02/04/2026
CHIPHUNZITSO CHA IMFA ndi KUWUKA KWA YESU KHRISTU
Aliyense amaopa imfa, ndipo ikafika nthawi imeneyi anthu amatha mnzeru:
- za imfa sitifuna kulingaliranso
- imfa palibe angailesetse.
- siyithawika
- paimfa ndalama ndi ma degree saapereka mayankho.
Zipembezo zambiri zimakamba za imfa, koma sizipereka mayankho enieni, mmalo mwake zimaonjezera chisoni ndi kulira.
📖:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::🕊️
Muli ndi ine Rev. Sangwati.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::
-- AHebri 9:27 --
- Ndipo popeza kwaikikatu kwa anthu kufa kamodzi, ndipo atafa, ciweruziro.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
Okondedwa wathu akamwalira, amakhala wangosintha malo okhala;
- Ngati wanyamuka alibe cholemetsa, amakasungidwa malo abwino, ongoyembekezera tsiku lenileni lomaliza
- Ngatinso sananyamuke bwino, amakasungidwanso malo, ozunzika, koma ongoyembekezera tsiku lomakizanso.
📖:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::🕊️
-- AHebri 2:14-15 --
14. Popeza tsono ana ndiwo a mwazi ndi nyama, Iyenso momwemo adalawa nao makhalidwe omwewo kuti mwa imfa akamuononge iye amene anali nayo mphamvu ya imfa, ndiye mdierekezi.
15. Nakamasule iwo onse amene, cifukwa ca kuopa imfa, m'moyo wao wonse adamangidwa ukapolo.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
Pa chifukwa choti imfa inali ndi mphamvu pa munthu, Yesu Khristu Anazipereka kukagonjetsa imfa mmalo mwathu, kuti tikawomboledwe ku chilango chathu.
Imfa inalengedwa ndi Mulungu, ndipo inali pambali pa moyo, mmunda mwa Eden muja, koma inalibe mphamvu ilionse pa munthu.
Why? Chifukwa munthu anali ndi ulamuliro wonse pa imfa, komanso zonse zinali mdzikoli.
Inali ngati, chinjuchi chopanda sting/mbola. Kapena mkango opanda mano.
Koma pali chinthu chimodzi chomwe chinalakwika kuti imfa ikakhale ndi mphamvu, kuti ikakhale yamoyo pa munthu.
📖:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::🕊️
-- Genesis 2:16-17 --
16. Ndipo Yehova Mulungu anamuuza munthuyo, nati, Mitengo yonse ya m'munda udyeko;
17. koma mtengo wakudziwitsa zabwino ndi zoipa, usadye umenewo; cifukwa tsiku lomwe udzadya umenewo udzafa ndithu.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
Kusamvera ndilo tchimo lomwe linapereka mphamvu ku imfa yomwe inali chete mdzikomu.
Meaning: Adam anali ndi choice chosankha kumvera, kapena kusamvera.
Therefore: rebellion made sin, and sin activated death, and death killed a man.
Kusamvera kunabweretsa tchimo, nde tchimo lipereka mphamvu imfa kuti ikayambe ntchito yake yomwe anaipangira. Kenaka imfa inaphano munthu.
Apanso zikutitsimikizira kuti;
Imfa inalengedwa ndi Mulungu, osati satana. Koma ntchito yomwe satana Lucifer amachita ndi kukunyenga, kukupusitsa, uparamule nde akuthawe.
Zikutanthauza kuti; munthu ali ndi choice cholibvomereza ntchimo, kapena ayi mopanda kukakamizika ndi satana.
📖:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::🕊️
-- Genesis 3:1-5 --
1. Ndipo njoka inali yakucenjera yoposa zamoyo zonse za m'thengo zimene anazipanga Yehova Mulungu, Ndipo inati kwa mkaziyo, Ea! kodi anatitu Mulungu, Usadye mitengo yonse ya m'mundamu?
