Evangelist Kondwani Gomani

Evangelist Kondwani Gomani Thy word is a lamp unto my feet, and a light unto my path. Psalm:119:105

18/01/2024

Kodi Yesu Khristu ndi mwana wa Mulungu?
Pamene taona kuti Quran likusimikizira ndi kuyikira umboni waukulu pa umphumphu wa Bible, tikuyeneranso kuona bwino Malo ena amene amatsutsana ndi bible.
Kodi Yesu Khristu ndi mwana wa Mulungu malingana ndi Quran? πŸ‘‡
Surat 6:10 'Iye ndi Mlengi wathambo ndi nthaka, zingatheke bwanji kukhala ndi mwana pomwe iye alibe mkazi......? πŸ‘‰Chifukwa chaperekedwa apa ndi kungochepsa mphamvu ya Mulungu kuti sangakhale ndi mwana popanda mkazi. πŸ‘‰ Surat 3:45 "....Mulungu akukuuza nkhani yabwino kuti ubereka mwana popanda mwamuna koma kupyolera mu mau" ➑️ mukaonetsetsa Quran ikuchephya mphamvu ya Mulungu ndi kupereka mphamvu Kwa Mariya. πŸ”ΆMariya anati atamva mau awa Kwa MngeroπŸ‘‡
Mbuye wanga! Ndingakhale bwanji ndi mwana pomwe mwamuna aliyense sadandikhuze aliyense? Mngero adati, ndi momwemo Mulungu amalenga chomwe wafuna. Akafuna chinthu amachiuza 'chitika ndipo chimachitikadi (Surat 3:47). πŸ‘‰ Mungathe kukhala ndi ganizo through this Ayah kuti Mulungu amalenga chimene akufuna. Tikuona mabadwidwe a Yesu odabwitsa kuti ndithu Yesu Khristu ndi mwana wa Mulungu. 'Mateyu 1:18-21 Cholandilidwa mwa iye chilicha Mzimu woyera'. Luka 1:35 πŸ‘‰ '...Mzimu woyera adzafika pa iwe, ndi mphamvu ya Wankulukulu idzakuphimba iwe; chifukwa chakenso choyeracho chikadzabadwa, chizatchedwa Mwana wa Mulungu'. Quran ikuchitira umboni kuti kubadwa Kwa Yesu ndi chozizwitsa Kwa anthu. πŸ‘‰ Surat 19:20-21, 19:29-30. Tili ndi anthu amene anachitira umboni kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu. 1. Nikodemo πŸ‘‰ Yohane 3:2, Yohane 20:30-31, Qur'an 3:49. Zizindikiro zimene Yesu anachita zili umboni wokwanira kuti Iye (Yesu) ali Mwana wa Mulungu.

Chifukwa china chaperekedwa pokana kuti Mulungu sangakhale ndi Mwana ndi "chakuti Chiyero chake Cha Mulungu" Quran 4:171 Ulemero wake ngotukuka kutali ndi kukhala ndi mwana" malingana ndi Quran nkwapatali Mulungu kukhala ndi mwana. Petro adayankha kuti; Inu ndinu Khristu Mwana wa Mulungu Wamoyo, Yesu anati ndiwe Odala Simon Bar-Yona....Mateyu 16:16-17. Mulungu mwini anayankhula kuti Yesu ndi Mwana wake; "Uyu ndie Mwana wanga wokondeka mwa Iyeyu ndikondwera" Mateyu 3:17. Mkulu wa Asilikari anati; πŸ‘‰ "Indedi Uyu ndi Mwana wa Mulungu " Mateyu 27:54. Mungathenso kuona mavesi osatirawa; Agalatiya 1:4, Aroma 1:1-4, Ahebri 1:1-2, Yohane 20:28. Ndi mavesi ena ambiri.
Conclusion; YESU KHRISTU NDI MWANA WA MULUNGU!

