Maphunziro a Baibulo

Maphunziro a Baibulo Maphunziro a Baibulo a Mpingo uliwonse

17/03/2026

*ANTHU AKUFA*

Timamva Bwanji tikamva za imfa kapena anthu akufa?

*Chiyambi cha imfa;*
- Munda mwa Eden Mulungu anati Mtengo wapakati akaudya azafa ndithu.
*koma satana Malingana ndi Yohane 8:44 Tate wamaboza onse akuti* 📌[Gen 3:4] Kufa simuzafa ayi,[KUFA MUZAFA INDE KOMA OSATI KUFELATU]

*Munthu akafa amapita kuti?;*
- ena timati ali kumwamba,ena wasanduka mizimu,ena ali panjira yamoyo ndi imfa,
*Baibulo likuti 📌Masalimo 146:4,✔️Mlaliki 12:7 Mzimu umapita kwa Mulungu,Fumbi nkubwerela komwe lachokera*

*Kodi akufa amaziwa kuti afa?;*
- _Masalimo 115:17,Mlaliki 9:5,6 okufa saziwa kanthu Bi!,olo mutazichekacheka pa Maliro sangakumveni_

*Munthu okufa ndi Galu wokufa zonsezi nzofana;*📌_Mlalik 3:19_

*Kodi olungama akafa amapita kumwamba?;*
- _AYI 📌Machitidwe 2:29,34, olo Davide ali mmanda pano sikuti akudyerela kumwamba ayi, ndipo sikuti anakakumana ndi Mulungu,Mzimu okhawo unakasungidwa malo osungilako mizimu ya anthu,kufikila Lipenga losiriza mpamene azaone Mulungu_

*Kodi okufa amatha kuyankhula ndi amoyo?;*
- _AYI_
*_Munthu akafa saziwanso kanthu_*

*Nanga aja amatilotesa kuti tiaphikile sadaka aja ndindani?;*
- ZIWANDA, 📌1Sam 28:13-14 kapena kuti milungu,

*INUYO MUWELUZE KODI MILUNGU NDI CHANI?*

*Langizo kwa Akhristu;* _1 Timo 4:1 Masiku osiriza ena azaphunzisa zosiyana ndi zomwe zili baibulo_

*Kodi okufa angathe kupempheredwa kuti alape?;* _AYI_
_Paja tawerenga masalimo ndi mlaliki kuti_ *okufa salemekeza Mulungu ndipo saziwa kanthu* _ndipo a Heberi 9:27, kwaikika kwa munthu kufa kamodzi,kwinako nkumadikila chiweruzo_

*NB SUMMARY*;
BAIBULO LIKUTI
_THUPI(fumbi) + MPWEYA (mzimu)= *MUNTHU*_
_THUPI (fumbi) - MPWEYA (Mzimu)= *AMALEMU*_

(nkhan ikupitilila ku comment)

19/11/2025

*M'BALE*

* Ndani anapha Abele?
M’bale wake
* Ndani anagulitsa Yosefe?
Abale ake.
* Ndani anathamitsa Yefeta?
Abale ake.
* Ndani anali wansanje ndi Davide?
M’bale wake.
* Ndani sanasangalale ndi kubwerera kwa mwana wolowerera?
M’bale wake.

Pakati pa zitsanzo zambiri m’Baibulo, timaona kuti onse amene anaperekedwa ndi kusamaliridwa molakwika ndi abale awo, adadalitsidwa kwambiri ndi kusungidwa ndi Mulungu.

M’moyo, anthu amene mumawaona ngati achibale anu angakukane, kukukana kwawo kungakhale njira imene Mulungu wakonzekera ulemerero wanu. Kungoti, musakhale ndi chikaiko, pitani kumene mudzaonedwa, kuyamikidwa ndi kulemekezedwa.

Ngakhale ngati achibale anu sakukhulupirirani, kumbukirani kuti Mulungu ali ndi chifuno chachikulu mwa inu!!!

GOODNIGHT 🙏🏾❣️

19/11/2025

*YESU ANANENA PAFUPIFUPI MA FANIZO 40 MU CHIPANGANO CHATSOPANO*

*MAFANIZO OPEZEKA MA BUKU ANGAPO*
1. Fanizo la Mbeu ya Mpiru (Mateyu 13:31-32, Marko 4:30-32, Luka 13:18-19)
2. Fanizo la Wofesa (Mateyu 13:1-23, Marko 4:1-20, Luka 8:4-15)
3. Fanizo la Alimi Oyipa (Mateyu 21:33-46, Marko 12:1-12, Luka 20:9-19)

*MAFANIZO OPEZEKA BUKU LIMODZI LOKHA*
Fanizo la Namsongole (Mateyu 13:24-30)
Fanizo la Chuma Chobisika (Mateyu 13:44)
Fanizo la Ngale (Mateyu 13:45-46)
Fanizo la Ukonde (Mateyu 13:47-52)
Fanizo la Mtumiki Wosakhululuka (Mateyu 18:21-35)
Fanizo la Ogwira Ntchito M'munda Wamphesa (Mateyu 20:1-16)
Fanizo la Ana Aŵiri (Mateyu 21:28-32)

