Lisanjala SDA Church

Lisanjala SDA Church Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Lisanjala SDA Church, Church of God, Robert Mugabe Highway, Blantyre.

The official Facebook presence of Lisanjala Seventh-day Adventist Church located in Bangwe, Blantyre under Malabvi District in Eastern Malawi Conference of Seventh-day Adventists

𝗔𝗕𝗨𝗦𝗔 𝗔 π— π—’π—­π—”π—Ÿπ—”π—‘π——π—˜: "π—§π—œπ—¦π—”π— π—”π—Ÿπ—˜ 𝗑𝗧𝗛𝗔π—ͺπ—œ" 𝗔𝗨𝗭𝗔 𝗔𝗑𝗧𝗛𝗨 𝗣𝗔 π— π—”π—Ÿπ—œπ—₯𝗒 𝗔 π— π—”π—¬π—œ 𝗠𝗒π—₯π—˜π—˜π—‘ π—¦π—˜π—‘π—šπ—”Akhristu adasonkhana mmudzi mwa a Maganga k...
08/08/2026

𝗔𝗕𝗨𝗦𝗔 𝗔 π— π—’π—­π—”π—Ÿπ—”π—‘π——π—˜: "π—§π—œπ—¦π—”π— π—”π—Ÿπ—˜ 𝗑𝗧𝗛𝗔π—ͺπ—œ" 𝗔𝗨𝗭𝗔 𝗔𝗑𝗧𝗛𝗨 𝗣𝗔 π— π—”π—Ÿπ—œπ—₯𝗒 𝗔 π— π—”π—¬π—œ 𝗠𝗒π—₯π—˜π—˜π—‘ π—¦π—˜π—‘π—šπ—”

Akhristu adasonkhana mmudzi mwa a Maganga ku Bangwe pa mwambo wa maliro a Mayi Moreen Kampani Senga omwe anamwalira pa
6 August 2026 ali ndi zaka 46. Mayi Senga anabadwa pa 16 September 1979.

Pa utumiki wa malirowo, abusa a Orlac Mozalande achigawo cha Malabvi adapereka ulaliki womwe mutu wake unali "KUMASAMALA NTHAWI".

M'busa Mozalande analimbikitsa akhristu kuti atsatire Yesu chifukwa Iye yekha ndi amene amadziwa za nthawi ya moyo wa munthu aliyense. Iye anati palibe mmodzi mwa ife amene amadziwa za mawa, ndipo ndi chifukwa chake ndikofunika kwambiri kumpatsa Ambuye moyo wathu kuti aulamulire.

"Ino sinthawi yochita zibwana ndi nthawi yopanga zauchimo. Tiyenera kukhala tcheru chifukwa tikuneyera kufa tili ndi Yesu," adatero m'busa Mozalande polimbikitsa mabanja ndi okhulupirira omwe anali pamalirowo.

Iye anatinso "mphindi yatsoka sifanana" ndipo anachenjeza akhristu kuti asamakopere ena pochita zoipa ponena kuti mwina anzathuwo atha kuzalapa pamaliro athu atadzidzimuka. "Aliyense adzayankha yekha kwa Mulungu. Tiyeni tiyende m'njira ya Ambuye osati kutsatira zitsanzo zoipa za anthu," adatero.

M'busa Mozalande anamaliza ndi kukumbutsa mpingo kuti moyo uli m'manja mwa Mulungu, choncho tiyeni tigwiritse ntchito tsiku lililonse pothandiza ntchito ya Mulungu ndi kukhala okonzeka kubweranso kwa Khristu.

Mayi Senga anali nkhristu wa mpingo wa Lisanjala SDA, Mgomanjira B - Jesus Way.

Akubanja adandaula koma akuti alimbikitsika ndi uthenga komanso kupezeka kwa anthu pamodzi ndi akhristu pozawatonthoza.

