Ntcheu SDA Church

Ntcheu SDA Church PROCLAIMING THREE ANGELS MESSAGES
&
COMMUNICATING CHRIST WITH CLARITY

Tiyeni tigulitetu asanathe
28/05/2026

Tiyeni tigulitetu asanathe

Health Emphasis Week Day 4
27/05/2026

Health Emphasis Week
Day 4

MANJA NDI MAPAZI A KHRISTU: Ulendo wa Ntcheu Dorcas ku Gumbu Resource CentrePa 24 May 2026, amayi a Ntcheu Dorcas ochoke...
25/05/2026

MANJA NDI MAPAZI A KHRISTU:

Ulendo wa Ntcheu Dorcas ku Gumbu Resource Centre

Pa 24 May 2026, amayi a Ntcheu Dorcas ochokera ku Ntcheu SDA Church anayendera Gumbu Resource Centre yomwe ili pa Gumbu Primary School, komwe kumaphunzira ana omwe ali ndi mavuto osiyanasiyana a thupi.

Ngakhale ana amenewa amakumana ndi zovuta zambiri, akupitiriza maphunziro awo ndi chiyembekezo chokwaniritsa maloto awo mtsogolo. Ntcheu Dorcas anapita kukawathandiza pa zosowa zauzimu komanso zakuthupi.

Amayiwa anapereka zinthu zosiyanasiyana monga mafuta ophikira, soya pieces, sopo, ufa wa chimanga, mazira, mchere, nyemba komanso ma exercise books othandiza pa maphunziro a ana. Zinthu zimenezi zithandiza kuti ana azikhala ndi chakudya komanso malo aukhondo ophunzirira.

Kupatula thandizo la zinthu, panalinso uthenga wa Mulungu womwe unaperekedwa ndi Mrs. Masauko kuchokera m’Baibulo Loyera, kulimbikitsa ophunzira, aphunzitsi komanso mamembala a Dorcas kuti Mulungu amakonda ndi kusamalira aliyense.

Ulendowu unakhalanso wosangalatsa chifukwa cha nyimbo zotamanda Mulungu zomwe zinayimbidwa ndi amayi a Dorcas pamodzi ndi ophunzira a ku Gumbu Resource Centre.

Ogwira ntchito pa sukuluyi anayamikira kwambiri Ntcheu Dorcas chifukwa cha chikondi ndi thandizo limene anapereka. Ophunzirawo nawo anathokoza ponena kuti thandizoli lithandiza kuti aziphunzira bwino komanso kuchita bwino pa mayeso awo.

“Ndithu ndinena kwa inu, chilichonse chimene munachita kwa mmodzi wa aang’ono awa, munandichitira Ine.” — Mateyu 25:40

Tiyeni tipitirize kuwonetsa chikondi cha Khristu kudzera mu utumiki ndi kuthandiza ena.

Isaac Chisale Dauka
Ntcheu Communication Team

🌅 PHUNZIRO LA M’MAWA 🌅Mlaliki: Elder MsowoyaZinthu Zolepheretsa Kupita PatsogoloNyimbo: 49📖 Mlaliki 5:6🙏 Mawu a Phunziro...
24/05/2026

🌅 PHUNZIRO LA M’MAWA 🌅

Mlaliki: Elder Msowoya
Zinthu Zolepheretsa Kupita Patsogolo
Nyimbo: 49

📖 Mlaliki 5:6

🙏 Mawu a Phunziro 🙏

Monga Akhristu, Mulungu amafuna kuti tizikula mwa uzimu komanso kupita patsogolo pa ntchito yake. Chinthu chilichonse chimene chimalepheretsa kukula kwathu chimakhala chopinga pa kufalitsa uthenga wabwino.

📖 Zefaniya 1:12 ikutiphunzitsa kuti kukhala pamalo amodzi osasuntha ndi koopsa. Mlimi akabzala mbeu amaembekezera kuti ikule. Momwemonso, chikhulupiriro chathu ndi ntchito za mpingo ziyenera kukula tsiku ndi tsiku.

Tisalole ntchito ya Mulungu kuyima. Tiyeni titenge mbali pomanga nyumba ya Mulungu komanso kuthandiza ntchito yake mokhulupirika. Tisafooketsedwe ndi mawu a anthu chifukwa ntchito yomwe tikuchita ndi ya Mulungu.

✨ Chinthu chimodzi chomwe chimalepheretsa uthenga kufika bwino ndi MKWIYO.

📖 Aefeso 4:26

Mkwiyo umasokoneza zinthu zambiri ndipo anthu ambiri amapanga zisankho zolakwika chifukwa cha mkwiyo. Munthu akakhala wokwiya zimavuta kukhala ndi kudziletsa. Munthu wokhala ndi mkwiyo sangathe kulalikira uthenga wabwino mwamtendere komanso moyenera.

📖 Miyambo 22:24
📖 Miyambo 29:22
📖 Mlaliki 7:9

Ngati tikufuna kulumikizana bwino ndi anzathu mdziko lino la phokoso, tiyenera kukhala oleza mtima komanso opewa mkwiyo. Mulungu amasangalala ndi munthu amene walola kuti Mulungu azimulamulira moyo wake.

