Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo

Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo Mulungu wamoyo amakukondani 🌹,
Lapani Tembenukani mtima. Acts 2 vc 40

Ku Imfa ⚰️ kulibe Kulapa📖 Mateyu 3 vc 2

🕊️Evangelist R R Malambo 🕊️
(1)

MBUSA WA NKHOPE ZIWIRIPART 11Usiku unali wamdima kwambiri.Evangelist Yohane sanagone konse pambuyo pa imfa ya Mr Gama.Ma...
22/07/2026

MBUSA WA NKHOPE ZIWIRI

PART 11

Usiku unali wamdima kwambiri.

Evangelist Yohane sanagone konse pambuyo pa imfa ya Mr Gama.

Mawu aja olembedwa pa khoma la selo ankangobwereza m’maganizo mwake:

“CHOONA SICHINATHE…” 😳🔥

M’mawa mwake Evangelist Yohane anayitana Inspector Kalito mwachinsinsi.

“Tiyenera kudziwa anthu amene anali kumbuyo kwa Mr Gama.”

Inspector Kalito anangotsitsa mutu.

“Ndikukuuzani zoona… anthu amenewa ndi oopsa kwambiri.”

Mwadzidzidzi phone ya Inspector Kalito inayamba kulira.

Atayankha, nkhope yake inasintha.

“Kodi chiyani?!”

Evangelist Yohane anayamba kuchita mantha.

“Kwachitika chiyani?”

Inspector Kalito anayankha mwamantha:

“Church yanu yayaka moto!” 😭🔥

Nthawi yomweyo anathamangira ku church.

Atangofika, anthu ambiri anali kulira uku akuyang’ana moto wawukulu.

Mai Esther anayamba kukuwa:

“Bible zonse zapsa!”

Brother Chisomo anayamba kuthira madzi koma moto unkakulirakulira.

Evangelist Yohane anayima chete uku akuyang’ana church yake ikuyaka.

Koma mwadzidzidzi anaona munthu atavala hoodie wakuda ataima kutali uku akuyang’ana motowo.

Munthuyo atangoona Evangelist Yohane anayamba kuthawa.

“IMANI!” anafuula Evangelist Yohane.

Iye ndi Inspector Kalito anayamba kumuthamangitsa.

Munthuyo analowa m’nyumba yakale yosiyidwa.

Atalowa m’kati anapeza mdima waukulu kwambiri.

Mwadzidzidzi panamveka mawu kuchokera pamwamba:

“MUKUSEWERA NDI ANTHU AMENE SIMUKUWADZIWA…” 😳🔥

Inspector Kalito anayatsa torch.

Koma zimene anaona zinawachititsa mantha kwambiri.

Pa khoma panali zithunzi zambiri za ma pastor, ma evangelist ndi anthu ena amene anamwalira kale.

Ndipo pakati pa zithunzizo panali chithunzi chatsopano cha…

😳🔥

Evangelist Yohane

Pansi pa chithunzicho panalembedwa mawu amodzi:

“NEXT.”

Maiwe! 😭🔥

Kodi ndani akufuna kupha Evangelist Yohane?

Nanga chifukwa chiyani church yake yayakidwa moto?

TO BE CONTINUED… 🔥😳

📞 +265 88 42 83 545
WhatsApp

Dinani link ili musiyi kuti muzisate bwino.
Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo

Mwatenga kale uthenga/audio ???
15/07/2026

Mwatenga kale uthenga/audio ???

MBUSA WA NKHOPE ZIWIRIPART 4Church yonse inangokhala chete kwambiri Pastor Daniel atagwa pansi kachiwiri.Anthu ena ankan...
09/07/2026

MBUSA WA NKHOPE ZIWIRI

PART 4

Church yonse inangokhala chete kwambiri Pastor Daniel atagwa pansi kachiwiri.

Anthu ena ankangolira. Ena ankangoyang’anana modabwa.

“Zachitika zoona izi?” ena ankafunsa mwamantha.

Evangelist Yohane anayandikira thupi la Pastor Daniel uku akupemphera mwakachetechete.

Koma mwadzidzidzi mayi wina anayimirira mu church.

Anali Mai Esther.

Misozi inkayenda pa nkhope yawo.

“Zimene pastor wanenazi ndi zoona…” anatero mwamantha.

Church yonse inatembenukira kwa iwo.

