23/04/2026
KODI HEALING SCHOOL NDICHANI?Healing school kapena kuti Sukulu yamachiritso ndi utumiki wa machiritso wa prophet Ray Harris umene cholinga chake ndikusonkhanitsa anthu odwala komanso ena amene ali zosowa komanso mavuto osiyana siyana kuti aphunzitsidwe mmene angagwiritsire ntchito mau a Mulungu kuti alandire zozizwa, machiritso, mamasulidwe ndi zina zotero mudzina la Yesu Khristu.
Kuchokera pamene Prophet Ray anayamba kupangitsa healing school anthu ambiri akhala akuchiritsidwa kumatenda osiyana siyana monga Khunyu, stroke, misala, ndi matenda ena omwe kuchipatala sankatheka koma atabwera ku healing school Mulungu anawachiritsa kudzera mwa Prophet Ray Harris ndipo anthu amene anali ndi zosowa zosiyana siyana monga kusowa ntchito, banja, kusabereka, mavuto a business, a chuma ndi zina zotero Mulungu anawadalitsa ndipo ali ndi maumboni
▪️Kodi Anthu Amene Amabwera Ku Healing School Amachokera Kuti Nanga Amalipira Ndalama?
Healing school ndiya ulere sitimalipiritsa ndipo anthu amene amabwera ku healing school ndi anthu azipembezo zosiyana siyana ndipo amachokera mmadera ndi maboma osiyana siyana.
▪️Kodi Ndalama Zoyendetsera Healing School Zimachokera Kuti?
Ndalama zoyendetsera healing school zimaperekedwa ndi mamembala a Hill City Church International, ma partners a Prophet Ray komanso anthu akufana kwabwino.
▪️Kodi Healing School Ina Ixachitika Liti?
Ndife okondwa kukuyitanani ku healing school yomwe izachitike lamulungu pa 10 May 2026 kuyambirana 8 koloko mmawa mpaka 5 koloko madzulo. Malo: Mudzi Motel kwa Khama - Machinjiri, Blantyre.
▪️Kodi Mukamabwera
Ku Healing School Muyembekezere Chani?
Mukabwera ku healing school muyembekezere kuzamva mau a Mulungu amene azasintha moyo wanu komanso azalimbikitsa chikhulupiriro chanu ndipo ndipo muyembekezere zozizwa, machiritso, mamasulidwe, kubooleza ndi madalitso. Nonse amene muli ndi chosowa bwerani ndipo Prophet Ray azakupemphererani ndipo Mulungu azasintha nyengo zanu kuti mudziwe zambiri imbani 0994566544