MPhunzitsi wa mpingo

MPhunzitsi wa mpingo Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from MPhunzitsi wa mpingo, Church of God, Mnsambachikho, Lilongwe.

25/03/2022

MUSADANDAULE NDI ZAMAWA
◆◆◆◆

Ndi zachidziwikire kuti anthufe mwa chibadwa timadandaula kwambiri, timalira nthawi zambiri, timadera nkhawa nthawi zambiri, koma ngakhale ziri choncho Mulungu akutipempha kuti tikweze maso kwa iye,

Mvetserani zimene bukuli likunena
Mateyu 6:34
"Cifukwa cace musadere nkhawa za mawa; pakuti mawa adzadzidera nkhawa iwo okha, Zikwanire tsiku zobvuta zace"

Kumbukirani kuti inu ndinu mkristu, ndi zowona kuti zosowa m'zambiri pa umoyo uno, maka polingalira kuti mawa tidzadya chani"
Koma Yesu akutipempha kuti "Tiyang'ane iye nthawi zonse", ndipo Yesu ndiye angalongosole za mawa lathu...
Nkutheka mawa mukupita kukaweruzidwa ku bwalo la milandu, ndipo mukudzifunsa kuti "Ndikayankha chani"?
Koma Yesu akutilonjeza kuti tikweze maso kwa iye' ndipo adzatithandiza...
Ngati ndinu mkristu kumbukirani kuti"Mulungu anakuchitirani chinthu chachikulu kwambiri pokupatsani mwayi kuti mukhulupirire Yesu' ndeno sangalephere kukuthandizani zochepazi....

Luka 12:29-30
"Ndipo inu musafunefune cimene mudzadya, ndi cimene mudzamwa; ndipo musakayike mtima. Pakuti izi zonse mitundu ya anthu a pa dziko lapansi amazifunafuna; koma Atate wanu adziwa kuti musowa zimenezi".

Chilichonse chimene muchisowa Mulungu akudziwa kuti muchisowa, ndipo monga mwa kuchuluka kwa chuma chake Mulungu adzakupatsani inu....
Ndi zoona imafika nthawi kuona kuti mavuto siyakuchoka pa nyumba lanu, koma kumbukira kuti "Pamene uli pafupi kulandira chabwino umavutika koopsa mpaka kulakalaka utapanga njira zina" Koma mupirire mukanthawika pakuti simudzadera nkhawa mpaka muyaya ayi...
Ndi chifukwa chake ndikukuuzani kuti "Tisafooke pakuti Yesu akuona" ndipo sadzalola kuti kapolo wake avutike mpaka nthawi yaikulu ayi....Koma iye adzapereka njira zoti mupezere chakudya ndi chobvala,
Ndimangofuna ndikulankhuleni mauwa basi,
ndingoti Ambuye akudalitseni kwambiri

onani musaiwale kupanga Like page ndiponso kupanga Share post kuti mauthenga ena yasakuphonyeni

tili ndi group ku WhatsApp, group la mau a Mulungu. ..ndipo ngati mukufuna kulowa eni nambala izi
+258878750070
+258862533330
+258868947783

Wolemba ndi Domingos Anthony
842405539
+258868947783

12/03/2022

STORY YOLIRITSA UKUWERENGAYI

Ntsikana wina wa zaka15 zakubadwa, iye anali mwana yekhayo mubanja la kwawo.

Ndiyeno tsiku lina Ntsikana uja analota maloto oopsa kwambiri okhudza makolo ake...
Iye analota makolo ake yatamwalira pangozi ya Galimoto...
Ndiyeno pamene Ntsikana Uja anadzuka anayamba kuuza makolo ake kuti:"
::
- Amama ndinso inuyo adaddy, lero musapite kulikonse pakuti ine ndalota choipa chachikulu chitakuchitikirani, ndipo ndalota inuyo mutamwalira pangozi ya Galimoto..

Amayi ake anauza Ntsikana uja kuti "Mwana wanga palibe chimene chitichitikire ife wamva"..
ndiyeno pita ukadye chakudya chako ukatha upite ku school..
Ndipo patadutsa ma minutes ochepa bambo ndi mayi ananyamuka ulendo kupita ku ukwati wanzawo..
Ndipo Pamene amayenda kumeneko anachita ngozj yoopsa kwambiri mpaka onse anafa...