2. Mkaziyo ndipo anati kwa njoka, Zipatso za mitengo ya m'mundamu tidye.
3. Koma zipatso za mtengo umene uti m'kati mwa munda, Mulungu anati, Musadye umenewo, musakhudze umenewo, mungadzafe.
4. Njokayo ndipo inati kwa mkaziyo, Kufa simudzafai;
5. Cifukwa adziwa Mulungu kuti tsiku limene mukadya umenewo, adzatseguka maso anu, ndipo mudzakhala ngati Mulungu, wakudziwa zabwino ndi zoipa.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
Tonse amene tinabadwa ku mbewu ya Adam tinabadwa mu mbewu ya uchimo ndithu, ndipo tchimo linasefukira kuchoka kwa munthu mmodzi/banja lija.
Kutanthauza kuti: Adam ndi mkazi wake ngati munthu mmodzi anafa kuti Mawu a Mulungu, lomwe linali lamulo, akakhale owona, chifukwa Mulungu Akalankhula limakhala lamulo pompopompo.
Anachita kutsimikiza, "udzafa ndithu" kunali kulumbira, kuti ufune usafune, ukadzadya udzafa ndithu.
Adam anafa kuti Mulungu mawu Ake akhale owona;
- popeza Iye ndi okhulupilika pa Mawu Ake, ndipo Akalankhula, Naye Mulungu Amawatsatira Mawu Ake.
- ndipo limakhala lamulo ngakhale kwa Iye Mulungu, kuti Akhale owona ndi okhulupilika pa mawu Ake.
.. All people became the victims of sin. So Jesus Christ came to deal with the spirit of sin, not death, bcoz sin brought death to a man.
Why? He (Jesus )was not fearing death, bcoz he came obeying everything that God wanted.
Apapa munthu anakhala kapolo wa imfa kudzera mwa munthu mmodzi uja Adam, nde Yesu, ngati Adam omaliza, Anabwera kudzamvera chilichonse chomwe Adam oyamba uja anachikanika, nangoluzapo mphamvu ndi ulamuliro wake.. pokhala padziko lapansi.
Tchimo lomwe linaipitsa dzikoli ndi kubweretsa mabvuto omwe tikuwaona lerowa ndilo "KUSAMVERA"
Nde Mulungu sanakondwelebe kuti munthu opanga Yekha, kuti akalangidwe ndi ukali Wake wonse ayi. Chinamuwawa kwambiri Mulungu.
Apa ndi pamene pagona chikondi cha Mulungu.
Komabe poti Mawu Ake kuti akakhale okhulupilika, kumayenerabe kuti munthu wina AKAMUZINGE, AKAKHETSE MWAZI kuti munthu akafe ndithu, kukwaniritsa Mawu a Mulungu, koma anthu onse akhalebe opulumuka ku chilamulo cha imfa.
Koma nanga ndi ndani anakakwanitsa zimenezi, popeza anthu onse ndi ochimwa?
Chifukwa akafa ochimwa, imfa ikawasungabe ku ndende. Ndipo satana zimenezi amazidziwa bwino lomwe, moti anali kuseka phwete lamwano pamaso pa Mulungu kuti tikuwonerani kuti musova bwanji, ma key ndalama popeza munthu wanu wandimvera ine.
Nde Yehova Mulungu wamphamvu zonse Analamula mwana wa nkhosa, wofatsayo, wokhala ku dzanja lache la manja kuti, MWANA WANGA, PITA UKAKHALE Munthu pakati pawo, chilango Ichi ukachibvale ndi iwe, ukachite zonse zomwe ndakulamula, ukhale chitsanzo chakumvera.
