Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo

Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo Mulungu wamoyo amakukondani 🌹,
Lapani Tembenukani mtima. Acts 2 vc 40

Ku Imfa ⚰️ kulibe Kulapa📖 Mateyu 3 vc 2

🕊️Evangelist R R Malambo 🕊️
(1)

Anali mnyamata zaka 19, anakula mmoyo womvera malangizo a makolo komanso kumpingo,  koma patsogolo pake kwa iye, zonse z...
23/05/2026

Anali mnyamata zaka 19, anakula mmoyo womvera malangizo a makolo komanso kumpingo, koma patsogolo pake kwa iye, zonse zija zinakhala chipsinjo. Anzake amamuuza k*ti "Aliyense ali ndi ufulu opanga chimene akufuna". Ndipo pakupita kwa nthawi mnyamata uja analowerera, mkuyamba kupanga ziwerewere komanso anali kapolo wa khalidwe la ma********on, ankagwiritsa ntchito zimenezi powona k*ti zikhoza kumubweretsera mtendere.

pachiyambi zinali zabwino ndithu kwa iye komano pang'ono ndi pang'ono m'maganizo mwake munayamba kukhala mopanda kanthu maka k*ti ubale wake ndi Mulungu unali utazirala ndipo anayamba k*tenga anthu ngati zinthu zongopangira zokhumba zake, analowerera mu chimo. Komano nthawi zonse pamene ankayesetsa k*ti ayime/asiye zimapezeka k*ti sakukwanitsa akubwererabe kumapanga chimo lomwe lomwelo..

patadutsa zaka John anadziwana ndi mkazi dzina lake Hannah, mtsikana ameneyo anali munthu owopa Mulungu komanso odzichepetsa kwambiri . Ndipo kwaulendo woyamba analakalaka kumanga banja lowona. Anakwatirana ndipo maloto awo anali wodzakhala ndi ana, komano zinali zovuta k*ti apeze mphatso ya mwana, ndipo atapita m'zipatala anazindikira kunena k*ti John ndi amene anali ndi vuto la fertility related to infections (Neglecting your sexual health) ananena k*ti vuto limeneyi anakhala nayo kwa zaka zambiri.

John atamva zimenezi anavutika mumtima mwake ndipo analira kwambiri pokumbukira maulendo onse amene ananyozera malangizo amakolo ake komanso malangizo a mpingo poyamba kukhala moyo mwaufulu anadziimba mlandu posinthana ndi zilakolako za thupi chinthu chimene chinali chofunika kwambiri pamoyo wake.

John analapa kuchokera pansi pa mtima anabwerera kufunafunanso Mulungu ndipo anayambanso kukonza moyo wake anaphunzira kunena k*ti chikhululukilo cha Mulungu mchachikulu kwambiri kuposa zolakwa zathu.
Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo
Inu mwalapa kale ????

04/04/2026

𝑴𝒐𝒏𝒊 𝒕𝒐𝒏𝒔𝒆...
Ena amati tasowapo pano... Zoona tasekula WhatsApp group. Tilondoleni ndik*ti mukule mmoyo wa Uzimu ndikukapedza moyo osatha.

Kodi mumadziwa k*ti ukamafuna kupangira anzako choipa, choipanso chako chimakhala chakonzeka kuononga iwe ?Mulungu wanu ...
12/02/2026

Kodi mumadziwa k*ti ukamafuna kupangira anzako choipa, choipanso chako chimakhala chakonzeka kuononga iwe ?

Mulungu wanu wakusamalani bwanji kumeneko ?
Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo

*2026 is coming*▪️Delete negativity▪️Accept your past▪️Restart ▪️stay in love ▪️Christ Above All Ciweluzo Chilipo -Judge...
31/12/2025

*2026 is coming*

▪️Delete negativity
▪️Accept your past
▪️Restart
▪️stay in love
▪️Christ Above All
Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo
CHAKA CHA SOPANO ZOCHITIKA ZATSOPANO. NTHAWA TCHIMO

MITUNDU YA ZITSILU1. Womenya makolo ake ndi chitsilu2. Wonyoza makolo ake ndi chitsilu3. Wochitira mwano makolo ake ndi ...
08/12/2025