Mai Esther anapitiriza:

“Kwa nthawi yayitali tinkangoona zoipa zikuchitika koma tinkachita mantha kuyankhula.”

Anthu anayamba kung’ung’udza.

Mwadzidzidzi Brother Chisomo nayenso anayimirira.

“Inenso ndikudziwa zambiri…”

Nthawi yomweyo church yonse inayamba kusokonekera.

Ena ankati: “Ayi izi sizingakhale zoona!”

Ena ankangolira.

Koma Evangelist Yohane anayimirira pakati pa church nati:

“Abale… ino si nthawi yoweruza anthu ayi. Ndi nthawi yolapa ndi kubwerera kwa Mulungu.”

Nthawi yomweyo anthu ambiri anayamba kugwa pansi uku akupemphera.

Koma kunja kwa church panali munthu wina ataima mumdima…

Anali munthu amene Pastor Daniel ankanzake kwambiri mobisika.

Munthuyo anayankhula yekha:

“Ngati anthu ayamba kudziwa zonse… ndatha.”

Kenako anatulutsa phone n’kuimba munthu.

“Zinthu zayamba kuwonongeka… tiyenera kuletsa Evangelist Yohane ASAP.”

Usiku womwewo Evangelist Yohane ali kunyumba kwake akupemphera, anamva munthu akugogoda chitseko mwamphamvu.

BWAM! BWAM! BWAM!

Atatsegula pang’ono anadabwa kuona anthu awiri ovala zakuda ataima panja…

Mmodzi anayankhula:

“Takubweretsera uthenga…”

TO BE CONTINUED… 🔥😳

Kodi ndiuthenga wanji omwe anabwelesa anthuwa?

NANGA anthuwa anali ndan?

Komaso akuti katundu wawo awonongeka ngati sawaimisa pastar yohanne inu mukutipo bwanji?

Ma comment Anu ndiomwe angapangise khaniyi kuti ibwele Sanga mukhale ndimasana abwino

DINAN blue 👇 PANGAN FOLLOW PAGE INO KUTI ZABWINO ZISAKUPHONYEN
Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo
📞 +265 88 42 83 545
WhatsApp

MBUSA WA NKHOPE ZIWIRIPART 3Chonde WELENGAN mofasaPastor Daniel atadzuka pamalo aja anayamba kunjenjemera kwambiri.Moto ...
24/06/2026

MBUSA WA NKHOPE ZIWIRI

PART 3

Chonde WELENGAN mofasa

Pastor Daniel atadzuka pamalo aja anayamba kunjenjemera kwambiri.

Moto unkawaka mbali zonse. Anthu ankakuwa uku akuthawa koma palibe njira yotulukira.

“Ndili kuti ine?” anafuula mwamantha.

Mwadzidzidzi anthu awiri owopsa anamugwira manja.

“Ayi! Ndisiyeeni!” anakuwa.

Koma mawu amphamvu anamveka:

“Pamene unkachenjezedwa sunamvere.”

Pastor Daniel anayamba kulira.

“Ndipatseni mwayi wina! Ndilapa!”

Nthawi yomweyo anawonetsedwa ngati chithunzi cha moyo wake wonse.

Anaona mmene ankanyengerera azimai a mu church. Anaona mmene ankaba ndalama za nsembe. Anaonanso mmene ankanyoza Evangelist Yohane pamene amamuchenjeza.

Pastor Daniel anagwa pansi uku akulira kwambiri.

“Ndinalakwitsa…”

Koma mawu aja anayankhanso:

“Unkadziwa choona koma sunachite choonacho.”

Nthawi yomweyo moto unayamba kuyaka kwambiri pafupi naye.

Pastor Daniel anayamba kufuula mwamantha.

“Koma anthu anga ku church akuganiza kuti ndili kumwamba!”

Mwadzidzidzi kunangokhala chete.

Kenako mawu aja ananena:

“Ukufuna kubwerera ukawauze choona?”

Pastor Daniel anadabwa.

“Inde! Chonde! Ndikufuna ndichenjeze anthu!”

Mwadzidzidzi kuwala kwakukulu kunawoneka.

Nthawi yomweyo Pastor Daniel anadzuka pa bokosi lake la maliro!

“AHHHH!”

Anthu onse pa funeral anayamba kuthawa mwamantha.

“Wauka! Wauka!”

Mai ena anayamba kulira.

Koma Pastor Daniel anayamba kufuula:

“Tamverani! Tamverani! Mulungu sanyengedwa!”

