Islamic Issues II

Islamic Issues II Iyi ndi Page yomwe m***a kutumiza nkhani zokhuza chipembezo cha Chisilamu, , ndinu olandilidwa

04/02/2026
30/01/2026

Chifukwa chani Quran idabwera bible lilipo kale 👇👇

14/10/2025

Palibe chifukwa chomutchulila yesu kuti Mulungu , amene mukufuna kumva ZAMBILI , like and follow this page

14/10/2025

Follow this page for more lessons

06/08/2025

NDI ANGATI AMENE TAKHALA TIKUNYOZA ANTHU OMWE AKWATILAPO MITALA?

Assalam alaycum

Machimo enawa tiziwapewa, mitàla kuchisilamu sitchimo ayi.

Choyenera kudziwa NDI chakuti Mulungu amadziwa ndipo ife sitimadziwa kanthu.

Kukwatila kuchisilamu NDI sunna osati FARADHWI.

Koma sunna yake ndiyofunikila kwambili yomwe kuisiya ukhoza kugwera kudzenje lauchimo.

Kukhala opanda mkazi sitchimo
Kukhala ndimkazi mmodzi ☝️ sitchimo
Kukhala nawo awili malile 4 sitchimo.

MNCHIFUKWA CHANI ANAIKA MALILE 4?

Sura 4v3 Allah mumnzeru zake Adaika malile akazi 4
Powona kuti ngati saika malile kudzakhala chisawawa chopanda discipline.

Tsono Allah akufuna chilungamo.
Ukwatila Kaya sukwatila bola ukhale wachilungamo
Osapanga zauhule.

Chilungamo chosamala akazi mofanana.

Tsono Allah pololeza mitala , osailetsa adawona zinthu izi

1. Mamuna amafuna mkazi nthawi zonse , mkazi safuna mamuna nthawi zonse.
2. Mkazi Ali ndi vuto la mnsambo ndi ubereki lomwe limapangitsa kusakhala NDI mamuna mwachikakamizo.
3. Munthawi yoletsedwa kukhala ndimamuna , ndinthawi yomwe thupi lamamuna limafuna popumila.
4. Akazi NDI ambili mnchilengedwe poyerekezera amuna.

Tsono inu mitala simumaikonda ayi
Chisakhale chiphinjo kwa iwo amene amaikonda.
Musawanyoze
Musawatukane
Musawaeruze.

Kutelo kuli ngati
Mwanyoza Allah ndi mtumiki wake
Omwe adaloleza
Mtumiki adapanga mitalayi

Tiyeni tipewe kulankhula zopanda umboni

بارك الله فيكم

02/06/2025

Wina aliyense ali ndi chipembedzo , ndipo zipembedzo zilipo magawo awili

1. Chipembedzo cha Muluñgu
2. Chipembedzo cha satana

Ambili ali muchipembedzo cha satana koma sadziwa

02/06/2025

KODI FODYA MU CHISILAMU NDI HARAM KAPENA MAKRUH?

Brothers and sisters , tidziwe Kuti sibwino kumalankhula zinthu zopanda umboni mu din yathu.

Pali kusiyana kowonekera pakati pa ma MAKRUH NDI HARAM

Haram NDI chinthu chimene Allah waletsa osati kuloleza.
Pali zimene Allah analoleza osati kulamulila
Monga mitala.

Mulungu waletsa chiwerewere, kuledzera, katapila, kudya nkhumba, zakufa zokha, magazi , zozingidwa ndi anthu omwe SA asilamu.

Kuletsedwa uku mwachindunji , kupanga izi NDI Haram.

Tsono MAKRUH ndizinthu zimene zili zosakhala BWINO mnsilamu kupanga , kima ukapanga sizikuteñgera ku uchimo.

MAKRUH ndimachitidwe omwe ukawakakamila atha kukuwonongera tchito zabwino.

Zitsanzo NDI
Kusunga zikhadabo ,

Kusunga zikhadabo si Haram koma MAKRUH
Zikhadabo zikhoza kusunga najsi mkuwonobga swala yako.

Tikafika kunkhani ya FODYA Ili mmagawo awa
1. FODYA amaika umoyo wa munthu pa risk
2. FODYA wina amasokoneza kaganizidwe.
3. FODYA ndichinthu chomwe mnchovuta kuchisiya.

👉 Chilichonse choika umoyo wamunthu pachiwopsezo ndi Haram, Allah akuti 👉 usaziphe wekha
👉 Chonse chosokonesa bongo ( kullu muskirin ) mncholetsedwa chili mu gulu la zoledzeretsa.

Automatically FODYA NDI Haram osati MAKRUH..

Follow this page for more updates

05/05/2025

Mtumiki s.a.w adati , munthu yemwe abereke Mwana wamkazi mkumulera bwino
Mkumupilila mkaleledwe , mkumupezera mamuna wachisilamu

Adzakalowa ku janna

Atsikana chooonde musalore kukwatiwa ndi munthu yemwe sali mnsilamu.

Ndipo musapusitsike kuti akutsani ambiliwa NDI onama
Pempherani kuti muzapeze wa din wabwino.

Chonde amuna Inu pezani atsikana a chisilamuwa kuti Iwo apeze mwayi wabanja lachisilamu lodalilika

Allahumma Amin 🤲

03/05/2025

Palibe Chipembedzo chowonadi kuposa chipembedzo Cha Abraham 👉 sura 2v130.

Palibe okapulumuka patsiku lachiweruzo kupatula chisilamu 👉 surq 3v85.

Imfa yabwino , ndiyamunthu amene amamwalila ali mnsilamu 👉 sura 3v102

Mnsilamu ndi amene ali otsatira aneneri Onse a MULUNGU 👉 sura 2v285

Pali funso ngati 🤷

26/04/2025

KUFUNIKILA KWA UTSOGOLERI ,

kodi mumadziwa Inu , utsogoleri ndi ofunikila.

Pachilengedwe chonse , mtsogoleri wathi ndi Muluñg jAllahu s.w amene amatilenga mkutipatsa zofunikila pamoyo wathu

Mkutichitila zomwe akufuna pamoyo wathu.

Pazolengedwa zonse mtsogoleri wa zolengedwa pakati pazolengedwa NDI Mtumiki wathu okondedwa Muhammad s.à.w ,

Pakati pa aneneri ooonse, mtsogoleri wa aneneri onse ndi Mneneri Muhammad s.a.w.

Pakati pa ma buku oyeretsedwa , buku lalikulu NDI buku la Quran , chifukwa mu Quran muli

Gawo la torah , uthenga adaulandila Mose

Gawo la zabur, uthenga adaulandila Davide
Gawo la injil , uthenga adaulandila Davide
Gawo la ma swuhuf , makalata adawapàndila aneneri

Komanso muli uthenga womwe mmabuku onsewa mulibe
Quran idaponda paliponse mkukhala yankho lamnsilamu pachilichonse.

M'banja mtsogoleri adaikidwa kukhala mtsogoleri
Iye ndi wopilila, wamphamvu, wodekha, wa memory yamphamvu.

Pakati pa Angelo mtsogoleri NDI mngelo Gabriel.

Kwa okhulupilila mtsogoleri bwenzi lawo ndi Mulungu.

Kwa ochimwa mtsogoleri wawo NDI iblis asatana.

Mkofunika Kwa ife okhulupilila kuwamvera atsogoleri anthu pamene akutilamulila pazabwino

Baaraka Llahu fiikum
Wassalam alaykum

Address

Blantyre

Telephone

+258877625697

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Islamic Issues II posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share