Mtumiki Joshua

Mtumiki Joshua TIYENI TIYITANILE YEHOVA PA NYENGO YANU, NDIPEPHELO NDIPO NDICHIKHULUPILILO YEHOVA ASINTHA NYENGOYO (NDI MULUNGU NDIZOTHEKA (MATEYU 19:26) CALL/WSP 0988449135

30/05/2026

(Miyambo 3 : 6)
6. Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.

29/05/2026

Zambiri zikuchitika Ku dziko ili, tsiku ndi tsiku anthu akusikila kulichete, kutengeledwa zipatala, ngozi zosiyanasiyana *KOMA MULUNGU AKUKHALABE NTHANDIZO PA MOYO WANU PA MOYO WANGA*
Nthawi yimene Mulungu akutipasa ndikutisiyila tisayisewelese koposa kuti, tiyigwilise nchito bwino pomutumikila, chifukwa sitikuziwa chamawa Hallelujah 🙌🙌

Pangani Follow page iyi

28/05/2026

Tisanayambe kuwelenga tipemphele Kaye, ndipo tikamaliza tipempheleso
Dalitsikani Amen

(Masalimo 1 : 1-6)
1. Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2. Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3. Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4. Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5. Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6. Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.
Hallelujah 🙌🙌🙌🙌🙌


0982144285 WSP/call

Sinu woyamba kudusa munyengo yolimba koma Mulungu mwa Mulungu, Yobu anadusaso munyengo yolimba koma Mudzonse analemekeza...
26/05/2026

Sinu woyamba kudusa munyengo yolimba koma Mulungu mwa Mulungu, Yobu anadusaso munyengo yolimba koma Mudzonse analemekeza Mulungu, munyengo yanuyo musanyonze Mulungu koma Mudzonse mulemekezeni popenza Iye salakwitsa Hallelujah 🙌🙌🙌🙌

Ndikukupemphelelani kuti muyimebe, chifukwa kumapeto kwazonsezo kuli madalitso Kuli mayankho Hallelujah 🙌

Pangani follow page iyi

26/05/2026

Ukakhala pa mvuto anthu amene amakuthandiza ndi anthu amene siwumaganizila Hallelujah 🙌🙌

25/05/2026

Muli Bwanji abale mwambuye kulikonse komwe muli mu nthawi ino?

Kupitilinza kukumbusana zakubadwa mwatsopano....
Pa funso lonena kuti
*(Abusa amafunikila Bwanji pamene munthu ukufuna kumulandila Yesu kapena kubadwa mwatsopano?)*

____________
Tisanafike m'kuyankha kwa funso ili ndichite mobweleza, pachimene ndimatumikila dzulo ..... Kunena kuti
KUBADWA MWATSOPANO, ndichisankho chomwe timachita kwatonkha.... Titantha kumva mau, ndikuwakhulupilila Hallelujah 🙌🙌🙌

Nde Atsogoleli kapena azibusa amafunikila pazifukwa IZI;

1, KUKUPEMPHELELA KAPENA KUKUYIKIZA MANJA MWA MULUNGU WUTANTHA KUMVOMELEZA MACHIMO AKO
Paulo akulakhuala ichi
*(Aefeso 1 : 17-19)*
17. Ndimapemphera kuti Mulungu wa Ambuye athu Yesu Khristu, Atate a ulemerero akupatseni mzimu wa nzeru ndi wa vumbulutso, kuti mumudziwe kwenikweni.
18. Ndimapempheranso kuti maso a mitima yanu atsekuke ndi cholinga choti mudziwe chiyembekezo chimene Iye anakuyitanirani, chuma cha ulemerero chomwe chili mwa anthu oyera mtima.
19. Ndiponso ndikufuna kuti mudziwe mphamvu zake zazikulu koposa zimene zili mwa ife amene timakhulupirira. Mphamvuyi ndi yofanana ndi mphamvu yoposa ija
Hallelujah 🙌🙌🙌🙌

Nde ukakhala kuti wangomvomeleza kwawekha popanda Pemphelo, enanu ndi mboni
Mutamvomeleza kuti
Kubunyula ndichimo
Ndisiye ndimulandile Yesu
Nokha ndikungopemphela
*Pano munayambilaso uchimowo*

Pamafunika kuti timvesese kunena kuti, ziwanda zomwe zimatilamulila kuchita chimo kapena choyipa, sizingangochoka wamba ..... Pamafunika wina amene Ali wodzuka muuzimu, kuti akuthandizile kukutulusa mumakhalidwe akale utantha kumvomekeza Hallelujah 🙌🙌🙌🙌
Nde Abusa amafunika kuti ayime nawe mupemphelo
Lakumulandila Yesu khristu Hallelujah 🙌🙌🙌

2, ABUSA amafunika kuti azikulimbikisa ndikukuwunikila tsiku ndi tsiku Hallelujah 🙌🙌🙌🙌

