24/05/2026
Muli Bwanji abale mwambuye kulikonse komwe muli mu nthawi ino?
Tikumbusane mau wopenzeka m'buku la
*(1 Yohane 1 : 9)*
9. Koma tikavomereza machimo athu, Iye ndi wokhulupirika ndi wolungama ndipo adzatikhululukira machimo athu, nadzatiyeretsa ndi kutichotsera chosalungama chilichonse.
_______________
Chosalunga chilichonse chomwe timachita, chimatithandizila kuti tikhale muuchimo, kusayeluzika kulikonse komwe timachita, kumatipanga ife... Kukhala wosayenela pamaso pa Mulungu, kapena kulekanisidwa ndi Mulungu..... *(Yesaya 59:1-2)* Hallelujah 🙌🙌
Nde mau amene akupezeka pa 1 Yohane 1:9
Ndi mau amene akhonza kutilumikizisaso ndi Mulungu, kapena kutichosa ife mu ukapolo wauchimo Hallelujah 🙌🙌🙌
Titakhala kuti tawamva mauwa ndikuchita monga momwe mau akufotokonzela Hallelujah 🙌🙌
1, MAU AKUTI TIMVOMELEZE
-Yichi ndichisankho chomwe tikhonza kuchita patokha, chifukwa zoyipazo timachita kwatokha Hallelujah 🙌
Nde ndiudindo wathu tsopano ngati tikufuna chipulumutso kumvomekeza kuti, Ambuye wochimwayo ndine ndikumvomeleza
Pamaso pache Hallelujah 🙌🙌
2, MULUNGU ALI WOKHULUPILIKA NDI WOLUNGAMA KUTIKHULULUKILA
-Titantha kumvomekeza, timakhala ngati tamusegulila nkhomo Ambuye Mulungu, ndipo Iye azakhululuka mphulupulu zathu zonse , nde kuti ubale uzabwezelesedwa chipulumutso chizakhala pa njila yathu Hallelujah 🙌🙌
Kusonyeza kuti ngati sititenga step yakumvomeleza ndekuti tikuzipha tokha Hallelujah 🙌🙌
3, AZATIYELESA HALLELUJAH 🙌🙌
-Machimo omwe timachita amatipanga ife kukhala wodesedwa Amen
Nde chifukwa chakumvomeleza, tizayelesedwa kuchonseledwa chosalungama chilichonse Hallelujah 🙌🙌
(Nde enanu muli ndi funso lonena kuti, nde Abusa amafunikila Bwanji kutengela ndikuphuzitsa kwanu, si ndiye kuti ukhonza kungochita pawenkha Hallelujah 🙌🙌)
Mawa zisomo za Ambuye zikapenzeka tizapitilinza chiphuzitso chakulapachi Amen