📖:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::🕊️
-- Yesaya 52:13-15 --
13. Taonani, Mtumiki wanga adzacita mwanzeru; adzakwezedwa ndi kutukulidwa pamwamba, nadzakhala pamwambamwamba.
14. Monga ambiri anazizwa ndi iwe Israyeli, momwemo nkhope yace yaipitsidwa ndithu, kupambana munthu ali yense, ndi maonekedwe ace kupambana ana a anthu;
15. momwemonso Iye adzawazawaza mitundu yambiri; mafumu adzamtsekera Iye pakamwa pao; pakuti cimene sicinauzidwa kwa iwo adzaciona, ndi cimene iwo sanamva adzazindikira.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
Ndipo lonjezo ili lakubadwa kwa Yesu Khristu linaperekedwa ku;
-- Genesis 3:14-15 --
14. Ndipo anati Yehova Mulungu kwa njokayo, Cifukwa kuti wacita ici, wotembereredwa ndiwe wopambana ndi zinyama zonse ndi zamoyo zonse za m'thengo: uziyenda ndi pamimba pako, uzidya pfumbi masiku onse a moyo wako:
15. ndipo ndidzaika udani pakati pa iwe ndi mkaziyo, ndi pakati pa mbeu yako ndi MBEU YACE; NDIPO IDZALALIRA MUTU WAKO, ndipo iwe udzalalira citende cace.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
Mbewu iyi, yomwe ili Mesiya mwiniwake, inali solution yomwe inaperekedwa munthu atangochimwa, ngakhale Adam asanafunsidwe kuti wachita chiyani.
Zikutanthauza kuti;
Mulungu mwiniwake.. anazikhalitsa munthu, nkuzipachika Yekha, kuti akathetse chilamulo cha imfa pa munthu chisakagwire ntchito.
This is the HIGHEST LOVE OF GOD.
Popeza Yesu akuti; Ine ndi Atate ndi Amodzi,
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
-- Yohane 10:30 --
Ine ndi Atate ndife amodzi.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
So, satana akuwonelera mission yonseyi, koma chomwe saakudziwa ndi choti;
- zitheka bwanji kuti iwe (Yesu) ufe, chifukwa munthu kuti afe akuyenera kukhala ochimwa.
- Iwe ndi oyera, ndipo zowona sunachimwepo. Koma ufa bwanji. That's why satanayu akubwera kudzamuyesa, mchipululu muja, kuti ngati uli Mwana wa Mulungu, sanditsa mwalawo ukhale mkate udye, ndipo ziponye adzakuwakha.
Mateyu 4:1-11
Mariko 12-13
Luka 4:1-13
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
Pamafunika mwazi wa munthu ukakhetsedwe ndithu, popeza msembe za nyama zimafunika chaka ndi chaka pa munthu aliyense.
- Nde sitinalakwanitsa aliyense azipha ng'ombe kapena nkhosa chaka chilichonse ndi ana athu onse.
- Komanso chilango cha imfa chija chinanenedwa pa munthu, osati pa nyama.
Lonjezo la kudza Kwake linabvumbulutsidwanso kwa Yesaya mneneri.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
-- Yesaya 53:2-12 --
2. Pakuti ameneyo adzaphuka pamaso pace ngati mtengo wanthete, ndi ngati muzu womera m'nthaka youma; Iye alibe maonekedwe, pena kukongola; ndipo pamene timuona palibe kukongola kuti timkhumbe.
3. Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wazisoni, ndi wodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu wombisira anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamlemekeza.
4. Zoonadi Iye ananyamula zowawa zathu, ndi kusenza zisoni zathu; koma ife tinamuvesa wokhomedwa wokanthidwa ndi Mulungu, ndi wobvutidwa.
5. Koma Iye analasidwa cifukwa ca zolakwa zathu, natundudzidwa cifukwa ca mphulupulu zathu; cilango cotitengera ife mtendere cinamgwera Iye; ndipo ndi mikwingwirima yace ife taciritsidwa.
6. Tonse tasocera ngati nkhosa; tonse tayenda yense m'njira ya mwini yekha; ndipo Yehova anaika pa Iye mphulupulu ya ife tonse.
7. Iye anatsenderezedwa koma anadzicepetsa yekha osatsegula pakamwa pace; ngati nkhosa yotsogoleredwa kukaphedwa, ndi ngati mwana wa nkhosa amene ali du pamaso pa omsenga, motero sanatsegula pakamwa pace.
8. Anacotsedwa ku cipsinjo ndi ciweruziro; ndipo ndani adzafotokoza nthawi ya moyo wace? pakuti walikhidwa kunja kuno; cifukwa ca kulakwa kwa anthu anga Iye anakhomedwa.
9. Ndipo anaika manda ace pamodzi ndi oipa, ndi pamodzi ndi olemera mu imfa yace, ngakhale Iye sanacita ciwawa, ndipo m'kamwa mwace munalibe cinyengo.
10. Koma kunakomera Yehova kumtundudza; anammvetsa zowawa; moyo wace ukapereka nsembe yoparamula, Iye adzaona mbeu yace, adzatanimphitsa masiku ace; ndipo comkondweretsa Yehova cidzakula m'manja mwace.
