Kukhwima mwa Khristu

Kukhwima mwa Khristu Kukhwima mwa Khristu ndi utumiki umene cholinga chake ndicho kuthandiza akhristu kuti akule muuzimu

TSIKU 37 LA MASIKU 176 MUSABATA 6 YA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (14 August 2025)ulendo wa m’Baibulo➡️Muc...
14/08/2025

TSIKU 37 LA MASIKU 176 MUSABATA 6 YA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (14 August 2025)
ulendo wa m’Baibulo

➡️Muchititse mlubza maso anga ndisapenye zachabe, mundipatse moyo mu njira yanu.(MASALIMO 119:37)

🛐Ambuye, mawu anu amapereka chimene ine ndimafuna, ndicho moyo. Mundithandize kuti maso anga asatanganidwe ndi zinthu zopanda pake koma mmalo mwake akhale tchelu pa mawu anu. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Ndime zalero

Marko 14:26-72
➖➖➖➖➖➖

Kodi mukukwanitsa Kuwerenga ndime za tsiku ndi tsiku? Kapena mukumachitanso kuwonjezera, kapena mwina zikumachuluka? Koma ngati mukuwerenga tsiku ndi tsiku ziribwino pamenepo.

TSIKU 36 LA MASIKU 176 MUSABATA 6 YA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (13 August 2025)ulendo wa m’Baibulo➡️Lin...
13/08/2025

TSIKU 36 LA MASIKU 176 MUSABATA 6 YA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (13 August 2025)
ulendo wa m’Baibulo

➡️Lingitsani mtima wanga kumboni zanu, si ku chisiriro ai.(MASALIMO 119:36)

🛐Ambuye munandipatsa ine zonse za pa moyo ndi chipembezo. Mawu anu ndimboni zaichi kuti ndisasirire. Kotero ndikupemphera kuti chidwi changa chikhazikike kumboni zanu osati ku chisiriro. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Ndime zalero

Marko 13:1-37
Marko 14:1-25
➖➖➖➖➖➖

Musayike chidwi chanu pongofuna kamaliza ndime yalero, tengani nthawi yowonanso momwe mwadutsamo dzulo kapena sabata yapitayo.

TSIKU 35 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 YA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (12 August 2025)ulendo wa m’Baibulo➡️Mun...
13/08/2025

TSIKU 35 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 YA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (12 August 2025)
ulendo wa m’Baibulo

➡️Mundiyendetse mopita malamulo anu; pakuti ndikondwera m'menemo.(MASALIMO 119:35)

🛐Ndikayenda munjira ya malamulo anu ndikhala okondwera ndi wansangala. Koma pandekha sindingathe pokhapokha inuyo Ambuye mundiyendetsemo. Ndiripano Ambuye, ndiyendetsenimo. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Ndime zalero

Marko 12:1-44
➖➖➖➖➖➖

Yesetsani kuti nthawi imene mwakonza kuti muwerenge mawu ikhale yopanda zina zochitika.

DAY 34 OF 176 DAYS IN WEEK 5 OF 25 WEEKS OF READING THE NEW TESTAMENT (11 August 2025)a journey through the Bible➡️Give ...
13/08/2025

DAY 34 OF 176 DAYS IN WEEK 5 OF 25 WEEKS OF READING THE NEW TESTAMENT (11 August 2025)
a journey through the Bible

➡️Give me understanding, and I shall keep thy law; yea, I shall observe it with my whole heart. (Psa 119:34)

🛐Lord, I don't just want to memorize your word without understanding. If I understand them then I can observe them whole heartedly. I pray therefore that you give me understanding generously. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Today's scriptures

Mark 11:1-33
➖➖➖➖➖➖

Try to read the passage of the day with background knowledge for better understanding.

