Corpus ChristNtcheu parish ,Dedza Diocese

Corpus ChristNtcheu parish ,Dedza Diocese Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Corpus ChristNtcheu parish ,Dedza Diocese, Religious organisation, Corpus Christi Ntcheu Catholic Church, Ntcheu.

To proclaim the Gospel of Jesus Christ, nurture Spiritual growth , and serve all people with love , compassion and dignity ,guided by the teachings of the Catholic Church

Mwambo wokumbukira moyo wa yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr. Saulos Klaus Chilima, ukuchitika lero...
13/06/2026

Mwambo wokumbukira moyo wa yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr. Saulos Klaus Chilima, ukuchitika lero kumudzi kwawo ku Nsipe m'boma la Ntcheu. Mwambowu wayamba ndi nsembe ya Ukaristia yomwe akutsogolera ndi episkopi wa dayosizi ya Zomba, Ambuye Alfred Mateyu Chaima. Ulaliki unachokera m'mabuku a Yesaya 25:6 mpaka 9 komanso kalata ya Paulo woyera kwa Aroma 8:31 mpaka 39.

Nduna ya zamaphunziro Bright Msaka ndiwo ali mlendo olemekezeka. Akulu akulu ena omwe afika pa mwambowu ndi Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko Lino Dr Jane Ansah, Mtsogoleri wa chipani cha UTM Dalitso Kabambe, yemwe anali Wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko Lino Michael Usi, Mtsogoleri wakale wa dziko Lino Mayi Joyce Banda, nduna zosiyana siyana mwa ena.

Panthawi ya zoyankhulayankhula, Mkazi wa malemu Saulos Chilima mayi Mary Chilima wati kwa zaka ziwiri zomwe zadutsa kuchokera pomwe a Chilima anatisiya moyo wawo wakhala wopweteka. Iwo ati amawakumbukira amuna awo ngati mwamuna wodziwa kukonda ndikusamala banja lake komanso wokonda kutumikira Mulungu.

A Clement Chilima, oyimilira akubanja, ati wachiwiri kwa mtsogoleri wakale wa dziko lino, a Saulos Klaus Chilima anali mphatso yapaderadera kwa akubanja kufikira nthawi ya imfa yawo.
Iwo apempha aMalawi kuti apitilire kupemphelera banja la aChilima, ndipo ati mitima ya akubanja imakhala pansi akaona chikondi chomwe anthu mdziko lino amawaonetsera.

Pa mwambo uno, panalinso kuwonetsa chiliza cha malemuwa chomwe chamangidwa mwa makono.

Dr. Saulos Chilima omwe anabadwa pa 12 February 1973, anamwalira pa 10 June 2024 pa ngozi ya ndege yomwe inachitika mu nkhalango ya chikangawa yomwe inatenganso miyoyo ya anthu ena asanu ndi atatu omwe anali nawo mu ndegeyo pomwe amkapita ku maliro a woyimira anthu pa milandu, Ralph Kasambara m'boma la Nkhatabay.

Pamene mapemphero okumbukira komanso kukondwelera moyo wa yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino a Saulos Chilima uli mkati ku Msipe, nako ku Ntcheu Stadium zokonzekera zili mkati kukonzekera mwambo wa masana wokumbukira a Chilima.
Uwu ndi mwambo womwe akonza ndi achipani cha UTM, chipani chomwe malemu Saulos Klaus Chilima anali mtsogoleri wake. Zina mwa zomwe zikhale zikuchitika ku mwambo waku stadium ndi monga kuyatsa makandulo komanso kukhale oyimba.

Zithuzi zili munsimu ndimwazina mmene mwambo unalili
# Corpus Christi Ntcheu Parish #

07/06/2026
31/05/2026

Oyimira Bungwe la YCW ku Ntcheu section kutambasulira zokhuza YCW ku Nsipe parish

31/05/2026

Mpingo wakatolika umalimbikitsa mabungwe osiyanasiyana kumayenderana monga momwe maria anayendera msuweni wake Elizabeth. Achinyamata a Bungwe la Young Christian Workers Ntcheu section anayendera akhristu a Parish ya Nsipe ndicholinga chokakhazikitsa bungweli kumeneko. Achinyamatawa anatenga nawo gawo pachipembedzo poperekera mphatso zapaguwa.

A chair a Nsipe parish anayamikira achinyamatawa chifukwa chobwera kuzakhazikitsa bungweli ndipo analimbikitsa achinyamatawa kuti adekhe pomema achinyamatawa ngati momwe amapangira msozi amene akuweza nsomba akapanda kupeza nsomba pafupi amasenderako kozama mpaka atagwirako nsomba ndiye nawonso akhale odekha pantchito yomwe ayiyambayi.

Bambo mfumu a Nsipe parish Fr. Manyenga anayamikira achinyamatawa chifukwa chopanga ganizo lokhazikitsa Bungwe lomwe amalisaukira pa parish imeneyi ndipo anapempha achinyamata a Nsipe parish kuti atsalire akumane ndi achinyamata anzawowo.

Oyimira Bungwe la YCW , Chisomo Kayambankadzanja anatambasulira bwino thumba la tambe lomwe anabwera nalo powunikira omwe ali oyenera kulowa bungweli kuti amayenera kukhala wakatolika, wa zaka zapakati pa 18 malire 40 zakubadwa komanso otakataka mu mpingo.

