27/05/2026
Pali nkhani yomwe inalembedwa mu Buku Lopatulika (Bible) yomwe anthu ambiri samaimvetsa.
Nkhani imeneyi ndi yomwe ikuoneka pa chithunzi chomwe chikuonekachi.
Nkhani imeneyi yakhala ikusoneza anthu ambiri mitu ndipo anthu ambiri akhala akuphunzitsa mosemphana ndi momwe chapter-chi chilili.
Ndawerengapo mabuku a zipembezo zosiyanasiyana, ma buku enanso omwe anthu ena amene anaphunzira za mau a Mulungu (Theology) analemba (Bible commentary) koma ndinapeza kuti nkhaniyi anthu samaimvesa mpaka pano
Tsono lero ndafuna kuti ndifotokozere za chapter chimenechi.
Chapter analemba chonchi:
Genesis 6:1-8
Ndipo panali pamene anthu anayamba kucuruka padziko, ndi ana akazi anawabadwira iwo, kuti ana amuna a Mulungu anayang'ana ana akazi a anthu, kuti iwo anali okongola; ndipo anadzitengera okha akazi onse amene anawasankha.
Ndipo anati Yehova, Mzimu wanga sudzakangana ndi anthu nthawi zonse, cifukwa iwonso ndiwo thupi lanyama: koma masiku ace adzakhala zaka zana limodzi kudza makumi awiri.
Pa dziko lapansi panali anthu akurukuru masiku omwewo ndiponso pambuyo pace, ana amuna a Mulungu atalowa kwa ana akazi a anthu, ndipo anabalira iwo ana, amenewo ndiwo anthu amphamvu akalekale, anthu omveka.
Ndipo anaona Yehova kuti kuipa kwa anthu kunali kwakukuru pa dziko lapansi, ndiponso kuti ndingaliro zonse za maganizo a mitima yao zinali zoipabe zokhazokha.
Ndipo Yehova anamva cisoni cifukwa anapanga munthu pa dziko lapansi, ndipo anabvutika m'mtima mwace.
Ndipo anati Yehova, Ndidzafafaniza anthu amene ndawalenga pa dziko lapansi; anthu, ndi nyama, ndi zokwawa, ndi mbalame za m'mlengalenga: pakuti ndimva cisoni cifukwa ndapanga izo.
Koma Nowa anapeza ufulu pamaso pa Yehova.
Nkhaniyo ndi imeneyi, kwinako ikupitilira koma ife tikufuna tione bwino pamenepa
Kwambiri anthu pomwe pamawasokoneza anthu ndi apa
Genesis 6:
1 Ndipo panali pamene anthu anayamba kucuruka padziko, ndi ana akazi anawabadwira iwo,
2 kuti ana amuna a Mulungu anayang'ana ana akazi a anthu, kuti iwo anali okongola; ndipo anadzitengera okha akazi onse amene anawasankha.
3 Ndipo anati Yehova, Mzimu wanga sudzakangana ndi anthu nthawi zonse, cifukwa iwonso ndiwo thupi lanyama: koma masiku ace adzakhala zaka zana limodzi kudza makumi awiri.
4 Pa dziko lapansi panali anthu akurukuru masiku omwewo ndiponso pambuyo pace, ana amuna a Mulungu atalowa kwa ana akazi a anthu, ndipo anabalira iwo ana, amenewo ndiwo anthu amphamvu akalekale, anthu omveka.
Motengera ndi zimene ndinapeza nditawerenga mabuku angapo, anthu amaphunzitsana kuti anthu omwe akunenedwa kuti ndi ana a Mulunguwo anali angelo amene anagwetsedwa kuchokera kumwamba atalakwa pamaso pa Mulungu pomwe ana a anthu ndi omwe anali olengedwa (kapena kuti ana a Abraham).
Ndiye amanena kuti akuti angelo amenewo atagwetsedwa kuchoka kumwamba anabwera pa dziko lapansi ndi kuvala matupi a anthu ndikuwatira akazi a dziko lapansi kenako nkuzabereka ana omwe anali a mphamvu kwambiri kuposa munthu wamba.
Umu ndi momwe anthu amaphunzilira.
Koma kodi chilungamo cha nkhaniyi ndi chiti?
Malinga ndi dzina la page ino. Ndinaika dzina loti "Choknadi ndi Chiti?" Chifukwa cholinga chake ndi kibweretsa chilungamo pa mau a Mulungu omwe ena samawamvesa kapena anawapotoza kwa anthu.
Tiyeni tione chindunji cha chapter chimenechi kuti chikutanthauza Chiyani....
Aroma 9:6-16
Koma sikuli ngati mau a Mulungu anakhala cabe ai. Pakuti onse akucokera kwa a Israyeli siali Israyeli; kapena cifukwa ali mbeu ya Abrahamu, siali onse ana; koma anati, Mwa Isake, mbeu yako idzaitanidwa.