18/01/2024

Buku Lopatulika 1992 Mateyu 5:8 Odala ali oyera mtima; cifukwa adzaona Mulungu.

Ndi Oyera mtima okha omwe adzaone Mulungu. Without holiness no man shall see the kingdom of Heaven. Be wise my brethrens.

17/01/2024

Kodi munayamba mwaliringalirapo za moyo wanu?

Tawumvetsereni mtimawo, muumva uli Gu-gu gu-gu..... Chogundacho chikangosiya maliro. Nzanga usapusisike ndi chigulu Cha anthu chimene chimangokuchemerera ukamapanga zoputsa zakozo koma palibe angathe kulanditsa moyo wako utadwala, Tsiku limenero amakhala owonerera amenewo. Azakutenga anthu oposa 2000 ulendo kukhalango, koma chodabwitsa azakusiya wekha mkazenje ka 7 fit iwo nkubwerera ku nyumba zawo. Kodi palibenso chochitira matama apa?

Nzanga moyo uwuwu tikanati tidzidziwa kumene ukupita kapena utakathere tikanasiya kaye ziwana nkukonza moyo. Munthu wachuma uja akadadziwa kumene moyo wake ukathere ineyo ndikukhulupirira kuti akanakonza! (Luka 16:19-31)

Ndikuyankhula ndi iweo chifukwa ndikudziwa kuti umadziwa kuti uzafa tsiku lina, nthawi Ina, Chaka china. Buku Lopatulika 1992 Mlaliki 9:5 Pakuti amoyo adziwa kuti tidzafa; koma akufa sadziwa kanthu bi, sadzalandira mphotho; pakuti angoiwalika. Buku Lopatulika 1992 Yeremiya 9:21 Pakuti imfa yakwera m'mazenera athu, yalowa m'nyumba mwathu; kucotsa ana kubwalo, ndi: anyamata kumiseu. Inu mumadziwa kuti kufika lero tikhala titasiyana nawo okondeka athu aja? Ena anagona mwakachetechete pano kuli ziiiiiii, anapita! Imfa inalowera pamazenera.

Buku Lopatulika 1992 Mlaliki 12:3 tsikulo omwe asunga nyumba adzanthunthumira, amuna olimba nadzawerama, akupera nadzaleka poperewera, omwe ayang'ana pamazenera nadzadetsedwa;
Amuna amphamvu amamyata imfa ikagogoda. Nzanga imfa mchirombo, ena ananyamuka bwino bwino pakhomo koma sanabwererenso pano kuli ziiiiiii! 😭😭😭😭. Ena anasanzikana tionanso mawa koma kutacha sizinathekenso kuonana wina anagona pano kuli ziiiiiii 😭😭😭😭😭.

Nzanga wapulumukapo kangati iweo pa ngozi? Wapulumukapo kangati iweo Kwa okuba, achifwamba kapena olanda? Wapulumukapo kangati iweo ndi moyo? Kodi siunja umafuna kufa nawo uja iwe? Unayamba wazifunsa kuti ndinapulumuka chifukwa chani? Anzako ali kuti? Mayi ako ali kuti? Achemwali ako ali kuti? Bambo ali kuti?

Remedy ya imfa ndi Yesu Khristu yekha basi (Yohane 3:16 Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wace wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha.

Chisankho chili mmanja mwako ndipo opanga chisankhoyo ndi iweo! Yesu Khristu ali pankho la mtima wako Revelation 3:19-20

17/01/2024

Moyo uwu munthu anayenera kukhala ochenjera ndi osamalitsa kwambiri.

