St Francis Parish Kanengo,Kanengo Deanery,Lilongwe Arcdiocease

St Francis Parish Kanengo,Kanengo Deanery,Lilongwe Arcdiocease St francis parish is located in Lilongwe, Malawi Area 25c.Parish was established in 1976 by Missionaries Of Africa

04/02/2026




*4 FEBRUARY, 2026*

_*LACHITATU LA MULUNGU WA 4 PACHAKA*_

*MAU OYAMBA, MAWU A MBUKU LACHIWIRI LA SAMUELI 24:2,9-17*

Mfumu Davide adauza Yowabu ndi atsogoleri ankhondo amene adali naye pamodzi kuti: “Pitani pakati pa mafuko onse a Israeli kuyambira ku Dani mpaka ku Beereseba, mukawerenge anthu kuti ndidziwe chiwerengero chawo. Tsono Yowabu adapereka chiwerengero cha anthu onse kwa mfumu. Ku dziko la Israeli kudali anthu 800,000 otha kumenya nkhondo, ndipo ku Yuda kudali anthu 500,000 pamodzi. Pambuyo pake Davide adadzitsutsa mu mtima mwake atatha kaundulayo, ndipo adapemphera kwa Chauta kuti: “Ndachimwa kwambiri pochita zimenezi. Koma tsopano, Inu Chauta, ndikukupemphani kuti mundikhululukire tchimo langa, ine mtumiki wanu, popeza kuti ndachita zopusa kwambiri. Tsono Davide atadzuka mmawa, Chauta adamulankhula ndi Gadi, mneneri wa Davide, namuuza kuti: “Pita ukamuuze Davide kuti: ‘Ine Chauta ndikunena kuti: ndikuika pamaso pako zinthu zitatu zoti ndikuchitire. Tsono usankhepo chimodzi ndipo ndidzakuchitira.”

Choncho Gadi adabwera kwa Davide namuuza kuti: “Musankhe kuti kodi pabwere zaka zitatu za njala m’dziko mwanu, kapena inu mukhale mukuthawa adani anu pa miyezi itatu, kapena pakhale mliri wa masiku atatu mu dziko mwanu? Ganizani bwino, ndipo mutsimikize chiri chonse choti muyankhe kuti ine ndikauze amene adandituma ineyo.” Apo Davide adauza Gadiyo kuti: “Iyayi, ine pamenepa ndavutika kwambiri mu mtima. Makamaka tigwe m’manja mwa Chauta, popeza kuti chifundo chake nchachikulu, koma chonde, tisagwe m’manja mwa anthu, ayi.” Choncho Chauta adagwetsa mliri pakati pa Aisraele kuyambira mmawa mpaka pa nthawi imene adafuna Mwini wake. Mwakuti kuchokera ku Dani mpaka ku Beereseba, adafa anthu okwanira 70,000 pamodzi. Ndipo pamene mnjelo adatambalitsa dzanja lake kuloza mzinda wa Yerusalemu kuti auwononge, Chauta adasintha maganizo a chilangowo nauza mnjelo, amene ankaononga anthu aja, kuti:

“Iyayi, basi tsopano. Kwakwanira. Bweza dzanja lakolo.” Nthawi imeneyo nkuti mnjelo wa Chautayo atayima pamalo wopunthira tirigu wa Arauna, Myebusi. Davide adaona mnjelo uja, ndipo adalankhula ndi Chauta adati: “Ndachimwa ndine, ndipo ndachita choipa. Koma nkhosa izi, kodi zachita chiyani? Amangonditsatira chabe. Tsono dzanja lanu likhale pa ine ndi banja la bambo wanga?”

*Mau a Ambuye*

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 32: 1-2, 5, 6, 7
*Inu Chauta, mundikhululukire kulakwa kwanga* (5c).

Ngodala amene zolakwa zake zakhululukidwa,
Amene machimo ake afafanizidwa.
Ngodala amene Chauta samuŵerengera mlandu wake,
Amene mu mtima mwake mulibe chinyengo.
*Inu Chauta, mundikhululukire kulakwa kwanga*.

