Mangochi CCAP

Mangochi CCAP We are a Church called to share the Gospel of Our Lord Jesus Christ, which is salvation to all mankind. Matthews 28: 19-20

'CHIKONDI CHA KHRISTU CHIONEKERE NGAKHALE KU NTCHITO' Akhristu a mpingo wa Mangochi CCAP awalimbikitsa kuti adzionetsera...
02/08/2026

'CHIKONDI CHA KHRISTU CHIONEKERE NGAKHALE KU NTCHITO'

Akhristu a mpingo wa Mangochi CCAP awalimbikitsa kuti adzionetserana chikondi pakati pawo kuyambira ku mpingo mpaka kulikonse monga malo a ntchito, bizinesi ndi ena pofuna kulimbikitsa umodzi.

M'busa wa mpingowu a Chikondi Banda ndiomwe apereka chilimbikitsochi Lamulungu pamene mamembala a Mangochi CCAP omwenso ndiogwira ntchito ku nthambi ya Immigration anatsogolera chipembezo cha Chichewa.

"Zimakhala zomvetsa chisoni kuti anthu opemphera komanso kugwira ntchito limodzi asamagwirizane chifukwa choti izi sizimapereka chithunzithunzi chabwino cha Khristu Yesu," atero a busa a Banda.

Mu uthenga wake omwe unachokera m'mabuku a Genesis 11 verse 6 komanso 1 Akorinto 13 verse 4 mpaka 7, a Blessings Kam'nyamata a mlaga wa Mtalimanja A, agwirizana ndi abusa a Banda ponena kuti 'Ulemerero Wa Mulungu Ndi Umodzi Ndi Chikondi'.

Mamembala a mpingo wa Mangochi CCAP omwe ndi ogwira ntchito ku immigration alipo oposa 40 pomwe mamembala okwana 20 ndiomwe anatenga nawo mbali potsogolera chipembedzochi.

Malingana ndi abusa a Banda, mamembala onse a mpingowu kuchokera m'madera awo osiyanasiyana ogwirako ntchito ali ndi mwayi otsogolera chipembezo ngati atafuna kutero.

MangochiCCAPMediaTeam

02/08/2026
Mangochi CCAP: The giant that hosts giants.
01/08/2026

Mangochi CCAP: The giant that hosts giants.

MUBAS ILI MU MPANDA WA MANGOCHI CCAP TSOPANO M'busa wa Mangochi CCAP Chikondi Banda wayamikira akhristu komanso abusa on...
25/07/2026

MUBAS ILI MU MPANDA WA MANGOCHI CCAP TSOPANO

M'busa wa Mangochi CCAP Chikondi Banda wayamikira akhristu komanso abusa onse omwe atumikira pa mpingowu kaamba ka masomphenya omwe akuti tsopano ayamba kukwaniritsidwa.

Poyankhula pambuyo posayina m'gwirizano ndi sukulu ya ukachenjede ya Malawi University of Business and Applied Sciences (MUBAS), a busa a Banda ati kubwera kwa sukuluyi kwapherezera zolinga za mpingowu posafuna kungodalira pa zopereka za akhristu zokha mu ntchito zake.

"Masomphenya okhala ndi Office Complex anali oti mpingo udzipeza ndalama popangitsa rent zipinda za nyumbayi zomwe zilipo 32 ndipo izi zayamba kutheka," anatero a Banda uku akumwetulira.

Iwo alimbikitsa onse omwe akufuna malo ngati kutsekula ofesi ndi zina kuti malo komanso chitetezo chokwanira zilipo ku Mangochi CCAP ponena kuti mwa zipinda 32 mu Office Complex-yo, zipinda 7 zokha ndizomwe ena atenga kale.

Malingana ndi mkulu wa nthambi ya Institute of Continued Education (ICE) ku MUBAS a Andrew Chimpololo, centre yawo ya chigawo chaku m'mawa ikuyamba maphunziro ake Lolemba pa 27 July 2026 ndi ophunzira oposa 30 pamene kulembetsa kuli m'kati.

A Chimpololo ati palibenso chifukwa choti anthu okhala ku Mangochi komanso m'chigawo chonse chaku m'mawa adzipita ku Lilongwe kapena ku Blantyre kukafuna maphunziro a pa mwamba.

Iwo ati m'gwirizano omwe asayinirana lero ndi Mangochi CCAP ndiokhazikika omwe udziunikidwa chaka ndi chaka ndipo pakadali pano akuyamba ndi ma course awiri a Diploma in Business Management komanso Diploma in Community Development.