MITUNDU YA ZITSILU

1. Womenya makolo ake ndi chitsilu

2. Wonyoza makolo ake ndi chitsilu

3. Wochitira mwano makolo ake ndi chitsilu

4. Wotukwana makolo ake ndi chitsilu

5. Chitsilu ndi chomwe chikunjoya mu town; pamene makolo ake akuvutika zachisoni

6. Chitsilu ndi chomwe makolo ake alibe sopo; zovala ndi zofunda; ndi chakudya. Pamene icho ndalama chik*thera akazi oyendayenda

7. Chitsilu ndi chomwe chikukhala nyumba ya bwino; pomwe makolo ake akukhala nyumba yodontha

8. Ndipo sichibwera icho kuzawaona makolo ake ku mudzi

9. Kunyoza mamuna wako ndi uchitsilu

10. Kupanga uhule uli pa banja ndi uchitsilu

11. Kuchitira mwano apongozi ako ndi uchitsilu

12. Kupanda khalidwe ndi uchitsilu

13. Kumenya mkazi wako ndi uchitsilu

14. Kuzunzitsa mkazi ndi wana ndi uchitsilu

15. Kusasiya ya ndiwo pa khomo ndi uchitsilu

16. Kungokhalira kumwa mowa ndi uchitsilu

17. Mwezi ukatha ndalama kungothera mahule ndi uchitsilu

18. Kusabweza ngongole yomwe unatenga ndi uchitsilu

19. Mayi inu kukhalira miseche pa line ndi uchitsilu

20. Kudana ndi anzako akamachita bwino ndi uchitsilu

21. Kusagwira ntchito kungokhalira kusewera bawo ndi uchitsilu

22. Kukacha m'mawa ukumachoka kwanu k*ti ukapemphetse kwa anzako. Kagwire ntchito chitsilu iwe! Ulesi basi... iya!!!

23. Kuvala molawula ndi uchitsilu

24. Kupanga zibwenzi zoposera chimodzi ndi uchitsilu

25. Kugonana ndi mwana wako ndi uchitsilu

26. Kugwilira mwana wamung'ono ndi uchitsilu

27. Kufunsira mkazi wamnzako ndi uchitsilu

28. Kupeleka mimba ndikuyikana ndi uchitsilu

29. Kubela azinzako ndi uchitsilu

30. Kutambira azinzako... ngati ndiwe fiti; ndiwe chitsilu!!!

MIYAMBO 12:1
Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo
Follow and like for more information

M***a kupitiliza k*tchula zitsilu Zina.....

14/10/2025

*THAMBO LAKUDA LAGWA*
😭😭😭😭😭😭😭

Apa nKudziwitsa Okhulupirira nonse k*ti ndaluza kholo mmalo mosangalala mother's day, tiri kulira agogo omwe amatenga Udindo wa mayi
😭😭😭😭😭😭😭😭

_Okhulupirira Imani nane munyengoyi_ *Mulungu wamoyo* tonthozani osweka mtimafe
😥😥😥😥😥😥

MAYO MUDZI WANGA WALOWA BWINJA😥😥😭😭🤔🤔😭ABWENZI modandaula ndikulengedza kachiwiri k*ti amene tinaonapo chisomo cha Mulungu...
11/10/2025

MAYO MUDZI WANGA WALOWA BWINJA
😥😥😭😭🤔🤔😭

ABWENZI modandaula ndikulengedza kachiwiri k*ti amene tinaonapo chisomo cha Mulungu wamoyo pamoyo wathu tiyeni tisekule gulu loti tizisonkha tindalama k*ti tizithandiza ena... 😭

As I'm saying ndathandizapo anthu 4, mmodzi ndi wophunzira amene pamka pano fees yake amadalira Ine. 3 okalamba

Koma ndadandaula kwambiri chifukwa Pali mwana wina amene wayamba form 1, pa Khwalala community day secondary school, koma Motengera ma dandaulo ake sukulu ikhonza kumukanika. Ndi wamasiye makolo onse palibe. 😥

Amene tiri ndi mtima othandiza ena tiyeni tigwirane Manja please, ngati mugakwanitse nokha tiyankhuleniso...

