Kauma Baptist Church KBC

Kauma Baptist Church KBC A place where Faith, Hope and Love abounds. (1 Cor. 13:13)

Mwa chimwemwe tithokoze achinyamata anthu amene anakatiimilira ku msonkhano, Central Region Youth Conference, omwe unach...
31/08/2026

Mwa chimwemwe tithokoze achinyamata anthu amene anakatiimilira ku msonkhano, Central Region Youth Conference, omwe unachitikila ku Baptist College kuyambila pa 28 mpaka pa 30 August.

Ana a Isaka ife ndife okondwa, ndipo timakunyadilani pa ntchito yotamandika imene mukugwila limodzi ndi Mulungu.

Ambuye akudalitseni

Rev Kamkwamba

Sunday service on 23 August 2026YOUTH DAYBuku: Yobu 2:1-10MULUNGU AKUGWILA NTCHITO INENSO NDIGWILA NAYEMunthu ogwila ntc...
27/08/2026

Sunday service on 23 August 2026
YOUTH DAY
Buku: Yobu 2:1-10

MULUNGU AKUGWILA NTCHITO INENSO NDIGWILA NAYE

Munthu ogwila ntchito ndi Mulungu amafunika kukhala olimba mtima

1. Ogwila ntchito ndi mulungu amakumana ndi mavuto
* yobu anakumana ndi mavuto ku chapter 1, ana ake kufa, chuma kutha thupi lonse zilonda koma analimba be mtima kukhulupilika kwa Mulungu
* Akhristuso adzazunzika mu nijra zosiyanasiyana chifukwa cha dzina la Mulungu
* Ngati sistilimba mtima, ntchito ya Mulungu ititkanika

2. Okhulupilira amakumana ndi mayesero
* Okuyesa amakhala abwenzi amene akuzungulira
* Tiyeni tidzisankha bwino anthu ocheza nawo
* Nthawi zina malankhulidwe athu amakhala yeselo kwa ena, tidzisamala ndi amalnkhulidwe athu, milomo imoanonga ngati tilankhula monga opusa.

3. Nchifukwa chani tikuyenela kulimba mtima
* Kulimba mtima ndi lamulo limene Mulungu mwini akupeleka kwa ogwila naye ntchito
* Yoswa 1:9, Mulungu akumuuza Yoswa kuti anachita chomulamulira kuti akhale olimba mtima.
* Daniel 3:17-19, anyamata awa analimba mtima osafuna kukondweletsa munthu koma Mulungu

Tikhale olimba mtima pakutumikila ndi Mulungu

by Brother Rodwell

Sunday service on 16/08/26Buku :Aefeso 5 vs 1 to 21MULUNGU AKUGWIRA NTCHITO INESO NDIGWIRA NAYE Zimene MULUNGU amamupats...
17/08/2026

Sunday service on 16/08/26

Buku :Aefeso 5 vs 1 to 21

MULUNGU AKUGWIRA NTCHITO INESO NDIGWIRA NAYE

Zimene MULUNGU amamupatsa munthu amene akugwira ntchito ndi MULUNGU

1 Amamupatsa nzeru
✓Munthu amene akugwira ntchito ndi MULUNGU amafunika nzeru kuti adziwe kusiyanitsa chabwino ndi choipa komanso kupanga zisankha zabwino
✓munthu amene akugwira ntchito ndi MULUNGU sayenera kudalira nzeru zake zokha, ayenera kufunafuna kufunafuna nzeru zochokera kwa MULUNGU hallelujah

2) MULUNGU amakupatsa ulemelero weniweni

✓ulemelero umene MULUNGU amakupatsa sikungokhala ndi ndalama kapena kutchuka ndi Chisomo ndi kukwezedwa kumene kumachokera kwa MULUNGU hallelujah
✓zimene MULUNGU wapereka zimakhala ndi cholinga

✓moyo wako umayamba kusiyana ndi wakale komanso umakhala chitsanzo kwa ena hallelujah
✓Anthu amayamba kuona khristu mwa iwe

3) MULUNGU amapereka mphamvu ya mzimu woyera
✓ pamene ukugwira ntchito ndi MULUNGU samakusiyani kuti mugwire nokhayi ,amakupatsa mzimu woyera kuti akhale mphamvu yanu
✓pamene mayesero abwera amakuthandiza kupilira
✓pamene mukuchita mantha amakupatsani kulimbika mtima
✓pamene simukudziwa chochita amakutsogolerani hallelujah

Amapereka umboni
✓umboni sikungonena kuti ndimagwira ntchito ndi MULUNGU
✓munthu amene akugwira ntchito ndi MULUNGU ayenera kukhala ndi moyo umene umapereka umboni kuti MULUNGU Ali naye
✓anthu ayenera kuona umulungu mwa iwe pa makhalidwe ako
✓ komanso pakuleza mtima kwako hallelujah

Done by pastor Emanuel Yòtam

@ KBC Media

"Mwaswera bwanji? Tisaiwale mawa tukasosa pamalo atsopano a mpingo wathu. Tiyeni tonse tikumane 6.00 mmawa ku church.Osa...
14/08/2026

"Mwaswera bwanji?
Tisaiwale mawa tukasosa pamalo atsopano a mpingo wathu.
Tiyeni tonse tikumane 6.00 mmawa ku church.
Osaiwala kutengako zida zogwilira ntchito ngati muli nazo."