Pamene Ntsikana uja ankachokera ku school anaona anthu ambiri ali pakhomo pawo, ndipo ntsikanayo ankafuula kuti
''Amama!! Amama!! ndabwererako ku school nanga inu muli kutiko? .
Anthu amene anakhala pakhonde panyumba sanapirira kukhala chete ndiye anayamba kulira mokweza mau chifukwa sankadziwa chimene akanachita.

Ndipo agogo ake a Ntsikana uja anafika pafupi ndi iye ndipo anati"
-"Mwana wanga usadandaule!! ukhulupirira wamva? "..
Ntsikana uja anayankha kuti zili bwino ndipo kenako anafunsa kuti:: Nanga mayi ndi bambo anga ali kutiko?

Agogo ake anati:- Iwo wachita ngozi lero moti mwamwalira posachedwapa!!

Ntsikana uja sanapirire kudzigwira basi anakomoka!!...
��������
Abale kodi mukudziwa kuti tsiku lina tidzafa? Kodi mukudziwa kuti moyo uno uli ngati mpweya?
Nanga mwakonzekera?
Chonde lapani machimo anu kuti ngati nkuchita ngozi idzakupezeni muli oyera Mtima... Kodi ndi ndani amene amadziwa tsiku limene adzafe?
Ndeni ngati iweyo sudziwa...Konzeratu moyo wako udakali kupuma..lero.. Kodi Ambuye Yesu atabwera lero ungakafikire kuti?? Inu lapani machimo anu onsewo...
Ngati inu simutembebuka mtima mudzapita ku Gehena wamoto wosazima (Mt. 25:42'46)
Ndiyeno lero ndilo tsiku labwino loti tilape ndi kutembenuka mtima, lero ndilo tsiku labwino kuti titembenukire Kwa Yesu tsopano.....Tisachite manyazi pakuti tikatero nayenso adzatikana(Mt.10:32-33).
Konzekani za kubweranso kwa Yesu, sinthani machitidwe anu anthuni, pakuti mkwiyo wa yndi woopsa

Jesus "Amen & Amen"

Musaiwale kupanga Like page kuti nkhani zina zisakuphonyeni.
ndiponso mwa kukonda anzanu ena please pangani Share Uthengawu.

Nkhaniyi yalembedwa ndi Domingos Anthony
+258868947783

09/03/2022

KODI NDINGADZIWE BWANJI KUTI NDINE MKRISTUDI?

M'musimu Muli mfundo seven (7), zomwe zikutiphunzitsa mmene tingadziwire kuti ndifedi akristu, ndiponso zikutiphunzitsa mmene tingakwezere uzimu wathu...

Mfundo yoyamba
-KUZITSIMIKIZIRA(2Timo.1:3)
mpofunika kuti ife tizidzitsimikizira za chipulumutso chathu, ndiponso mpofunika tizitumikira Mulungu ndi chikumbumtims choyera, nde mkristu weniweni amazitsimikizira kuti ndi opulumuka.

Mfundo yachiwiri
-NJALA NDI KUMVERA MAU A MULUNGU (Yoh.5:4; 14:21; 1petr.2:2-3)
Mkristu weniweni amakhala ndi njala ya kumva mau a Mulungu ndi kuchita, ndipo akatero uzimu wake sungakhale chimodzimodzi.

Mfundo yachitatu
-KHUMBO LA KUPEMPHERA (Arom.12:12; Akolos.4:2; 1Atesal.5:17-18)
Kristu weniweni amakhala ndi khumbo la kupemphera, amakonda kupemphera, amalakalaka atapemphera, amasirira kupemphera nthawi zonse, ndipo munthu wotere uzimu wake sukhala chimodzimodzi.

Mfundo yachinayi
-CHIKONDI NDI AKRISTU ANZAKE (Yoh.13:34-35; Aheb.10:24-25)
Mkristu weniweni amakhala ndi chikondi ndi akristu anzake, sadana ndi akristu anzake ayi, koma amondwera akamacheza ndi kumvetsera akristu anzake, ndipo ngati inu mumakonda akristu anzanu mumachita bwino, ndipo Uzimu wanu sungakhale chimodzimodzi.

