Mtumiki Joshua

Mtumiki Joshua TIYENI TIYITANILE YEHOVA PA NYENGO YANU, NDIPEPHELO NDIPO NDICHIKHULUPILILO YEHOVA ASINTHA NYENGOYO (NDI MULUNGU NDIZOTHEKA (MATEYU 19:26) CALL/WSP 0982144285

22/06/2026

*(Ezekieli 18:31-32)
31 Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?

32 Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

Hallelujah hallelujah πŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™Œ

Follow #

18/06/2026

AKUFA KU TCHIMO AMOYO MWA MULUNGU

Aroma 6 : 11-14
11. Kotero inunso, mudzione nokha ngati akufa ku tchimo koma a moyo kwa Mulungu mwa Khristu Yesu.
12. NΚΌchifukwa chake, musalole tchimo lilamulire matupi anu amene anafa kuti mumvere zilakolako zonyansa.
13. Musapereke ziwalo zathupi lanu ku tchimo, ngati zipangizo zamakhalidwe oyipa. MΚΌmalo mwake, mudzipereke kwa Mulungu, ngati amene achoka ku imfa kupita ku moyo. Ndipo mupereke ziwalo zathupi lanu ngati zipangizo zachilungamo.
14. Tchimo silidzakhalanso ndi mphamvu pa inu, chifukwa Malamulo sakulamulira moyo wanu koma chisomo.
HALLELUJAH πŸ™ŒπŸ™Œ

Follow

14/06/2026

LERO NDI TSIKU LIMENE MULUNGU WATIPANSASO

MADALITSO, MACHILISO, MAMASULIDWE
ZIKHALE ZIPEZEKE PA MOYO WANU PA BANJA LANU MU DZINA LA YESU πŸ™πŸ™πŸ™πŸ™

13/06/2026

DALITSIKANI LIMBIKISIKANI

CHISOMO CHOMWECHO

Follow

12/06/2026

Apa nthawi ndi *(03:16 am)

MULUNGU AKULAKHULA MAU AWA PA MOYO WA MUNTHU WINA PA NYENGO YA MUNTHU WINA AMEN

(Deuteronomo 31 : 6)
6. Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite nawo mantha kapena kunjenjemera pamaso pawo, chifukwa Yehova Mulungu wanu apita nanu. Sadzakusiyani kapena kukutayani.”
Hallelujah πŸ™ŒπŸ™Œ

10/06/2026

*(Numeri 23 : 23)
23. Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo, palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli. Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti, β€˜Onani zimene Mulungu wachita!’

Hallelujah πŸ™ŒπŸ™Œ

Mwaka nthawi kochepa chabe tamveselani ......

Tikamayang'ana za Yakobo ndi munthu amene anayenda molungama pamaso pa Mulungu
Israel anayendaso molungama pamaso pa Mulungu
Zofooka zina sizinalemphele pa Iwo, koma anakhulupilika pamaso pa Ambuye......

Uthengawu ukupitaso Kwa inu ndi INE ngati timayenda mokhulupilika pamaso pa Mulungu
*Palibe masenga amene angalimbane ndi inu*
Palibe nyanga yomwe yingalimbane ndi inu.....
Palibe za ufiti zimene zingalimbane ndi inu...
*CHIFUKWA MULUNGU NDIWAKULU KUPOSA ZONSEZI, NDIWA MPHAMVU KUPONSA ZONSEZI*

Mulungu akakhala MWA iwe CHIPAMBANO CHIMAKHALA PALI YAKO

AMBUYE ATIDALITSE AMEN

Mtumiki Joshua Joshua
SHALLOM SHALLOM

09/06/2026

CHIMANDISATA NDICHANI??