Rev. Kamkwamba
(Lead Pastor)

Uthenga9 August 26Hagai 1:1-10"Zotsatila za kuchita nao zimene Mulungu akufuna"Lingalirani mozama za njira zanu* Timalin...
11/08/2026

Uthenga
9 August 26
Hagai 1:1-10

"Zotsatila za kuchita nao zimene Mulungu akufuna"

Lingalirani mozama za njira zanu
* Timalingalira mozama za zinthu zathu zina zonse koma sitilingalira mozama za kupembedza kwathu
* Tichotse malingaliro pa zinthu zathu ndikuika pa za Mulungu
* Za Mulungu ndizofunika kuziika patsogolo

1. Mulungu amalemekedwa
* Mulungu akuwauza kuti mukakwela ndi kumanga nyumba yanga kudzandikomela ndipo ndidzalemekezedwa
* Mulungu amalemekezedwa tikaika chidwi chathu pa zimene zikumukomela iye
* Tilemekeze Mulungu pochita zimene iye akufuna osati zomwe ife tikufuna

2. Ntchito ya Mulungu sagwila munthu mmodzi
* Ntchito ya Mulungu siyamunthu mmodzi
* Tikabweletsa chuma chathu, nzeru zathu, kuthekela kwathu ndi mphatso zathu tidzamanga ufumu wa Mulungu.
* Wina aliyense wa ife ndiofunika

3. Mulungu amakhala pakati pathu
* Yesu akuwapatsa ntchito ophunzila kuti amuke nakalalikile, anawauza kuti adzakhala pamodzi nao masiku onse
* Tikamagwila ntchito ndi Mulungu amakhala pakati pathu
* Mulungu akulonjeza kupezeka pamene pali awiri pali atatu oitanila pa dzina lake.
* Kumadziwika kuti mau ake ndioona akakhala pakati pathu pamene tikusanalira za ntchito yake.

By Rev. Kamkwamba
Lead Pastor

Media team

Uthenga 2 August 26 Machitidwe Atumwi 28:1-10"Phindu lakugwila ntchito ndi Mulungu"1. Mulungu amakhala muombolo* Paulo a...
03/08/2026

Uthenga
2 August 26
Machitidwe Atumwi 28:1-10

"Phindu lakugwila ntchito ndi Mulungu"

1. Mulungu amakhala muombolo

* Paulo akanatha kufela panyanja patauka namondwe ndi kuswa ngalawa, koma Mulungu anamuombola.
* Paulo akatha kufa ndi ululu wa njoka imene inamuluma, koma Mulungu anamuombola.

2. Mulungu amaonetsa ekha chilungamo chake mwa ife

* Itamuluma njoka, anthu anamunenela kuti ndi ochimwa ndipo akuyenela kufa ndithu.
* Paulo sanayankhe kapena kudzifotokoza ekha kuti ndi olungama ai, kufikila anthu omwe aja ananena kuti uyu ndi Mulungu.
* Pamene akhristu tikugwila ntchito ndi Mulungu nkumabeza mau kwa iwo amene akunenela zoipa, timanyozetsa dzina la Mulungu.
* Paulo sanafune kunyozetsa dzina la Mulungu, ndipo Mulungu anaonetsela chilungamo chake mwa Paulo.

3. Mulungu amadzutsa anthu kuti akhale thandizo
* Publio amene anali osamudziwa Mulungu anabwela nakhala thandizo kwa Paulo.
* Atamuthandiza Paulo, banja lake linalandila machilitso
* Ukamagwila ntchito ndi Mulungu umakhala gwelo la madalitso pa banja lako ngakhaleso ku mtundu wakwanu.

*Moyo wa Paulo unatsimikizika kutumikila Mulungu, olo mavuto anali ochuluka koma sanabweleleso m'mbuyo.
*Akhristu tikhale anthu olapa mtima, olo zitavuta bwanji, tisabweleleso ku uchimo umene tinachokako kale.

