20/07/2026
KUMAWAKUMBUKIRA AJA ANATITHANDIZA!
Zilipo nthawi zina tinazingidwa ndi mavuto ndipo sitinadziwe koti titembenukire. Anthu ambiri, kuphatikizapo amene tinkawadalira, analephera kutithandiza. Koma panabwera munthu amene mwina sankadziwika kwambiri, ndipo atatimvera chisoni anatithandiza.
Munthu ameneyo musadzamuiwale mukadzadalitsidwa. Ana ake musadzawaiwale. Chitirani iwo zabwino monga momwe iwo anakuchitirani zabwino.
Mawu a Mulungu akuti:
Miyambo 3:27
"Oyenera kulandira zabwino usawamane; pokhoza dzanja lako kuwachitira zabwino."
M'moyo uno:
1. Alipo amene tinali m'mavuto anatithandiza.
2. Alipo amene anatipatsa chakudya pamene tinalibe.
3. Alipo amene anatithandiza kupeza ntchito kapena mwayi wina.
4. Alipo amene anatipempherera ndi kutilimbikitsa pamene tinkafooka.
5. Alipo amene anatitsegulira chitseko chimene chinasintha moyo wathu.
Musawaiwale anthu amene Mulungu anagwiritsa ntchito kukuthandizani. Kuyamikira ndi chizindikiro cha mtima wabwino.
Copied pr chataika