Wolemba : McAllan Mapinda
Lisanjala Media

Happy Sabbath
07/08/2026

Happy Sabbath

π—§π—›π—¨π—£π—œ π—Ÿπ—” π—žπ—˜π—Ÿπ—©π—œπ—‘ π—¦π—”π— π—¨π—˜π—Ÿ π—ͺ𝗔 π— π—£π—œπ—‘π—šπ—’ π—ͺ𝗔 π—šπ—”π——π—” π—Ÿπ—”π—Ÿπ—’π—ͺ𝗔 𝗠𝗠𝗔𝗑𝗗𝗔Chisoni chinakuta anthu a mmudzi mwa Suya ku Chirimba pomwe thupi ...
07/08/2026

π—§π—›π—¨π—£π—œ π—Ÿπ—” π—žπ—˜π—Ÿπ—©π—œπ—‘ π—¦π—”π— π—¨π—˜π—Ÿ π—ͺ𝗔 π— π—£π—œπ—‘π—šπ—’ π—ͺ𝗔 π—šπ—”π——π—” π—Ÿπ—”π—Ÿπ—’π—ͺ𝗔 𝗠𝗠𝗔𝗑𝗗𝗔

Chisoni chinakuta anthu a mmudzi mwa Suya ku Chirimba pomwe thupi la malemu Kelvin Samuel amene anali Pathfinder pa wa mpingo wa Gada chigawo cha Namisu limalowa m'manda lero ku Chirimba ku Blantyre.

Kelvin anabadwa pa 15 May 2013 ndipo watisiya pa 6 August 2026 ali ndi zaka 13 zakubadwa. Malinga ndi akubanja, Kelvin anadandaula Wednesday kuti pamtima pake pamamuwawa ndipo atapita kuchipatala adapeza kuti ali ndi chibayo. Kelvin watisiya pa 6 August 2026 ndipo anali atalemba mayeso a Standard 8.

Banja la malemuli lati lili ndi chisoni chachikulu chifukwa Kelvin watisiya patadutsa masabata awiri okha mkulu wakenso atamwalira.

Pamalirowa, abusa a Smart Chimwaza a chigawo cha Chirimba ndi omwe analalikira. Powerenga Yobu 21:22, iwo anakumbutsa akhristu kuti ngakhale Yobu anali wowopa Mulungu anakumana ndi mavuto, ndipo palibe munthu amene angalangize Mulungu. "Tilore chifuniro cha Mulungu chichitike, koma tikachita bwino Iye adzatipatsa mayankho," adatero m'busa Chimwaza.

M'busa Chimwaza adachenjezanso achinyamata kuti asatayilire pochita nzonyasa poyembekezera kuti angamwalire ndi achikulire okha. "Imfa ikutenga aliyense, tiyeni tikonzekere za kubweranso kwa Yesu Khristu," adatero.

Amfumu a Suya a dera la Chirimba omwe analipo pamalirowo adapempha anthu onse kuti apeze chipembedzo ndikukhala ndi moyo wopemphera. Naonso akulu a pa sukulu ya Chisenjere mu Lunzu Zone komanso oimira achipani adandaula kwambiri ndi imfa ya mnyamatayu.

Mpingo wa Gada wapempha anthu kuikiza anamfedwa mmapemphero pa nthawi yachisoniyi.

Kumalirowa kunalinso achinyamata oimira EMC komanso BT-CZ Zone.

Wolemba : McAllan Mapinda
EMC Media

π—ͺπ—”π—–π—›π—œπ—¦π—’π—‘π—œ: π— π—”π—¬π—œ 𝗠𝗒π—₯π—˜π—˜π—‘ π—¦π—˜π—‘π—šπ—” π—‘π—žπ—›π—₯π—œπ—¦π—§π—¨ π—ͺ𝗔 π—Ÿπ—œπ—¦π—”π—‘π—π—”π—Ÿπ—” π—”π—§π—œπ—¦π—œπ—¬π—”Mpingo wa Seventh-day Adventist wa Lisanjala uli ndi chisoni c...
07/08/2026

π—ͺπ—”π—–π—›π—œπ—¦π—’π—‘π—œ: π— π—”π—¬π—œ 𝗠𝗒π—₯π—˜π—˜π—‘ π—¦π—˜π—‘π—šπ—” π—‘π—žπ—›π—₯π—œπ—¦π—§π—¨ π—ͺ𝗔 π—Ÿπ—œπ—¦π—”π—‘π—π—”π—Ÿπ—” π—”π—§π—œπ—¦π—œπ—¬π—”

Mpingo wa Seventh-day Adventist wa Lisanjala uli ndi chisoni chachikulu kulengeza za imfa ya mayi Moreen Senga nkhristu wa wathu.