Mfundo yachisanu
-KUTHAWA UCHIMO/KUUCHOKERA UCHIMO (Tit. 2:11-22; 1Akor. 6:9-11; 1Petr. 1:14-16).
Mkristu weniweni amathawa uchimo, akamana uchimo, amadana ndi chimo, ndipo sakondwera Mu uchimo, pakuti anabadwa mwatsopano, Ndipo amene amatha kupanga izi uzimu wake sukhala chimodzimodzi.

Mfundo yachisanu ndi chimodzi
-KULEKANA NDI ZAMIZIMU/KUPEMBEDZA MAFANO (Mach. 19:18-20; 1Atesal. 1:9).
Mkristu weniweni amasiya kukhulupirira mizimu, amalekana ndi zamizimu kaya kukhulupirira Oombeza, zonsezi mkristu weniweni amazisiya, pakuti anabadwa mwatsopano.

Mfundo yachisanu ndi chiwiri
-KUCHITIRA UMBONI ZA CHIKONDI CHA MULUNGU (Machit.1:8; 4:20; 1Petr.3:15)
Mkristu weniweni amawawidwa mtima chifukwa cha kutaika kwa anthu, ndipo amauza anzake za chikondi cha Mulungu (Yohan.3:16), Mkristu weniweni amalalikirako anzake, amawauza chimene mkristuyo amakhulupirira...
inunso teroni ndithu..

Nkhaniyi yalembedwa ndi Domingos Anthony. ...ngati mukufuna kumva zambiri tengani +258868947783.

Musaiwale kupanga like page yathuyi Kuti nkhani zina zimene ndikufuna kuponya zisakuphonyeni

08/03/2022

NKHANIYI NDI KOYAMBA KUKUUZANI
Part (2) two
Ndinanena kuti zimene zikuchitika kuchokera kwa azibusa enawa ndi zinthu zonyansa kwambiri.
M'busa winawake anatsirika tchalitch lake Kuti anthu azibwera ambiri, ndiponso azipanga zozwizitsa zosiyanasiyana, ndipo tsiku Lina m'busayo ankadzitamandira ponena kuti":"Sindikufuna kuti mumpingo muno aliyense azidwaladwala, matenda yalibenso mphamvu pa ife".
Abale dziwani Kuti ife tiri ndi LAPANSI pano, limene limathanso kudwala, ndipo even Timothy Mu baibulo muja ankadwala, Koma Paulo sanati Kuti ndikufuna ndikupempherere Kuti usakadwalenso.
Nkhani yaikulu imene ndinganene ndi yakuti:"Pamene tikupita kutchalitch tisamapitire kufuna kukaona zozwizitsa ayi, musamapitire Kuti mukalemere ayi, inu munati chifukwa mulibe mwana basi ndipite kwa aprophet akandipempherere, mmmm dziwani Kuti anthu ena mwa inu ndi amene munataya mimba muli ntsikana.
Ndingoti musamale ndi matchalitch angoti mbweewa, sikuti onsewa amaphunzitsa choonadi ayi, chimenenso mukuyenera kudziwa ndi chakuti, Ife akristu tikuyenera kupanga changu kufalitsa Uthenga Wabwino, tikuyenera kulalikira za Kulapa, ndipo kulapako ndiye machiritso aakulu.
M"busa Ngati ali ndi chiwanda, m'busayo akamapempherera anthu amakhalanso akugawa ziwanda kugawira anthu, nchifukwa chake tikhale maso Mu zonse, pakuti Ambuye anati:"Samalani ndi aneneri onyenga....Mateu7:15.
Sikuti Satana amafuna kukuchitsani mumpingo ayi, Koma amafuna kukuchotsani pamaso pa Mulungu, ndiyeno Pali mipingo ine yalibe chidwi chá kulalikira Uthenga wolapitsa, ndipo amapereka ufulu kwa anthu Kuti akhoza kumachimwako pang'ono no problem,
Koma inu funafunani mpingo imene ukhoza kukweza chikhulupiriro chanu mwa Uthenga wolalikidwa, musatsate machiritso Kaya Chuma chapansi pano, Koma konzani chuma chá m'mwamba kudzera pa Kulapa machimo anu,
Sikuti munthu olumala/opunduka sakalowa muufumu wakumwamba ayi, sikuti osabereka sakalowa muufumu wakumwamba ayi, Koma Ngati munataya mimba Mulungu adzakufunsani komwe ali anawo, Ngati mukakwanitsa kumulozera kudzala kumene munakatayira mimbayo.
Nchifukwa chake tikuyenera kukhala anthu a seriuos osati achibwana ayi, tikonze za Moyo wathu wauzimu,
CHINTHU CHINA TISAIWALE KUTI TSIKU LA KUFA KWATHU, pamene moyo Uli Ngati mpweya wotuluka mkamwa.

