Mussa Adam

Mussa Adam أبو نجوى الباحث

Book labwino kwambiri ili
12/01/2026

Book labwino kwambiri ili

29/05/2025

Tili mmasiku opambana adziko lapansi ,tayesetsani kugwira ntchito yabwino osawononga tsiku opanda kuzigulira Malo ku Jannah

07/11/2023

In Jannah there is no sadness, no suffering, no sickness, no problems. Just happiness forever.

May Allah grant us all Jannah.

Ma phunziro awulere anzanu akupindula ,timanena mobwereza bwereza kuti mwayi wamaphunziro ukapezeka kumaphunzira zenizen...
11/02/2023

Ma phunziro awulere anzanu akupindula ,timanena mobwereza bwereza kuti mwayi wamaphunziro ukapezeka kumaphunzira zenizeni mpaka umburi wo udzipsa mtima zeni zeni....

Palibe chomwe munthu chingamuthandize moyo uno komanso omwe uli mkudza kuposa kulimbikira kuphunzira deen ndikugwiritsa ntchito zomwe waphunzira zo

Amene tili ndikhombo lofuna kuwonjesera knowledge tiyeni tizisakasaka ma phunziro wo basi deen iyi timayenera kuphunzira daily osazimva kuzindikira kwambiri mpaka kusiya kuphunzira, chifukwa ena ake amakutchani sheikh kapena muft ndi zopanda pake zisakuchedwetseni aliyense ali ndi kuperewera mmaphunziro ake lets work hard pamaphunziro a deen...

Palibe kuthetsa umburi , Bid'ah,shirk popanda kuphunzira deen yi moyenera .....zigawenga zoopseza ndi Bid'ah zili paliponse zikufwambani deen yanuyo ngati muperewere mmaphunziro anu...

Tipemphe Allah atipatse maphunziro opindulitsa ,natipindulitsa muzomwe taphunzira...

Ofuna kuchita join class imeneyi pali timayeso tophweka toti alembe mkulowa nawo mkalasi, zimangofuna wachidwi basi chofuna kuphunzira...

Link yake pansipa

https://chat.whatsapp.com/EzSa5kJVYrKElKVg3EhMSw

26/01/2023

KUSAMALA NTHAWI ZONSE KUKHALA NDI ZOVALA ZABWINO KWA YEMWE ANGATHE KUPEZA

Kutchena kwa msilam ndi chinthu chofunikira kwambiri, msilamu aziwoneka bwino,msilamu azitchena ,zovala zabwino ukakhala nazo uzivala ,msilamu azitchena nthawi yomwe akuchita ibaadah ,pa swalah sipovala nyangwita ,chonsecho uli ndi zovala zabwino ukusungira ,pa swalah osamavala ngati nsing’anga ,pa swalah sipovala ngati munthu okhwima wanyanga,msilamu zoona azivala ngati omanga mvula? Msilamu azipha ulusi msilam azisita chovala,ngati mmavala mikanjo kupha mikanjo yabwino ,ngati umapha ma suit iphani jacket yabwino ka necktie kabwino ,kutchena sikuletsedwa mchislam as long as zovalazo sizinalowe mgulu la zinthu zoletsedwa ,zozimana zija kukanika kugula nsapato chikang’a mkuphulika ,pozemba kuti musachite manyazi mkumati ndi sunnah kukhala ndi zikang’a ayi bodza limenero kanamireni kwina..

Allah (ﷻ) amasangalatsidwa ndikuwona mtendere omwe wamupatsa kapolo wake ukuwonekera poyera,tsiku lina Mtumiki (ﷺ) anamuwona mkulu wina wavala tinyangwita chonsecho Allah (ﷺ) anamudalitsa anampatsa makobiri,ali mkuthekera kogula zovala zabwino ,choncho Mtumiki (ﷺ) atamuwona mkuluyi sanakhale chete koma kumudzudzula mchitidwe ovala nyangwitawu anati:
.....ألك مال؟ قال: نعم، قال من أي المال؟ قال: قد اَتاني الله من الإبل والغنم والخيل والرقيق، قال: فإذا اَتاك الله مالا فلير أثر نعمته عليك وكرامته...

…...Kodi Allah (ﷻ) anakupatsa chuma? anayakha kuti: Inde! Mtumiki (ﷺ) anafunsanso kuti: ndi chuma chanji chomwe Allah (ﷻ) anakupatsacho? Anayankha nati: anandipatsa ngamila ,nkhosa ma horse (hatchi) komanso akapolo…Mtumiki (ﷺ) Allah (ﷻ) akakupatsa chuma ,ziziwoneka zizindikiro za mtendere wakewo pa iwe komanso kufewa mtima kwake….