TSIKU 33 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (10 August 2025)ulendo wa m’Baibulo➡️Mun...
13/08/2025

TSIKU 33 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (10 August 2025)
ulendo wa m’Baibulo

➡️Mundiphunzitse, Yehova, njira ya malemba anu; ndidzaisunga kufikira kutha kwake.(MASALIMO 119:33)

🛐Ambuye, sipangakhale mphunzitsi wina oposa inu. Kutero ine ndikuphunzira kuchokera kwa mphunzitsi wabwino kuposa onse. Pachifukwa ichi ndiri otsimikizika kuti ndiyenda mmawu anu mpaka kumapeto. Chilimbikitso changa sichiri mwa ine koma mwa inu Ambuye. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Ndime zalero

Marko 10:1-52
➖➖➖➖➖➖

Kumbukirani kuti ndime ya Masalimo ili apayi ndiyakuti okupatseni chilimbikitso chowerenga mau lero. Iringalileni ndikupemphero.

TSIKU 32 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (9 August 2025)ulendo wa m’Baibulo➡️Ndid...
09/08/2025

TSIKU 32 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (9 August 2025)
ulendo wa m’Baibulo

➡️Ndidzathamangira njira ya malamulo anu, mutakulitsa mtima wanga.(MASALIMO 119:32)

🛐Atate, ndikuthukoza chifukwa mwamasula mtima wanga kuti ndithe kuthamanga munjira ya mawu anu, osangoti kuyenda chabe. Pamene ndikuphunzira mawu anu mochuluka ndi pamenenso nditathamange michulukanso kukafikira ku ulemerero wa dzina lanu. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Ndime zalero

Marko 9:1-50
➖➖➖➖➖➖

Pamene tikugawana mawu ndi ena, tipereke mpata kuti afunse mafunso. Izi zitithandizira kuti tithe kuwona kuchuluka kwa chidziwitso chathu.

TSIKU 31 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (8 August 2025)ulendo wa m’Baibulo➡️Ndim...
09/08/2025

TSIKU 31 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (8 August 2025)
ulendo wa m’Baibulo

➡️Ndimamatika nazo mboni zanu; musandichititse manyazi, Yehova.(MASALIMO 119:31)

🛐Ambuye, ndayika moyo wanga onse pa mawu anu. Malangizo ndi malonjezano anu ndi maziko amene ndikumangapo moyo wanga. Ndithandizeni kuwamvetsetsa mawu anu kuti ndisawaphonye. Musalore kuti ndichite manyazi chifukwa chokhulupirira mawu anu. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Ndime zalero

Marko 8:1-38
➖➖➖➖➖➖

Werengani, lingalirani ndiponso gawanani ndi ena mawu a Mulungu.

TSIKU 30 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (7 August 2025)ulendo wa m’Baibulo➡️Ndin...
09/08/2025

TSIKU 30 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (7 August 2025)
ulendo wa m’Baibulo

➡️Ndinasankha njira yokhulupirika; ndinaika maweruzo anu pamaso panga.(MASALIMO 119:30)

🛐Ambuye, ndinapanga chisankho choyenda mu njira yanu. Komatu izi ndizotheka pokhapokha nditadziwa mawu anu. Ndichifukwa chake ndapatula ma sabata amenewa kuti ndiphunzire malemba anu. Ndiphunzitseni mawu anu nthawi zonse zimene maso anga apenyamo. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Ndime zalero

Marko 7:1-37
➖➖➖➖➖➖

Pokhala kuti ino ndi sabata yachisanu, ndikulimbiketseni kuti m***a kuyesa kuwonjezera ndime zowerenga patsiku ngati mwafuna kutero. Izi m***a kupanga pakuwonjezera ndime zothandizira kufotokozera

TSIKU 29 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 YA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (6 August 2025)ulendo wa m’Baibulo➡️Mund...
06/08/2025

TSIKU 29 LA MASIKU 176 MUSABATA 5 YA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (6 August 2025)
ulendo wa m’Baibulo

➡️Mundichotsere njira ya chinyengo; nimundipatse mwachifundo chilamulo chanu.(MASALIMO 119:29)

🛐Ambuye, ndikudziwa kuti pandekha sindingazichotsere njira za chinyengo. Mukandiphunzitsa ine mau anu mosawerengera mphulupulu zanga, ndikudziwanso kuti njira zanga zidzakhala zowonadi. Ndiripano ambuye, ndiphunzitseni kuchokera mu Baibulo. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Ndime zalero

Marko 6:1-56
➖➖➖➖➖➖

Kodi mwagawanako mawu a Mulungu ndi ndani? M***a kupitiriza kugawana ndi omwewo kapenanso m***a kuyesera ndi anthu ena.