11. Iye adzaona zotsatira mabvuto a moyo wace, nadzakhuta nazo; ndi nzeru zace mtumiki wanga wolungama adzalungamitsa ambiri, nadzanyamula mphulupulu zao.
12. Cifukwa cace ndidzamgawira gawo ndi akuru; ndipo adzagawana ndi amphamvu zofunkha; pakuti Iye anathira moyo wace kuimfa; ndipo anawerengedwa pamodzi ndi olakwa; koma ananyamula macimo a ambiri, napembedzera olakwa.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
This is the real Jesus Christ the messiah
Komanso ku
-- Malaki 3:1-6 --
Za mthenga wokonzeratu njira ya Ambuye:
1. Taonani, ndituma mthenga wanga, kuti akonzeretu njira pamaso panga; ndipo Ambuye amene mumfuna adzadza ku Kacisi wace modzidzimutsa; ndiye mthenga wa cipangano amene mukondwera naye; taonani akudza, ati Yehova wa makamu.
2. Koma ndani adzapirira tsiku la kudza kwace? ndipo adzaima ndani pooneka Iye? pakuti adzanga moto wa woyenga, ndi sopo wa otsuka;
3. Ndipo adzakhala pansi ndi kuyenga ndi kuyeretsa siliva, nadzayeretsa ana a Levi, nadzawayengetsa ngati golidi ndi siliva; pamenepo iwo adzapereka kwa Yehova zopereka m'cilungamo.
4. Pamenepo copereka ca Yuda ndi Yerusalemu cidzakomera Yehova, ngati masiku a kale lija ndi ngati zaka zoyamba zija.
5. Ndipo ndidzayandikiza kwa inu kuti ndiweruze; ndipo ndidzakhala mboni yakufulumira kutsutsa obwebweta, ndi acigololo, ndi olumbira monama; ndi iwo akunyenga wolembedwa nchito pa kulipira kwace, akazi amasiye, ndi ana amasiye, ndi wakuipsa mlandu wa mlendo, osandiopa Ine, ati Yehova wa makamu.
6. Pakuti Ine Yehova sindisinthika, cifukwa cace inu ana a Yakobo simunathedwa.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
Khristu Anabvomera kuwusiya ulemelero wonse, wa Mulungu, nachibvumbulutsa ichi kwa aneneri akale aja.
Remember Jesus is not an Angel. Si mngero Yesuyu, koma Angelo amagwada natumikira Iye ngati Prince okalowa mnyumba ya Mulungu.
Palibe analowamo mnyumba ya Mulungu, koma Christ Jesus/Yesu Khristu ndiye akudziwamo.
Uyu ndi yemwe amanyamuka pemphero la inu ndi ine, kukatipepesera pamaso pa Atate.
Ngati tipemphera osatchula Dzina La Yesu, pemphero silifika kwa Atate.
Ndipo Atate Amayankha pomukonda Mwana wawo Wokondedwa uyu.
Remember uwu ndi Ufumu, si boma la democracy lofuna kuvota, kusintha mtsogoleri ayi. So, boma la chifumu, zonse za mdzikomo zimakhala za mfumuyo.
Ndipo mabvuto onse a mdzikomo okonza imakhala mfumuyo.
Nde kwa mfumu, sumupita nokha direct.
📖:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::🕊️
Choncho amene akupachikidwa pa Good Friday ndi Mwana woyamba wa mwamuna, wa Mfumu,
- kufera mbabva zonse zili kunjako,
- kufera onse oyenda ndi maliseche.
- kufera onse onyoza ndi kutama mnzeru zawo ndi chuma chawo.
- kufera onse otama kukongola kwawo.
- kufera onse amene amati Mulungu kulibe, napembeza azising'anga, nalowa usatanic, nakhwima, kuchita zaufiti ndi zambiri
Chifukwa cha kuzichepetsa kwake pamaso pa Atate Wake, analibvala thupi la munthu, koma sanalore kuti akabadwe ndi mbewu yamwamuna, munthu ochimwa ujanso ayi, ngakhale sanakhudzana ndi thupi la mkazi ayi.
