Ntcheu SDA Church

Ntcheu SDA Church PROCLAIMING THREE ANGELS MESSAGES
&
COMMUNICATING CHRIST WITH CLARITY

KODI MULUNGU AKAKHALA CHETE, ZIKUTANTHAUZA KUTI WAKUIWALANI?Nthawi zina timapemphera kwambiri koma sitiona yankho. Timaf...
30/08/2026

KODI MULUNGU AKAKHALA CHETE, ZIKUTANTHAUZA KUTI WAKUIWALANI?

Nthawi zina timapemphera kwambiri koma sitiona yankho. Timafunsa Mulungu kuti atithandize, koma zinthu zikupitirizabe kukhala zovuta. Pamenepo munthu angayambe kuganiza kuti, “Kodi Mulungu akundimva?”

Koma Baibulo limatiphunzitsa kuti kukhala chete kwa Mulungu sikutanthauza kuti Mulungu kulibe. Nthawi zina Mulungu amakhala akugwira ntchito ngakhale ife sitikuona zimene akuchita. Mu Yesaya 55:8-9, Mulungu akutitsimikizira kuti maganizo ake ndi njira zake zili pamwamba pa zathu.

Yobu anakumana ndi nthawi imene sankamvetsa zimene Mulungu anali kuchita. Koma pamapeto pake anazindikira kuti Mulungu anali akadali naye. Izi zikutiphunzitsa kuti musasiye kukhulupirira Mulungu chifukwa chakuti yankho lanu lachedwa.

Mwina lero pali munthu amene wapemphera kwa nthawi yaitali ndipo akumva ngati Mulungu sakuyankha. Pitirizani kupemphera. Pitirizani kukhulupirira. Nthawi ya Mulungu si nthawi yathu, koma Mulungu samachedwa pa zimene ali nazo pa moyo wathu.

💬 FUNSO: Kodi munakumanapo ndi nthawi imene Mulungu anachedwa kuyankha pemphero lanu, koma pambuyo pake munazindikira chifukwa chake? Gawani testimony yanu mu comments. 👇🏽

Ngati mukukhulupirira kuti Mulungu akugwirabe ntchito ngakhale simukuona, lembani ” mu comments.

KODI MWAPEREKA CHIPINDA KWA NDANI?Lero, mpingo wa Ntcheu Central Seventh-day Adventist Church watumikiridwa kuchokera mu...
29/08/2026

KODI MWAPEREKA CHIPINDA KWA NDANI?

Lero, mpingo wa Ntcheu Central Seventh-day Adventist Church watumikiridwa kuchokera mu Nehemiah 13, pamene taona mmene Aisraeli ena anayambira kulowerera chifukwa cha maubwenzi omwe anawapangitsa kuiwala malamulo a Mulungu. Nehemiah 13:4 imati: “Chinkana ichi, Eliyasibu wansembe, woikidwa asunge zipinda za nyumba ya Mulungu wathu, anachita chibale ndi Tobiya.” Eliyasibu ankadziwa lamulo la Mulungu, koma chifukwa cha ubale wake ndi Tobiya, anamulola kulowa m’nyumba ya Mulungu.

Eliyasibu anamupatsa Tobiya chipinda chachikulu chomwe poyamba chinkasungiramo zinthu zofunika pa utumiki wa Mulungu monga lubani, vinyo ndi zinthu zina za m’kachisi. Tobiya, yemwe sanali wa mtundu wa Aisraeli, anapatsidwa malo omwe anayenera kusungiramo zinthu za Mulungu. Izi zikutiphunzitsa kuti nthawi zina tingalole maubwenzi kapena zinthu zina kutenga malo omwe anayenera kukhala a Mulungu.

Tikukumbutsidwanso mu Ahebri 8:10 kuti Mulungu akufuna kulemba malamulo ake m’mitima yathu ndipo akhale Mulungu wathu, ifenso tikhale anthu ake. Ifenso ndife akachisi amene Mulungu akufuna kukhala mwaife. Choncho tiyenera kudzifunsa kuti: Kodi m’mitima yathu tapereka malo kwa ndani? Kodi tikupereka malo kwa Yesu Khristu kapena tikulola zinthu zosayenera kulamulira moyo wathu?

1 Petro 2:9 imati: “Koma inu ndinu mbadwa yosankhidwa, ansembe achifumu, mtundu woyera mtima, anthu a mwini wake…” Monga anthu osankhidwa a Mulungu, tiyenera kusunga miyoyo yathu kukhala malo oyenera kukhalamo Mulungu. Sitiyenera kupanga “chipinda” cha Yesu Khristu n’kuperekanso malo kwa zinthu zomwe zingatisiyanitse ndi Iye.

Choncho uthenga wa lero ukutifunsa kuti: Kodi mwapereka chipinda kwa ndani? Tiyeni tiyang’ane zimene timalola kulowa m’mitima yathu, chifukwa zimene timapatsa malo m’moyo wathu zingayambe kutilamulira. Mulungu atithandize kuti mitima yathu ikhale malo oyera, okonzeka kulandira Yesu Khristu nthawi zonse. Mulungu akhale nanu pamene mukulingalira ndi kugwiritsa ntchito uthengawu pa moyo wanu wa tsiku ndi tsiku.