Hadith ya saheeh ndipo ikupezeka mma book monga (أبوداود) (4063) komanso (النسائي) (5224) komanso ili ndi ma umboni kuchokera mma hadith monga a ibn Mas’ood, Abdullah bin Amri, Abu Hurayrah,komanso Omran bin Huswayn ndi ena ambiri…

Anthu ena amaletsa kutchena amvekere osamayiwala ndife akapolo a Allah (ﷻ) nde ofunika munthu ukayima pamaso pa Allah (ﷻ) uzivala mnyozeka, zoona pamaso pa Allah (ﷻ) muzivala monyozeka kuvala nyangwita ,koma moti tsiku lina mutachita mwayi oyitanidwa ndi mtsogoleri wadziko ku state house mungapiteko mutavala nyangwita? Mesa mukhoza kusakasaka zovala zabwino zapamwamba kuzilemekeza kusangalatsa munthu chifukwa choti ndi president wadziko, kulibwanji kuzilemekeza kuvala zapamwamba pofuna kusangalatsa Allah (ﷻ) bwana wa ma bwana president wa ma president?
Amene mmaletsa anzanu kutchena dziwani kuti mukulimbana ndi malamulo a Allah (ﷻ), Allah (ﷻ) akunena mu Qur’an yake yolemekezeka kuti:

قُلْ مَنْ حَرَّمَ زِينَةَ اللَّهِ الَّتِي أَخْرَجَ لِعِبَادِهِ وَالطَّيِّبَاتِ مِنَ الرِّزْقِ قُلْ هِيَ لِلَّذِينَ آمَنُوا فِي الْحَيَاةِ الدُّنْيَا خَالِصَةً يَوْمَ الْقِيَامَةِ كَذَلِكَ نُفَصِّلُ الْآيَاتِ لِقَوْمٍ يَعْلَمُونَ

Nena: "kodi ndi ndani waletsa zokongoletsa za Allah (ﷻ), (kuvala zovala zabwino), zomwe Iye (Allah) adawatulutsira akapolo ake ndi zakudya zabwino?" Nena: "Zinthu zimenezo (kutchena komanso kudya zakudya zabwino) nzololedwa kwa amene akhulupirira (Asilamu) pamoyo wapadziko lapansi. (Zidzakhala) zawozawo tsiku la chimaliziro. M'menemo ndi mom we Tikulogosolera ma verse athu kwa anthu ozindikira."
Mmamva bwanji mukamawerenga verse limeneri amene mmavalabe nyangwita chonsecho muli ndi kuthekera kopeza zovala zabwino? Mmamva bwanji mukamawawona asilamu anzanu akusowa zovala zabwino chonsecho muli mkuthekera kowathandiza? Mmamva bwanji mukamatenga nyangwita zomwe inu simuzifuna mkumawapatsa anzanu mowatayira chonsecho mmawerenga kuyankhula kwa Allah (ﷻ) konena kuti:

لَنْ تَنَالُوا الْبِرَّ حَتَّى تُنْفِقُوا مِمَّا تُحِبُّونَ وَمَا تُنْفِقُوا مِنْ شَيْءٍ فَإِنَّ اللَّهَ بِهِ عَلِيمٌ

Simudzapeza zabwino mpaka mutapereka zomwe mmazikonda. Ndipo cha ulere chilichonse chomwe mupereka, ndithudi, Allah (ﷻ) amachidziwa...

Kutchena sikuzikweza ngati mmene ena amaganizira ,ngakhalebe pena zikhoza kusokonekera kugwera mukuzitukumula malingana ndi niyah ya munthu,koma kuchenako pakokha sikuzitukumula ayi…kuchokera mu hadith ya saheeh yomwe anayilandira ibn Mas’ood (رضي الله عنه) kuchokera kwa Mtumiki (ﷺ) yemwe anaphunzitsa kuti:

لا يدخل الجنة من كان في قلبه مثقال ذرة من الكبر، فقال رجل: إن الرجل يحب أن يكون ثوبه حسنا، ونعله حسنة، قال: إن الله جميل يحب الجمال، الكبر بطر الحق، وغمط الناس...

Sakalowa ku Jannah amene mumtima mwake muli kuzikweza ngakhale kochepa ngati njere,munthu wina ananena kuti: ndithudi munthu amakonda nthawi zonse kuti zovala zake zikhale zabwino nsapato zakenso zabwino,anaynkha Mtumiki (ﷺ) kuti: ndithudi Allah (ﷻ) ndi wabwino ndipo amakonda zobwino ,akati kuzikweza ndiko kukana chilungamo komanso kuwawona anthu ngati apansi kwambiri iweyo wapamwamba..