Mayi Senga amwalira usiku wapitawu pa 6 August 2026 kuchipatala cha Queen Elizabeth Central. Ndipo lero pa 7 August nthawi ya 2 koloko masana zovutazi zinyamulidwa kuchoka kunyumba yachisoni ya Queens kupita ku Bangwe komwe amakhala. Thupi la mayi Senga ake likuyembekezeka kuikidwa mmanda mmawa la Sabata pa 8 August 2026.

Iwowa amakhala mmudzi mwa Mgonanjira, TA Machinjiri ku Bangwe, pafupi ndi Nanalira Private School.

Chifukwa cha zovutazi, utsogoleri wa mpingo ukudziwitsa anthu nonse zakusintha kwa phwando la nyimbo lomwe gulu la ana athu a Gospel Carriers-Lisanjala linakonza pa 8 August 2026. Pulogalamu ya "Choral Sabbath" tsopano ichitika la abata pa 15 August 2026 pa Lisanjala.

Banja la mpingo likupempha onse okhulupirira ndi abwenzi kuti apempherere banja lomwe latsala pa nthawi yachisoniyi. Tiyeni tipitirize kupempha chitonthozo kwa Mulungu, gwero la mtendere ndi chiyembekezo.

Wolemba : McAllan Mapinda
Lisanjala Media

Amen
06/08/2026

Amen

𝗠'𝗕𝗨𝗦𝗔 π—π—¨π—¦π—§π—œπ—‘ π—£π—›π—œπ—₯π—œ π—”π—Ÿπ—œπ— π—•π—œπ—žπ—œπ—§π—¦π—” π— π—”π—¦π—’π— π—£π—›π—˜π—‘π—¬π—” 𝗔 π—˜π— π—– 𝗣𝗔 π— π—œπ—¦π—’π—‘π—žπ—›π—”π—‘π—’ 𝗬𝗔 π— π—œπ—¦π—”π—¦π—” π—žπ—¨ π—–π—›π—œπ—žπ—’π—ͺ𝗔Mtsogoleri owona za mautumiki-Person...
06/08/2026

𝗠'𝗕𝗨𝗦𝗔 π—π—¨π—¦π—§π—œπ—‘ π—£π—›π—œπ—₯π—œ π—”π—Ÿπ—œπ— π—•π—œπ—žπ—œπ—§π—¦π—” π— π—”π—¦π—’π— π—£π—›π—˜π—‘π—¬π—” 𝗔 π—˜π— π—– 𝗣𝗔 π— π—œπ—¦π—’π—‘π—žπ—›π—”π—‘π—’ 𝗬𝗔 π— π—œπ—¦π—”π—¦π—” π—žπ—¨ π—–π—›π—œπ—žπ—’π—ͺ𝗔

Mtsogoleri owona za mautumiki-Personal Ministries ku Eastern Malawi Conference m'busa Justin Phiri sabata ino wayendera ku Chikowa m'chigawo cha Bwaila kukachereza akhristu pa misonkhano ya misasa yomwe ikuchitika kumeneko.

Polankhula ndi gulu la okhulupirira, m'busa Phiri wati cholinga chachikulu cha EMC ndi kulalikira mau a Mulungu ndi tsogozo la "Patsogolo Ndi Uthenga Ndi Kudzipereka". Iye wati masomphenya amenewa akuyenera kukwaniritsidwa kudzera mu mapulogalamu osiyanasiyana kuphatikizapo Impact Machinga yomwe ilipo mu October komanso AMO Congress yomwe ukuyembekezeka kuchitika mwezi wa September chaka chino.

M'busa Phiri watsimikizira akhristu kuti kuti ntchito ya kupindula miyoyo iyende bwino, mpingo ukuyenera kutsatira "Njira ya Khristu" ya kupindula anthu. Wati njira imeneyi ndi kuyamba ndikufikira zosowa za anthu, kenako kulimbikitsa olema, ndipo pamapeto pake kuwaitanira kwa Yesu.