1. Kodi ndi nthawi yayitali bwanji imene mumakhala mukuwerenga bible or any other gospel literatures?
2. Kodi pa maola 24 amene timakhala nawo pa tsiku, ndi maola angati amene mumapatula nthawi yanu mkupemphera?
3. Kodi munayamba mwaliringalirapo za kanthu kena kotchedwa imfa? Nanga munayamba mwaliringalirapo za moyo wina umene uli kutsogoloku moyo una utantha?
4. Kodi mumakhulupirira kuti muzafa? Nanga mumakhulupirira kuti tsiku lina akufa azakhalanso ndi moyo?
5. Kodi mumakhulupirira kuti kuli moyo osatha? Munayamba mwazifunsapo kuti amene azakhale ku mpaladizo ndi ndani?
6. Kodi mumakhulupirira kuti kuli Gehenna? Munayamba mwazifunsapo kuti amene atadzakakhale ku Gehenna ndi ndani?

Ndimati ndikukumbutseni kuti tsiku lina iweyo udzafa ndithu (Buku Lopatulika 1992 Ahebri 9:27 Ndipo popeza kwaikikatu kwa anthu kufa kamodzi, ndipo atafa, ciweruziro. Taona matchona akuchoka mmatauni atagona kukayikidwa kumidzi kuthengo kwenikweni reason imfa. Once you die;
1. Kukongola kumatha πŸ˜₯πŸ˜₯πŸ˜₯
2. Unyamata umatha πŸ˜₯πŸ˜₯πŸ˜₯
3. Kutchuka kumatha πŸ˜₯πŸ˜₯πŸ˜₯
5. Ma certificate (ma diploma, ma masters PHD) zimatha. πŸ˜₯πŸ˜₯πŸ˜₯
6. Ulemero umatha, anthu amatulutsidwa nyumba yomanga okha nkukalowa pansi pa matope. πŸ˜₯πŸ˜₯πŸ˜₯
7. Chikondi chimatha, apa za u honey, sweet chocolate zimatha izi. 😭😭😭

Nzanga ndimati ndikukumbutse kuti moyo unowo siokhalitsa tsiku lina imfa idzakhala pa iweo. Buku Lopatulika 1992 Ahebri 13:14 Pakuti pano tiribe mudzi wokhalitsa, komatu tifunafuna ulinkudzawo. Bwanji osalapa? Bwanji osatembenuka mtima?

Kuli bwenzi limodzi Yesu Khristu amene chikondi chake sichimatha ngakhale abwenzi onse athawa. Bwanji kupanga naye ubwenzi Yesu Khristu ameneyi? πŸ“–πŸ“–πŸ“–Yohane 1:12, Machitidwe 2:38-40, Yohane 11:25, Yohane 3:2-8,15-16 Aroma 10:8-10.

Nzanga, usakomedwe ndi moyo uwu ndiwabodza! Imafika nthawi yoti palibe angakulanditse, aliyense amakhala owonerera. Ndi nthawi yabwino yokonza kofikira moyowu ukatha