Koma ine ndidavomera tchimo langa kwa Inu,
Sindidabise kuipa kwanga.
Ndidati: “Ndidzaulula machimo anga kwa Chauta.”
Pomwepo Inu mudakhululukiradi mlandu wa machimo anga.
*Inu Chauta, mundikhululukire kulakwa kwanga*.

Nchifukwa chake munthu aliyense wosamala za Inu
Apemphere kwa Inu.
Akadzafika mavuto, akadzafika madzi a chigumula,
Zonsezo sizidzamufika, ndipo Inu ndinu kobisalira kwanga.
Inu mumanditchinjiriza nthaŵi yamavuto.
Potero ndimaimba nyimbo zotamanda chipulumutso chanu.
*Inu Chauta, mundikhululukire kulakwa kwanga*.

*Aleluya*: (Yohane 10: 27) Nkhosa zanga zimamva mawu anga, akutero Ambuye: ndimazidziwa ndipo izo zimanditsatira Ine, *Aleluya*.

*MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA MARKO WOYERA 6:1-6*

Yesu adafika kumudzi kwawo. Ophunzira ake adatsagana naye. Litafika tsiku la Sabata, Iye adayamba kuphunzitsa m’nyumba ya mapemphero. Anthu ambiri, amene adalikumvetsera, adadabwa kwambiri, ndipo ankafunsana kuti: “Kodi Iyeyu zimenezi adazitenga kuti? Nzeru zimene adalandirazi nzotani? Akutha bwanji kuchita zinthu zamphamvu chotere? Kodi Iyeyu si mmisiri wa matabwa uja, mwana wa Mariya? Kodi si mbale wa Yakobe ndi Yose ndi Yuda ndi Simoni? Kodi alongo ake si alinafe konkuno? Motero adampeputsa. Koma Yesu adawauza kuti: “Mneneri amalemekezeka kwina kuli konse kupatula kumudzi kwawo, kwa abale ake kapenanso ku banja kwake.” Choncho kumeneko sadathe konse kuchita zinthu zamphamvu. Adangosanjika manja pa anthu pang’ono chabe odwala ndi kuwachiritsa, ndipo adadabwa kuti anthu a kumeneko sadamkhulupirire. Pamenepo Yesu adapita kumidzi yozungulira namangophunzitsa anthu.

*Mthenga wa Ambuye*

03/02/2026

MUNAMVAPO ZA MKATOLIKA AMENE ANASUNGA UKARISTIA 1915?

Chaka Cha 1915 chimadziwika ndi John Chilembwe( Chilembwe uprising).

A EUGENIO JOSEPH NAVING'OMBA ndi mkatolika wa ku Nguludi Mission, amene mchaka Cha 1915 anathawitsa Ukaristia pamene otsatira a John Chilembwe anakachita chipolowe pa tchalichi.

Pamene John Chilembwe ndi otsatira ake anayamba kuthira nkhondo azungu, pa 24/25 January anakaononga Mission ya Nguludi mpaka ansembe ndi asistere anathawira ku Mikolongwe. Iwo amati azungu a Katolika amagwirizana ndi atsamunda panthawiyo.

Pachipolowecho, alonda ena anaphedwa ndipo wansembe wachizungu Swelsen (ambiri amangoti Swelezeni) anabaidwa ndi kuvulazidwa.

Poopa kuti anthu achita chipongwe mu tchalichi ndi Ukaristia, a Augenio Joseph Naving'omba anathawitsa Chikho Cha Ukaristia ndikukasunga. Pambuyo pake anazawapatsa ansembe.

Pamene tikukondwelera kuti Mpingo ku Malawi ukukula, anthu ngati a Naving'omba tidziwakumbukira.

Naving'omba anali mkatolika weniweni kufikira pamene anamwalira mchaka Cha 1964. Manda ake ali pa mission ya Nguludi Mbiri yake imakambidwa mpaka lero.