Shalom.

Wolemba: Gift M***a
CMC MEDIA-NTCHEU

27/08/2026

Dziko Likupita by Ntcheu Future Adventist Men

 ?TILIGU SEVENTH-DAY ADVENTIST CHURCH — DIVINE SERVICE22 October 2026Preacher: Grivin Modzi Sermon Title: Mwaima Pati pa...
22/08/2026

?

TILIGU SEVENTH-DAY ADVENTIST CHURCH — DIVINE SERVICE

22 October 2026

Preacher: Grivin Modzi
Sermon Title: Mwaima Pati pa Ulendo Wanu Wopita Kumwamba?
Song: 195
Singing Group: Kasale AY

Nyimbo ya Khristu nambala 195, “Tifuna Mzimu Wanu,” ndiyo inatitsogolera pa mapemphero athu lero. Taphunzitsidwa za Bartimeyo, munthu wakhungu amene sanali kuona, koma anali kumva. Ngakhale anali ndi chilema cha kusaona, Bartimeyo sanalole kuti chilema chake chimulepheretse kufunafuna Yesu. Atamva zambiri zokhudza Yesu Khristu, anakhala ndi chikhumbo chachikulu chofuna kukumana naye kuti alandire machiritso. Izi zikutiphunzitsa kuti zopinga zomwe timakumana nazo siziyenera kutilepheretsa kufunafuna Yesu.

Mu Luka 19:1–10, timapezanso nkhani ya Zakeyo, mkulu wa amisonkho ku Yeriko. Ngakhale kuti amisonkho ankawonedwa ngati anthu ochimwa kwambiri, Zakeyo anali ndi mtima wofuna kukumana ndi Yesu. Iye sanalole udindo wake, mbiri yake kapena zopinga zimene zinalipo kumulepheretsa kufunafuna Mpulumutsi. Pamene anakumana ndi Yesu, mtima wake unasinthika. Bartimeyo ndi Zakeyo onse anasonyeza kuti munthu sayenera kungodikira kuti Mulungu amupeze, koma ayenera kukhala ndi chikhumbo chofuna kukumana ndi Mulungu.

Choncho, tiyeni tidzifunsenso kuti: Kodi ndi zopinga ziti zomwe zikukulepheretsani kukumana ndi Yesu Khristu? Mwaima pati pa ulendo wanu wopita kumwamba? Kodi ndi nthawi iti yomwe mwalakalaka kuyandikira Yesu koma zinthu zina zakufooketsani? Lero tikuitanidwa kusankha Yesu Khristu kukhala Mbuye ndi Mpulumutsi wa miyoyo yathu. Tisamangonena kuti, “Tidzalapa, tidzalapa,” koma tidzifunze kuti, “Ndidzalapa liti?” Nthawi yabwino yobwerera kwa Yesu ndi lero.

Mulungu akhale pakati pa mitima yathu, atithandize kuchotsa zopinga zonse zomwe zikutilekanitsa ndi Iye, komanso atikonzekeretse kubwera kwake. Tsiku limene Khristu adzabwere, tikufuna tidzakumane naye maso ndi maso ndikumulandira Iye mwachimwemwe. Mulungu atithandize kuti tisangoyamba ulendo wopita kumwamba, koma tifikire kumapeto kwake tili okhulupirika kwa Yesu Khristu.

Shalom.

Wolemba
Gift M***a
CMC MEDIA–NTCHEU

21/08/2026

18/08/2026

NTCHEU AMO

16/08/2026
DEATH (IMFA)15 October 2026Preacher: Elder Moses AdamSermon Title: Imfa (Death)Song: 104Singing Group: Adventist Men Org...
15/08/2026

DEATH (IMFA)

15 October 2026

Preacher: Elder Moses Adam
Sermon Title: Imfa (Death)
Song: 104
Singing Group: Adventist Men Organisation (AMO)

During the Divine Service, Elder Moses Adam shared an important message on the subject of death, drawing lessons from the book of Genesis. He explained how God warned Adam that eating from the forbidden tree would result in death. From the beginning, God gave humanity a clear instruction and a condition: obedience would bring life, while disobedience would result in death.

The preacher emphasized that death is certain, although the circumstances surrounding each person's death may differ. Some may die through illness, accidents, old age, or while asleep. Therefore, the important question is not only how we will die, but how we are living today and whether we are prepared to meet our Creator.

Referring to Isaiah 40:6–8, Elder Moses reminded the congregation that human life is temporary:

“The grass withers, the flower fades, but the word of our God stands forever.”

He further referred to Psalm 90:10, which reminds us of the limited nature of human life. Living beyond 90 years should not be taken for granted, but rather received as a blessing and grace from God.