Pa nkhani ya umodzi mu mpingo, mtsogoleriyu walimbikitsa akhristu onse kuika patsogolo kukondana posasunga zakale kukhosu malinga ndi Levitiko 19:18 . Iye wati ndi njira ya Satana kupangitsa anthu kukangana ndi kukumbukira zakale kuti ataye chidwi cha kupindula miyoyo. "Ntchito ya Mulungu kuti ipite patsogolo, tonse ngati Conference tiyenera kuyiwala zakale ndi kuyanjana monga amodzi," adatero.

M'busa Phiri anali limodzi ndi m'busa Benson L Mbewe, yemwe ndi mtsogoleri wa Udindo Wachikhristu ku Eastern Malawi Conference. M'busa Mbewe nayenso walimbikitsa akhristu kuti akhale okhulupirika komanso kuti moyo wawo uziyenderana ndi chikhulupiriro chawo cha chikhristu.

Iye walimbikitsanso kuti mipingo ikhale ndi ndondomeko zolongosoka pankhani ya chuma. "Akhristu asaiwale kupereka chakhumi ndi zopeleka chifukwa ndi njira yomwe Mulungu walamulira anthu ake kuti madalitso achuluke," adatero m'busa Mbewe.

Akhristu a ku Chikowa ati alandira uthengawo ndi manja awiri ndipo adalonjeza kugwira ntchito limodzi kuti masomphenya a EMC akwaniritsidwe.

Wolemba : McAllan Mapinda
EMC Media

π— π—§π—¦π—’π—šπ—’π—Ÿπ—˜π—₯π—œ π—ͺ𝗔 π—˜π— π—– π—”π—žπ—¨π— π—”π—‘π—” π—‘π——π—œ 𝗠𝗙𝗨𝗠𝗨 π—¬π—”π—œπ—žπ—¨π—Ÿπ—¨ π—žπ—”π—ͺπ—œπ—‘π—šπ—” π—£π—’π—žπ—’π—‘π—­π—˜π—žπ—˜π—₯𝗔 π— π—œπ—¦π—’π—‘π—žπ—›π—”π—‘π—’ 𝗬𝗔 π—œπ— π—£π—”π—–π—§ π— π—”π—–π—›π—œπ—‘π—šπ—”Ngati mbali imodzi yokonzek...
06/08/2026

π— π—§π—¦π—’π—šπ—’π—Ÿπ—˜π—₯π—œ π—ͺ𝗔 π—˜π— π—– π—”π—žπ—¨π— π—”π—‘π—” π—‘π——π—œ 𝗠𝗙𝗨𝗠𝗨 π—¬π—”π—œπ—žπ—¨π—Ÿπ—¨ π—žπ—”π—ͺπ—œπ—‘π—šπ—” π—£π—’π—žπ—’π—‘π—­π—˜π—žπ—˜π—₯𝗔 π— π—œπ—¦π—’π—‘π—žπ—›π—”π—‘π—’ 𝗬𝗔 π—œπ— π—£π—”π—–π—§ π— π—”π—–π—›π—œπ—‘π—šπ—”

Ngati mbali imodzi yokonzekera misonkhano ya kholora ya Impact Machinga yomwe ukuyembekezeka kuyamba pa 4 October 2026, mtsogoleri wa mpingo wa Seventh-day Adventist nchigawo chaku mmawa m'busa Dr Sanned Lubani lero wayendera ndikukacheza ndi mfumu yaikulu ya a Yao, Paramount Chief Kawinga kunyumba kwao ku Ntaja m'boma la Machinga.

M'busa Dr Lubani wati kukumana kwao ndi Paramount Chief Kawinga nkopindulitsa kaamba akambirana zolimbikitsa umodzi, mtendere komanso kukhalirana bwino wina ndi nzake. Iye wati ndikofunikira kuti mpingo ndi mafumu azigwirira ntchito limodzi kuti uthenga wabwino ufike kwa anthu onse.

Kumbali yake, Paramount Chief Kawinga wati ndiokondwa kwambiri ndi ubale omwe ulipo pakati pa mpingo wa Seventh-day Adventist ndi anthu ake kuderali. Mfumuyi yalonjeza kuthandizira kuti misonkhano ya Impact Machinga ikhale yopambana.

Paulendowu, Dr Lubani anaperekezedwa ndi m'busa wachigawo cha Ntaja a Wilfred Kachingwe.

