25/06/2026
Pali phunziro limodzi limene Ambuye anandiphunzitsa lomwe linasintha momwe ndimawonera ulendo wa chikhulupiriro.
Kwa nthawi yaitali ndinkaganiza kuti kuyenda ndi Mulungu kumatanthauza kukhala wokonzeka kukumana ndi mavuto osatha. Nditaona ena akugwa, ena kubwerera m'mbuyo, ndi ena kutaya chikhulupiriro chawo, ndinayamba kuganiza kuti zovuta ndiye mbali yaikulu ya ulendo uwu.
Koma tsiku lina Ambuye analankhula mumtima mwanga nati:
"Pa ulendo wako ndi Ine, vuto lako lalikulu si zovuta. Vuto lako lalikulu ndi zosokoneza."
Ndinadabwa kwambiri.
Kenako Iye anapitiriza kuti:
"Mdani safuna kungokupweteka. Amafuna kukusokoneza. Safuna kungokulepheretsa. Amafuna kukuchotsa pa zimene ndakulankhulira. Anthu ambiri samagwa chifukwa chakuti mavuto awo anali aakulu; amagwa chifukwa analola zosokoneza kuwachotsa pa mawu anga."
Nthawi imeneyo ndinamvetsa kuti chilichonse chimene chimabwera pa moyo wanga sichibwera kuti chindigonjetse, koma kuti chindisokoneze. Choncho ntchito yanga si kungomenyana ndi vutolo, koma kuteteza masomphenya, mawu, ndi lonjezo limene Mulungu wandipatsa.
Ndiye ngati pali chimene mukukumana nacho lero, musachitchule kuti ndi chovuta. Chitchuleni kuti ndi chosokoneza.
Mawu a Mulungu pa moyo wanu sanasinthe.
Lonjezo lake silinatheretu.
Tsogolo lanu silinawonongeke.
Khalani olimba. Pitirizani kuyenda. Zimene mukukumana nazo sizikutanthauza kuti Mulungu wakusiyani; zikungoyesa kukusokonezani.
Musalole zosokoneza zikulande zimene Mulungu anakuwuzani.
Mapeto anu akadali m’manja mwa Mulungu, ndipo mudzafika kumene Iye anakonzerani.