Ndikulandileni abale mwambuye maka mu nthawi ino, mwaka nthawi kochepa chabe tiyeni tisatile uthenga uwu Hallelujah πŸ™Œ

Uthengawu mutu wake ndiwonena kuti Chimandisata ndichani... Limeneso Lili funso ... Limene munthu amantha kuzifunsa yenkha atatha kuchita chithu China chake, *Chimene amachichita asadaganizile kuti angathe kuchichita* koma chithu chimene munthu amachita ndikuzifunsa funso ili, kawiri kawiri chimakhala cholakwika Hallelujah πŸ™ŒπŸ™Œ

Pali zithu zina zomwe timazichita, chifukwa cha amene akulamulila Kati mwathu, amatikakhila kuchita zithu zimene ngakhale tokha sitimatha kuzimvesa Hallelujah πŸ™ŒπŸ™Œ

Kufuna timafuna titamachita zabwino, koma zomwe timachita ndizoipa osati zabwinoso ayi
*(Aroma 7 : 19)*
19. Ine sindichita zabwino zimene ndimafuna koma ndimachita zonyansa zimene sindikuzifuna.
Hallelujah πŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™Œ

Kufuna mumafuna mutakhala wokhulupilika Kwa mkazi wanu
Koma mukangoona mkazi wina mumafusila paka kugona naye

Kufuna mumafuna mutakhala wokhulupilika Kwa mwamuna wanu, koma mtima wosakhutisidwa ...wina akakufusilani simukana, kothela kwake agone Nanu

Kufuna mumafuna, mutakhala wokhulupilika pa nchito, koma chifukwa chakuchepa kwamalipi mumapezeka kuti mukubaso

Kufuna timafuna titakhazikika kutumikila choonadi, koma chifukwa chofuna ma members ndichopeleka, tikapezeka kuti tikutumikila zonama kuti anthu azitikonda

Kufuna timafuna titasiya kutukwana mamphuzo, boza, kunyonza, koma timapenzeka kuti tikuchitabe zoipazi

NDE ZIKAZIWIKA BANJA NDIKUTHA, NCHITO KUTHA UTIMIKI KUSOKONEKELA, TIMAZAZIFUNSA KUTI *(CHIMANDISA CHIYANI?)* zithu apa zimakhala zalakwika Hallelujah πŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™Œ

Chimene chikukusatana, ndi dyerekezi amene munapatsa khomo kuti alamulile mkati mwanu, ndipo amakupangani control kuti muzingochita zoipa

Choyenela kuchita ndi ichi
*( Yakobo 4 : 7)
7. Dziperekeni nokha kwa Mulungu. Mukaneni Mdierekezi ndipo adzakuthawani.
HALLELUJAH πŸ™ŒπŸ™Œ

WAKUMVA WAMVA WOSAMVA SANAMVE AMBUYE AKUDALISENI


SHALLOM SHALLOM

09/06/2026

HALLELUJAH!!

NDAIKA YEKHA PA TSOGOLO PANGA

Masalimo 16 : 8-9
8. Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
9. Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera; thupi langanso lidzakhala pabwino,
_______________
Kuti zithu zonse zomwe tikuchita zitiyendele kapena kutichitila ubwino Mulungu akhale patsogolo

Lero kwachelamu tili ndi nkhawa kuti zachuma sizikuyenda bwino
Nthupi mwathu sitikupeza bwino
Banja lathu sizikuyenda bwino
Ana athu sakutimvela
Mphatso yamwana yikusowa
Business siyikuyenda
Ndimagawo ena ambiri......

Musaganize zopita Kwa asing'anga tangoyikani Mulungu patsogolo
Pa nyengo yanuyo
Ndipo zonse zikhala bwino Hallelujah πŸ™ŒπŸ™ŒπŸ™Œ

MUKHALE NDI TSIKU LACHIPAMBANO AMEN

Mtumikijoshua

Zamphamvu
03/06/2026

Zamphamvu

30/05/2026

(Miyambo 3 : 6)
6. Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.

Address

T/A MAGANGA
Benoni

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mtumiki Joshua posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share