Church yonse inangokhala chete.

Pastor Daniel anayamba kulira uku akunena:

“Musamanditengere ngati munthu opatulika. Ndinkakhala moyo wachinyengo!”

Anthu onse anadabwa kwambiri.

“Ine ndinkalalikira chilungamo koma mobisika ndinkachita zoipa!”

Evangelist Yohane anayamba kulira uku akupemphera.

Pastor Daniel anapitiriza:

“Pali moto wowopsa kwa anthu osalapa. Lapani musanachedwe!”

Anthu ambiri anayamba kugwa pansi uku akulira ndi kulapa.

Koma mwadzidzidzi Pastor Daniel anayamba kufooka.

Anayang’ana kumwamba uku misozi ikuyenda.

“Zikomo Mulungu pondipatsa mwayi…”

Kenako anagwa pansi kachiwiri.

Nthawi ino sanadzukenso.

Church yonse inangokhala chete kwambiri…

TO BE CONTINUED… 🔥
Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo
📞 +265 88 42 83 545
WhatsApp

✍️ Evangelist R R Malambo

😳🔥 PART YATSOPANO IKUBWERA…Usiku wa funeral anthu onse anayamba kuthawa atangoona bokosi la maliro likuyenda…Kenako mawu...
23/06/2026

😳🔥 PART YATSOPANO IKUBWERA…

Usiku wa funeral anthu onse anayamba kuthawa atangoona bokosi la maliro likuyenda…

Kenako mawu anamveka:

“NDINABWERA KUDZAKUUZANI CHOONA…” 😭🔥

Kodi pastor anabweradi kuchokera ku imfa kapena panali chinsinsi china? 😳

Sindipanganso forward nkhaniyi , pangani follow page ya Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo kuti mutsatire pamka gawo 30 .
Dinani mawu a blue ndipo dinani Follow and like

COMMENT “PART 3” kodi nkhani ipitirire 👇🔥 ????

📞 +265 88 42 83 545
WhatsApp

✍️ Evangelist R R Malambo

MBUSA WA NKHOPE ZIWIRIPART 2Patapita masiku angapo kuchokera pamene Evangelist Yohane anachenjeza Pastor Daniel, zinthu ...
23/06/2026

MBUSA WA NKHOPE ZIWIRI

PART 2

Patapita masiku angapo kuchokera pamene Evangelist Yohane anachenjeza Pastor Daniel, zinthu zinayamba kusintha pang’onopang’ono.

Usiku wina Pastor Daniel anachoka panyumba mwachinsinsi. Anthu ambiri ankaganiza kuti wapita ku mapemphero, koma kwenikweni anapita kukakumana ndi mayi wina wa mu church yake dzina lake Ruth Mbewe.

M’chipinda cha hotelo munali chete kwambiri.

“Pastor kodi izi mukuchita ndi zolondola?” anafunsa Ruth mwamantha.

Pastor Daniel anaseka.

“Palibe adzadziwe. Ine ndine munthu wa Mulungu.”

Koma nthawi yomweyo kunja kunayamba mvula yamphamvu ndi mabingu.

Kutali uko Evangelist Yohane anali pa mapemphero.

Mwadzidzidzi anayamba kumva kuwawa mumtima mwake.

“Ambuye… pali choipa chikuchitika.”

M’mawa mwake Evangelist Yohane anapitanso kwa Pastor Daniel.

Atafika pa church, anthu ambiri anayamba kung’ung’udza.

“Uyu wabweranso?” ena ankatero.

Evangelist Yohane anayandikira Pastor Daniel nati:

“Mulungu akunena kuti lapani nthawi isanathe.”

Pastor Daniel anakwiya kwambiri.

“Usadzabwerenso kuno! Ukundichititsa manyazi pamaso pa anthu!”

Koma Evangelist Yohane anangoyankha:

“Choona sichifa.”

Anthu onse anangoseka.

Koma patangopita masiku awiri, Pastor Daniel ali pa ulaliki wamphamvu kwambiri mu church yake, mwadzidzidzi anayamba kugwira pachifuwa.

“Ahhhh!”

Anthu onse anachita mantha.

Microphone inagwa pansi.

Pastor Daniel nayenso anagwa pansi pa altar.

Anthu anayamba kuthamanga uku akufuula.

“Pastor! Pastor!”