TSIKU 28 LA MASIKU 176 MUSABATA 4 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (5 August 2025)ulendo wa m’Baibulo➡️Moyo...
06/08/2025

TSIKU 28 LA MASIKU 176 MUSABATA 4 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (5 August 2025)
ulendo wa m’Baibulo

➡️Moyo wanga wasungunuka ndi chisoni: Mundilimbitse monga mwa mau anu.(MASALIMO 119:28)

🛐Ambuye, mawu anu ndi mankhwala a zowawa ndi zisoni. Zikomo chifukwa cha mphatso imeneyi ya mawu anu. Ndithandizeni kuti ndiwalemekeze iwo ndipo ndipatseni ludzu la mawuwa nthawi zonse. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Ndime zalero

Marko 5:1-43
➖➖➖➖➖➖

Yang'anani kumbuyo ndikuwonanso mwachangu ndime zimene mwawerenga sabata ino. Zikonzekeretseni sabata ikuyambayi powona patalipatali ndime zasabata ikubwerayi.

TSIKU 27 LA MASIKU 176 MUSABATA 4 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (4 August 2025)ulendo wa m’Baibulo➡️Mund...
06/08/2025

TSIKU 27 LA MASIKU 176 MUSABATA 4 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (4 August 2025)
ulendo wa m’Baibulo

➡️Mundizindikiritse njira ya malangizo anu; kuti ndilingalire zodabwitsa zanu.(MASALIMO 119:27)

🛐Ambuye, ndikufuna ndikalingalire ndi kukamba za zozizwa zantchito zanu. Ndipatseni zonena. Tsegulani maso anga kuti ndikazione pamene ndikuwerenga mawu anu. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Ndime zalero

Marko 4:1-41
➖➖➖➖➖➖

Kumbukirani kuti mukuyenera kuwerenga ndime zimene zakonzedwa kuti ndizalero powonjezera pa ndime imene tapempherera koyambirirako.

TSIKU 26 LA MASIKU 176 MU SABATA 4 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (3 August 2025)ulendo wa m’Baibulo➡️Ndi...
06/08/2025

TSIKU 26 LA MASIKU 176 MU SABATA 4 LA MASABATA 25 OWERENGA CHIPANGANO CHATSOPANO (3 August 2025)
ulendo wa m’Baibulo

➡️Ndinafotokozera njira zanga, ndipo munandiyankha: Mundiphunzitse malemba anu.(MASALIMO 119:26)

🛐Ambuye, zikomo chifukwa mumandimva ndikayankhula za njira zanga ndipo mumachitapo kanthu moyenera. Ndingakonde kuti nanenso ndikanakhala ndi chidwi ndi mawu anu mmene inu muliri ndi mau anga. Chonde ndithandizeni Ambuye. Amen.

➖➖➖➖➖➖
🔳Ndime zalero

Marko 2:1-28
Marko 3:1-35
➖➖➖➖➖➖

Mwapeza kale munthu amene mungagawane naye mau? Musavutike kufuna munthu wachilendo kapena wakutali. Yambani kugawira ena tsopano.

Address

Blantyre
000

Opening Hours

Monday 09:00 - 17:00
Tuesday 09:00 - 17:00
Wednesday 09:00 - 17:00
Thursday 09:00 - 17:00
Friday 09:00 - 21:00
Saturday 09:00 - 12:00

Telephone

+265880906989

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Kukhwima mwa Khristu posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Place Of Worship

Send a message to Kukhwima mwa Khristu:

Share