03/02/2026

Nyimbo ya salimo by St Anne choir :Salimo 146:7,8-9a,9bc-10

03/02/2026

*3 FEBRUARY, 2026*

_*LACHIWIRI LA MULUNGU WA 4 PACHAKA*_

*MAU OYAMBA, MAWU A MBUKU LACHIWIRI LA SAMUELI 18:9-10,14b,24-25a ,30-19:3*

Mwadzidzidzi Abisalomu adakomana ndi ankhondo a Davide. Abisalomuyo adali atakwera pa bulu wake. Ndipo buluyo adalowa kunsi kwa mthambi za mtengo wa thundu. Pamenepo Abisalomu adatsalira ali lendee mutu wake utapanika pa mthambiyo, pamene bulu adamkwerayo atapitilira. Munthu wina ataona zimenezo, adauza Yowabu kuti: “Ndamuona Abisalomu ali lendee pa mtengo wa thundu.” Apo Yowabu adati: “Ukunditayitsa nthawi.” Ndipo adatenga mikondo itatu m’manja mwake nakabaya Abisalomu m’chifuwa asadafe, akali lendee mu mtengo wa thunduwo. Nthawi imeneyo nkuti Davide atakhala pakati pa zipata ziwiri, chakubwalo ndi chamkati. Mlonda adakwera khoma nakaimirira pa denga la chipata, ndipo adati, atayang’ana, adaona munthu wina akuthamanga, ali yekhayekha. Ndipo mlondayo adafuula nauza mfumu. Mfumuyo idati: “Ngati ali yekhayekha ndiye kuti ali ndi nkhani yabwino. Tsono munthu uja adafika ndithu nayandikira pafupi. Pompo mfumu adati: “Patuka ukaime apo.” Iye adapatuka nakaima poteropo.

Mlendo wa Chikusi uja adafika pafupi nati: “Mbuye wanga amve mthenga wabwino. Lero Chauta waalipsira onse okuchitirani chipongwe.” Mfumu idati kwa Mkusi uja: “Kodi mwana wanga, Abisalomu, zikumuyendera bwanji? Mkusiyo adayankha kuti: “Adani anu, mbuyanga mfumu, pamodzi ndi anthu onse amene amakuukirani, zawaonekera zomwe zamuonekera mwana wanuyo.” Pamenepo mfumu idagwidwa ndi chisoni chachikulu nikwera ku chipinda cha m’mwamba cha chipata nikalira. Tsono polira inkati: “Mwana wanga, Abisalomu! Mwana wanga, Abisalomu! Kalanga ine. Achikhala ndikadafa ine m’malo mwako. Iwe Abisalomu, mwana wanga! Iwe Abisalomu, mwana wanga!” Tsiku lomwelo anthu adalowa mu mzinda kachetechete monga momwe anthu amalowera mu mzinda mwa manyazi akamathawa ku nkhondo.

*Mau a Ambuye*

NYIMBO YA SALIMO: SALIMO 86: 1-2, 3-4, 5-6
*Tcherani khutu, Inu Chauta, ndipo mutiyankhe* (1a).

Tcherani khutu, Inu Chauta, ndipo mundiyankhe,
Pakuti ndine wosauka ndi wosoŵa.
Sungani moyo wanga, pakuti ndine womvera Inu.
Pulumutseni ine, mtumiki wanu, amene ndimadalira Inu.
Inu ndinu Mulungu wanga.
*Tcherani khutu, Inu Chauta, ndipo mutiyankhe*.

Mundikomere mtima, Inu Ambuye,
Popeza kuti ndimalirira Inu tsiku lonse.
Sangalatsani mtima wa ine, mtumiki wanu,
Pakuti ndikupereka mtima wanga kwa Inu Ambuye.
*Tcherani khutu, Inu Chauta, ndipo mutiyankhe*.

Inu Ambuye, ndinu abwino,
Ndipo mumakhululukira anthu anu.
Chikondi chanu chosasinthika ndi chachikulu
Kwa onse amene amakupembedzani.
Tcherani khutu, Inu Chauta, kuti mumve pemphero langa.
Mverani kulira kwanga kopemba.
*Tcherani khutu, Inu Chauta, ndipo mutiyankhe*.

*Aleluya*: (Mateyo 8: 17) Yesu Khristu adatenga zofooka zathu, ndipo adasenza nthenda zathu zonse, *Aleluya*.

