23/05/2026
Anali mnyamata zaka 19, anakula mmoyo womvera malangizo a makolo komanso kumpingo, koma patsogolo pake kwa iye, zonse zija zinakhala chipsinjo. Anzake amamuuza k*ti "Aliyense ali ndi ufulu opanga chimene akufuna". Ndipo pakupita kwa nthawi mnyamata uja analowerera, mkuyamba kupanga ziwerewere komanso anali kapolo wa khalidwe la ma********on, ankagwiritsa ntchito zimenezi powona k*ti zikhoza kumubweretsera mtendere.
pachiyambi zinali zabwino ndithu kwa iye komano pang'ono ndi pang'ono m'maganizo mwake munayamba kukhala mopanda kanthu maka k*ti ubale wake ndi Mulungu unali utazirala ndipo anayamba k*tenga anthu ngati zinthu zongopangira zokhumba zake, analowerera mu chimo. Komano nthawi zonse pamene ankayesetsa k*ti ayime/asiye zimapezeka k*ti sakukwanitsa akubwererabe kumapanga chimo lomwe lomwelo..
patadutsa zaka John anadziwana ndi mkazi dzina lake Hannah, mtsikana ameneyo anali munthu owopa Mulungu komanso odzichepetsa kwambiri . Ndipo kwaulendo woyamba analakalaka kumanga banja lowona. Anakwatirana ndipo maloto awo anali wodzakhala ndi ana, komano zinali zovuta k*ti apeze mphatso ya mwana, ndipo atapita m'zipatala anazindikira kunena k*ti John ndi amene anali ndi vuto la fertility related to infections (Neglecting your sexual health) ananena k*ti vuto limeneyi anakhala nayo kwa zaka zambiri.
John atamva zimenezi anavutika mumtima mwake ndipo analira kwambiri pokumbukira maulendo onse amene ananyozera malangizo amakolo ake komanso malangizo a mpingo poyamba kukhala moyo mwaufulu anadziimba mlandu posinthana ndi zilakolako za thupi chinthu chimene chinali chofunika kwambiri pamoyo wake.
John analapa kuchokera pansi pa mtima anabwerera kufunafunanso Mulungu ndipo anayambanso kukonza moyo wake anaphunzira kunena k*ti chikhululukilo cha Mulungu mchachikulu kwambiri kuposa zolakwa zathu.
Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo
Inu mwalapa kale ????