CHAWA CCAP Nkhoma SYNOD

CHAWA CCAP Nkhoma SYNOD Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from CHAWA CCAP Nkhoma SYNOD, Religious organisation, BOX 2, Lobi.

Ana a Sunday School ozungulira Station zone mu mpingo wa Chawa CCAP pansi pa Presbytery ya Mphuzi mu Synod ya Nkhoma aso...
12/04/2026

Ana a Sunday School ozungulira Station zone mu mpingo wa Chawa CCAP pansi pa Presbytery ya Mphuzi mu Synod ya Nkhoma asonkhana pamodzi pa Station pomwe kuli mwambo otsekera Sunday school. Pa mwambowu anawa amanena mawu a pamtima omwe akhala akuphunzira term yoseyi osaonera palipose.

Mwambo ngati omwewu ukuchitikaso ku madera odyera mgonero mu Chawa CCAP. Madera ndi Mulira zone, Kanjedza zone, Mtayandodo zone, Chimvule zone komaso Gulugulu zone.

Anawa amaloweza mawu apamtima, kutsogolera nyimbo, kunena Chikhulupiliro cha chikhristu, kupemphera, kunena maina a mabuku a mbaibulo ngakhaleso kulalikira kumene. Limakhala tsiku la mtengo wapatali kwa ana kuima kutsogolo kwa mpingo ndikumaonetsa maluso awo.

LUKA 23:43-49, LUKA 24:1-12ZOCHITA PA MASAUTSO, IMFA NDI KUUKA KWA AMBUYE WATHU YESU KHRISTU ZITANTHAUZA CHIYANI PA IFE?...
05/04/2026

LUKA 23:43-49, LUKA 24:1-12

ZOCHITA PA MASAUTSO, IMFA NDI KUUKA KWA AMBUYE WATHU YESU KHRISTU ZITANTHAUZA CHIYANI PA IFE?

1. Kuti tilandire Mtendere. Yesu adazuzika kuti ife tikalandire mtendere.

2. Choonadi. Yesu akutiphunzitsa kuti pakati pathu pazikhala choonadi. Petro adakana kuti sadzamukana Yesu koma zidachitika. Yudasi adali nawo mugulu lofunsa kuti kodi ndine pamene Yesu adati wina wa ife adzandipereka chosecho omperekayo ndiyeyo.

3. Kupereka Chenjezo. Yesu akupereka chenjezo akupita kokapachikidwa kuti mudzililire nokha.

4. Kulandira Chipulumutso/ Chikondi. Yesu akufa m'malo mwathu kuti ife tikapulumuke kusonyeza chikondi.

5. Kupambana/Kugonjetsa. Kuuka kwakufa kwa Yesu kudasonyeza kupambana kwa Yesu Khristu kugonjetsa imfa.

YOHANE 3 : 1616. Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wake wobadwa yekha, kuti yense wakukh...
29/03/2026

YOHANE 3 : 16

16. Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wake wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira Iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha.

MPHAMVU YA MTANDA KWA IWO AKUKHULUPIKIRAWO

1. Chikondi cha Mulungu

Mulungu akuwonetsa chikondi chake mwa Yesu Khristu podzipereka kudzafa m'malo mwathu. Yesu sadabwere kudzachotsa chilango ayi, chilango chilipo ndithu chomwe chidzaperekedwa kwa osakhulupilirawo

2. Kupilira pakumva zowawa

Yesu akutiphunzitsa kupilira pamene tikumva zowawa. Yesu sadafune kubwezera pamene amazunzika koma adapempha chikhululukira kwa atete pa anthu omwe amamuzunzawo.

3. Iwo amene amakhulupilira mtanda wa Khristu amalandira chipambano

Yesu adapereka chiyembekezo cha moyo wasatha kwa okhulupilira. Yesu adagonjetsa imfa nauka kwakufa kutipatsa chiyembekezo kuti tikakhulupilira tidzakhala ndi moyo wosatha.
Tilape machimo athu ndikukhulupilira mtanda wa Yesu Khristu (Mulungu). Timtumikire Mulungu ndi kuchita chifuniro chake nthawi zonse. Tikhale anthu opilira pakumva zowawa.

22/03/2026

LUKA 22:47-53

1. Kuchoka pamaso pa Yehova ndi tsoka.

Yudasi adali m'modzi wa akuphunzira a Yesu koma adachoka pamaso pa Mulungu ndikumupereka Yesu mapeto ake Yudasi adadzipha yekha.