Hadith ya saheeh ndipo ikupezeka mu (مسلم) (91) komanso (أبو داود) (4092) ndi ma book ena

PHUNZIRO MU HADITH IMENEYI

Kuchokera mu hadith imeneyi muli ma phunziro angapo omwe tikuphunziramo monga:

1) Kuvala zabwino kapena kuzisamalira munthu mkumawoneka bwino sizitanthauza kuti munthu yo akuzikweza ayi…

2) Allah (ﷻ) ndiwabwino ndipo amakonda zabwino ,choncho msilam ozisamalira wawukhondo otchena bwino ndi wabwino kuposa yemwe akuvala masanza ngati nsing’anga chonsecho ali ndikuthekera kovala bwino

3) Mu hadith imeneyi kuzikweza amatanthauza munthu otsutsana ndi chilungamo chikamufikira ,mkumachitabe makani ,monga anthu a bid’ah ndi ozikweza pambuyo poti alangizidwa sunnah

4) Mtumiki (ﷺ) amalimbikitsa zovala zabwino choncho ma sahabah ake analinso kuvala bwino,mchifukwa atamva hadith anadabwa ndikufunsa kuti amvetsetse kuzikweza kweni kweni ndi kuti

عدم الإسراف في اللباس

KUPEWA KUWONONGA (CHUMA) PA ZOVALA

Ngakhale kuti kutchena kuli kofunikira Allah (ﷻ) watiletsa kuwononga kutaya chuma chambira mosasamala Kamba kogula zovala chabe,pena mawanja akumasokonekera akazi kuvuta kwambiri nkhani yatchenedwe mwamuna kukhala pa mpeni tipewe kuwononga kwambiri kumakhala moderate ,osati kalikonse mukawone mukhale nako ayi….Allah akunena kuti:

يَا بَنِي آدَمَ خُذُوا زِينَتَكُمْ عِنْدَ كُلِّ مَسْجِدٍ وَكُلُوا وَاشْرَبُوا وَلَا تُسْرِفُوا إِنَّهُ لَا يُحِبُّ الْمُسْرِفِينَ…

Oh! inu ana a Adam! tengani (valani) zovala zanu zabwino pamene mukukapemphera swalah iliyonse ndipo idyani ndi kumwa; koma musapyole muyeso (kuwononga). Iye (Allah (ﷻ)) sakonda opyoza muyeso (owononga)…
Mtumiki (ﷺ) naye ananena kuti:

كُلوا واشرَبوا وتَصدَّقوا والْبَسوا ما لم يخالِطْهُ إسرافٌ أو مَخيَلةٌ.....

Idyani ndi kumwa ,ndi kuperekani swadaqa,ndipo valani (zabwino) mpanda kulwetsa kuwononga kapena kufuna kuzitukumuula…

Ndi hadith ya hassan ndithu imeneyi iikupezeka mu (النسائي) (2559) komanso (ابن ماجه) (2605) ndi ma book ena ambiri ngakhalenso imam Bukhar anayichita ta’aleeq pa topic ya zovala.

PHUNZIRO MU HADITH IMENEYO

Hadith imeneyi ikutiphunzitsa zambiri, komanso ikutiphuzitsa zinthu zomwe nzofunikira pa moyo wa munthu zomwe ndi:

1) Kupeza cha chakudya mopanda kuwononga

2) Kupeza chakumwa koma apewe kuwononga

3) Kupeza zovala zabwino koma apewe kuwononga

4) Kupereka swadaqah apewe kuzkweza

18/01/2023

You will die alone, burried alone, be question alone, answer alone, and you will stand alone before Allah....

Wife material is the one who is of good character and has good manners. She is not known for foul speech, meanness or ba...
16/01/2023

Wife material is the one who is of good character and has good manners. She is not known for foul speech, meanness or bad manners; rather she is good-natured, pure of soul and clean of heart, speaks in a gentle manner and treats people kindly.More important than all of that, she accepts advice and listens to it attentively and wholeheartedly; she is not one of those who are used to arguing stubbornly and arrogantly.

The best of women is the one who, if she is given she is grateful, and if she is deprived she is patient; you feel happy when you look at her, and she obeys you if you instruct her to do something.

She is the one who upholds her connection to her Lord and always strives to increase her level of faith and piety. She does not omit any obligatory duty, and she is keen to do some nafl (supererogatory) deeds. She gives precedence to pleasing Allah..

15/01/2023

of the greatest tests of character is how you handle opposition. In fact, opposition is part of Allah’s will for your life; it prepares you for the opportunities ahead.

If you’re going to make something of your life, not everyone is going to like it. You’re always going to find people who feel it’s their job to criticize every dream or project Allah puts on your heart. Their favorite word is “no,” and their favorite phrase is, “You can’t do that.”

One tactic that comes from Shaytan's whispering,ridicule. People (choice) use this tactic to try to stop you from doing Allah’s will.

Here are some three ways people might use "ridicule" to oppose you:

1) People will attack your character and identity.

When someone attacks you, it’s typically with their emotions, not their logic. In fact, by the time they’re attacking you, they have stopped thinking clearly. When people are angry or afraid, they resort to name-calling and even lies. Their words can hurt, but those words do not change your identity or purpose, you're M***a you will remain M***a.

2) People will accuse you of having wrong motives

The truth is, no one ever really knows another person’s motivation for doing something. We all have mixed motivations. We often can’t even figure out our own motivation for doing something! Only Allah knows !!

3) People will predict your failure.

If you set a goal, announce a vision, or begin a business, many will be quick to forecast your failure..

Address

Cairo

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mussa Adam posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share