12/04/2026
Ana a Sunday School ozungulira Station zone mu mpingo wa Chawa CCAP pansi pa Presbytery ya Mphuzi mu Synod ya Nkhoma asonkhana pamodzi pa Station pomwe kuli mwambo otsekera Sunday school. Pa mwambowu anawa amanena mawu a pamtima omwe akhala akuphunzira term yoseyi osaonera palipose.
Mwambo ngati omwewu ukuchitikaso ku madera odyera mgonero mu Chawa CCAP. Madera ndi Mulira zone, Kanjedza zone, Mtayandodo zone, Chimvule zone komaso Gulugulu zone.
Anawa amaloweza mawu apamtima, kutsogolera nyimbo, kunena Chikhulupiliro cha chikhristu, kupemphera, kunena maina a mabuku a mbaibulo ngakhaleso kulalikira kumene. Limakhala tsiku la mtengo wapatali kwa ana kuima kutsogolo kwa mpingo ndikumaonetsa maluso awo.