Fanizo la Mbeu Yomwe Ikukula (Marko 4:26-29)

Fanizo la Msamariya Wabwino (Luka 10:25-37)
Fanizo la Chitsiru Cholemera (Luka 12:13-21)
Fanizo la Atumiki Olinda (Luka 12:35-40)
Fanizo la Ndalama Yotayika (Luka 15:8-10)
Fanizo la Mwana Womwazika (Luka 15:11-32)
Fanizo la Mtsogoleri Wosakhulupirika (Luka 16:1-13)
Fanizo la Mwamuna Wolemera ndi Lazaro (Luka 16:19-31)
Fanizo la Mfarisi ndi Wa Msonkho (Luka 18:9-14)

07/09/2022

KUKHARA WOKONZEKA

Zizindikiro zakubwera kwa Yesu zikukwaniritsidwa tsiku ndi tsiku koma za chisoni anthu ambiri tikuoneka kuti ngakhare Yesu ananeneratu zonse zochitika kumapeto kwa nthawi ambiri sitikuzindikirabe.

Marko 13:33 Khalani maso! Khalani tcheru! Simudziwa pamene nthawi imeneyo idzafike. 36 Ngati atabwera mwadzidzidzi, asadzakupezeni inu muli mtulo. 37 Zimene ndikunena kwa inu, ndikunena kwa aliyense: ‘Khalani tcheru!’ ”

Kukhara tcheru kapena kukhara maso kumatanthauza kukhara wokonzeka. Tikuyenera kukonzekera tsiku lobwera Yesu kuti tsikuli lisatifikire ngati modzidzimutsa.

Pamene anthu akukwatiwa ndi kukwatira, kudya ndi kumwa, kudzala ndi kumanga, kuchita malonda wogula ndi kugulitsa, kulimbirana maudindo, wokonda zokondweretsa moyo akudzadzanabe m'malo azisangalalo, chilichonse chikuchitika tikuyenera kudziwa kuti tsiku lotsekedwa chitetezero likuyandikira.

Mlandu wina uliwonse watsara pang'ono kutsekedwa kuti chigamulo chiperekedwe. Satana akuona ndipo akudziwa kuti nthawi yatsara pang'ono, ndipo akuchita chilichonse kuti
munthu akhare wotanganidwa kwambiri mpaka tsiku limene khomo la chifundo litatsekedwe kwamuyaya, kuti palibenso angalape.

Wokondedwa kharani wokonzeka ndikukhara woyera pamaso pa Mulungu. Mulandireni Yesu lero kukhara Ambuye ndi Mpulumutsi wanu.

Mulungu akudalitseni.

06/08/2022

MORNING DEVOTION

MKUYU WOSABALA

Mtengo wa Mkuyu umati ukakhara wabereka zipatso umawoneka ndi masamba wochuluka komanso wobiriwira bwino kusonyeza kuti ndi nthawi ya nkhuyu.

Marko 11:13 Ataonera patali mtengo wamkuyu uli ndi masamba, anapita kuti akaone ngati unali ndi chipatso chilichonse. Atafika, sanapezemo kanthu koma masamba, chifukwa sinali nthawi ya nkhuyu.14 Ndipo Iye anati kwa mtengo, “Palibe amene adzadyenso chipatso kuchokera kwa iwe.” Ndipo ophunzira ake anamva Iye akunena izi.

20 Mmamawa, pamene ankayenda, anaona mtengo wamkuyu uja utafota kuyambira ku mizu. 21 Petro anakumbukira nati kwa Yesu, “Aphunzitsi, taonani! Mtengo wamkuyu munawutemberera uja wafota!”

Nthawi iyi mitengo inailiyonse ya Mkuyu imaoneka ngati mmene imawonekera ikakhara yopanda zipatso, koma mtengo uwu unapereka chiyembekezo kwa Yesu unawoneka ndi masamba wobiriwira, koma Yesu atafika pafupi anapeza kuti munalibe chipatso chilichonse.

Mtundu wa Israyeli Mulungu anawusankha ngati mtundu wapadera, naupatsa zofunikira zonse chidziwitso cha Mulungu komanso malamulo a Mulungu kuti ukhare nyali ku mitundu yonse yapadziko lapansi. Ndipo Israyeli amadzimva kuti amadziwa Mulungu komanso ali ndi malamulo a Mulungu.

Koma Yesu atabwera koyamba anapeza kuti Israyeli analibe chipatso cha chilungamo, zimene amazitamandira nazo amangozidziwa koma amalephera kuzichita. Akhristu a lero ambiri tili chimodzimodzi ngati mmene analiri Israyeli wakale, timazitcha ife anthu wopemphera ndikumaoneka nawo mawonekedwe achipembedzo koma makharidwe athu ali wosalemekeza Mulungu wakumwamba.

Mulungu watipatsa chilichonse kuphatikizapo malamulo ake kuti tikakhare nyali ya dziko lapansi koma zipatso za Chikhristu chathu sizikuoneka, ndife anthu wodzikweza, wopanda chikondi komanso aundeka, timangoganizira za ife tokha. Palibe munthu angasunge malamulo a Mulungu ndikungokhara wosalalikira za chikondi cha Mulungu kwa anthu ena.