Anamutengera kuchipatala mwachangu… koma atafika doctor anangopukusa mutu.

“Pepani… wamwalira.”

Tauni yonse inalira.

Anthu a mu church yake ankati:

“Zedi Pastor ali kumwamba tsopano.”

Koma usiku womwewo zinthu zoopsa zinayamba kuchitika…

Pastor Daniel anadzuka ngati munthu wa tulo koma anapeza ali pamalo amdima kwambiri.

Moto unkawaka mbali zonse.

Anthu ankakuwa uku akulira.

Pastor Daniel anayamba kuchita mantha.

“Ili kuti?”

Mwadzidzidzi mawu amphamvu anamveka:

“Unaphunzitsa choona ndi pakamwa… koma moyo wako unali wachinyengo.”

Pastor Daniel anayamba kunjenjemera.

“Ayi! Ine ndinali pastor!”

Koma moto unayamba kuyaka mozungulira iye…

TO BE CONTINUED… 🔥?Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambobo
Like and follow page kuti zisakudutseni

📞+265884283545
WhatsApp

MBUSA WA NKHOPE ZIWIRI PART 1M’tauni ina munkakhala ma church awiri osiyana kwambiri.Church yoyamba inkatsogoleredwa ndi...
22/06/2026

MBUSA WA NKHOPE ZIWIRI

PART 1

M’tauni ina munkakhala ma church awiri osiyana kwambiri.

Church yoyamba inkatsogoleredwa ndi Pastor Daniel. Anthu ambiri ankakonda church yake chifukwa ankadziwa kulalikira mwamphamvu, kuvala bwino komanso kuyankhula mawu okopa anthu.

Nthawi zonse ankati:

“Abale musamachimwe! Khalani oyera pamaso pa Mulungu!”

Anthu ankafuula:

“Amen! Amen!”

Koma mobisika moyo wake sunali wabwino. Ankanyenga azimai ena a mu church ndipo ankachita zinthu zobisika zomwe anthu sankadziwa.

Kumbali ina kunali church yaing’ono kwambiri ya Evangelist Yohane.

Church yake inali yosauka. Nthawi zina anthu ankangokhala 7 kapena 10 okha.

Koma Evangelist Yohane ankaphunzitsa choona chokha.

“Mulungu amafuna moyo oyera osati maonekedwe akunja,” ankatero.

Anthu ena ankanyoza church yake chifukwa inalibe anthu ambiri kapena ndalama zambiri.

Tsiku lina usiku Evangelist Yohane ali pa mapemphero, Mulungu anayankhula naye mumtima mwake.

“Pita ukachenjeze Pastor Daniel. Akusintha anthu koma moyo wake uli kutali ndi Ine.”

M’mawa mwake Evangelist Yohane anapita ku church ya Pastor Daniel.

Atafika, anthu ena anayamba kuseka.

“Uyu ndi mbusa wa anthu ochepa aja,” ena ankatero.

Evangelist Yohane anayandikira Pastor Daniel nati modekha:

“Mtumiki wa Mulungu, siyani moyo wachinsinsi. Mulungu akuona zonse.”

Pastor Daniel anayamba kuseka.

“Inu mukufuna kundiphunzitsa ine? Taona church yanu kaye!”

Anthu ambiri anayamba kuseka Evangelist Yohane.

Koma Evangelist Yohane anangonena:

“Mulungu salabadira kuchuluka kwa anthu ayi… amaona moyo wa munthu.”

Pastor Daniel anakwiya kwambiri.

“Tulukani pa church yanga!”

Evangelist Yohane atachoka anayamba kupemphera uku misozi ikuyenda.

“Ambuye, ndachita gawo langa…”

Koma Pastor Daniel sanadziwe kuti nthawi yake inali kuyandikira…

TO BE CONTINUED… 🔥
Chilipo -Judgement -by R R Malambo
PART 2

Tikufuna kuyamba season iyi, mwakozeka ????Pangani follow pageyi Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo kuti zisaku...
21/06/2026

Tikufuna kuyamba season iyi, mwakozeka ????

Pangani follow pageyi Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo kuti zisakudutseni ma part onse.
Kukula moyo wa Uzimu

Inu muli mmaso ? Whatsapp me kuti mutenge audio
17/06/2026

Inu muli mmaso ? Whatsapp me kuti mutenge audio

Address

Lesperance Pvt School, Post Office Box 97, Mayaka, Zomba
Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share