2. Chikondi chopanda malire cha Ambuye wathu Yesu Christu.

Ngakhale Yesu amadziwa kuti anthu abwerawa akudzamugwira kuti akazunzike ndi kuphedwa, adaletsa akuphunzira ake kuchita nawo nkhondo komaso adachiza khutu la lomwe lidadulidwa ndi akuphunzira ake la m'modzi wa iwo odzamugwirawo.

3. Kukhala munthu odziwa nyengo.

Yesu adadziwa kuti nyengo yomwe akudutsamo inali ndithu nyengo imene amayenera kudutsamo. Yesu akadatha kudzipulumutsa panthawi imene amadzamugwira koma adadziwa nyengo ndichifukwa chake adanena kuti nyengo ino ndiyanu.
Tiyesetse kukhalabe chiimire pamaso pa Mulungu, tisachoke pamaso pa Mulungu.
Tikhale anthu a Chikondi chopanda malire chonga cha Yesu.
Tizindikire kuti tili mu nyengo ya masiku otsiriza (masiku a chimaliziro cha nthawi ya pansi pano).

A khristu pa mpingo wa Mwalawang'ombe mu presbytery ya mphunzi pansi pa Nkhoma Synod akupitiliza kukhuza imfa ya abusa a...
18/03/2026

A khristu pa mpingo wa Mwalawang'ombe mu presbytery ya mphunzi pansi pa Nkhoma Synod akupitiliza kukhuza imfa ya abusa a CD Njete omwe a mwalira dzulo pa Chipatala cha nkhoma m'boma la Lilongwe.

Abusa anjete a mwalira atadwala Kwa Ka nthawi kochepa kamba Ka Vuto la BP yomwe idapangitsa kuti agwe mwadzidzi kunyumba kwawo.

Thupi la malemu abusa a Njete lilowa m'manda la chitatu pa 18 march 2026 Ku Mudzi kwawo kudibi m'boma la Mchinji.

CCAP
'ombe CCAP

30/11/2025

2 Mafumu 5:1-19 / 1 Petro 5:5-19

MFUNDO ZIKULUZIKULU

1. Kudzikuza
a. Kalata yomwe inalembedwa inaliyodzikuza
b. Momwe adafikira Namani kwa Elisa
2. Kusazindikira
a. Mfumu idang'amba zovala posadziwa kuti ntchito inali ya Elisa
3. Kudzichepetsa
a. Namani adadzichepetsa kukasamba mu yolodani
4. Kuvomereza
a. Namani adavomereza kuti kulibeso Mulungu wina oposa wa Israel

ZOTSATIRA ZA KUDZIKUZA NDI KUDZICHEPETSA PAMASO PA MULUNGU

A. KUDZIKUZA

1. Mulungu amakukaniza kupita patsogolo ndi masomphenya ako {Mulungu akaniza odzikuza (1 Petro 5:5)}
2. Mulungu amakutsitsa
3. Anthu satha kutumikirana wina ndi nzake
4. Mulungu amakukaniza kukula

B. KUDZICHEPETSA

1. Mulungu amatipatsa chisomo
2. Mulungu atisamalira
3. Mulungu amatikweza
4. Anthu amatumikirana bwino wina ndi nzake

Kodi inu ndinu odzikuza kapena odzichepetsa?

02/11/2025

Sunday service 2nd October, 2025

Luka 23:32-49, Aefeso 4:32

KUKHULULUKA SI NTCHITO YA MUNTHU WAMBA.

Khululuka si ntchito ya munthu wamba chifukwa;

1. Okhululukirayo amaoneka ozerezeka/opepera (kape).
2. Okhululukirayo amafunika akhale wa chisoni chenicheni.
3. Okhululukirayo amafunika akhale ndi chikondi chenicheni.
4. Okhululukirayo amafunika akhale ndi chifundo chenicheni.

Kodi inu ndi ine timakhululuka zenizeni???

TINGATANI KUTI TIFIKE PA MULINGO OKHULULUKIRA ENA?

sikupita ku church
sikupereka chakhumi
sikukhala pa udindo ku church

NANGA TITANI?

Tilandire Yesu akhale Mbuye ndi mpulumutsi wa moyo wathu

Address

BOX 2
Lobi

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when CHAWA CCAP Nkhoma SYNOD posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share