Happy Sabbath

26/07/2022

Tili ndi maliro kuno kuthabwa Mayi mandere amwalira ndipo maliro ndioika mawa
Mayendedwe ndioti tikafika pathabwa kuyandikira pomwe timalowa popita ku Church paja mbali inayo kulinso kanjira ndiye kusesereka nawo njirayo

04/07/2022

MORNING DEVOTION

MAZIKO

Chinthu kuti chikhare cholimba kapena chabwino chimayenera chikhare ndi maziko abwino. Chinthu chimene chiribe maziko abwino sichichedwa kutha komanso chikakumana ndi mabvuto chimagonjetsedwa. Nyumba yopanda maziko abwino imagwa ndi mphepo komanso ndi mvura ya mphamvu.

1 Akorinto 3:11 Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu. 12 Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,

13 ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense. 14 Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.

Ngakhare nyumba yanu mungamangire zinthu zowoneka bwino chotani koma ngati maziko ake sali abwino, mvura ndi mphepo zamphamvu zikabwera idzagwa koma maziko akakhara abwino imalimba.

Maziko eni eni a moyo wa Chikhristu ndi Yesu. Pamene tikukhara tsiku ndi tsiku tidziwe kuti tikumanga makharidwe athu munthu amene ife tikufuna tikhare, koma zomanga zathu kuti zikhare zopambana maziko ake akuyenera kukhara Yesu. Tidziphunzira kwa Yesu tsiku ndi tsiku zoyenera kuchita kuti timange makharidwe abwino tikhare golide.

Tsiku lachiweruziro lidzaonetsera mmene tamangira makharidwe athu kuti maziko ake anali chani, lero tikhonza kumanamizana kuti tonse ndife anthu wopemphera koma wokondedwa tikuyenera kudziwa kuti Mulungu ndi moto ndipo pomadzabwera iye onse amene anamangira maziko ena adzanyeketsedwa koma onse amene maziko awo anali Yesu adzalimba nadzakhara ndi moyo wamuyaya.

Ambuye akudalitseni, mukhare ndi tsiku lopambana.

30/06/2022

*SATANA SAKONDWERA AKAMATIONA ZIKUTIYENDERA*

*YOBU MUNTHU OLIMBA MTIMA*

*YOBU 2:4*

4-Nayankha Satana nati kwa Yehova ,Khungu kulipa khungu ,Inde munthu adzapereka zonse alinazo kuombola moyo wake.

5-Koma tambasulani dzanja lanu ndikukhuza fupa lache ndi mnofu wake ,ndipo adzakuchitirani mwano pamaso panu.

*Uthenga*

Nthawi zambiri satana amapanga zoti ifebe tizivutika ndi moyo uno.

Apatu satana akukambirana ndi Mulungu za moyo wa Yobu. Yobu anadalitsidwa ndi chuma komanso ana koma munthawi yochepa chifukwa cha satana zonse anali nazo zinatha psiti munthawi imodzi

Komabe Mulungu anamulola satana kuvhita naye Yobu.

Ngakhale zinali tero Yobu sanachoke pamaso pa Mulungu.

Taonani tsono mu vesi 4 satana tsopano akufuna moyo wake ndipo Mulungu akulolerabe kuti Yobu avutike ndi nthenda yachilendo ndipo zinatheka.

Okondedwa izi sizinamusinthe Yobu ndipo zinampamga iye kupitabe chitsogolo ndi Mulungu wake

Kumbukirani nkhani ya Daniel ndi amzake aja mung'anjo ya moto analankhula molimba mtima kuti ngakhale atapanda kuwapulumutsa Mulungu kumoto okomzedwa koma sadzasiya kutumikira Mulungu wamoyo.

Okondedwa Yobu akumudziwa Mulungu yemwe amamutumikira

Inu ndine timatumikira Mulungu uti

Ambuye atithandize

Amen

22/05/2022

*TIKHALE OOPA TCHIMO*

*Sunday 22nd May 2022*

1 Yohane 3v4

Yense wakuchita tchimo achitanso kusaweruzika ,ndipo tchimo ndilo kusaweruzika.

*Uthenga*

Ngati ana a Mulungu tikuyenera kuopa kuchita tchimo.Tiyeni tiyende mchilungamo cha Mulungu wakumwamba.

Monga tonse tidziwa kuti Yesu ali pafupi kubwera tikuyenera kukomzekera kubwera kwake.

Yesu anabwera koyamba ngati mwana komanso ngati Mpulumutsi koma kubwera uku kwachiwiri Yesu akubwera ngati oweruza komanso kuzabwedzera chili chonse chonyansa chimene anthu sanachilape.

Mwayi ulipo lero oti inuyo ndi ine tingathe kulapa tchimo lathu.

Ambuye atithandize

Amen

*Mmawa wabwino*

Address

Blantyre

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Maphunziro a Baibulo posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Place Of Worship

Send a message to Maphunziro a Baibulo:

Share