13/05/2026
Sheikh M***a Adam writes:
𝐊𝐔𝐋𝐀𝐋𝐈𝐊𝐈𝐑𝐀 𝐏𝐀 𝐌𝐀𝐋𝐈𝐑𝐎 /𝐊𝐔𝐌𝐀𝐍𝐃𝐀
Anthu ambiri lero atembenuza zinthu akuchita mosemphana ndi mmene ziyenera kuchitikira kapena mmene anaphunzitsira Mtumiki (ﷺ), kulalikira pa maliro kapena kumanda ndi nkhani ya bwino ndipo ndi ntchito yoti ili ndi ma umboni.
Mwachitsanzo imaam Bukhar (رحمه الله) anayika mutu mu book lake la saheeh Bukhar onena kuti:
باب موعظة المحدث عند القبر وقعود أصحابه حوله
Topic yofotokoza za (kuvomerezeka kwa) kulalikira ku manda oyankhula atakhala ndi omvera atakhala momuzungulira mbari mwake ,kuchokera pa mutu umenewu imaam bukhar anasonkhanitsa ma hadith omwe Mtumiki (ﷺ) anali kuphunzitsa ndi kulalikira pa maliro kapenanso ku manda ,monga hadith ya Allie (رضي الله عنه) yonena kuti:
كنا في جنازة في بقيع الغرقد, فأتانا النبي , فقعد وقعدنا حوله, فقال: ما منكم من نفس منفوسة إلا كتب مكانها في الجنة أو النار....
Tinali ku maliro ndipo tili ku manda otchedwa (Baqī‘ aI-Gharqad) anatipeza Mtumiki (ﷺ) anakhala pansi ndipo tinakhala mbari momuzungulira ndipo Mtumiki (ﷺ) ananena kuti: palibe kuchokera mwa inu mzimu omwe wawuziridwa kupatula kuti unalemberedwa malo ake (okakhala) ku Jannah kapena ku moto….
Mu hadith imeneyi muli chilolezo cholalikira kapena kuphunzitsa pa maliro kapenanso ku manda, ma hadith ngati amenewa alipo ambiri komanso a saheeh…
Apa tidziwe kuti kulalikira pa maliro komanso ku manda ndi zinthu zovomerezeka zili ndi ma umboni okhazikika komanso odziwika ,kulalikira pa maliro kapenanso ku manda sizingakhale bid’ah ngati mmene anthu ena akuphunzitsira…
Dziwani kuti ngati pafunikira kuti anthu akufunikira kuphunzitsa zina zake mwachangu changu ndiye kuti sipakufunikanso kuchedwetsa koma kuwaphunzitsa anthu... Qaidah imanena kuti:
عدم جواز تأخير البيان عن وقت الحاجة
Ndi zoletsedwa kuchedwetsa ulaliki nthawi yomwe ukufunikira kwambiri, kutanthauza kuti ngati papezeka chifukwa china chake chomwe pakufunikira kuti anthu awunikiredwe ,ndizoletsedwa kuchedwetsa kuwaphunzitsa anthu pomwe akufunikira kuphunzitsidwa kwambiri..
𝑲𝒐𝒎𝒂𝒏𝒐 𝒏𝒈𝒂𝒌𝒉𝒂𝒍𝒆 𝒛𝒊𝒍𝒊 𝒄𝒉𝒐𝒏𝒄𝒉𝒊 𝒑𝒂𝒍𝒊 𝒛𝒊𝒏𝒕𝒉𝒖 𝒛𝒊𝒏𝒈𝒂𝒑𝒐 𝒛𝒐𝒇𝒖𝒏𝒊𝒌𝒊𝒓𝒂 𝒌𝒖𝒛𝒊𝒘𝒖𝒏𝒊𝒌𝒊𝒓𝒂 𝒎𝒐𝒏𝒈𝒂 𝒊𝒛𝒊:
1) Mtumiki (ﷺ) zolalikira pa maliro zi kapena kumanda sichinali chizolowezi chake amkalalikira pokha pokha pomwe pafunikirapo ,simaliro aliwonse omwe amkalalikira ayi, panayikidwa maliro ambiri mu umoyo wa Mtumiki (ﷺ) omwe sipanalalikidwepo…. choncho zinthu zomwe Mtumiki (ﷺ) sanazisandutse chizolowezi zimakhalanso zoletsedwa kuzisandutsa chizolowezi, kumeneko kumakhala kusemphana ndi Mtumiki (ﷺ)...
2) Mtumiki (ﷺ) pa maliro kapena ku manda amkalalikira atakhala pansi komanso anthu omvera amakhala momuzungulira ,choncho pofuna kutsata chiphunzitso cha Mtumiki (ﷺ) pakafunikira kulalikira olalikira yo ayenera akhale pansi komanso omvera ulalikiwo akhale pansi..izi zikuthanthauza kuti omwe amayima lero lino mkumalalikira anthu atakhala khala ndi zosemphana ndi chiphunzitso cha Mtumiki (ﷺ)..chifukwa ma hadith onse akuphunzitsa kuti Mtumiki (ﷺ) anakhala ndipo ife tinakhala mbari mwake momuzungulira…palibe hadith yoyima mkumalalikira ku maliro kapena ku manda...
3) Mtumiki (ﷺ) amkalalikira uku mkuti ntchito yokonza manda ikugwirika osati ntchito imayima ayi …
Choncho apa tidziwe kuti anthu omwe amayima mkumalalikira amakhala akulakwitsa chifukwa zoyenera mogwirizana ndi chiphunzitso cha Mtumiki (ﷺ) ndi kulalikira olalikira yo atakhala pansi komanso omvera akhale pansi,kmanso zisasanduke chizolowezi chifukwa Mtumiki (ﷺ) sizinali chizolowezi chake..kuti maliro ali onse afumikra alalikire ayi.