*MTHENGA WABWINO MONGA ADALEMBERA MARKO WOYERA 5:21-43*

Yesu adaoloka nyanja. Pamene adafikanso patsidya, chikhamu chachikulu cha anthu chidasonkhana pa mphepete pa nyanja pamene padali Iyepo. Kudafika munthu wina dzina lake Yairo, amene adali mkulu wa nyumba ya mapemphero kumeneko. Pamene adaona Yesu, adagwada ku mapazi ake namudandaulira kwambiri nati: “Mwana wanga wamkazi ali pafupi kufa. Tiyeni mukamusanjike manja kuti achire ndi kukhala ndi moyo.” Yesu adanyamuka napita naye. Anthu ambiri adali kumutsatira ndi kumpanikiza. Padali mkazi wina amene adali kuvutika zaka khumi ndi ziwiri ndi nthenda ya mwazi. Adavutika kwambiri ndi asing’anga ochuluka amene adayesa kumuchiritsa. Adatha chuma chake chonse, komabe osapeza bwino. M’malo mwake matendawo adanka nakulirakulira.

Mkaziyo adali atamva za Yesu. Tsono adalowa mu khamu la anthu lija napapatiza mpaka kukafika kumbuyo kwa Yesu nakhuza chovala chake. Adali kuganiza kuti: “Ndikangokhuza ngakhale chovala chake, ndichira.” Ndipodi nthawi yomweyo kutayika kwa mwazi kwake kuja kudaleka. Ndipo iye mwini adamva mthupi mwake kuti matenda ake aja atha. Nthawi yomweyo Yesu adazindikira kuti mphamvu zina zatuluka mwa Iye. Tsono adatembenukira anthu aja nawafunsa kuti: “Kodi ndani wandikhuza zovala?” Ophunzira ake adati: “Inu nomwe mukuona kuti anthu akukupanikizani. Nanga bwanji mukufunsa kuti: ‘Ndani wandikhuza.’” Koma Yesu adayang’anayang’ana kuti amuone yemwe wamuchitira zimenezi. Mayi uja adachita mantha, nayamba kunjenjemera chifukwa adadzindikira zimene zidamuchitikirazo. Adabwera pafupi nadzigwetsa pamaso pa Yesu, namfotokozera zonse zomwe zidamuchitikira. Yesu adamuuza kuti: “Mayi iwe, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita ndi mtendere. Kuvutika kwako kwatheratu.”

Yesu alikulankhulabe, kudafika anthu ochokera ku nyumba ya mkulu wa mapemphero uja. Adamuuza mkuluyo kuti: “Mwana wanu uja watsirizika. Musawavutenso aphunzitsiwa.” Koma Yesu sadasamale zomwe anthuwo adali kunena. Adauza mkulu uja kuti: “Musaope ayi. Inu ingokhulupirirani.” Ndipo sadalole kuti winanso atsagane naye, koma Petro ndi Yakobe ndi Yohane, mbale wa Yakobeyo. Atafika ku nyumba ya mkulu uja, Yesu adaona chipiringu cha anthu chikuchita phokoso, kubuma ndi kulira kwambiri. Iye adalowa nawafunsa kuti: “Chifukwa chiyani mukuchita phokosoli ndi kubuma? Mwanayu sadafe ayi. Wangogona tulo.” Koma anthuwo adamuseka monyodola. Iye adawatulutsa panja onse, nangotenga bambo ndi mayi a mwanayo, kudzanso amene adali naye aja. Adalowa m’chipinda kumene kudali mwanayo. Adagwira dzanja la mwana uja namulamula kuti: “Talita kumi” (ndiye kuti: ‘msungwana iwe, ndikuti: dzuka’). Pomwepo msungwana uja adadzukadi nayamba kuyenda pakuti adali wa zaka khumi ndi ziwiri. Pamenepo anthu aja adazizwa kopambana, koma Yesu adawalamula kolimba kuti zimenezo zisamveke konse kwa ena. Ndipo adawauza kuti ampatse chakudya msungwanayo.

*Mthenga wa Ambuye*

18/01/2026

Address

P. O BOX 40009, Kanengo
Lilongwe

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when St Francis Parish Kanengo,Kanengo Deanery,Lilongwe Arcdiocease posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share