21/05/2026
๐ ๐๐ฆ๐๐๐จ ๐๐๐ ๐๐๐ญ๐๐ช๐๐๐
Mpingo wa Seventh-day Adventist nchigawo chakumawa cha Eastern Malawi Conference walengeza pulogalamu yayikulu ya ulaliki yotchedwa Kholola Machinga kapena Kuti IMPACT MACHINGA nchingerezi yomwe idzachitike m'boma la Machinga kuyambira pa 4 mpaka 31 October chaka chino cha 2026. Ntchitoyi igawika m'magawo awiri: Gawo Loyamba kuyambira 4 mpaka 17 October, ndipo Gawo Lachiwiri kuyambira 18 mpaka 31 October. Cholinga chake ndi kufikitsa uthenga wa chipulumutso kwa anthu ambiri m'derali kudzera mu ulaliki, mapemphero, ndi ntchito zachifundo.
Malingana ndi Pastor Dr. Sanned Lubani, yemwe ndi mtsogoleri wachigawochi ino ndi nthawi yoyenera kulalikira chifukwa posachedwa zinthu sizidzabwerera mwakale. Iye wati tiyenera kugwiritsa ntchito mwayi umenewu pamene zitseko zilipobe zotseguka, chifukwa masiku akudza pamene ntchito ya Mulungu idzakhala yovuta kuchita momasuka. "Tiyeni tigwire ntchito usiku ndi usana, chifukwa usiku ukudza pomwe palibe amene angagwire ntchito," adatero.
Msonkhanowu ukupempha thandizo la ndalama kuchokera kwa anthu okoma mtima, abusa, ndi mabungwe osiyanasiyana kuti ntchitoyi ikayende bwino. Zosowa zazikulu zikuphatikizapo zakudya za oitanidwa, zipangizo za ulaliki, ndi zoyendera za amishonale omwe adzakhale akugwira ntchito m'madera osiyanasiyana a Machinga. Aliyense amene akumva mu mtima mwake kuthandiza ntchito ya Ambuye ali olandiridwa.
IMPACT MACHINGA ikuyembekezeka kubweretsa chitsimutso chauzimu komanso kusintha kwa miyoyo ya anthu ambiri. Tiyeni tonse tigwirizane mu pemphero ndi mu ntchito kuti dzina la Ambuye lilemekezedwe.
Olemba : McAllan Mapinda
EMC Media