Zomba Cathedral Parish

Zomba Cathedral Parish Evangelisation

Mwambo wansembe ya Ukaristia ya Chaka Cha Ulimbitso komanso wotsekulira mwezi wa Bible pa mzere wa Dayosizi uli mkati ku...
06/09/2026

Mwambo wansembe ya Ukaristia ya Chaka Cha Ulimbitso komanso wotsekulira mwezi wa Bible pa mzere wa Dayosizi uli mkati ku Holly Trinity Matawale Parish mu Diocese ya Zomba ndipo ukutsogoleredwa ndi Ambuye Alfred Mateyu Chaima omwe ndi Episkopi wa Diocese ya Zomba.

Ku mwambowu kwafika akhristu eni ake ochokera mma out church ozungulira Holly Trinity Matawale Parish pofuna kudzachitira umboni kulimbitsidwa kwa Ana awo. Ana amene akulandira Sacrament la Ulimbitso mu tsiku la lero ndi ana okwanira 200.

Mu ulaliki wawo Ambuye Alfred Mateyu Chaima alangiza makolo a ana amene alandira Sacrament la Ulimbitsoli kuti ayesetse kuwalimbikitsa anawa kulowa mmagulu osiyanasiyana a mumpingo komaso kuti ayenera kumabwera ku church mokhulupirika. Ndipo Iwo anatsindika ponena kuti mwa anawa akuonamo Asistere komaso Ansembe.

Chaka ndi Chaka mwezi wa September mpingo wa Katolika umachita Chaka Cha Bible ndipo ku Dayosizi ya Zomba mwambo waukulu wotsekulira mwezi wa Bible ukuchitikira ku Holly Trinity Matawale Parish.

03/09/2026
Mwambo wansembe ya Chaka Cha Ulimbitso uli mkati ku St Matias Nankhunda parish mu Diocese ya Zomba. Amene akutsogolera M...
09/08/2026

Mwambo wansembe ya Chaka Cha Ulimbitso uli mkati ku St Matias Nankhunda parish mu Diocese ya Zomba. Amene akutsogolera Mwambo wa Nsembe ya Ulimbitso imeneyi ndi Olemekezeka Ambuye Alfred Mateyu Chaima Episcope wa Diocese ya Zomba. Kumwambowu kwafika akhristu eni ake ochuluka ochokera mma out church ozungulira Nankhunda parish , kufuna kuzaikira umboni kulimbitsidwa kwa Ana awo. Ana amene alandira Sacrament la Ulimbitso mu tsiku la lero ndi ana okwanira 158. Polankhulapo pa ulaki wawo Ambuye Alfred Mateyu Chaima alangiza makolo a ana amene alandira Sacrament la Ulimbitso li kuti ayesetse kuwalimbikitaa anawa kulowa magulu osiyanasiyana a mupingo komaso kuti ayenera kumabwera ku church mokhulupilika.

Ana okwana 203 alandira Sacrament la Ukalistia lero La Mulungu Ku Sacred Heart Parish, Zomba Cathedral. Mwambo wa nsembe...
26/07/2026

Ana okwana 203 alandira Sacrament la Ukalistia lero La Mulungu Ku Sacred Heart Parish, Zomba Cathedral. Mwambo wa nsembe ya Ukalistia imeneyi unatsogoleredwa ndi bambo Hemesi Malata mothandidzana ndi a Dikoni Andasoni Mpereya.

Bambo Malata alangiza anawa kuti akonde kutumikira komaso apempha makolo kuti anawa asawasandutse alonda tsiku la Mulungu likakwana.

Wapampando wa church council anayamikira aphunzitsi omwe asula anawa kuti afike polandira Sacrament la Ukalistia .

Nsembe ya Ukalistia ya mwambo wa Chilundu omwe ukuchitika Ku Zomba Cathedral ndipo akutsogolera nsembe ya Ukalistia imen...
18/07/2026

Nsembe ya Ukalistia ya mwambo wa Chilundu omwe ukuchitika Ku Zomba Cathedral ndipo akutsogolera nsembe ya Ukalistia imeneyi ndi a Vicar General bambo Bernard Chipole. Mothandizana ndi a Pastoral secretary bambo Anthony Chidumu, a Dean a Zombie Deanary bambo Raphael Bendera, bambo Mulangidzi a bungwe la amayi bambo Mike Nkhomeni, ndi ansembe ena.
Nsembe ya Ukalistia imeneyi ndi ya Chilundu Fundraising yomwe amayi a Zomba Diocese amalidza ngati imodzi mwanjira yioezera chuma choyendetsera bungweli mu Dayoseziyi.
Amayi ochokera ma Parrish onse 20 amu Dioseziyi ndiomwe afika Ku mwambowu.

Mpingo wakatolika ku Diocese ya Zomba lero wakhazikitsa Gulu la Atumiki a Chifundo. Mwambo Wu unayamba ndi mdipiti omwe ...
06/06/2026

Mpingo wakatolika ku Diocese ya Zomba lero wakhazikitsa Gulu la Atumiki a Chifundo. Mwambo Wu unayamba ndi mdipiti omwe unayambira kwa Jali Trading center kukathera ku Our lady Pirimit Parish. Ndipo mau akulu patsiku li anali Bwerani Mudzaone (Yohane 1:38-39. Anatsogolera Mwambo wa Nsembe ya Ukaristia ndi Olemekezeka Ambuye Alfred Mateyu Chaima Episcope wa Diocese ya Zomba. Bungwe la Atumiki Achifundo kuno ku Zomba Anayambitsa ndi Mayi Jane Mkandawire

Amati Akatolika amodzi pa Utumiki.Uwu ndi mutu umene Bambo Stanislaus Confidence Mchenga adagawana nawo azimayi a CWAZom...
22/02/2026

Amati Akatolika amodzi pa Utumiki.
Uwu ndi mutu umene Bambo Stanislaus Confidence Mchenga adagawana nawo azimayi a CWAZomba Deanery Ku Zomba Cathedral Church.

Fr Mchenga walangidza amayi kuti utumiki si mpikitsano ayi
Ndipo bambowa apempha amayi kukhala ozichepetsa monga amayi Maria ankachitita, Iwo ati ngati amayi azithanso kukhala ndi udindo opempherera ena komanso Mpingo.
Potsilidza Iwo awapempha amayi kuti akagawane ndi amayi amdzawo za zomwe amva Ku Bindikiro kuti onse ayendere limodzi.
Mayi Caro Solomon Kayange yemwe ndi wapampando mu Zomba Denary wayamikira amayi chifukwa chobwera mwa unyinji Ku Bindikirowu mayi Kayange walimbikitsa amayi omwe anabwera kuti akagawireko amayi anzawo za bindikirowu

Amayi a Zomba Deanery akhala ndi Bindikiro wawo mawa Ku Zomba Cathedral, ndipo udzayamba  nthawi ya 8 koloko mawa. Ochit...
20/02/2026

Amayi a Zomba Deanery akhala ndi Bindikiro wawo mawa Ku Zomba Cathedral, ndipo udzayamba nthawi ya 8 koloko mawa.
Ochititsa ndi a Dean a Zomba Deanery FR R Mbendera omwenso ndi bambo mfumu a Sacred Heart Parish.
Amayi nonse mukupemphedwa kufika mwa unyinji.

Address

Sacred Heart Zomba Cathedral, P. O Box 106, Zombaa
Zomba

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Zomba Cathedral Parish posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share