M'busa ameneyo anandifunsa Kuti:"Kodi ndi ndani m'dera ino amene akhoza kupempherera munthu ndi kuchira pompopompo?"
Ine ndinaona Kuti munthuyo akudzitama kwambiri, pakuti ndine mwana sangandimvetse, Koma fine.

08/03/2022

NKHANIYI NDI KOYAMBA KUKUUZANI
Ndinkacheza ndi munthu winawake ndipo iyeyo anati:" Abusa akwathu amakonda kunena kuti 'Ngati munthu wapemphereredwa ndipo wachira' kodi sungampangire chinachake wokupemphererayo?"
Ndipo munthuyo anapitiriza kuti:"Aaa zimenezi sizimandisangalatsa chifukwa si bwino kuti munthu ukapempherera mnzako uziyembekeza kuti akutamande, kaya kukupatsa zinthu, usayembekezere malipiro".
Chabwino, Kodi mukudziwa? mtumwi paulo pa 2 Akorinto 2:17 anati:" Pakuti sitikhala monga ambiriwo, akucita malonda nao mau a Mulungu; koma monga mwa coona mtima, koma monga mwa Mulungu pamaso pa Mulungu, tilankhula mwa Kristu.

Sikuti munthu ungayembekeze kuti ulandire malipiro pamene alalikira Uthenga, pakuti mtumwi paulo akuti 'Sitiri monga ambiriwo akuchita malonda ndi mau a Mulungu'.
Uthenga umalalikiridwa kwa ulere, koma pali azibusa ena adyera, amene amaopa Kulalikira Uthenga Wolapitsa anthu kuopa kutu mwina anthu akhoza kuthawa mumpingo kapeba akhoza kukhumudwa ndi kusiya kuwathandiza...koma please lalikirani Uthenga Wolapitsa anthu.
M'busa wina tsiku lina atafika ku tchalitch, basi anayamba kufunsa mamembala ake zimene amalota, basi aliyense amanena zomwe walota, then m"busa uja amatenga zinthu zooneka ngati mafuta odzola mkuyamba kupatsa mamembala ake kuti adzole.
Ndipo kenako tsiku lina amadzawafunsanso kuti akulota zotani!!
M"busa ameneyu amagulitsa zinthu zooneka ngati mafuta odzolazo pa ndalama yokwana 300 MT (Mozambique money), ndiponso mu chipinda chimene amapemphera mumakhala nyali zoyaka zimene zimazima zokha,
And mumakhala zinthu zambiri zochititsa mantha, ndipo kumbukirani kuti m"busayu amakakamiza mamembala ake kuti agule mafutawo,
Izi zikuonetsa kuti m"busayi akuchita malonda.
Ndisanapite patsogolo ndinene kuti:'Ku Satanic azibusa/azitumiki amapatsidwa zinthu zooneka ngati mafuta Ndipo amatchedwa kuti:"Touch and go"..kuti akasambitse mamembala ake, ndi kuwapatsa akadzole.
M"busayu amakonda kuonera channel ya aziprophet amene amakhala akuchiritsa/kuukitsa & kupanga zozizwitsa, ndipo iye akatha kuonera basi amalimbikitsika ndipo mpake amazipopa kuti kuti ine ndikhoza kuchiritsa munthu olo kuukitsa...koma Chenjerani.
Kodi mukudziwa kuti azibusa enawa anachita ubale ndi Satana kuti ayambe mpingowo? Ndipo azibusa otere salalikira za Kusiya uchimo, koma amalalikira za machiritso akuthupiwa, nchifukwa chake tikhale osamala kwambiri, inde mukhoza kudzola nafutawo, koma sangafufute machimo alimkatimo....

