America In Prophecy

America In Prophecy Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from America In Prophecy, Religious Center, Blantyre.

26/06/2023

kumvetsetsa bukhu la danier gawo7 lomaliza.

Danier 1:17 koma anyamata amenewa anai, mulungu anawapatsa chidziwitso ndi luntha la m'mabuku ali onse, ndi nzeru; koma Danieli anali nalo luntha la m'masomphenya ndi maloto onse. apa tikuona okondedwa kuti Danier anali wanzeru za masophenya. amaziwa kutanthauzira malota; nkhani imeneyi yokhunza Danier kumasulira maloto. tiyiwona mu gawo 8 ikubwelayo kuchokera pa danier chapter 2.ndiye amnzake adanier anapatsidwa nzeru ndi chidziwitso cha mabukhu. anali anthu, anzeru amawaziwa mabukhu sinakha anali anthu ophunzira magraduate anali ndi madegree. amawatanthauzira bwino mabukhu chifukwa anali ophunzira ngakhale anali ophunzira amaopa mulungu. pakuti chiyambi cha nzeru ndi kuziwa mulungu (miyambo 1:7) danier 1:18 atantha masiku inanenawo mfumu kuti alowe nao, mkuru wa adindo analowa nao pamaso pa nebukadinezara.ndipo mfumu inalakhula nao, koma mwa iwo onse sanapezeke monga Danier, Hananiya, misaeli, ndi Azariya; naimirira iwo pamaso pa mfumu.ndipo m'mau ali onse anzeru ndi aluntha, amene mfumu inawafunsira, inawapeza akuposa alembi ndi openda onse m'ufumu wake wonse. nakhala moyo Danier mpaka chaka choyamba cha koresi.mfumu nubukadinezara, inazizwa ndi anyamata inanena ndi mkuru wa adindo kuti abwele ndi anyamata anai danier ndi anzake. Koma mfumu, inanena kwa danier ndi amnzake amene angoyima chiriri pamaso pa amfumu. mfumu inati kwa danier ndi anzake kuti sipazapezeka mwa inu ku Babulo kuno anzeru ngati inu. Chifukwa anthu awa kunena zoona nzeru zawo zili ten times times nzeru zoopya.ifenso mulungu, amatikonda kwambili; tikhonza kukhala ndi nzeru zotele osazidelela. chongofunika kukhala wokhulupilika pamanso pa mulungu komanso kumvera malamulo amulungu ndi malamulo azanthanzi. mneneli, danier ndi amnzake anali mu chaka choyamba cha mfumu koresi. Koresi tizamuona kutsogoloko ndi amene anali mfumu ya amedi ndi apelesi . tizamuona kutsogoloko kuti koresi anagwira ntchito yolanda mzinda wa Babulo. Ankolo ake akoresi ali mfumu Dariyo .

Yatsala part 8.

22/06/2023

kumvetsetsa bukhu la danier gawo 6.