Pambuyo pake a Lubani afikanso pa mpingo wa Mbenjere komwe kuli msonkhano wa misasa womwe ukuchitika ndipo utha la Sabata pa 8 August 2026. Kumeneko adakumana ndi mtsogoleri wa mpingo wa Seventh-day Adventist m'dziko muno m'busa Petro Sukali pamodzi ndi abusa a Shadreck Msuka komanso mlaliki Dr Ernest Kaonga omwe akutumikira pamisasapo.

Msonkhano wa Impact Machinga ukuyembekezeka kukhala mwa misonkhano ikuluikulu ya kulalikira uthenga wa chiyembekezo kwa anthu a m'boma la Machinga ndi madera oyandikana nawo.

Wolemba : McAllan Mapinda
EMC Media

π— π—§π—¦π—’π—šπ—’π—Ÿπ—˜π—₯π—œ π—ͺ𝗔 π— π—”π—Ÿπ—”π—ͺπ—œ π—¨π—‘π—œπ—’π—‘ π—–π—’π—‘π—™π—˜π—₯π—˜π—‘π—–π—˜ π—”π—Ÿπ—œ 𝗣𝗔 π— π—¦π—’π—‘π—žπ—›π—”π—‘π—’ π—ͺ𝗔 π— π—œπ—¦π—”π—¦π—” π—ͺ𝗔 π— π—•π—˜π—‘π—π—˜π—₯π—˜ π—žπ—¨ 𝗑𝗧𝗔𝗝𝗔Mtsogoleri wa mpingo wa Seventh-day...
05/08/2026

π— π—§π—¦π—’π—šπ—’π—Ÿπ—˜π—₯π—œ π—ͺ𝗔 π— π—”π—Ÿπ—”π—ͺπ—œ π—¨π—‘π—œπ—’π—‘ π—–π—’π—‘π—™π—˜π—₯π—˜π—‘π—–π—˜ π—”π—Ÿπ—œ 𝗣𝗔 π— π—¦π—’π—‘π—žπ—›π—”π—‘π—’ π—ͺ𝗔 π— π—œπ—¦π—”π—¦π—” π—ͺ𝗔 π— π—•π—˜π—‘π—π—˜π—₯π—˜ π—žπ—¨ 𝗑𝗧𝗔𝗝𝗔

Mtsogoleri wa mpingo wa Seventh-day Adventist m'dziko muno m'busa Petro Sukali ali pa mpingo wa Mbenjere ku Ntaja m'boma la Machinga komwe kuli msonkhano wa misasa.

Atumiki ena ndi m'busa Shadreck Msuka komanso mlaliki Dr Ernest Kaonga.

Msonkhano wa misasawu wayamba dzulo pa 4 August 2026 ndipo ukuyembekezeka kutha la Sabata pa 8 August 2026. Ili ndi gawo lachiwiri la misonkhano ya misasa chaka chino pomwe la Sabata lapitali gawo loyamba linatsekedwa.

Mwini wachigawochi a W. Kachingwe ati ndiokondwa ndi momwe msonkhanowu ukuyendera. Iwo ati mauthenga akufika ndi amphamvu ndipo akhristu akupindula kwambiri ndi kuphunzitsidwa kwa Mau a Mulungu.

Miyezi ya August ndi September ndi miyezi yofunika kwa mpingo wa Seventh-day Adventist chifukwa ndi nthawi ya misonkhano ya misasa pomwe akhristu ochokera m'madera osiyanasiyana amasonkhana kwa masiku angapo kudyera limodzi mau a Mulungu, kupemphera ndi kulimbikitsana pa ntchito yautumiki.

Atsogoleri a mpingo wa Mbenjere ati akuyembekeza kuti msonkhanowu udzathandiza kulimbikitsa chikhulupiriro cha okhulupirira komanso kukopa miyoyo yatsopano kwa Khristu.

Wolemba: McAllan Mapinda
EMC Media

05/08/2026

NAYI NYIMBO YA MSONKHANO WAMISASA YA 2026

Osaiwala kuti pa 100064451541962:2048:Lisanjala tikuyamba pa 25 mpaka pa 29 August 2026 osamphonya. Part 8

Address

Robert Mugabe Highway
Blantyre

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Lisanjala SDA Church posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share

Category