The preacher encouraged the congregation to remember that life is uncertain and death can come at any time. As reflected in the song presented by the men of AMO, tomorrow is not guaranteed. Therefore, every day should be used as an opportunity to honour God, serve others, and prepare spiritually.

Elder Moses also highlighted Psalm 115:17–18, which reminds us that those who have gone down into silence do not praise the Lord, while the living have the opportunity to praise Him. He therefore encouraged everyone to use the present time to worship and serve God faithfully.

The message was further strengthened by the Quarterly Sabbath School Lesson, which encouraged believers to grow in love, faith, and obedience to God.

As the service concluded, the congregation was reminded to remain faithful to God while they still have the gift of life.

“May the Lord continue to bless you and your children.”— Psalm 115:14

Shalom.

Written by:
Gift M***a
CMC Media – Ntcheu

CHIKONDI CHENICHENI | DIVINE SERVICE08 AUGUST 2026 🌸 DORCAS SEMINARPreacher: Shepherdess Manase🎶 Christ in Song: No. 17 ...
08/08/2026

CHIKONDI CHENICHENI | DIVINE SERVICE
08 AUGUST 2026 🌸 DORCAS SEMINAR

Preacher: Shepherdess Manase
🎶 Christ in Song: No. 17 & 133
🎵 Singing Group: DORCAS

“Mtima wofatsa, wachikondi ndi wokhululuka ndi mtima umene Mulungu amafuna mwa mwana wake.”

Pa Divine Service ya pa 08 August 2026, mpingo unakhala ndi Dorcas Seminar yomwe inatsogoleredwa ndi Shepherdess Manase. Uthenga wa tsikuli unakhazikika pa mutu wakuti “Chikondi Chenicheni,” ndipo tinaphunzira kuchokera mu nkhani ya Davide, Sauli ndi Yonatani.

Mu 1 Samueli 17, tinaona mmene Davide anagonjetsera Goliati chifukwa chokhulupirira Mulungu. Sauli atamupatsa zovala za nkhondo, Davide anakana chifukwa sanazolowere kuvala zovala zimenezo. Ngakhale kuti anali atapeza chipambano chachikulu, Davide sanadzikuze, koma anakhalabe wodzichepetsa. Izi zikutiphunzitsa kuti chipambano, udindo kapena kutamandidwa ndi anthu zisatichotse pa kudzichepetsa.

Yonatani ndi Davide anatisonyeza chitsanzo cha chikondi chenicheni ndi ubwenzi wokhulupirika. Yonatani sanayang’ane komwe Davide anachokera, udindo wake kapena zomwe anali nazo. Anamukonda m***a mtima ndipo anali wokonzeka kumuchitira zabwino. Chikondi chenicheni sichiyang’ana phindu limene tingapeze kwa munthu, koma chimafuna kuona zabwino mwa munthu wina ndi kumuthandiza pamene tingathe.

Ngakhale kuti Sauli ankafuna kupha Davide, Davide sanakondwere ndi imfa ya Sauli. M’malo mwake, analira maliro ake. Izi zikutiphunzitsa kuti tisamakondwere munthu amene watichitira zoipa akakumana ndi mavuto. Mkhristu ayenera kukhala ndi mtima wachifundo ndi wokhululuka, osati wa chidani ndi kubwezera. Tiyenera kupempherera anthu amene amatichitira zoipa, chifukwa Mulungu amafuna kuti anthu alape ndi kusintha moyo wawo.

Yonatani atamwalira, Davide sanaiwale ubwenzi wawo. Anakumbukira zabwino zimene Yonatani anamuchitira ndipo anafunsa ngati panali munthu aliyense wa m’banja la Yonatani amene akanamuchitira chifundo. Izi zikutisonyeza kuti chikondi chenicheni sichiyiwala zabwino zimene ena anatichitira.

Uthenga wa lero watikumbutsa kuti chikondi chenicheni chiyenera kuonekera mu mawu athu, zochita zathu, ubwenzi wathu komanso mmene timachitira ndi anthu ena. Tisamangonena kuti timakonda Mulungu, koma chikondi chimenecho chionekere mwa kukhululukira, kuthandiza, kulemekeza, kupempherera komanso kuchitira ena zabwino.

Mulungu akuchotseni mtima wa nsanje, chidani ndi kubwezera womwe unali mwa Sauli, ndipo akupatseni mtima wa chikondi, chifundo, kudzichepetsa ndi kukhulupirika womwe unaonekera mwa Davide ndi Yonatani.

Tiyeni tizikondana m***a mtima, kukhululukirana komanso kuchitirana zabwino, chifukwa chikondi chenicheni chimayambira mumtima ndipo chimaonekera mu zochita.

🙏 Mulungu atithandize kukhala anthu a chikondi chenicheni.

✍️ Wolemba: Gift M***a
📸 Wojambula: Kalabo Mchenga

Pezani Ticket lanu lero Ndi M***ah Gift
05/08/2026

Pezani Ticket lanu lero

Ndi M***ah Gift

Address

Ntcheu Central SDA
Ntcheu

Telephone

+265997653297

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Ntcheu SDA Church posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share