Danier 1:12 muyesetu anyamata anu masiku khumi; atipatse zomera m' nthaka tidye, ndi madzi timwe.apa tikuona danier akuyibetchela mfumu nebukadinezara kuti awapatse madzi ndi zakudya zomera mu m'nthaka.cholinga adye chifukwa samafuna kudya zakudya za amfumu zimene zinali zodetsedwa. Pa vesi 13 ikuti pamenepo mupenye maonekedwe athu ndi maonekedwe anyamata akudya chakudya cha mfumu; ndi monga umo muonera, muchitire anyamata anu.vesi 14 ndipo anawamvera mau awa, nawayesa masiku khumi.vesi 15 Atatha masiku khumiwo tsono, anaona kuti maonekedwe awo ndi kunenepa kwao anoposa anyamata onse adadyawo zakudya za mfumu. vesi 16 pamenepo kapitaoyo anachotsa chakudya chawo ndi vinyo akadamwa nawapatsa zomera m'nthaka.apa tikuona kuti danier, anayiuza mfumu nubukadinezara, kuti pamene mukutipatsa masiku khumi amene ali (10 days) kuti tizidya masamba ndi kumwa madzi musangolekera p***a ayi.komanso masiku khumi akantha muone maonekedwe anthu ndi maonekedwe anyamata anuwo ngati afanana.koma mfumu, inazichepetsa kumvera zonena za anyamatawa ndi kuwachotsela zakudya zodetsedwa ndi kuwapatsa madzi, ndi zamasamba, monga mavegeterian. pakutha masiku khumi choziziswa chinachitika anyamata ananenepa kwambili kuposa anyamata amfumu ya ku Babulo. Vesi 17 koma anyamata amene anai mulungu anawapatsa chidziwitso ndi luntha la m'mabuku ali onse, ndi nzeru; koma danier anali nalo luntha la m'masophenya ndi maloto onse. Danier, ndi amzake, anali amnzeru funso chifukwa iwo anabvela yehova mulungu anaona kuti zakudya zomera zinali za nthanzi kwa iwowa. ngati inunso mukufuna kukhala anzeru satirani monga iwowa kudya zakudya zopatsa nthanzi zomera komanso madzi tazimwaniko. Danier and Revelation by pg temple page 16,and 15 and 17. zakudya zimapangitsa munthu kuti aziganiza moyenera kapenanso kuwaononga maganizo ake. pakali pano anthu tikudya zakudya zosapatsa nthanzi kafukufuku wina anapeza kuti matenda ena akubwela chifukwa chodya nyama. sicholinga cha mulungu kuti tizidya nyama. koma pa chiyambi mulungu anakonza diet yoyambilila kwa adamu imeneli vegeterial diet . Genesis 1:29 koma atachoka adamu, kubwela nthawi ya nowa. mulungu adamuza nowa atatuluka chingalawa kuti muzidya nyama.koma mafuta muchotse ndi mwanzi; Genesis 9 :4 komano mulungu anafunabe kuti tibwelele ku diet yoyambilila.ana Israeli anapatsidwa manna chifukwa mulungu amawaphunzitsa simple diet ya health. komano ndi makani awo anakakamila nyama; tipeza kuti life style pakali pano moyo wa munthu wa munthu unachepetsedwa ndi zaka zake zinachepa .zakudya zimene anthu tikudya monga: nyama, sugar, zimachepetsa moyo wa munthu ( councils on diet and food by Ellen g white book) (meat crisis book by Vance ferrel. Koma yesu khristu ngakhale nthanzi lanthu tinaliononga koma amatikonda kwambili amatitenga abale.(ministry of healing chapter 10) Ku nthawi ya Ku mapeto ino satana akulimbana ndi maubongo awanthu. chifukwa ndi amene amawachita study kotelatu amawuchita study ubongo wa munthu. (mind and character personality book chapter 3 by ellen g white

Yatsala part 7

21/06/2023

Kumvetsetsa bukhu la Danier gawo 5.

Apa tiyeni tiwoneni gawo 5. Danier 1:8:9: koma Danier anatsimikiza mtima kuti asadzidetse ndi chakudya cha mfumu, kapena ndi vinyo amamwa; chifukwa chake anapepha mkuru wa adindo amlore asadzidetse.ndipo mulungu anamkometsera Danier mtima wa mkuru wa adindo, amchitire chifundo.nati mkuru wa adindo kwa DanieL, ine ndiopa mbuyanga mfumu, amene anakuikirani chakudya chanu ndi chakumwa chanu; pakuti aoneranji nkhope zanu zachisoni zoposa za anyamata olingana ndi inu? momwemo mudzaparamulitsa mutu wanga kwa mfumu.apa tikuona kuti Danier ali ku Babulo ndi amzake atatu aja. anakumana ndi mayesero okhuza nkhani ya chakudya. koma chosangalatsa Danier akukanitsitsa kuti sangadye chakudya chimenecho komanso ndi vinyo okonzedwa ndi mfumu yaku Babulo. Tikuonanso kuti mkuru wa adindo, akudandaulira danier, kuti si ine ndakuitanira chakudya koma ndi amfumu. mukachikana chakudyacho ndi vinyo mundipamulitsa kwa mfumu. kumeneko kunali kuopa kwa mkuru wa adindo; pa vesi 11 ikuti nati Danier kwa kapitao, amene mkuru wa adindo adamuikayo ayang'anile Danier, Hananiya, misaeli, ndi azaliya, maina awa: anayi anyamatawa, tiwafotokoza mu gawo 4 kuti mfumu, inawasinthira mayina awo ndi kuwapatsa mayina amilungu ya kuBubulo. Vesi 12 ikuti muyesetu anyamata anu masiku khumi; amene ali masiku (10) atipatse zomera m'nthaka tidye, ndi madzi timwe. danier ndi amzake sanafune kudya chakudya cha mfumu. chifukwa chinali chakudya chopelekedwa ku mafano amilungu ya ku Babulo. monga ana okonda mulungu samayenera kudya chakudya chimenecho; komanso chinali chakudya chodetsedwa chimene mulungu amuletsa mose, ndi aroni, komanso ana israeli mu bible. bukhu la Levitiko chapter 11........ chonse komanso Deuteronomy 28...….. chapter analemba zakudya zoyenera kudya ndi zosayenera kudya; kuteloko danier, kusadya zakudya zimenezo kwa ife ndi zinthu zofunikira kwambili; danier akuyibetchera mfumu kuti tatipatseni masiku khumi tizidya masamba ndi kumwa madzi.

Yatsala part 6

Address

Blantyre

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when America In Prophecy posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share