Pamene wamulandila Yesu Umakhala ngati ndiwe mwana muuzimu, ndipo tikamayang'ana za mwana ndi munthu amene sazichitila zonse pa yenkha Hallelujah 🙌🙌
Nde kuuzimutso sumatha kuzichitila zonse pawenkha, Ndiye Busa uja amayima tsopano ngati thandize
Pang'ono ndipa ng'ono umayamba kubwelamo ndichiziwitso pa mau a Mulungu Hallelujah 🙌🙌🙌
Koma wenkha wenkha kopanda womakuunikila zithu zina kapena kukumphuzitsa kumakhala kosamvuta
Kubwelelaso kuzoipa Hallelujah 🙌🙌
*(Mateyu 28 : 20)*
20. ndi kuwaphunzitsa amvere zonse zimene ndinakulamulirani. Ndipo onani, Ine ndidzakhala pamodzi ndi inu kufikira kutha kwa dziko lapansi pano.”
Hallelujah 🙌🙌🙌
Ndicholinga choti ukule kuchauzimu chako umafunika mau a Mulungu pafupipafupi Hallelujah 🙌🙌🙌🙌

AMBUYE AKUDALISENI CHIFUKWA CHA NTHAWI YANU KUSATILA UTHENGAWU AMEN

Muli Bwanji abale mwambuye kulikonse komwe muli mu nthawi ino?*TIZIMVELE TONKHA!!!*(Masalimo 34 : 12-14)12. Aliyense wa ...
25/05/2026

Muli Bwanji abale mwambuye kulikonse komwe muli mu nthawi ino?

*TIZIMVELE TONKHA!!!*

(Masalimo 34 : 12-14)
12. Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,
13. asunge lilime lake ku zoyipa ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.
14. Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; funafuna mtendere ndi kuwulondola.
Hallelujah 🙌🙌

24/05/2026

Muli Bwanji abale mwambuye kulikonse komwe muli mu nthawi ino?

Tikumbusane mau wopenzeka m'buku la
*(1 Yohane 1 : 9)*
9. Koma tikavomereza machimo athu, Iye ndi wokhulupirika ndi wolungama ndipo adzatikhululukira machimo athu, nadzatiyeretsa ndi kutichotsera chosalungama chilichonse.

_______________
Chosalunga chilichonse chomwe timachita, chimatithandizila kuti tikhale muuchimo, kusayeluzika kulikonse komwe timachita, kumatipanga ife... Kukhala wosayenela pamaso pa Mulungu, kapena kulekanisidwa ndi Mulungu..... *(Yesaya 59:1-2)* Hallelujah 🙌🙌

Nde mau amene akupezeka pa 1 Yohane 1:9
Ndi mau amene akhonza kutilumikizisaso ndi Mulungu, kapena kutichosa ife mu ukapolo wauchimo Hallelujah 🙌🙌🙌

Titakhala kuti tawamva mauwa ndikuchita monga momwe mau akufotokonzela Hallelujah 🙌🙌

1, MAU AKUTI TIMVOMELEZE
-Yichi ndichisankho chomwe tikhonza kuchita patokha, chifukwa zoyipazo timachita kwatokha Hallelujah 🙌
Nde ndiudindo wathu tsopano ngati tikufuna chipulumutso kumvomekeza kuti, Ambuye wochimwayo ndine ndikumvomeleza
Pamaso pache Hallelujah 🙌🙌

2, MULUNGU ALI WOKHULUPILIKA NDI WOLUNGAMA KUTIKHULULUKILA
-Titantha kumvomekeza, timakhala ngati tamusegulila nkhomo Ambuye Mulungu, ndipo Iye azakhululuka mphulupulu zathu zonse , nde kuti ubale uzabwezelesedwa chipulumutso chizakhala pa njila yathu Hallelujah 🙌🙌
Kusonyeza kuti ngati sititenga step yakumvomeleza ndekuti tikuzipha tokha Hallelujah 🙌🙌

3, AZATIYELESA HALLELUJAH 🙌🙌
-Machimo omwe timachita amatipanga ife kukhala wodesedwa Amen
Nde chifukwa chakumvomeleza, tizayelesedwa kuchonseledwa chosalungama chilichonse Hallelujah 🙌🙌

(Nde enanu muli ndi funso lonena kuti, nde Abusa amafunikila Bwanji kutengela ndikuphuzitsa kwanu, si ndiye kuti ukhonza kungochita pawenkha Hallelujah 🙌🙌)

Mawa zisomo za Ambuye zikapenzeka tizapitilinza chiphuzitso chakulapachi Amen

23/05/2026

*DZIKO LAPANSI LIMADANA NDIKUUNIKA*

*(Luka 23 : 22-25)*

22. Kachitatu anawafunsanso iwo kuti, “Chifukwa chiyani? Kodi munthu uyu wachita choyipa chanji? Ine sindinapeze cholakwa mwa Iye chakuti aphedwe choncho ndingomukwapula ndi kumumasula.”
23. Koma ndi mawu ofuwulitsa, analimbikirabe kuti Iye apachikidwe, ndipo kufuwulako kunapitirira.
24. Choncho Pilato anatsimikiza kuchita zofuna zawozo.
25. Iye anawamasulira munthu amene anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe ndi kupha, amene ankamufunayo, ndipo anawapatsa Yesu mwakufuna kwawo.
________________

__________________

Mtumiki Joshua

21/05/2026

Mulungu azilemekeze yekha pa nyengo yanu Utsiku Uno Amen Amen

Address

T/A MAGANGA
Benoni

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mtumiki Joshua posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share