16/05/2026
Aroma 12:2
"Musafanizidwenso ndi makhalidwe a dziko lino koma musandulike pokonzanso maganizo anu. Ndipo mudzadziwa ndi kuzindikira chifuniro chabwino cha Mulungu chomwe ndi chokondweretsa ndi changwiro."
Pamene Yesu anasandulika maonekedwe, maonekedwe ake ndi zonse za iye zinasintha. Kusandulika sikuli kwa thupi lokha, komanso ndi kwa mzimu. Titha kukhala ndi mwayi wolowa m'Ufumu wa Mulungu tikamasandulika. Timachoka pokhala akapolo n’kumatchedwa ana komanso mabwenzi a Mulungu. Osatinso atumiki, koma mabwenzi, odziwa ntchito ya Atate ndikukhala ndi zonse zimene amatiphunzitsa.
Pachifukwa chimenechi pemphelo lathu likhale motele
"Atate Athu Akumwamba, chonde mundisinthe ndi kundipatsanso mtima watsopano. Ndithandizeni kuti ndisatengere makhalidwe a dziko lino, koma m'malo mwake ndiumbikenso ndi Mawu Anu. Ndilengereni mtima woyera, ndipo musandulike moyo wanga ndi zonse zimene zimandikhudza. Ndikukhulupirirani Inu, Ambuye. M'dzina la Yesu, Ameni."