and his clothes became as bright as a flash of lightning.

*Prayer changes lives and changes situations. Your life and situations cannot remain the same if you truly seek God through prayer. The transfiguration of Jesus Christ happened when He was praying. If you want to see God transforming your life and working on your problems, pray without ceasing. When a believer prays, God touches his life and meets his needs. Remain at the place of prayer so that God should continue working on your life as well as on your problems. Kupemphera koonadi kumasintha makhalidwe, machitidwe, mayankhulidwe, ndi mawonedwe azinthu komanso nyengo zako. Osangopemphera kuti Mulungu asinthe nyengo zanu koma kuti asinthenso moyo wanu ukhale ofanana ndi Ambuye Yesu. Help me Lord to pray without ceasing!*

Have a blessed Tuesday
Bishop WJ Ching’amba *0884507838/0999201500 Chilobwe Assemblies Of God*

01/05/2026

*MAVESI OTSOGOLERA LERO 1 MAY 2026*
Genesis 26:12-13 Isake anadzala mbewu mʼmunda, ndipo chaka chomwecho anakolola zinthu zambiri chifukwa Yehova anamudalitsa. Isake analemera. Chuma chake chinkachulukirachulukira mpaka anasanduka munthu wolemera kwambiri.

*Isake adali olemera kwambiri komanso owopa ndi omvera Mulungu. Bambo Yobu adalinso olemera kwambiri kuposa anthu onse amasiko amenewo. Koma ngakhale adali olemera kwambiri, Yobu anali munthu wachiyero, olungama ndi owopa Mulungu. Izi zikutiphunzitsa kuti sikulemera kwambiri kumene kumapangitsa anthu kukhala osalabadira za Mulungu, osamapemphera komanso osamapita ku tchalitchi. Koma kusaopa, kusamvera ndi kusadalira Mulungu ndi zimene zimapangitsa anthu olemera ngakhalenso osauka kusalabadira za Mulungu. Musalore kulemera kapena kusauka kukupangitseni kuyiwala Mulungu. Khalani monga Isake ndi Yobu, amene adawopa ndi kumvera Mulungu pamene adali olemera kwambiri komanso adachita chimodzimodzi pamene adalibe kanthu. Pangani chisankho chokhala munthu omvera ndi owopa Mulungu pamavuto ndi pamtendere. Khalani munthu olemera koma opemphera kwambiri ndi othandiza ntchito ya Ambuye ndi atumiki ake.*

Mukhale ndi Lachisanu Lopambana
*Bishop WJ Ching’amba 0884507838/0999201500 Chilobwe Assemblies Of God*

27/04/2026

Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga
kuti ndisakuchimwireni. Masalimo 119:11
"Siyani kusunga mangawa mu mtima mwanu ndipo yambani kusunga mawu a Mulungu"

26th April 2026Malawi assemblies of God National Children's Day
26/04/2026

26th April 2026
Malawi assemblies of God National Children's Day

26/04/2026

Munthu ankhonza kukhala ndi zinthu kapena ndalama zochuluka; koma ngati mtima wake sunapange chisankho chopereka molowa manja ndi kulipira zakhumi mokhulupirika, ngakhale mutamuwopyeza ndi matemberero sangaperekebe molowa manja ndi kulipira zakhumi mokhulupirika. Kupereka molowa manja ndi chisankho!

25/04/2026

*TODAY’S KEY VERSES 25 APRIL 2026*
Luke 6:12-13 At that time Jesus went to a mountain to pray. He spent the whole night in prayer to God. When it was day, he called his disciples. He chose twelve of them and called them apostles.

*We must seriously pray to God before making decisions and choices. Wise and godly decisions and choices are made when you ask God to guide you. God will not choose or decide for us but if we ask Him He will guide us in making wise and godly decisions and choices. Decisions and choices are powerful enough to build or destroy our lives. What we are today are the outcomes of the decisions and choices which make daily. However If we are not happy with what we are today, we must start thinking and choosing differently. If Jesus Christ prayed before choosing the 12 apostles, this teaches as the importance of prayer in decision making. Therefore we must learn to seriously pray to God before making decisions and choices. “God, help me to pray and fast before making decisions and choices. Amen!”*

Have a blessed Saturday
*Bishop WJ Ching’amba 0884507838/0999201500 Chilobwe Assemblies Of God*

23/04/2026

*MAVESI OTSOGOLERA LERO 23 APRIL 2026*
AFILIPI 4:6-7 Musadere nkhawa konse; komatu m’zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi chiyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu. Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana chidziwitso chonse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Khristu Yesu.

*Kudandaula sikumabweretsa mayankho koma kumawonjezera mavuto. Kudandaula kumakuchotsera mtendere wamumtima ndipo umakhala opanda chiyembekezo. Ukasoweka mtendere wamumtima suganiza bwino, zotsatira zake umapanga ziganizo zolokwikwa. Choncho siyani kudandaula ndipo ikani maso anu pa Mulungu amene ali ndi mayankho amavuto onse. Tulani nkhawa zanu zonse kwa Mulungu. Lingalirani za ukulu wa Mulungu ndi chikondi chake. Muyamikeni chifukwa cha mphatso yamoyo ndipo pemphererani zosowa zanu ndi chikhulupiriro. Pempherani ndi kulingalira mawu a Mulungu tsiku ndi tsiku kuti mukhale ndi mtendere wamumtima.*

Mukhale ndi Lachinai Lopambana
*Bishop WJ Ching’amba 0884507838/0999201500 Chilobwe Assemblies Of God*

Address

Blantyre

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Chilobwe Assemblies Of God Christ Tabernacle posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share