By Mrs Chimbende

Media

Uthenga 26 July 26 Machitidwe Atumwi 23:12-35"Phindu lakuyenda ndi Mulungu"1. Mulungu amativumbulutsila zobisika (16)* A...
27/07/2026

Uthenga
26 July 26
Machitidwe Atumwi 23:12-35

"Phindu lakuyenda ndi Mulungu"

1. Mulungu amativumbulutsila zobisika (16)
* Ayuda 40 anasala kudya ndi zolinga zolakwika, amapemphera kuti Paulo afe.
*Mulungu anatetezela uthenga wake kuti ukafukile patali.
*Mulungu anagwilitsa ntchito kamwana kuti aike poyera upo omwe akuluakulu anapangila Paulo.
*Ana ndi anthu ofunikila pamaso pa Mulungu
*Komaso Paulo anali pa ubale wabwino ndi abale ake komaso anthu omuzungulira.
* Odala munthu amene ali pa ubale wabwino ndi Mulungu chifukwa adzakhala ndi ubale wabwino ndi anthu omuzungulira

2. Mulungu amatitetezela komanso kutikweza (v23-35)
*Paulo anayenda ndi asilikali 470 omutetezela.
*Mulungu anapeleka convoy kwa paulo munthu oti chikhalire ankayenda pansi koma tsiku ili anayenda pa horse.
* Chitetezo chathu nchosayamba, Mulungu wathu ndi owina.
*Mulungu anamukweza paulo.
*Kalata wa Paulo inalembedwa kuti analibe tchimo loyenela imfa.
*Moyo wathu wa tsiku ndi tsiku ndi kalata.
* Kodi kalata wathu walembedwa kuti chani?

By Mama T. Kamkwamba

Osajomba ku churchAuzeni a neighbor awauze anzawo kuti anzawowo awuzenso Ena
24/07/2026

Osajomba ku church
Auzeni a neighbor awauze anzawo kuti anzawowo awuzenso Ena

Sunday 19th July 2026Macitidwe 3 vs 1-10. Mutu: Mulungu Akamagwira Ncthito Ndi Anthu Ake Chimachitika Ndi Chani? 1. Amaw...
19/07/2026

Sunday 19th July 2026
Macitidwe 3 vs 1-10.
Mutu: Mulungu Akamagwira Ncthito Ndi Anthu Ake Chimachitika Ndi Chani?

1. Amawona zinthu mosiyana.
- Akhristu tiziwona zinthu mosiyana ndi dziko.
- Petro ndi Yohane atadzadzidwa ndi mzimu woyera akudutsa pakhomo lakachisi anawona munthu wopepha mosiyana ndi ena kuti munthuyo samasowekela ndalama yokha.
- Tikadzadzidwa ndi mzimu woyera timawona mavuto mkati mwathu amene Mulungu samukondweletsa.
- Akhristu tisamawone zimene anthu akunena za kunja kwathu koma tiziwona zamkati mwathu zimene Mulungu sakondwera nazo.
2. Mulungu amawonetsera mphamvu yake pamene pephero likupezeka.
- Pemphero limamulumikizitsa mkhristu ndi Mulungu. Ndipo Akhristu tiyenela kukhala m'pemphero kuti zisisi zina ziululidwe Kwa ife.
- Sitingawone mphamvu ya mzimu woyera ngati sitiyima pa Pemphero.
- Mkhristu amene sadalira Pemphero salumikizika ndi Mulungu ndipo phindu lake silidziwika.
- Amene salumikizika ndi Mulungu sadziwa chili nkati mwawo kotero ndi womvetsa chisoni Ndipo ngati Akhristu tiyenela kukhala wosamala za zomwe zili mkati mwathu.
3. Amawonetsera ndi dziko lapansi.
- Anthu woyenda ndi Yesu amawonedwa mosiyana ndi dziko lapansi chifukwa ulemerelo wa Mulungu umawoneka mwa iwo.
- Amakhala ndi mbiri yosiyana ndi yakale.
- Ngati Akhristu tiyenela kudziwa kuti padziko lapansi palibe cha chinsinsi.
- Mulungu amayembekezela kuti dziko lione umboni kuchokera kwa ife. Mkhristu wodzadzidwa ndi mzimu woyera amapezeka mkachisi. Mkhristu amawona zinthu mosiyana.

Reverend Kamkwamba. (Lead Pastor)

Kauma Baptist Church KBC

Uthenga wa Lero Sunday 12 July 2026Machitidwe 2 vs 42-47Mutu: Makhalidwe a mpingo umene Mulungu amagwira nawo ncthito. 1...
12/07/2026

Uthenga wa Lero
Sunday 12 July 2026
Machitidwe 2 vs 42-47

Mutu: Makhalidwe a mpingo umene Mulungu amagwira nawo ncthito.

1. Mpingo wokhala ndi njala yakumva mau a Mulungu.
- Anthu ake amakhala akufunitsitsa kudziwa zambiri za chifuniro cha Mulungu.
- Mu church tiyenela kukhala anthu wotumikila m***a mtima ndi motsogozedwa ndi Mulungu osat ndi nzeru zathu.
- Mulungu sakhala mu chinyumba koma mitima ya iwo akumufuna iye.
- khalidwe la anthu wopezeka mu church lizipangitsa ena kufuna kubwera chifupi ndi Mulungu.

MOYO WANGA NDI UTHENGA WABWINO

Rev. Kamkwamba (Lead Pastor)

Address

Madalitso Rodgers
Lilongwe

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Kauma Baptist Church KBC posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Shortcuts

Share

Category