MangochiCCAPMediaTeam

'KASAMALENI MAYITANIDWE'Mpingo wa Mangochi CCAP wafunira zabwino  abusa atatu omwe amaliza maphunziro komanso nthawi yow...
19/07/2026

'KASAMALENI MAYITANIDWE'

Mpingo wa Mangochi CCAP wafunira zabwino abusa atatu omwe amaliza maphunziro komanso nthawi yowayang'anira (probation) pomwe akuyembekeza kudzodzedwa pa 23 August 2026 pa mwambo omwe ukachitikire ku Limbe CCAP.

Poyankhula atawayitani kuti adzawapatse mafuno abwino, moderator wa mpingowu m'busa Chikondi Banda walimbikitsa atumiki atsopanowa kuti asamalire mayitanidwe awo poyika Mulungu patsogolo ndikukhala achikondi ndi akhristu komanso abusa anzawo.

Pa tsikuli abusa atsopanowa anathandizira ntchito monga ulaliki, ubatizo wa ana ndi akulu komanso kudyetsa m'gonero wa Ambuye.

Atatuwo ndi a Geoffrey Kalema Banda omwe probation yawo apangira ku mpingo wa Chisawani CCAP ku Thuchila Presbytery, a Emmanuel Majawa omwe ali ku mpingo wa Pasani CCAP ku Thuchila Presbytery komanso a Kelvin Uladi omwe ali ku Malindi CCAP mu Mangochi Presbytery.

Mangochi CCAP yati ikhala ikuyitana abusa osiyanasiyana omwe angomaliza kumene maphunziro a ubusa kuti adzawalimbikitse ndikuwafunira zabwino pa utumiki wawo.

MangochiCCAPMediaTeam

When serving takes its toll!
19/07/2026

When serving takes its toll!

MANGOCHI CCAP YAWONJEZERA ABAMBO 48 MU UTUMIKI.M'busa wa Mangochi CCAP Chikondi Banda wati ndiwokondwa kuona kuti utumik...
12/07/2026

MANGOCHI CCAP YAWONJEZERA ABAMBO 48 MU UTUMIKI.

M'busa wa Mangochi CCAP Chikondi Banda wati ndiwokondwa kuona kuti utumiki wa abambo ukukula mu mpingowu pomwe lero awonjezera chiwerengero cha abambo ena okwana 48.

Poyankhula pa mwambo wakumaliza maphunziro a utumiki wa abambo 35 aku Mangochi CCAP komanso 13 aku Nkungulu Prayer House, abusa a Banda ati chamukomera Ambuye kuti lero likhale tsiku lakukhazikitsa utumiki wa abambo okhazikika ku Nkungulu CCAP.

"Kuyamba n'kuyamba kungofikira pa chiwerengero cha abambo 13 sichinthu chapafupi. Mukudziwa abambo amabwerera m'mbuyo pa za uzimu koma chamukomera Mulungu mwini kuti lero utumiki wa abambo uyambe motere ku Nkungulu CCAP," atero abusa a Banda.

Wapampando wa utumiki wa abambo ku Mangochi Presbytery ya mpingo wa CCAP a Kenneth Magasa agwirizana m'mawu awo ndi abusa a Banda ponena kuti zikupereka chilimbikitso momwe abambo akulowera utumikiwu ndipo alengeza kuti Presbytery yi ichititsa msonkhano wa utumiki wa abambo pa 4 ndi pa 5 September 2026 ku Namiyasi pofuna kuzamitsa utumiki wa abambo.

Ena mwa abambo omwe avala chigwirizano lero ndi alembi oyamba a mpingo wa Mangochi CCAP a Feston Elias Chonde komanso a Joseph Makwinja omwe angodalitsa ukwati wawo m'miyezi yochepa yapitayi, kutsimikizira kuti utumiki wa abambo ndi wa amuna onse osati achikulire okha.

MangochiCCAPMediaTeam

12/07/2026

CHICHEWA SERVICE
MEN'S MINISTRATION DAY

12/07/2026

ENGLISH SERVICE
PREACHING: MRS ZINGA

Tsiku lija ndi mawa!Tiyeni tikayipatse moto!
11/07/2026

Tsiku lija ndi mawa!

Tiyeni tikayipatse moto!

Address

P. O BOX 39 Mangochi
Mangochi

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mangochi CCAP posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share