✨ China chomwe chimalepheretsa uthenga kulandiridwa bwino ndi BOZA.

Anthu ambiri amagwiritsa ntchito boza kuti apindule zinthu zina, koma mapeto ake amakhala chiwonongeko. Anthu akazolowera kuti munthu ndi wabodza, zimapangitsa kuti asamamukhulupirire.

📖 Miyambo 10:18
📖 Yohane 8:44

Baibulo limanena kuti Satana ndiye tate wa boza. Choncho ngati ndife ana a Mulungu tiyenera kuyankhula zoona nthawi zonse. Boza, kuononga ndi kunyenga ndi ntchito za Satana ndipo zimalepheretsa uthenga wabwino kufika bwino kwa anthu.

🙏 Pemphero:
Ambuye, tithandizeni kuchotsa mkwiyo, boza ndi zinthu zonse zomwe zimalepheretsa uthenga wanu kufika bwino. Tithandizeni kukula mwa uzimu ndi kukhala olumikiza uthenga wanu mokhulupirika mdziko lino la phokoso. Amen.

✨ ✍️Gift M***a ✨

A DOLIKA A CHICHEPERE ATSOGOLERA ZILINGANIZO MOPATSA CHIDWILero pa 23 May, 2026 linali tsiku la mtengo wapatali mu mbiri...
23/05/2026

A DOLIKA A CHICHEPERE ATSOGOLERA ZILINGANIZO MOPATSA CHIDWI

Lero pa 23 May, 2026 linali tsiku la mtengo wapatali mu mbiri ya Mpingo wa Ntcheu pomwe gulu la a Dolika achichepere anatsogolera zilinganizo pa tsiku lasabata.

Yemwe anatsitsimula anthu ndi uthenga olamitsa ochokera m'buku lopatulika ndi Nesi Nkosi ndipo anakhazikika pa buku la Mateyu 4:18-22 pomwe anatambasula momwe yesu anasankhira ophunzira ake kuti amutsatire iye.

Iye anazukutanso mabuku a Chivumbukutso 2:7 ndi Chivumbukutso 2:11 pomwe mpingo onse unadzidzimuka pakumva mmene ma vesiwa anatsidikila molumumikizana zokhudza nkhani yomvera Yehova.

Ulaliki unatha ndi nyimbo # 271 *Mkana tchimo nlalikulu* yomwe inapereka Chiyembekezo kuti machimo amakhululukidwa ndithu chomcho akhristu tikuyenera kulapa machimo athu ndikutsatira Yehova ndipo tidzikhala okomzeka.

Kunali zochititsa chidwi mchigawo cha masama pomwe asungwanawa anapitiriza kujijirika ndi uthenga omwe anazikika pa mutu oti *"Kutumikira Yehova tikanali achichepere"* ndipo mkati mwa chilinganizo munaphulika mingoli yoimbidwa ndi asungwanawa komanso magulu ena oimba a pa mpingo wa Ntcheu.

Poyankhula ndi mmodzi wa mamembala agululi a Shamaen Matewere, ati ndiokondwa kuti kukomzekera kwao kwa chilinganizo chi kwapindula chichifukwa zonse zayenda bwino ndipo akuyamika Yehova.

✍️ _Victor Van Mangwalala_

CMC Media

Dziko Likupita by Ntcheu Future Adventist Men
21/05/2026

Dziko Likupita by Ntcheu Future Adventist Men

Dziko_Likupita song from Gift M***ah. Release Date: May 20, 2026.

UKUCHITANJI KOMWE ULIKO?Preacher: Pastor Botolo📍 1 Mafumu 19:9-10,15Mneneri Eliya anali mtumiki wamphamvu wa Mulungu ame...
20/05/2026

UKUCHITANJI KOMWE ULIKO?

Preacher: Pastor Botolo
📍 1 Mafumu 19:9-10,15

Mneneri Eliya anali mtumiki wamphamvu wa Mulungu amene anachita zozizwitsa zambiri. Anali munthu wolimba mtima komanso woopa Mulungu kwambiri. Koma nthawi ina, atangoopsezedwa ndi Yezebeli, anayamba mantha ndipo anathawa mpaka kukabisala kuphanga.

Nthawi zambiri ifenso timafanana ndi Eliya. Tikakumana ndi mavuto, zokhumudwitsa kapena zinthu zikalephera kuyenda bwino, timayamba kubwerera m’mbuyo pa moyo wauzimu. Ena amasiyira Mulungu n’kuyamba kutsatira zinthu zosangalatsa za dziko lino. Koma Mulungu amafunsa kuti: “Ukuchitanji pano?”

Eliya anasiya malo amene Mulungu anamuyikapo ndi ntchito yomwe anapatsidwa. Lero lino, kodi ifenso sitinachoke pa malo amene Mulungu anatiika? Kodi tikukhala moyo umene ukukondweretsa Mulungu? Mulungu amaona zonse zimene timachita tsiku ndi tsiku.