17/01/2024

Kodi buku la Qur'an linadza chifukwa chani? Asilamu amakhulupirira kuti Qur'an ndi buku lotsiridza lomwe linabvumbulutsidwa ndi Muhammad. Kodi chifukwa chiyani Quran linalembedwa? Umboni ochokera mu Qur'an;πŸ‘‡πŸ‘‡πŸ‘‡πŸ‘‡πŸ‘‡
1. Kutsimikizira bible ndi kutionetsa kuti mu bible muli kuunika πŸ‘‰ Quran 3:3-4 (likusimikizira zomwe zinalipo patsogolo pake, ndipo adabvumbulutsa Torah ndi Injili {Chipangano Chakale ndi Chatsopano}) kuti mabukuwa akhalo otsogolera anthu.
2. Kuyikira umboni bible komanso kukhala mtetedzi wa bible πŸ‘‰ Quran 5:48
3. Kuonetsa kuperewera kwathu popanda bible πŸ‘‰ Quran 5:68 Nena E inu anthu a buku! Simuli kanthu (pa chipembezo chanu) mpaka muyimirire (kusatira malamulo) a Torah ndi Injili.
4. Kutionetsa kuti mu bible muli chiongoko ndi Kutionetsanso kuti mu bible muli uthenga wabwinoπŸ‘‰ Quran 5:46
5. Kutidziwitsa kuti mau a Mulungu sangasinthidwe πŸ‘‰ Quran 6:34 ......palibe wosintha pa mau a Mulungu πŸ‘‰ Quran 10:64 ....palibe kusintha pa mau a Mulungu. Uku ndiko kupambana kwakukulu.
πŸ“–Quran likuonetsera ungwiro, kukwanira, umphuphu, kusaperewera ndi kudalirika Kwa Malembo Oyera (Bible). Quran yatsusa anthu onse amene amati bible linasinthidwa, ena amati bible linagwa. Mu Qur'an mulibe pamene amanena kuti bible linagwa palibe even a single Ayah, izi amangonena ndi anthu amene sadziwa Quran. Aliyense amene anganene kuti bible linaonongeka ndie kuti akutsutsana ndi Quran. Popanda Bible, Quran kunalibe koma kopanda Quran Bible linalipo. Buku Lopatulika 1992 2 Timoteo 3:16-17 Lemba liri lonse adaliuzira Mulungu, ndipo lipindulitsa pa ciphunzitso, citsutsano, cikonzero, cilangizo ca m'cilungamo: kuti munthu wa Mulungu akhale woyenera, wokonzeka kucita nchito iri yonse yabwino. 2 Petro 1:20-21. Bible ndilo mau a Mulungu sangatheke kuonongeka kapena kusinthidwa angakhale wina atafuna kuononga monga anthu ambiri anayetsera koma analephera πŸ‘‰ Mateyu 5:18, 24:35, Luka 16:16-17, 2 Petro 1:19.
πŸ‘‰βž‘οΈ πŸ“– Kukana zonena za Bible ndiko Kukana zomwe Quran latsimikizira.

15/01/2024

I don't think if there is a woman amene ati akaonongeke/kulephera kulowa kumwamba chifukwa amalalikira uthenga wabwino mkachisi I doubt. Marko 9:38 Yohane ndi ophunzira ena anati Kwa Yesu Khristu tinamuletsa wina akuchotsa ziwanda mdzina lanu, and immediately Jesus reply; Marko 9:40 Pakuti iye wosatsutsana ndi ife athandizana nafe. We are the Sons and Daughters of Jesus Christ, the messengers of Kingdom of Heaven. Ellen G White anali mzimayi the founder of Seventh Day Adventist, Kodi sadzalowa kumwamba chifukwa anayamitsa mpingo? Kulalikira koma ma reference onse from Ellen G White. Early Writing, Desire of Ages, The Great Controversy, Evangelism, Steps to Christ etc. Nkumati mzimayi asalalikire, tsono ma reference-wa! Ndanenabe.