Ndikubwera ndi part 2 (Two).
Bless

07/03/2022

"Komatu zonse zimene zinandipindulira, zomwezo ndinaziyesa citayiko cifukwa ca Kristu. Komatu zeni zeninso ndiyesa zonse zikhale citayiko cifukwa ca mapambanidwe a cizindikiritso ca Kristu Yesu Ambuye wanga, cifukwa ca Iyeyu ndinatayikitsa zinthu zonse, ndipo ndiziyesa zapadzala, kuti ndikadzionjezere Kristu"__Afilipi 3:7-8.

Mtumwi Paulo akuti "Zonse zimene ndinkaziona ngati zaphindu kalekalelo, ndinaziyesa zopanda pake chifukwa cha Yesu Kristu"
Tonse tikudziwa bwino kuti "Mtumwi Paulo anali munthu woipa, wopha anthu, wachigololo, wochita zoipa koposa"
Koma atatembenuka mtima, zonse anaziyesa zopanda phindu, ndiponso zakudzala.
Abale ndi Alongo pamene inu ndi ine tinatembenuka mtima,Chifukwa cha Kristu tiziyese zakudzala, zopanda phindu, zosapindula zonse zoipa zimene tinkakonda, tisakondenso uchimo umene tinkakonda.
Tilipo lero anthu ambiri, amene timapita kumpingo kukapemphera, koma njira zathu ndi zokhotakhota, ndi zoipa, Ngati inu ndi ine kale timkakonda kuonela zolaula, pamene tiyamba kupemphera tiyese Zolaula kukhala zakudzala, Ngati kale inu munkakonda kupanga mastubation, pamene inu mwayamba kupemphera musiye kupanga Ma********on.

Mtumwi paulo akuti: "Inde, zenizeninso ndiziyesa chitaiko cha Kristu"
Inunso abale ndi alongo zonse zimene mumanyadira pansi pano muziyese zakudzala chifukwa cha Kristu,

alipo ena amene amadzitamandira pamene ali mu uchimo mkumati"Ziri bwino,ziri bwino"... Koma Chimene Mulungu akufuna ndi chakuti mudane ndi uchimo, muyese uchimo chinthu cha kudzala.

Mtumwi Paulo akuti:" chifukwa cha chizindikiritso cha Yesu Kristu zonse ndiziyesa za kudzala"
Abale ndi alongo chifukwa chakuti ife tinadziwa Yesu, tinazindikira Yesu, Tiyese zonse kukhala zakudzala,
ngati inu abale anga mudazindikira Yesu, muziyese zonse kukhala zakudzala chifukwa cha Kristu, Musamalakelake zoipa zimene munazisiya kale.

"Pamene ndinali mwana ndinkayankhula ngati mwana, ndinkaganiza ngati mwana, ndinkalingalira ngati mwana. Koma nditakula, zonse zachibwana ndinazisiya"__
1 Akorinto 13:11

Mtumwi Paulo akuti:"Pamene ndinali mwana.....ndinkapanga zinthu ngati mwana..... Koma pamene ndinakula zonse zachibwana ndinazisiya"

Pamene inu munali wachikunja munkapanga zinthu mwachikunja, munkakonda zachikunja. ....koma pamene mwakula (Mwatembenuka mtima) musiye zonse zachibwana,
Koma ena mulipo pano, simuonetsa kuti ndinu mkristu, mudakali mwana wakhanda, ndipo mudakali kupanga zachibwana, Koma mtumwi paulo akuti:"Zonse ndiziyesa zakudzala chifukwa chaK

Address

Mnsambachikho
Lilongwe

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when MPhunzitsi wa mpingo posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share

Category