Zomba Diocese catholic youths

Zomba Diocese catholic youths It's Zomba diocese Catholic youth

its another year to our former chair,Zomba diocese    Kondwani Chikuni
16/06/2026

its another year to our former chair,Zomba diocese

Kondwani Chikuni

kopita surtaday pa 20 kwapezeka tiyen uku
15/06/2026

kopita surtaday pa 20 kwapezeka tiyen uku

07/06/2026
06/06/2026

KODI CHIKUKU CHIMATANTHAUZANJI?

By Fr. J.E Manyoni, Dp - Namitete Parish, Lilongwe

Ndinalandira funso kuchokera kwa inu a Salah Kaunda komanso a Mary Msiska, kuti kodi Chikuku Chimatanthauzanji kwenikweni. Tsono ndinaona kuti funsoli lisangothera ku comment section koma lithandizenso ena kuti amvetse bwino za yankho lake.

✝️ Poyambirira penipeni tidziwisaneko kuti mau oti Chikuku ndi olakwika makamaka ngati tiwagwiritsa ntchito pofuna kutanthauza Chikondwerero cha Thupi ndi Magazi a Yesu Khristu.

Mau amenewa adayamba kugwiritsidwa ntchito ndi makolo athu kuno ku Malawi potengera zimene zinkachitika pa tsiku lokondwerera Ukaristia.

Paja tikamaliza Nsembe ya Ukaristia, wansembe atanyamura Ukaristia, mophathana ndi akhristu eni ake amayenda mdipiti wosangalalira Ukaristia. Ndipo pamdipiti umenewu wansembe amanyamura Ukaristia mu Monstrus ndipo anthu ena amamuphimba ndi ka tent kapena tinene kuti kachikuku.

Ndiye makolo athu chifukwa chosowekera mau olondora a chikondwerero chimenechi amauzana kuti akupita ku Misa ya Chikuku. Choncho mau amenewa adafalikira ndithu.

Koma pofuna kupereka tanthauzo lenileni la chikondwerero cha tsikuli, Mpingo kuno kwathu wakhara ukutipempha kuti tisiye kugwiritsa ntchito mau oti CHIKUKU. m'malo mwake tiziti CHIKONDWERERO CHA THUPI NDI MAGAZI A KHRISTU, Kapena kuti CHAKA CHA UKARISTIA.

Ngati tifuna kudziwa zambiri za CHIKONDWERERO CHA THUPI NDI MAGAZI A KHRISTU,

Ndikufunireni kukozekera kwabwino kwa CHIKONDWERERO CHA THUPI NDI MAGAZI A KHRISTU, chomwe chichitike Lamulungu likubwerari.

ZIKOMO KWAMBIRI POWERENGA, MULUNGU ATIDALITSE TONSE NDIKULIMBITSA CHIKHULUPIRIRO CHATHU.
🙏🙏

Happy birthday 🎈🎂 christinah from thondweCri Khumbanyiwa
05/06/2026

Happy birthday 🎈🎂 christinah from thondwe
Cri Khumbanyiwa

happy birthday felistus from Zomba cathedral
01/06/2026

happy birthday felistus from Zomba cathedral

01/06/2026

tiwafunile zabwino zonse anzathu omwe akukayamba mayeso awo Lero a form 2 , osaiwala kusogoza mulungu first

Mwambo woika m’manda thupi la bambo Samuel Nawasha wachitika lero ku manda a ansembe ku Zomba Dayosizi. Polankhula pa mw...
25/05/2026

Mwambo woika m’manda thupi la bambo Samuel Nawasha wachitika lero ku manda a ansembe ku Zomba Dayosizi.

Polankhula pa mwambo wa Misa ya ulemu yotsanzikana ndi bambo-wa, Episkopi wa Dayosizi ya Zomba, Ambuye Alfred Mateyu Chaima, anati kusula wansembe ndi ntchito yayikulu kwambiri kotero kuti akamwalira mpingo komanso achibale amakhala kuti ataya mtumiki wofunikira kwambiri.

M’mawu ake, yemwe anaimilira ansembe a chibadwiri m’dziko lino, bambo Gerald Bwemba, anati ansembe ndiwodandaula kwambiri kaamba ka imfa ya bambo Nawasha.

Ndipo yemwe anaimilira Akhristu eni ake mu Dayosizi ya Zomba, a Masiyano Mambo, anati ndiwothokoza Dayosizi-yi kaamba ka thandizo lomwe yakhala ikupereka kwa bambo Nawasha pa nthawi yomwe anali kudwala, kuphatikizapo kuwatumiza ku zipatala za kunja kuti akalandire thandizo la mankwala.

Pamenepa a Mambo analimbikitsa Akhristu kuti aziwolowa manja popereka ndalama zothandidzira ansembe kupeza thandizo la chipatala akadwala, lomwe limadziwika kuti medical scheme.

Bambo Nawasha anamwalira Loweluka pa 23/05/2026 atadwala nthenda ya imphyo kwa nthawi yaitali. Iwo anabadwa pa 29 December mchaka cha 1956 ndipo anazozedwa kukhala wansembe pa 11 July mchaka cha 1987.

Mzimu wawo uuse ndi mtendere!!

*DEATH* *ANNOUNCEMENT*It is with the deepest sorrow that I regret to announce the passing on of Fr. Samuel  Nawasha to t...
23/05/2026

*DEATH* *ANNOUNCEMENT*

It is with the deepest sorrow that I regret to announce the passing on of Fr. Samuel
Nawasha to the Father.

Fr. Samuel has passed on the early hours of today at Zomba Central Hospital where he was rushed for medical attention. More details will be communicated later but there is a higher probability that the burial may be on Monday.

We accompany our brother in prayers and may the soul of Fr. Samuel Nawasha rest in eternal Peace.

Address

Zomba

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Zomba Diocese catholic youths posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share