Ndiko kuti, ana a thupi sakhala iwo ana a Mulungu ai; koma ana a lonjezo awerengedwa mbeu yace. Pakuti mau a lonjezo ndi amenewa, Pa nyengo iyi ndidzadza, ndipo Sara adzakhala ndi mwana Ndipo si cotero cokha, koma Rebekanso, pamene anali ndi pakati pa mmodzi, ndiye kholo lathu Isake; pakuti anawo asanabadwe, kapena asanacite kanthu kabwino kapena koipa, kuti kutsimikiza mtima kwa Mulungu monga mwa kusankha kukhale, si cifukwa ca nchito ai, koma cifukwa ca wakuitanayo, cotero kunanenedwa kwa uyo, Wamkuru adzakhala kapolo wa wamng'ono.
Inde monga kunalembedwa, Ndinakonda Yakobo, koma ndinamuda Esau. Ndipo tsono tidzatani? Kodi ciripo cosalungama ndi Mulungu? Msatero ai. Pakuti anati ndi Mose, Ndidzacitira cifundo amene ndimcitira cifundo, ndipo ndidzakhala ndi cisoni kwa iye amene ndikhala naye cisoni. Cotero sicifuma kwa munthu amene afuna, kapena kwa iye amene athamanga, koma kwa Mulungu amene acitira cifundo.
Mukaona verse imeneyi ya ku Aroma yomwe Paulo mtumwi wa Khristu analemba, mutu wa nkhani analemba kuti "ULAMULIRO WA MULUNGU WA KUSANKHA ENA"
Mwachidule verse imeneyo Paulo amafuna afotokoze kuti pali anthu ena Mulungu anawasankha kuti akhale ana ake ndipo ena sanawasankhe. Kusonyeza kuti pa dziko lapansi si onse amene ali ana ake ayi monga mwa kusankha kwa Mulungu.
Enatu mmene amva zimenezi abalalika, ndipo akufunsa kuti mesa tonse anatilenga ndi Mulungu yemweyo ndiye zitheka bwanji kuti ena sakhale ana ake?????
Indeee ndi zotheka, Mulungu amapanga chomwe chamkonda ndipo samalakwitsa.
Paulo akupereka chitsanzo kuti Mulungu anamkonda Yakobo koma anamuda Esau.
Apa wina sangabwere kumamuimba Mulungu mulandu ayi chifukwa Mulungu anapanga ganizo ndipo zinakhaladi momwemo
Izi zinakhalanso chimodzimodzi ndi pa nthawi ya mmbuyomu zisanafike pa Esau.
Genesis 4:1-24
(Kuopa kutalikitsa kwambiri nkhani sindilemba verse imeneyi, muwerenfe nokha mu bible komanso ndiika mu comment)
Apa tikuona nsembe ya Abele ikulandilidwa koma ya Kaini inakanidwa ndipo zitatero Kaini anamupha mphwake Abele.
Pamapeto pake Mulungu akumuchotsa Kaini pamaso pa abale makolo ake.
Kaini atachoka anakabereka ana ake kumeneko. Tiona pa verse 16 ndi pomwe akukamba za mbumba ya Kaini.
Mbumba iyi ndi yomwe ikutchedwa kuti "ANA A ANTHU"
Tsono tikaona pa Genesis 4 yemweyo alemba izi
Kubadwa kwa Seti
25 Ndipo Adamu anadziwanso mkazi wace; ndipo anabala mwana wamwamuna, namucha dzina lace Seti: Cifukwa, nati iye, Mulungu wandilowezera ine mbeu yina m'malo mwa Abele amene Kaini anamupha,
26 Ndiponso kwa Seti, kwa iye kunabadwamwana wamwamuna: anamucha dzina lace Enosi: pomwepo anthu anayamba kuchula dzina la Yehova.
Mwana wa chitatu wa Adam atabadwa ndi pamene anthu pa dziko lapansi anayamba kutchula dzina la Yehova kusonyeza kuti mwa Seti Mulungu anaika mbewu yake.
Tsono pa chapter 5 ndi pomwe akulemba mbumba ya Seti.
Awa ndi omwe amatchedwa "ANA A MULUNGU"
Kusonyeza kuti lemba la pa Genesis 6 amakamba kuti ana a Seti ndi omwe amayang'ana pa ana a Kaini ndipo anakakwatira kumeneko nabala anthu a mphamvu osati angelo anakwatira akazi ayi
DZIWANI ICHI:
Nzosatheka kuti angelo akwatire mkazi mwa njira iliyonse ayi chifukwa mau oti mngelo okhawo apamakhala kuti cha umunthu mwa iwo mulibe.
Kukwatira pamafunika pakhale zilakolako ndiye mngelo sakhala ndi zilakolako ayi or atakhala ochimwa
Chinaso ndi chomwe analemba Yuda
Yuda 1:6 Angelonso amene sanasunga cikhalidwe cao coyamba, komatu anasiya pokhala pao pao, adawasunga m'ndende zosatha pansi pa mdima, kufikira ciweruziro ca tsiku lalikuru.
Angelo amene anachoka kumwamba Mulungu anawatsekera mu ndende ndiye sindikudziwa kuti angelo amene anthu amanena kuti anakwatirawo anachoka kuti????
Ngati pali funso, muli ololedwa kutero ndilipo ine.
M***a kuwatumiziranso anzanu kuti nawo apindule
Ambuye akudalitseni.... 🙏 🙏 🙏