30/06/2016
Pepani posakupatsirani uthenga wa ya last week.
Ok. Mutu wa nkhani unali oti: KUPANGA CHUMA. BY: DR ENSON LWESYA.
Nkhani inali yakuti, palibe munthu yemwe ali osaukitsitsa padziko lapasi pano. Chomwe tiyenera kudziwa ndichakuti, Mulungu anapeleka kwa aliyese kuthekela kokhala ndi chuma.
(1)Ena tinapatsidwa maluso osiyanasiyana. Imeneyo ndi mbewu yomwe Mulungu anatipatsa kuti tiyigwilitse ntchito pakupanga chuma pamiyoyo yathu.
(2)Ena chifukwa cha ntchito zomwe timagwira, timadznenera tikha kuti sitingachite bwino chifukwa choti tikugwira ntchito zomwe zimaoneka kuti ndizonyozeka kwa ena. Komwe dziwani kuti, chomwe mukuchipeza kuchokela muntchito yonyozeka yomweyo ndichomwe Mulungu amagwiritsa ntchito pakutukula Miyoyo yathu.
(3)Ena mpaka timafika pomati aaah, bola ndinakabadwila banja ilo sibwezi ndili osauka poti banjalo ndilolemela. Enaso timati mmmmh, bola ndinakabadwila ku America(kumatchula mayiko olemela). Ayi nkhani sikubadwila banja lolemela kapena dziko lolemela. Chimwe chikufunika ndikuzindikila mbeu yomwe Mulungu anaika mwainu. Mukaidzala mbeu imeneyo yembekezela kukolola mosakaika konse. Mau a Mulungu akuti, Dzanja lomwe lifesa zochuluka, zochulukaso ludzatuta, ndipo lomwe lifesa zochepa, zochpaso lidzatuta. Zingoonetseratu kuti Mulungu anaika mbeu m'dzanja la wina aliyese, kwatsala kwa ife kuti tiyifese mbeu imeneyi ndikukolola. Ndipo ngati tifuna kukundika zochuluka tiyeneraso tifese mbeu imeneyi muchuluka. MULUNGU AKHALE NANU.