25/08/2026
MUSAMADERE KHAWA NDI KUVUTIKA KWANU CHIFUKWA AMAKWEZA MUNTHU NDI MULUNGU.
Genesis 50 : 20 - 21
Yohane 3 : 30
1. CHINTHU CHIMENE CHIKUWONEKA NGATI TSOKA LERO,MULUNGU ADZACHISANDUTSA KUKHALA NJIRA YA MADALITSO NDI CHOLINGA CHAKE.
Mukawulondola bwino moyo wa Yosefe,zinalipo nyengo zimene iye anadutsamo kuti apambane. Abale ake a Yosefe anayesetsa kuti akhoza kupha loto la moyo wake pomugulutsa ku Egypt koma sizinaphule kathu,mapeto ake Yosefe anakakwezedwa kukhala wolamulira.
Zilipotu nyengo za moyo m'moyo uno zimene zimadza kudzalimbana ndi chipambano chanu koma maso anu asamakhale pa nyengozo chifukwa mukapilira ndi kukhala okhulupilika pamaso pa Mulungu Iye adzakukwezani.
2. MUZIDZICHEPETSA KWAMBIRI CHIFUKWA GWERO LA KUKWEZEDWA KWANU LAGONA MU NKUDZICHEPETSA KWANU.
Yohane 3 : 30
Mu m'moyo wa kudzichepetsa muli zambiri zimene Mulungu amayikizamo kupatula kuti ukadzichepetsa Mulungu amakukweza. Ukakhala m'moyo wodzichepetsa umakhala dalitso kwa anthu ena ndipo Chisomo cha Mulungu chimakulondora kulikonse. Chisomo cha Mulungu tikunenachi chimakuyankhulira m'ma bwalo aanthu amene amadzitcha a nzeru nadzitamandira ndipo Chisomo ichi chimayankhula kuposa malingaliro aanthu.
3. KUMADZIWA KUTI NYENGO ZA MOYO SIZIBWERA KUTI ZIKUWONONGENI KOMA KUTI ZIKUWUMBENI KUKHALA MUNTHU WENIWENI.
1 Samuele 1 : 10 - 11
Akuluakulu moyo uno kulibe chidule cha zinthu,kuti ufike poti wakwanilitsa khumbo la moyo umayenera udutsemo.
There's no shortcut in life,Ayi kulibe!!! Achimwene tamvani, mukhoza kukwanilitsa zokhumba zanu mu njira ya chidule koma zomwe mufuna kukwanilitsazo sizidzakhazikika pa moyo wanu, njira iliyonse ya chidule imapweteketsa ndipo dalitso kale limakhala la kathawi kochepa.
4. MUZIKHALA NAKO KULIMBIKA MTIMA KUTI PALIBE MUNTHU AMENE AKHOZA KULEPHELETSA TSOGOLO LA MOYO WANU.
Yobu 42 : 2
Yesaya 14 : 27
Nzeru ya dziko la pansi Mulungu anayipusitsa ndipo palibe munthu amene amadziwa za tsogoro la munthu koma Mulungu yekha kotero kuti musamachite matha ndi onse amayankhula za tsogolo lanu chifukwa tsogoro la moyo wanu amalidziwa ndi Mulungu ngakhale inu mwini simulidziwa.
Musamakhale ndi matha ndi onse amene amati akhoza kuyimitsa chipambano cha moyo wanu.
Chifukwa cha maloto amene ankasonyeza tsogoro la Yosefe,abale ake anayesetsa kubweretsa njira zofuna kulimbana naye ndipo atamuguritsa ankayesa kuti athana naye osadziwa kuti Mulungu ankalondora mwachidwi maloto a Yosefe kufikira kuti Yosefe anakwezedwa kukhala wolamulira.
Wolimbana nanu adzakhalapo inde!! Ofuna kukutsekelezani musapambane koma musamakhale nawo khawa chifukwa onse olimbana ndi tsogoro lanu amathandizira inu kuti mupambane.