15/01/2024

Nthawi zina timangolimbana ndi zinthu zimene zilibe even salvation.
In Matthew 28:19 Yesu Khristu akuuza ophunzira pitani ku dziko mukalalikire. Sakusankha kuti okalalikirayo ndi ndani, ndi mzimayi kapena M'zibambo no! Agalatiya 3:28 bible liri Clear kuti muno aliyense ndi ofanana ndi mzake mwa Yesu Khristu. I am not talking based on gender equality but I am talking based on Spiritual gifts. Some are apostles, prophets evangelist, pastors and teachers (Ephesians 4:11).
1 Corinthians the whole chapter from ndi nkhani ya Church Board. Ena akuti nanga Timoteo inamukhunza bwanji? Timoteo anali Church Elder wa chinyamata wa mpingo wa ku Akolinto ndi amene Paul ankamugwiritsa ntchito kwambiri kupita mumipingo yosiyanasiyana. Dziwani kuti Paul amayankha mafunso komanso mavuto amene analandira kuchokera ku Corinthians. 1. Kugawikana mumipingo (1 Akolinto 1:10-16, 3:1-8). 2. Case of in**st 1 Akolinto 5 (kugonana Kwa pakati pa brother and Sister, or father and daughter). 3. Milandu yapakati pa mamembala ampingo (1 Akolinto 4:1-5, 6:1-11, 7:1-40. 4. The abuse of Christian freedom 1 Akolinto 14:1-25). 5. Chikondwerero Cha mgonero (1 Akolinto 11:17-34). Awa ndi ena a madandaulo amene Paul analandira.
1 Akolinto 14:34 inabweretsa debate yayikulu kwambiri pakati pa Akhristu, kunali kagulu ka amayi kamene machitidwe awo sanali ovomerezeka pakati pa mpingo, monga Kunenera, malirime, ena ankameta tsitsi lawo mipala komanso mavalidwe osakhala bwino akatero akatumikire kutsogolo Kwa mpingo wonse. Zomwe zinabweretsa debate yayikulu kwambiri pakati pa mpingo wa Akolinto. Machitidwe omwewa anali kuchitikanso at a different time to different group of people. 1 Akolinto 14 34 Paul amaletsa ngakhale mzimayi Kunenera mumpingo, kutanthauzira uneneri and Judging the Prophets. Chifukwa Cha ichi ngakhale amayi kulalikira kunja Kwa mpingo sankaloledwa maka ku mpingo wa ku Akolinto. Koma mbali zina zimalola amayi kulalikira kapena Kunenera kunja Kwa mpingo.

14/01/2024
14/01/2024

Before I proceed with the lesson from Quran, let's come to Revelation 9, I had something more important to share with you brethrens.

Upon sounding the fifth trumpet, a star fell from heaven to the earth. Having ceased to be a minister of Christ, he who is represented by this star becomes the minister of the devil; and lets loose the powers of hell against the churches of Christ. On the opening of the bottomless pit, there arose a great smoke. The devil carries on his designs by blinding the eyes of men, by putting out light and knowledge, and promoting ignorance and error. Out of this smoke there came a swarm of locusts, emblems of the devil's agents, who promote superstition, idolatry, error, and cruelty. The trees and the grass, the true believers, whether young or more advanced, should be untouched. But a secret poison and infection in the soul, should rob many others of purity, and afterwards of peace. The locusts had no power to hurt those who had the seal of God. God's all-powerful, distinguishing grace will keep his people from total and final apostacy. The power is limited to a short season; but it would be very sharp. In such events the faithful share the common calamity, but from the pestilence of error they might and would be safe. We collect from Scripture, that such errors were to try and prove the Christians, 1Co 11:19. And early writers plainly refer this to the first great host of corrupters who overspread the Christian church.

Read again these word; The devil carries on his designs by blinding the eyes of men, by putting out light and knowledge, and promoting ignorance and error.
And ye shall know the truth, and the truth shall make you free. John:8:32

13/01/2024

What knowledge of Christ can that be, which sees not that he is most worthy of our entire obedience? And a disobedient life shows there is neither religion nor honesty in the professor. The love of God is perfected in him that keeps his commandments. God's grace in him attains its true mark, and produces its sovereign effect as far as may be in this world, and this is man's regeneration; though never absolutely perfect here. Yet this observing Christ's commands, has holiness and excellency which, if universal, would make the earth resemble heaven itself. The command to love one another had been in force from the beginning of the world; but it might be called a new command as given to Christians. It was new in them, as their situation was new in respect of its motives, rules, and obligations. And those who walk in hatred and enmity to believers, remain in a dark state. Christian love teaches us to value our brother's soul, and to dread every thing hurtful to his purity and peace. Where spiritual darkness dwells, in mind, the judgment, and the conscience will be darkened, and will mistake the way to heavenly life. These things demand serious self-examination; and earnest prayer, that God would show us what we are, and whither we are going.

Address

Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Evangelist Kondwani Gomani posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share