16/05/2026
KUYENDA NDI YESU
“Pamenepo Yesu analankhulanso nawo, nati, Ine ndine kuunika kwa dziko lapansi; wonditsata Ine sadzayenda mumdima, koma adzakhala nako kuunika kwa moyo” (Yohane 8:12). Mwa chisomo cha Mulungu, tinali ndi Sabata lodzaza ndi madalitso komanso mphamvu za Mzimu Woyera motsogozedwa ndi ma Adventurer pa nthawi ya Global Adventurers Week. Sabata limeneli linatipatsa mwayi wophunzira mozama za kufunika koyenda ndi Yesu pa moyo wathu wa tsiku ndi tsiku, osati pa nthawi ya mapemphero yokha, koma pa chilichonse chimene timachita.
Kupyolera mu nyimbo, maulaliki, maphunziro a m’Baibulo komanso umboni wa chikhulupiriro, ana, achinyamata komanso akuluakulu analimbikitsidwa kukhala pafupi ndi Mulungu ndi kumudalira nthawi zonse. Alaliki athu, Unity Pindani komanso Khumbo Mbewe, anatiphunzitsa kuchokera m’Mawu a Mulungu pogwiritsa ntchito zitsanzo za anthu amene anayenda ndi Mulungu mokhulupirika. Kuchokera pa Eksodo 12, tinaphunzira za Mose, munthu amene Mulungu anamusankha chifukwa cha kukoma mtima Kwake kuti atsogolere anthu Ake, ngakhale anali ndi zofooka zake.
Tinaphunziranso kuchokera mu Genesis chapter 5, makamaka verse 18 komanso verse 22 mpaka 24, za Yaredi ndi Enock. Baibulo limanena kuti Enock “anayenda ndi Mulungu,” zomwe zikutanthauza kuti moyo wake unali wodzipereka kwa Yehova tsiku ndi tsiku. Chifukwa cha chikhulupiriro chake ndi ubwenzi wake wapamtima ndi Mulungu, Enock anatengedwa kupita kumwamba osalawa imfa. Izi zikutiphunzitsa kuti Mulungu amalemekeza anthu amene amamuyandikira ndi mtima wonse komanso amakhala okhulupirika pa ntchito Yake.
M’maulaliki onsewa, tinakumbutsidwa kuti kuyenda ndi Yesu sikungochitika mwa mawu okha, koma mwa moyo wosonyeza chikondi, kumvera, kupemphera, kuwerenga Mawu a Mulungu komanso kusiya machimo. Dziko lero ladzaza ndi mdima wa uchimo, mayesero komanso zosokoneza zambiri, koma Yesu akutiuza mu Yohane 8:12 kuti Iye ndiye kuunika kwa dziko lapansi ndipo aliyense womutsata sadzayenda mumdima. Mawu amenewa alimbikitsa Akhristu ambiri kuti tizisankha kuyenda ndi Yesu tsiku lililonse chifukwa Iye ndiye gwero la moyo ndi chipulumutso.
Pamene Global Adventurers Week ikutha, pemphero lathu ndi lakuti ziphunzitso zonse zomwe taphunzira zisinthe miyoyo yathu ndipo zitiyandikitse kwambiri kwa Mulungu. Tiyeni tipitilize kukhala kuunika kwa ena mwa moyo wathu wabwino ndi umboni wathu. Tingayende ndi Yesu pokhapokha ngati talapa, tasiya machimo athu kwathunthu, ndipo tavomera kutsogozedwa ndi Iye tsiku ndi tsiku.
Shalom.
Gift M***a
CMC Media – Ntcheu