Call or whatsapp
+265996468340
[email protected]
+265884283545

Mateyu 5 vc 7 odala inu amene muchita chifundo.
Tisadikire k*ti tikule k*ti tzathandize wina. Tisadikire k*ti tikhale nawo zambiri please, Tisadikire k*ti titchuke... Mulungu pokupasani zomwe muli nawozo anakudalilani...
🤝🤝🤝🤝🤝🤝

10/10/2025

ANATI ALIBE NTHAWI YOTI AZIKAYANG'ANA POMWE ASIYA SINGANO LA K50..
Mai wina anaona mwana wake akumuyang'ana kwambiri ndipo Maiyo anati;
🤷‍♂️LANKHULA LINDA, NDAONA ULI NDI MAU..
Ndipo Linda anati;
🤔KODI AMAI MCHIFUKWA CHIYANI, IFE SITIPITA KUKAPEMPHERA NAO KWA ANEBA ATHU, ALANDLOAD AJA, MALO MWAKE TIMAZITSEKELA NYUMBA MUNO KUMAPEMPHERA TOKHA.
LIKAKHALA SI TSIKU LAKU CHARICHI, ANTHU AMACHOKA K*TALI KUMAZAPEMPHERA KWA ALANDLOAD IFE SITIPITAKO CHIFUKWA CHIYANI?..
Mai wake sanamuyankhe koma anangomutuma k*t akayatse mbaula ayambe kuphika..
Akupita kotenga mbaula, Linda samaiona mbaula ija chifukwa zinthu zonse zinali pamodz pafupi mpomwe iwo amagona.
Atayang'anayang'ana nkuipedza k*ti inali pafupi koma kaamba koti zinthu zonse zili pamodz kaamba kakuchepa kwa room, analinso ndi funso kwa Mai ake, iye anati;
🤔KODI INU AMAI, MCHIFUKWA CHIYANI KUKABWERA MUNTHU OFUNA NYUMBA, A LANDLOAD AMATISAMUSA IFE NKUMUPATSA MUNTHU UJA, PANO NDIIFE TIKUKHALA KANYUMBA KAKANG'ONO CHONCHI..?..
Mai ake anasiya zomwe amachita ndipo anati;
🤷‍♂️APAPA SOPANO WAZIYANKHA WEKHA FUNSO LAKO LOYAMBA LIJA, KODI SIIWE UNAPITA MASANA K*T UKATENGE SINGANO LATHU LOMWE ANABWEREKA A LANDLORD, UKUFUNA K*T USOKERE DRESS LAKO, PAJA ANAKUYANKHA K*T CHIYANI?
Mwana uja anayamba kugwetsa misoz, mokhuzika Linda anati;
😭ANANDIUZA K*T NTHAWI ZONSE MAI AKO AMASALA NDINGONGOLE YA RENT, AMAPEREKANSO NDALAMA YA RENT MOCHEDWA, NDIYE ANATI ALIBE NTHAWI YOTI AZIKAYANG'ANA POMWE ASIYA SINGANO LA K50..
Mai ake anamuuza k*t MWANA WANGA KUPEMPHERA NKOOPSA SIMMENE UKUGANIZIRA., BAIBULO LINATI KULI ANENERI ONYENGA, AMADZIWIKA K*TI NDIOPEMPHERA K*TALI UKOOO, ANEBA AWO, ANA AWO, ANZAO OSAMAWAONETSERA CHIKONDI CHA MOYO WACHIKHRISTU..
Mateyu 7 VS 16
Mudzawazindikira iwo ndi zipatso zawo. Kodi anthu amathyola mpesa pa mtengo wa minga, kapena nkhuyu pa nthula?
Khalidwe lanu ndilimene lizakope ena kupembedza Mulungu amene mumamutumira..
Kulalika, kusonkhana chigulu, kuchita fasting, kuchedzera mapemphero, zilibe kanthu koma kodi mukakhala kwanuko, aneba anu, abale anu, akuchimuna, akuchikaz amakuonaninso ngat opemphera....
Chinalipo chimene Mai uja samapitila k*t azikasonkhana nao kwa alandload angakhale a landlord amaiona opemphera koma awa samaonamo Mulungu owona mwa a Landload..
Kodi Chimene chikulepheretsa k*t muwakope, akaz anu, amuna anu, aneba anu, anzanu ocheza nao k*t azibwera kumene mumapemphera mchiyani..mwina vuto ndiinu..
Tiyeni tizikonze k*t tikope ambiri abwere kwa Yehova..
TSIKU LABWINO AMBUYE AZIKUDALITSANI AMEN AMEN

Khalani a changu pa za Uzimu

Address

Lesperance Pvt School, Post Office Box 97, Mayaka, Zomba
Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Ciweluzo Chilipo -Judgement -by R R Malambo posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share