Nthawi zina timasiya kupemphera, timasiya kutumikira Mulungu, timabisala m’zoipa kapena m’zokhumudwitsa monga Eliya anabisalira kuphanga. Koma uthenga wabwino ndi uwu 👇
✨ Mulungu sanataye Eliya.
✨ Mulungu anamubwezeretsa.
✨ Mulungu anamupatsa mwayi wachiwiri.

Nayenso Mulungu akukuitanani lero kuti mubwerere kwa Iye. Palibe amene Mulungu walephera kumukhululukira. Palibe moyo umene Mulungu sangathe kuwusintha.

Musakhale kutali ndi Mulungu pamene akukuitanani tsiku ndi tsiku kuti mubwerere kwa Iye.

🙏 “Tili ndi Mulungu amene amatipatsa mwayi wachiwiri. Tiyeni tibwerere kwa Iye lero.” 🙏

wolemba: M***ah Gift
CMC Media




19/05/2026

Ntcheu Adventures




GLOBAL ADVENTURE'S WEEK
17/05/2026

GLOBAL ADVENTURE'S WEEK

KUYENDA NDI YESU“Pamenepo Yesu analankhulanso nawo, nati, Ine ndine kuunika kwa dziko lapansi; wonditsata Ine sadzayenda...
16/05/2026

KUYENDA NDI YESU

“Pamenepo Yesu analankhulanso nawo, nati, Ine ndine kuunika kwa dziko lapansi; wonditsata Ine sadzayenda mumdima, koma adzakhala nako kuunika kwa moyo” (Yohane 8:12). Mwa chisomo cha Mulungu, tinali ndi Sabata lodzaza ndi madalitso komanso mphamvu za Mzimu Woyera motsogozedwa ndi ma Adventurer pa nthawi ya Global Adventurers Week. Sabata limeneli linatipatsa mwayi wophunzira mozama za kufunika koyenda ndi Yesu pa moyo wathu wa tsiku ndi tsiku, osati pa nthawi ya mapemphero yokha, koma pa chilichonse chimene timachita.

Kupyolera mu nyimbo, maulaliki, maphunziro a m’Baibulo komanso umboni wa chikhulupiriro, ana, achinyamata komanso akuluakulu analimbikitsidwa kukhala pafupi ndi Mulungu ndi kumudalira nthawi zonse. Alaliki athu, Unity Pindani komanso Khumbo Mbewe, anatiphunzitsa kuchokera m’Mawu a Mulungu pogwiritsa ntchito zitsanzo za anthu amene anayenda ndi Mulungu mokhulupirika. Kuchokera pa Eksodo 12, tinaphunzira za Mose, munthu amene Mulungu anamusankha chifukwa cha kukoma mtima Kwake kuti atsogolere anthu Ake, ngakhale anali ndi zofooka zake.

Tinaphunziranso kuchokera mu Genesis chapter 5, makamaka verse 18 komanso verse 22 mpaka 24, za Yaredi ndi Enock. Baibulo limanena kuti Enock “anayenda ndi Mulungu,” zomwe zikutanthauza kuti moyo wake unali wodzipereka kwa Yehova tsiku ndi tsiku. Chifukwa cha chikhulupiriro chake ndi ubwenzi wake wapamtima ndi Mulungu, Enock anatengedwa kupita kumwamba osalawa imfa. Izi zikutiphunzitsa kuti Mulungu amalemekeza anthu amene amamuyandikira ndi mtima wonse komanso amakhala okhulupirika pa ntchito Yake.

M’maulaliki onsewa, tinakumbutsidwa kuti kuyenda ndi Yesu sikungochitika mwa mawu okha, koma mwa moyo wosonyeza chikondi, kumvera, kupemphera, kuwerenga Mawu a Mulungu komanso kusiya machimo. Dziko lero ladzaza ndi mdima wa uchimo, mayesero komanso zosokoneza zambiri, koma Yesu akutiuza mu Yohane 8:12 kuti Iye ndiye kuunika kwa dziko lapansi ndipo aliyense womutsata sadzayenda mumdima. Mawu amenewa alimbikitsa Akhristu ambiri kuti tizisankha kuyenda ndi Yesu tsiku lililonse chifukwa Iye ndiye gwero la moyo ndi chipulumutso.

Pamene Global Adventurers Week ikutha, pemphero lathu ndi lakuti ziphunzitso zonse zomwe taphunzira zisinthe miyoyo yathu ndipo zitiyandikitse kwambiri kwa Mulungu. Tiyeni tipitilize kukhala kuunika kwa ena mwa moyo wathu wabwino ndi umboni wathu. Tingayende ndi Yesu pokhapokha ngati talapa, tasiya machimo athu kwathunthu, ndipo tavomera kutsogozedwa ndi Iye tsiku ndi tsiku.

Shalom.

Gift M***a
CMC Media – Ntcheu

16/05/2026

16 May 2026 Divine Service @ Ntcheu SDA Church

Preachers : Unity Pindani and Khumbo Mbewe

Rhythm: 133 and 40

Singing Group: Ntcheu Adventures and Senior Youth Choir

Address

Ntcheu Central SDA
Ntcheu

Telephone

+265997653297

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Ntcheu SDA Church posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share