Pamapeto pa Misa achinyamata okwana 23 ndi omwe anatsalira kuti amve zambiri zabungweri. Munthawi yankumanowu kunali kugawana mau a m'malembo oyera, kuimba nyimbo ya YCW komanso pemphero la bungweli. Adindo analongosola za zochitika zomwe bungweli limapanga akakumana. Pamapeto pa zonse anasankha adindo ogwirizira chabe a Nsipe Parish omwe wapampando wake ndi Cornelius Chisoni.

Cornelius Chisoni anathokoza a Ntcheu section chifukwa chobwera kuzayambitsa bungweli ku Nsipe ndipo analonjeza kuti agwira ntchito kutsogolera azawo mwa ntotomoyo.

Atamaliza zonse adindo ogwirizira a Nsipe section anakumana ndi adindo a Ntcheu section kwa mphindi zisanu zokha.

31/05/2026

Mdipiti wa ovinira lero ku Corpus Christi Ntcheu parish

31/05/2026

Choir ya Ntcheu CDSS kuimba nyimbo ya Mai Maria

31/05/2026

Mwambo odalitsa zipangizo zolembera mayeso..

Lero mpingo wakatolika padziko lonse  umakondwerera chaka Cha Utatu woyerayera wa Mulungu. Corpus Christi Ntcheu parish ...
31/05/2026

Lero mpingo wakatolika padziko lonse umakondwerera chaka Cha Utatu woyerayera wa Mulungu. Corpus Christi Ntcheu parish inali ndi chikondwerero chimenechi ndipo anaimbira Misa ya lero ndi ophunzira a sukulu ya Ntcheu CDSS .

Mau oyamba anawerengedwa kuchokera mubuku la Eksodo, Mutu wa 34 kuyambira ndime ya 4b mpaka 6 nkuzayambiranso ndime ya 8 mpaka 9. Mau achiwiri anachokera mubuku lachiwiri la Akorinto, mutu wa 13 kuyambira ndime ya 11 mpaka ya 13. Mau amthenga wabwino olembedwa ndi Yohane ndi omwe anawerengedwa; Yohane mutu wa 3 kuyambira ndime ya 16 mpaka 18.

Pamapeto pa nsembe ya Misa Fr. Kaidi anadalitsa ophunzira onse amene akuyamba mayeso awo a JCE.

29/05/2026

Big shout out to my newest top fans! Tee Kay, Stella Tembo, Theodora Kabvala, James Mbamba, Katengah Patrick, Simeon English, Ellen Evance, Emmanuel Chisoni, Umali Masamba, Dinna Lingison, Beib Nah, Marko Junior Nkhata, Delinder Mataka, Yankho Chisonga, Davie Chinkondo, Luwis Wais, Mwai Wa Junior Raphael, Dyson Chumba, Thoko Mbunama, Emmanuel Million, Jack Martin Kaidi, Atanazio Nkhoma Sadie, Mphatso Frackson

Dzulo linali la Mulungu lokumbukira kutsika kwa Mzimu Oyera kwa atumiki ake mu mpingo wakatolika pa dziko lonse lapansi....
25/05/2026

Dzulo linali la Mulungu lokumbukira kutsika kwa Mzimu Oyera kwa atumiki ake mu mpingo wakatolika pa dziko lonse lapansi.

Nsembe ya Ukaristia yalero inatsogoleredwa ndi Bambo Chimchenga omwe ndi Bambo Mfumu a Corpus Christi Parish. Mau oyamba anachokera m'buku la ntchito za Atumwi 2:1-11; Mau achiwiri anachokera mu mkalata yolembera a Korinto, 1 Akorinto 12: 3-7, 12-13 ndipo uthenga wabwino unachokera m'buku la Yohane 20: 19-23.

Mu ulaliki wao Bambo Chimchenga anafotokoza kuti: " Mzimu Oyera uli ngati mphamvu yomwe imatha kumulowa munthu ndikumachita zomwe iyo ikufuna ndipo Mzimu oyera akakugwira zinthu zingapo zimasintha. Pamene pali Mzimu Oyera pamakhala mtendere, kulimba mtima, chilungamo ndi ntchito zabwino. Mwachitsanzo atumwi aja anali ndi mantha ndipo anazitsekera mnyumba poopa Ayuda aja koma Mzimu Oyera atawatsikira anayamba kulalikira mwamphwamvu za Yesu ouka kwa akufa mopanda mantha". Choncho analimbikitsa akhristu kuti timulole Mzimu Oyera azigwira ntchito mwa ife kuti pakutero atithandize kuchita chifuniro cha Mulungu. Ngati njira yonyadira tsikuli, mapemphero a akhristu alero ananedwa mu zilankhulo zosiyana siyana monga: Chingoni, Chiyao, Chitumbuka, Chizungu, chilomwe ndi chisena.

Ntcheu Parish Catholic Men Association choir ndiyomwe inayimbira ndikukometsa chipembedzo tsiku lalero.

Zithunzi zili mmusizi zikusonyeza mmene zinalili pa mwambowu.

Address

Corpus Christi Ntcheu Catholic Church
Ntcheu
POSTOFFICEBOX75

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Corpus ChristNtcheu parish ,Dedza Diocese posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share