09/06/2026
CHIMANDISATA NDICHANI??
Ndikulandileni abale mwambuye maka mu nthawi ino, mwaka nthawi kochepa chabe tiyeni tisatile uthenga uwu Hallelujah π
Uthengawu mutu wake ndiwonena kuti Chimandisata ndichani... Limeneso Lili funso ... Limene munthu amantha kuzifunsa yenkha atatha kuchita chithu China chake, *Chimene amachichita asadaganizile kuti angathe kuchichita* koma chithu chimene munthu amachita ndikuzifunsa funso ili, kawiri kawiri chimakhala cholakwika Hallelujah ππ
Pali zithu zina zomwe timazichita, chifukwa cha amene akulamulila Kati mwathu, amatikakhila kuchita zithu zimene ngakhale tokha sitimatha kuzimvesa Hallelujah ππ
Kufuna timafuna titamachita zabwino, koma zomwe timachita ndizoipa osati zabwinoso ayi
*(Aroma 7 : 19)*
19. Ine sindichita zabwino zimene ndimafuna koma ndimachita zonyansa zimene sindikuzifuna.
Hallelujah πππ
Kufuna mumafuna mutakhala wokhulupilika Kwa mkazi wanu
Koma mukangoona mkazi wina mumafusila paka kugona naye
Kufuna mumafuna mutakhala wokhulupilika Kwa mwamuna wanu, koma mtima wosakhutisidwa ...wina akakufusilani simukana, kothela kwake agone Nanu
Kufuna mumafuna, mutakhala wokhulupilika pa nchito, koma chifukwa chakuchepa kwamalipi mumapezeka kuti mukubaso
Kufuna timafuna titakhazikika kutumikila choonadi, koma chifukwa chofuna ma members ndichopeleka, tikapezeka kuti tikutumikila zonama kuti anthu azitikonda
Kufuna timafuna titasiya kutukwana mamphuzo, boza, kunyonza, koma timapenzeka kuti tikuchitabe zoipazi
NDE ZIKAZIWIKA BANJA NDIKUTHA, NCHITO KUTHA UTIMIKI KUSOKONEKELA, TIMAZAZIFUNSA KUTI *(CHIMANDISA CHIYANI?)* zithu apa zimakhala zalakwika Hallelujah πππ
Chimene chikukusatana, ndi dyerekezi amene munapatsa khomo kuti alamulile mkati mwanu, ndipo amakupangani control kuti muzingochita zoipa
Choyenela kuchita ndi ichi
*( Yakobo 4 : 7)
7. Dziperekeni nokha kwa Mulungu. Mukaneni Mdierekezi ndipo adzakuthawani.
HALLELUJAH ππ
WAKUMVA WAMVA WOSAMVA SANAMVE AMBUYE AKUDALISENI
SHALLOM SHALLOM