18/07/2026
TIWADZIWE A DEACON ATHU
Deacon Nathan Banda, a Chipani Cha Capuchin Franciscans ( OFM.Cap) amachokera ku St. John Paul II church, Chindande, (Ludzi) Parish. Anabadwa m'banja la ana asanu ndi atatu; atsikana asanu ndi anyamata atatu ndipo iwo omaliza pobadwa.
Maphunziro a Primary anamphunzira sukuku ya Chidzibwe, Chindande Mchinji. Pomwe Secondary anaphunzira pa Magawa, Secondary School, Kamwendo Mchinji.
Anayamba ulendo wao wochita maphunziro a unsembe pa 13 February 2016, ku St.Francis Formation House, Ntcheu,Dedza Diocese.
Kenaka mu mchaka cha 2017 anakapitiliza maphunzilowa ku Zambia , Camerino Novitiate House, komanso ku St. Bonaventure University kwa zaka zitatu maphunziro a Philosophy. Pambuyo pake anakamaliza maphunziro awo a Theology ku Tangaza University Nairobi Kenya, kuchoka Chaka Cha 2021-2025.
Mawu owatsogolera ndi akuti " Sindinu munandisankha koma ndine ndinakusakha" (Yohane 15:16)