Mutafufuza bwinobwino, sipamakhala kukhudzana pakati pa mwana ndi mayi ake mmimba.
Chifukwa cha ululu pamtanda paja, anayesetsa kupempha Atate kuti mwina asinthe maganizo, koma Mulungu ndi okhulupilika pa lonjezano Lake, moti sanalorenso kuti kuti achibweze chilango ichi.
📖:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::🕊️
-- Mateyu 27:46 --
46. Ndipo poyandikira ora lacisanu ndi cinai, Yesu anapfuula ndi mau akuru, kunena, Eli, Eli, lama sabakitani? ndiko kunena kuti, Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji Ine?
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
It was too painful;
Thupi lake linaima pa misomali, and thupi lake kumva kuwawa kwake kunali komwe inu ndi ine timamva panalibe kuti uyu ndi mwana wa Mulungu.
📖:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::🕊️
-- Mateyu 27:50-53 --
50. Ndipo pamene Yesu analiranso mofuwula, anapereka mzimu wake.
51. Pa nthawi imeneyo chinsalu chotchinga cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati kuyambira pamwamba mpaka pansi. Dziko linagwedezeka ndipo miyala inangʼambika.
52. Manda anatsekuka ndipo mitembo yambiri ya anthu oyera mtima amene anafa inaukitsidwa.
53. Anatuluka mʼmanda mwawo, ndipo chitachitika chiukitso cha Yesu, anapita mu mzinda woyera naonekera kwa anthu ambiri.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
Apa ndi pamene pali pachimake pa kutulutsidwa kwa anthu a Mulungu, mu ndende yomwe imasunga aneneri onse omwe anachita bwino, koma amasungidwa ndi ndende za imfa zomwe zinali mmanja mwa Lucifer satana mdyelekezi.
Apa kunali koyamba mu history, imfa kuwona munthu osachimwapo chiyambile akulowa mu ndende.
Nde popeza imfa siyisunga munthu amene sanachimwepo, inagwada pansi kupereka mphamvu kwa Yesu Khristu ndi kulanda ma key a zipinda zonse zomwe zimasunga onse omwe amakhulupilira Mulungu.
Awa anatulutsidwa, ndikukasiyidwa malo a mtendele. That's why apo bible analemba ngati anauka kuwoneka ku dziko, koma zinachitika mu system ya kuuzimu, mu nthawi yomwe chinsalu chinang'ambika, ndinso chibvomerezi chinagwedeza, popeza kunali ma billion a mizimu ya athu kumalo kumeneku.
Mwa chifukwa ichi, mission ya Yesu Khristu, mu gawo loyamba inatheka.
Kwatsala kubweranso kwake, kudzatenga oyera mtima onse, mu mkwatulo, akakhalebe malo abwinowo, kufikira kutachitika chiweruzo chotsiriza. Akamubwezeretse munthu ku dziko lapansi, koma lokonzedwa mwatsopano, limene sitidzawonamo adani athu onse aja anakutsendezani, kukunyozani, kukulabvulani ayi.
Umu mulibe corruption, mulibe chinthu chako chako ayi, mulibenso mdima ayi, koma dziko lowala kowopsa, mmene simudzakhala kodetsa kalikonse.
📖:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::🕊️
-- Mateyu 6:33 --
Koma muthange mwafuna Ufumu wace ndi cilungamo cace, ndipo zonse zimenezo zidzaonjezedwa kwa inu.
:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::📖:
Inu ndi ine tiwufunefune ndi kukhala ana a ufumuwo, wa Mulungu, ndipo akuti zonse timazifunazo, zidzabwera mongowonjezera ngati kampunga komwe mwagula moyezetsa, amapatsira kumapeto. Moti sizingatheke kuyamba kuitanitsa owonjezera munagule, ndekuti sangakupatseni, muwoneka ngati okuba.
Ndekuti onse opempha asali ana a ufumuwo ndi akuba, awa akapeza amasiya kupemphera nkukalowelera, kukasakaza mwachikunja zabwino zija. Dalitso limapangidwa misuse.
Ambuye Akhale Nanu mu zonse 🙏
📖:::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::::🕊️
🕊️"EVERJOY MINISTRIES FAMILY"📖